< Yobu 8 >

1 Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
時にシユヒ人ビルダデ答へて曰く
2 “Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti? Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
何時まで汝かかる事を言や 何時まで汝の口の言語を大風のごとくにするや
3 Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama? Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
神あに審判を曲たまはんや 全能者あに公義を曲たまはんや
4 Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu, Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
汝の子等かれに罪を獲たるにや之をその愆の手に付したまへり
5 Koma utayangʼana kwa Mulungu, ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
汝もし神に求め 全能者に祈り
6 ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
清くかつ正しうしてあらば必ず今汝を顧み汝の義き家を榮えしめたまはん
7 Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.
然らば汝の始は微小くあるとも汝の終は甚だ大ならん
8 “Funsa kwa anthu amvulazakale ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
請ふ汝過にし代の人に問へ 彼らの父祖の尋究めしところの事を學べ
9 pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse, ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
(我らは昨日より有しのみにて何をも知ず 我らが世にある日は影のごとし)
10 Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera? Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
彼等なんぢを敎へ汝を諭し 言をその心より出さざらんや
11 Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho? Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
葦あに泥なくして長んや 萩あに水なくしてそだたんや
12 Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula; zimawuma msangamsanga kuposa bango.
是はその靑くして未だ刈ざる時にも他の一切の草よりは早く槁る
13 Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu; ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
神を忘るる者の道は凡て是のごとく 悖る者の望は空しくなる
14 Kulimba mtima kwake kumafowoka; zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
その恃む所は絶れ その倚ところは蜘蛛網のごとし
15 Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka; amawugwiritsitsa koma sulimba.
その家に倚かからんとすれば家立ず 之に堅くとりすがるも保たじ
16 Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa, nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
彼日の前に靑緑を呈はし その枝を園に蔓延らせ
17 mizu yake imayanga pa mulu wa miyala ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
その根を石堆に盤みて石の屋を眺むれども
18 Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo, pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
若その處より取のぞかれなばその處これを認めずして我は汝を見たる事なしと言ん
19 Ndithudi chomeracho chimafota, ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.
視よその道の喜樂是のごとし 而してまた他の者地より生いでん
20 “Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
それ神は完全人を棄たまはず また惡き者の手を執りたまはず
21 Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
遂に哂笑をもて汝の口に充し歡喜を汝の唇に置たまはん
22 Adani ako adzachita manyazi, ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”
汝を惡む者は羞恥を着せられ 惡き者の住所は無なるべし

< Yobu 8 >