< Yobu 7 >

1 “Kodi munthu sakhala ndi ntchito yowawa pa dziko lapansi? Kodi masiku ake sali ngati munthu waganyu?
Czy człowiekowi nie jest wyznaczony czas na ziemi? Czy jego dni [nie są] jak dni najemnika?
2 Monga ngati kapolo wolakalaka mthunzi wa nthawi yamadzulo, kapena ngati munthu waganyu woyembekezera malipiro ake,
Jak sługa pragnie cienia, jak najemnik oczekuje [zapłaty] za swoją pracę;
3 choncho ine ndapatsidwa nthawi yongovutika pachabe, ndiponso usiku wamasautso wapatsidwa kwa ine.
Tak moim udziałem są miesiące próżne, a przeznaczono mi noce bolesne.
4 Ndikamagona ndimaganiza kuti, ‘Kodi kucha liti?’ Usikuwo umatalika ndipo sindigona tulo mpaka mmawa.
Gdy się kładę, mówię: Kiedy minie noc, abym mógł wstać? I jestem pełny niepokoju aż do świtu.
5 Thupi langa ladzala mphutsi ndi zipsera, khungu langa langʼambika ndipo likutuluka mafinya.
Moje ciało pokryte jest robactwem i strupami w prochu, moja skóra pęka i ropieje.
6 “Masiku anga ndi othamanga kupambana makina wolukira nsalu, ndipo amatha wopanda chiyembekezo.
Moje dni biegną szybciej niż czółenko tkackie i przemijają bez nadziei.
7 Inu Mulungu kumbukirani kuti moyo wanga uli ngati mpweya; sindidzaonanso masiku achisangalalo.
Pamiętaj, że moje życie [jest] wiatrem, moje oko już nie zobaczy dobra.
8 Amene akundiona tsopano akundiona; mudzandifunafuna koma sindidzapezekanso.
Oko, które mnie widziało, już mnie nie zobaczy. Twoje oczy [są zwrócone] na mnie, a mnie [już] nie ma.
9 Monga mtambo umazimirira ndi kukanganuka, momwemonso munthu amene walowa mʼmanda sabwerera. (Sheol h7585)
[Jak] obłok się rozchodzi i przemija, tak ten, kto zstępuje do grobu, nie wraca. (Sheol h7585)
10 Iye sadzabweranso ku nyumba kwake ndipo onse omudziwa adzamuyiwala.
Nie wróci już do swego domu ani nie pozna go już jego miejsce.
11 “Nʼchifukwa chake ine sindidzakhala chete; ndidzayankhula mopsinjika mtima, ndidzadandaula mowawidwa mtima.
Dlatego nie mogę powstrzymać swoich ust, będę mówił w utrapieniu swego ducha, będę narzekał w goryczy swojej duszy.
12 Kodi ine ndine nyanja kapena chirombo chamʼnyanja kuti inu mundiyikire alonda?
Czy jestem morzem albo wielorybem, że postawiłeś przy mnie straż?
13 Pamene ndikuganiza kuti ndidzapeza chitonthozo pa bedi panga ndipo pogona panga padzachepetsa madandawulo anga,
Gdy mówię: Pocieszy mnie moje łóżko i moje posłanie ulży mojemu narzekaniu;
14 ngakhale nthawi imeneyo mumandiopseza ndi maloto ndi kundichititsa mantha ndi masomphenya,
Wtedy straszysz mnie snami i przerażasz mnie widzeniami;
15 kotero kuti ndimalakalaka kudzikhweza kapena kufa, kupambana kupirira zowawa zimene ndikuzimva mʼthupi mwanga.
Tak że moja dusza wybrałaby sobie uduszenie, raczej śmierć niż życie.
16 Ine ndatopa nawo moyo wanga; sindingakonde kukhala moyo nthawi zonse. Ndisiyeni ndekha pakuti moyo wanga ulibe tanthauzo.
Uprzykrzyło mi się [życie], nie chcę żyć wiecznie. Zostaw mnie, bo moje dni są marnością.
17 “Kodi munthu nʼchiyani kuti muzimuganizira chotere, kuti muzisamala zochita zake,
Czym [jest] człowiek, że go tak wywyższasz i że zwracasz ku niemu swoje serce?
18 kuti muzimusanthula mmawa uliwonse ndi kumamuyesa nthawi yonse?
Że nawiedzasz go każdego ranka i w każdej chwili doświadczasz?
19 Kodi simudzaleka kumandizonda kuti ndipezeko mpata wopumula?
Kiedy odwrócisz się ode mnie i zostawisz mnie, abym mógł przełknąć swoją ślinę?
20 Ngati ine ndachimwa, ndachita chiyani kwa Inu, Inu wopenyetsetsa anthu? Chifukwa chiyani mwachititsa kuti ndikhale ngati choponyera chandamale chanu? Kodi ndasanduka katundu wolemera kwa Inu?
Zgrzeszyłem, cóż mam czynić, stróżu człowieka? Czemu mnie wziąłeś za cel, abym był sam dla siebie ciężarem?
21 Chifukwa chiyani simukundikhululukira zolakwa zanga ndi kundichotsera machimo anga? Pakuti posachedwa ndilowa mʼmanda; mudzandifunafuna ine koma simudzandionanso.”
Czemu nie przebaczysz mojego przestępstwa i nie zmażesz mojej nieprawości? Teraz bowiem położę się w prochu i [gdy] rano będziesz mnie szukał, nie będzie mnie.

< Yobu 7 >