< Yohane 7 >

1 Zitatha izi Yesu anayendayenda mu Galileya, ndi cholinga chakuti asafike ku Yudeya chifukwa Ayuda kumeneko amadikira kuti amuphe.
And after these things was walking Jesus in Galilee; not for He was desiring in Judea to walk, because were seeking Him the Jews to kill.
2 Koma phwando la Ayuda lamisasa litayandikira,
Was now near the feast of the Jews of Booths.
3 abale a Yesu anati kwa Iye, “Inu muyenera kuchoka kuno ndi kupita ku Yudeya, kuti ophunzira anu akaone zodabwitsa zomwe mumachita.
Said therefore to Him the brothers of Him; do depart from here and do go into Judea so that also the disciples of You (will see *N+kO) of You the works that You are doing;
4 Palibe wina aliyense amene amafuna kukhala wodziwika amachita zinthu mseri. Popeza Inu mukuchita zinthu izi, mudzionetsere nokha ku dziko la pansi.”
No [one] for anything in secret does and seeks himself in public to be; If these things You do, do show Yourself to the world.
5 Pakuti ngakhale abale ake omwe sanamukhulupirire.
Not even for the brothers of Him were believing in Him.
6 Choncho Yesu anawawuza iwo kuti, “Nthawi yanga yoyenera sinafike; kwa inu nthawi ina iliyonse ndi yoyenera.
Says therefore to them Jesus; The time for Me not yet is come, but the time of you always is ready.
7 Dziko lapansi silingakudeni inu, koma limandida Ine chifukwa Ine ndimachitira umboni kuti zomwe limachita ndi zoyipa.
Not is able the world to hate you, Me myself however it hates, because I myself bear witness concerning it that the works of it evil are.
8 Inu pitani kuphwando. Ine sindipita tsopano kuphwando ili chifukwa kwa Ine nthawi yoyenera sinafike.”
You yourselves do go up to feast (this; *k) I myself (not *N+kO) am going up to feast this, for My time not yet has been fulfilled.
9 Atanena izi, Iye anakhalabe mu Galileya.
These things now having said (He himself *N+KO) He remained in Galilee.
10 Komabe, abale ake atanyamuka kupita kuphwando, Iye anapitanso, osati moonekera, koma mseri.
When however had gone up the brothers of Him to the feast, then also He himself went up not openly but as in secret.
11 Tsopano kuphwandoko Ayuda anakamufunafuna ndi kumafunsana kuti, “Kodi munthu ameneyu ali kuti?”
The therefore Jews were seeking Him at the feast and were saying; Where is He?
12 Pakuti pa chigulu cha anthu panali kunongʼona ponseponse za Iye. Ena ankanena kuti, “Iye ndi munthu wabwino.” Ena ankayankha kuti, “Ayi, Iye amanamiza anthu.”
And murmuring about Him there was much among the crowds. Some indeed were saying that Good He is, Others however were saying; No, but He deceives the people.
13 Koma panalibe amene ankanena kalikonse poyera za Iye chifukwa choopa Ayuda.
No [one] however publicly was speaking about Him because of the fear of the Jews.
14 Phwando lili pakatikati, Yesu anapita ku bwalo la Nyumba ya Mulungu ndi kuyamba kuphunzitsa.
Now also of the feast being in the middle went up Jesus into the temple and was teaching.
15 Ayuda anadabwa ndipo anafunsa kuti, “Kodi munthu uyu nzeru izi anazitenga kuti popanda kuphunzira?”
(and *k) Were marveling (then *NO) the Jews saying; How this one writings knows not having studied?
16 Yesu anayankha kuti, “Chiphunzitso changa si cha Ine ndekha. Chimachokera kwa Iye amene anandituma.
Answered (therefore *NO) them Jesus and said: My teaching not is of Myself but of the [One who] having sent Me;
17 Ngati munthu asankha kuchita chifuniro cha Mulungu, adzazindikira ngati chiphunzitso changa nʼchochokera kwa Mulungu kapena ngati ndi mwa Ine ndekha.
If anyone shall desire the will of Him to do, he will know concerning the teaching whether from God it is or I myself from Myself speak.
18 Iye amene amayankhula za Iye mwini amatero kuti adzipezere ulemu, koma amene amagwira ntchito kuti amene anamutuma alandire ulemu, ameneyo ndiye munthu woona; mu mtima mwake mulibe chinyengo chilichonse.
The [one] from himself speaking the glory [their] own seeks; the [One] however seeking the glory of the [One who] having sent Him, He true is, and unrighteousness in Him not is.
19 Kodi Mose sanakupatseni lamulo? Komatu palibe ndi mmodzi yemwe mwa inu amene akusunga lamulo. Nʼchifukwa chiyani mukufuna kundipha Ine?”
Not Moses (has given *NK+o) to you the law? and no [one] of you keeps the law! Why Me do you seek to kill?
20 Gulu la anthu linayankha kuti, “Iwe ndiye wagwidwa ndi ziwanda. Ndani akufuna kukupha?”
Answered the crowd (and said: *k) A demon You have; who You seeks to kill?
21 Yesu anawawuza kuti, “Ine ndinachita chodabwitsa chimodzi ndipo inu mwadabwa.
Answered Jesus and said to them; One work I did, and all you marvel.
22 Koma, chifukwa chakuti Mose anakulamulani kuti muzichita mdulidwe (ngakhale kuti sunachokere kwa Mose, koma kwa makolo anu), inuyo mumachita mdulidwe mwana tsiku la Sabata.
Because of this: Moses has given you circumcision — not that of Moses it is but of the fathers — also on Sabbath you circumcise a man.
23 Tsopano ngati mwana angachite mdulidwe pa Sabata kuti lamulo la Mose lisaswedwe, nʼchifukwa chiyani mukundipsera mtima chifukwa chochiritsa munthu pa Sabata?
If circumcision receives a man on Sabbath so that not shall be broken the law of Moses, with Me myself are you angry because entirely a man sound I made on [the] Sabbath?
24 Musamaweruze potengera maonekedwe chabe, koma weruzani molungama.”
Not do judge according to appearance, but the righteous judgment (do judge. *N+kO)
25 Pa nthawi imeneyi anthu ena a ku Yerusalemu anayamba kufunsana kuti, “Kodi uyu si munthu uja akufuna kumuphayu?
Were saying therefore some of those of Jerusalem; Not this is he whom they seek to kill?
26 Uyu ali apa, kuyankhula poyera, ndipo iwo sakunena kanthu kwa Iye. Kodi olamulira atsimikizadi kuti Iye ndi Khristu?
And behold publicly He speaks, and no [thing] to Him they say. otherwise otherwise Truly have recognized the rulers that this is (truly *K) the Christ?
27 Koma ife tikudziwa kumene achokera munthuyu; pamene Khristu adzabwere, palibe amene adzadziwa kumene akuchokera.”
But this [man] we know from where He is; The however Christ whenever He may come, no [one] knows from where He is.
28 Kenaka Yesu, akuphunzitsabe mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu anafuwula kuti, “Zoona, mukundidziwa Ine, ndipo mukudziwa kumene ndikuchokera. Ine sindili pano mwa Ine ndekha, koma Iye amene anandituma Ine ndi woona. Inu simukumudziwa,
Cried out therefore in the temple teaching Jesus and saying; Me Me you know and you know from where I am; and of Myself not I have come, but is true the [One] having sent Me whom you yourselves not know;
29 koma Ine ndikumudziwa chifukwa ndichokera kwa Iyeyo ndipo ndiye amene anandituma Ine.”
I myself (now *k) know Him, because from Him I am, and He and He Me sent.
30 Chifukwa cha izi iwo anayesa kumugwira Iye, koma palibe aliyense amene anayika dzanja lake pa Iye, chifukwa nthawi yake inali isanafike.
They were seeking therefore Him to take, but no [one] laid upon Him the hand, because not yet had come the hour of Him.
31 Komabe, ambiri a mʼchigulucho anamukhulupirira Iye. Iwo anati, “Kodi pamene Khristu abwera, adzachita zizindikiro zodabwitsa zambiri kuposa munthu uyu?”
Out of the crowd now many believed in Him and were saying (that: *k) The Christ When He may come, (Surely not *N+kO) more signs (than these things *k) will He do than this [man] has done?
32 Afarisi anamva chigulucho chikunongʼona zinthu zotere za Iye. Kenaka akulu a ansembe ndi Afarisi anatumiza asilikali a mʼNyumba ya Mulungu kuti akamumange Iye.
Heard the Pharisees the crowd murmuring about Him these things, and sent the chief priests and the Pharisees officers that they may seize Him.
33 Yesu anati, “Ine ndili ndi inu kwa kanthawi kochepa chabe, ndipo kenaka ndizipita kwa Iye amene anandituma Ine.
Said therefore (to them *k) Jesus; Yet time a little with you I am and I go to the [One] having sent Me.
34 Inu mudzandifunafuna koma simudzandipeza; ndipo kumene Ine ndili inu simungathe kubwera.”
You will seek Me and not will find Me, and where am I myself you yourselves not are able to come.
35 Ayuda anati kwa wina ndi mnzake, “Kodi munthu uyu akuganizira zoti apite kuti kumene ife sitingathe kumupeza Iye? Kodi Iye adzapita kumene anthu amakhala mobalalikana pakati pa Agriki, ndi kuphunzitsa Agriki?
Said therefore the Jews among themselves; Where He is about to go that we ourselves not will find Him? Surely to the Dispersion among the Greeks is He about to go and to teach the Greeks?
36 Kodi Iye amatanthauza chiyani pamene anati, ‘Inu mudzandifunafuna koma simudzandipeza,’ ndi ‘Kumene Ine ndili, inu simungathe kubwera?’”
What is word this that He said; You will seek Me and not will find (Me, *NK) and Where am I myself you yourselves not are able to come?
37 Pa tsiku lomaliza ndi lalikulu kwambiri laphwando, Yesu anayimirira nafuwula nati, “Ngati munthu ali ndi ludzu, abwere kwa Ine kuti adzamwe.
In now the last day the great [day] of the feast had stood Jesus and cried out saying; If anyone shall thirst, he should come to Me and should drink.
38 Malemba kuti ‘Aliyense amene akhulupirira Ine, mitsinje yamadzi amoyo idzatuluka kuchokera mʼkati mwake.’”
The [one] believing in Me myself, even as has said the Scripture: Rivers out of the belly of him will flow of water living.
39 Ponena izi Iye amatanthauza Mzimu Woyera, amene adzalandire amene amakhulupirira Iye. Pa nthawiyi nʼkuti Mzimu Woyera asanaperekedwe, pakuti Yesu anali asanalemekezedwe.
This now He said concerning the Spirit (which *N+kO) were about to receive those (having believed *N+kO) in Him; not yet for was [the] Spirit (Holy *KO) (given *O) because Jesus (not yet *N+kO) was glorified.
40 Pakumva mawu ake, ena a anthuwo anati, “Zoonadi munthu uyu ndi mneneri.”
(many *K) from the crowd therefore having heard (the *N+kO) (words *N+KO) these were saying (that: *o) This is truly the Prophet.
41 Ena anati, “Iye ndiye Khristu.” Komanso ena anafunsa kuti, “Kodi Khristu angachokere bwanji ku Galileya?
Others were saying; This is the Christ; (Those *N+kO) however were saying; Surely not for out of Galilee the Christ comes?
42 Kodi Malemba samanena kuti Khristu adzachokera mʼbanja la Davide, ndi ku Betelehemu mu mzinda umene Davide anakhalamo?”
(Surely *N+kO) the Scripture has said that out of the seed of David and from Bethlehem the village where was David comes the Christ
43 Kotero anthu anagawikana chifukwa cha Yesu.
A division therefore occurred in the crowd because of Him.
44 Ena anafuna kumugwira Iye, koma palibe amene anayika dzanja pa Iye.
Some now were desiring of them to seize Him, but no [one] (laid *NK+o) on Him the hands.
45 Pomaliza asilikali a mʼNyumba ya Mulungu anabwerera kwa akulu a ansembe ndi Afarisi amene anawafunsa iwo kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani simunamugwire Iye?”
Came therefore the officers to the chief priests and Pharisees, and said to them that; Because of why not did you bring Him?
46 Asilikali aja anati, “Palibe wina amene anayankhula ngati Munthu ameneyo nʼkale lonse.”
Answered the officers; Never spoke like this a man (as *ko) (this *KO) (man. *KO)
47 Afarisi anawadzudzula nati, “Kodi mukutanthauza kuti Iye anakunamizani inunso?”
Answered therefore them the Pharisees; Surely not also you yourselves have been deceived?
48 “Kodi alipo ena a olamulira kapena a Afarisi, anamukhulupirira Iye?
Surely not any of the rulers has believed on Him or of the Pharisees?
49 Ayi! Koma gulu limene silidziwa malamulo ndi lotembereredwa.”
But crowd this not knowing the law (cursed *N+kO) are.
50 Nekodimo, amene anapita kwa Yesu poyamba paja ndipo anali mmodzi wa iwo, anafunsa kuti,
Says Nicodemus to them, the [one] having come (at night *K) to Him (the *N) (former *NO) one being of them;
51 “Kodi lamulo lathu limatsutsa munthu popanda kumva mbali yake kuti tipeze chimene wachita?”
Surely not the law of us does judge the man only unless it shall hear (first *N+kO) from him and may know what he does?
52 Iwo anayankha kuti, “Kodi ndiwenso wochokera ku Galileya? Tayangʼananso, ndipo udzapeza kuti mneneri sachokera ku Galileya.”
They answered and they said to him; Surely not also you yourself from Galilee are? do search and do see that out of Galilee a prophet not (is raised. *N+kO)
53 Kenaka onse anachoka, napita kwawo.
(And *KO) (he went *K+o) (each to the home of him, *KO)

< Yohane 7 >