< Yobu 9 >

1 Ndipo Yobu anayankha kuti,
Joob answeride, and seide, Verili Y woot, that it is so,
2 “Zoonadi, ndikudziwa kuti zimenezi ndi zoona. Koma munthu angathe bwanji kukhala wolungama pamaso pa Mulungu?
and that a man comparisound to God schal not be maad iust.
3 Ngakhale wina atafuna kutsutsana naye, Iye sangamuyankhe munthuyo ngakhale mawu amodzi omwe.
If he wole stryue with God, he may not answere to God oon for a thousynde.
4 Mulungu ndi wa nzeru zambiri ndipo mphamvu zake ndi zochuluka. Ndani analimbana naye popanda kupwetekeka?
He is wiys in herte, and strong in myyt; who ayenstood hym, and hadde pees?
5 Iye amasuntha mapiri, mapiriwo osadziwa, ndipo amawagubuduza ali wokwiya.
Which bar hillis fro o place to anothir, and thei wisten not; whiche he distriede in his strong veniaunce.
6 Iye amagwedeza dziko lapansi kulisuntha pamalo pake ndipo amanjenjemeretsa mizati yake.
Which stirith the erthe fro his place, and the pilers therof schulen `be schakun togidere.
7 Iye amayankhula ndi dzuwa ndipo siliwala; Iyeyo amaphimba kuwala kwa nyenyezi.
Which comaundith to the sunne, and it risith not; and he closith the sterris, as vndur a signet.
8 Ndi Mulungu yekha amene anayala mayiko akumwamba ndipo amayenda pa mafunde a pa nyanja.
Which aloone stretchith forth heuenes, and goith on the wawis of the see.
9 Iye ndiye mlengi wa nyenyezi zamlalangʼamba ndi akamwiniatsatana, nsangwe ndi kumpotosimpita.
Which makith Ariture, and Orionas, and Hiadas, `that is, seuene sterris, and the innere thingis of the south.
10 Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingawerengeke.
Which makith grete thingis, and that moun not be souyt out, and wondurful thingis, of whiche is noon noumbre.
11 Akapita pafupi ndi ine sindingathe kumuona; akadutsa, sindingathe kumuzindikira.
If he cometh to me, `that is, bi his grace, Y schal not se hym; if he goith awey, `that is, in withdrawynge his grace, Y schal not vndurstonde.
12 Ngati Iye alanda zinthu, ndani angathe kumuletsa? Ndani anganene kwa Iye kuti, ‘Mukuchita chiyani?’
If he axith sodeynli, who schal answere to hym? ethir who may seie to hym, Whi doist thou so?
13 Mulungu sabweza mkwiyo wake; ngakhale gulu lankhondo la Rahabe linawerama pa mapazi ake.
`God is he, whos wraththe no man may withstonde; and vndur whom thei ben bowid, that beren the world.
14 “Nanga ine ndingathe kukangana naye bwanji? Ndingawapeze kuti mawu oti nʼkutsutsana naye?
Hou greet am Y, that Y answere to hym, and speke bi my wordis with hym?
15 Ngakhale nditakhala wosalakwa, sindingamuyankhe; ndikanangopempha chifundo kwa woweruza wanga.
Which also schal not answere, thouy Y haue ony thing iust; but Y schal biseche my iuge.
16 Ngakhale ndikanamuyitana ndipo Iye ndi kuvomera, sindikhulupirira kuti akanamva mawu angawo.
And whanne he hath herd me inwardli clepynge, Y bileue not, that he hath herd my vois.
17 Iye akanandikantha ndi mphepo yamkuntho, ndipo akanandipweteka popanda chifukwa.
For in a whirlewynd he schal al to-breke me, and he schal multiplie my woundis, yhe, without cause.
18 Mulungu sakanandilola kuti ndipumenso koma akanandichulukitsira zowawa.
He grauntith not, that my spirit haue reste, and he fillith me with bittirnesses.
19 Tikanena za mphamvu, Iye ndi wamphamvudi! Ndipo tikanena za chiweruzo cholungama, ndani angamuzenge mlandu?
If strengthe is souyt, `he is moost strong; if equyte of doom is souyt, no man dar yelde witnessynge for me.
20 Ngakhale ndikanakhala wosalakwa, zoyankhula zanga zikananditsutsa; ndikanakhala wopanda cholakwa, pakamwa panga pakanandipeza wolakwa.
If Y wole make me iust, my mouth schal dampne me; if Y schal schewe me innocent, he schal preue me a schrewe.
21 “Ngakhale ine ndili wosalakwa, sindidziyenereza ndekha; moyo wanga ndimawupeputsa.
Yhe, thouy Y am symple, my soule schal not knowe this same thing; and it schal anoye me of my lijf.
22 Zonse nʼzofanana; nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Iye amawononga anthu osalakwa ndi anthu oyipa omwe.’
O thing is, which Y spak, he schal waste `bi deth also the innocent and wickid man.
23 Pamene mkwapulo ubweretsa imfa yadzidzidzi, Iye amaseka tsoka la munthu wosalakwayo.
If he betith, sle he onys, and leiye he not of the peynes of innocent men.
24 Pamene dziko lagwa mʼmanja mwa anthu oyipa Iye amawatseka maso anthu oweruza dzikolo. Ngati si Iyeyo, nanga ndani?
The erthe is youun in to the hondis of the wickid; he hilith the face of iugis; that if he is not, who therfor is?
25 “Masiku anga ndi othamanga kwambiri kupambana munthu waliwiro; masikuwo amapita ine osaonapo zabwino.
Mi daies weren swiftere than a corour; thei fledden, and sien not good.
26 Amayenda ngati mabwato a njedza pa nyanja, ngati mphungu zothamangira nyama zoti zidye.
Thei passiden as schippis berynge applis, as an egle fleynge to mete.
27 Nʼtanena kuti, ‘Ndidzayiwala madandawulo anga, ndidzasintha nkhope yanga ndipo ndidzasekerera,’
Whanne Y seie, Y schal not speke so; Y chaunge my face, and Y am turmentid with sorewe.
28 ndikuopabe mavuto anga onse, popeza ndikudziwa kuti simudzavomereza kuti ndine wosalakwa.
Y drede alle my werkis, witynge that thou `woldist not spare the trespassour.
29 Popeza ndapezeka kale wolakwa ndivutikirenji popanda phindu?
Sotheli if Y am also thus wickid, whi haue Y trauelid in veyn?
30 Ngakhale nditasamba mʼmadzi oyera kwambiri ndi kusamba mʼmanja mwanga ndi sopo,
Thouy Y am waischun as with watris of snow, and thouy myn hondis schynen as moost cleene,
31 mutha kundiponyabe pa dzala, kotero kuti ngakhale zovala zanga zomwe zidzandinyansa.
netheles thou schalt dippe me in filthis, and my clothis, `that is, werkis, schulen holde me abhomynable.
32 “Mulungu si munthu ngati ine kuti ndithe kumuyankha, sindingathe kutsutsana naye mʼbwalo la milandu.
Trewli Y schal not answere a man, which is lijk me; nether that may be herd euenli with me in doom.
33 Pakanapezeka munthu wina kuti akhale mʼkhalapakati wathu, kuti atibweretse ife tonse pamodzi,
`Noon is, that may repreue euer eithir, and sette his hond in bothe.
34 munthu wina woti achotse ndodo ya Mulungu pa ine kuti kuopsa kwake kusandichititsenso mantha!
Do he awei his yerde fro me, and his drede make not me aferd.
35 Pamenepo ine ndikanatha kuyankhula mosamuopa Mulunguyo, koma monga zililimu, sindingathe.
Y schal speke, and Y schal not drede hym; for Y may not answere dredynge.

< Yobu 9 >