< Yobu 5 >

1 “Itana ngati ungathe, koma ndani adzakuyankhe? Kodi ndi kwa mngelo uti ungapezeko thandizo?
Therfor clepe thou, if `ony is that schal answere thee, and turne thou to summe of seyntis.
2 Mkwiyo umapha chitsiru, ndipo njiru imawononga wopusa.
Wrathfulnesse sleeth `a fonned man, and enuye sleeth a litil child.
3 Ine ndinaona chitsiru chitamera mizu, koma mwadzidzidzi nyumba yake inatembereredwa.
Y siy a fool with stidefast rote, and Y curside his feirnesse anoon.
4 Ana ake alibe ndi chitetezo chomwe; amaponderezedwa mʼbwalo la milandu popanda owateteza.
Hise sones schulen be maad fer fro helthe, and thei schulen be defoulid in the yate, and `noon schal be that schal delyuere hem.
5 Anthu anjala amamudyera zokolola zake, amamutengera ndi za pa minga pomwe, ndipo anthu akhwinthi amafunkha chuma chake.
Whos ripe corn an hungri man schal ete, and an armed man schal rauysche hym, and thei, that thirsten, schulen drynke hise richessis.
6 Pakuti masautso satuluka mʼfumbi, ndipo kuwukira sikuchokera mʼdothi.
No thing is doon in erthe with out cause, and sorewe schal not go out of the erthe.
7 Komatu munthu amabadwira kuti azunzike monga momwe mbaliwali zimathethekera mlengalenga.
A man is borun to labour, and a brid to fliyt.
8 “Koma ndikanakhala ine, ndikanamudandawulira Mulungu; ndikanapereka mlandu wanga kwa Iye.
Wherfor Y schal biseche the Lord, and Y schal sette my speche to my God.
9 Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingatheke kuwerengedwa.
That makith grete thingis, and that moun not be souyt out, and wondurful thingis with out noumbre.
10 Iye amagwetsa mvula pa dziko lapansi, ndipo amathirira minda ya anthu.
Which yyueth reyn on the face of erthe, and moistith alle thingis with watris.
11 Iye amakweza anthu wamba, ndipo iwo amene akulira amawayika pa malo otetezedwa.
Which settith meke men an hiy, and reisith with helthe hem that morenen.
12 Iyeyo amalepheretsa chiwembu cha anthu ochenjera, kotero kuti cholinga chawo sichipindula kanthu.
Which distrieth the thouytis of yuel willid men, that her hondis moun not fille tho thingis that thei bigunnen.
13 Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo, ndipo zolinga za atambwali amazithetsa msangamsanga.
Which takith cautelouse men in the felnesse `of hem, and distrieth the counsel of schrewis.
14 Mdima umawagwera nthawi yamasana; nthawi yamasana amayenda moyambasayambasa monga nthawi ya usiku.
Bi dai thei schulen renne in to derknessis, and as in nyyt so thei schulen grope in myddai.
15 Mulungu amapulumutsa amphawi ku lupanga la mʼkamwa mwawo; amawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amphamvu.
Certis God schal make saaf a nedi man fro the swerd of her mouth, and a pore man fro the hond of the violent, `ethir rauynour.
16 Choncho osauka ali ndi chiyembekezo, ndipo anthu opanda chilungamo amawatseka pakamwa.
And hope schal be to a nedi man, but wickidnesse schal drawe togidere his mouth.
17 “Wodala munthu amene Mulungu amamudzudzula; nʼchifukwa chake usanyoze chilango cha Wamphamvuzonse.
Blessid is the man, which is chastisid of the Lord; therfor repreue thou not the blamyng of the Lord.
18 Pakuti Iye amavulaza koma amamanganso mabalawo; Iye amakantha munthu, komanso manja ake amachiritsa.
For he woundith, and doith medicyn; he smytith, and hise hondis schulen make hool.
19 Pakuti adzakupulumutsa ku masautso nthawi ndi nthawi, mavuto angachuluke bwanji, sadzakukhudza ndi pangʼono pomwe.
In sixe tribulaciouns he schal delyuere thee, and in the seuenthe tribulacioun yuel schal not touche thee.
20 Pa nthawi ya njala adzakulanditsa ku imfa, ndipo nthawi ya nkhondo adzakupulumutsa ku lupanga.
In hungur he schal delyuere thee fro deeth, and in batel fro the power of swerd.
21 Adzakuteteza kwa anthu osinjirira, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha pamene chiwonongeko chafika.
Thou schalt be hid fro the scourge of tunge, and thou schalt not drede myseiste, `ethir wretchidnesse, whanne it cometh.
22 Uzidzaseka pa nthawi ya chiwonongeko ndi ya njala, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha ndi zirombo za mʼdziko lapansi.
In distriyng maad of enemyes and in hungur thou schalt leiye, and thou schalt not drede the beestis of erthe.
23 Pakuti udzachita pangano ndi miyala ya mʼmunda mwako, ndipo nyama zakuthengo zidzakhala nawe mwamtendere.
But thi couenaunt schal be with the stonys of erthe, and beestis of erthe schulen be pesible to thee.
24 Udzadziwa kuti nyumba yako ndi malo otetezedwa; udzawerengera katundu wako ndipo sudzapeza kanthu kamene kasowapo.
And thou schalt wite, that thi tabernacle hath pees, and thou visitynge thi fairnesse schalt not do synne.
25 Udzadziwa kuti ana ako adzakhala ambiri, ndipo zidzukulu zako zidzakhala ngati udzu wa mʼdziko lapansi.
And thou schalt wite also, that thi seed schal be many fold, and thi generacioun schal be as an erbe of erthe.
26 Udzafika ku manda utakalamba, monga mitolo ya zokolola pa nyengo yake.
In abundaunce thou schalt go in to the sepulcre, as an heep of wheete is borun in his tyme.
27 “Ife tafufuza zimenezi ndipo ndi zoona, choncho uzimvere ndi kuzitsata.”
Lo! this is so, as we han souyt; which thing herd, trete thou in minde.

< Yobu 5 >