< Yobu 42 >

1 Pamenepo Yobu anayankha Yehova kuti,
Tada Jov odgovori Gospodu i reèe:
2 “Ndikudziwa kuti Inu mungathe kuchita zinthu zonse; chimene mufuna kuchita wina sangaletse konse.
Znam da sve možeš, i da se ne može smesti što naumiš.
3 Munandifunsa kuti, ‘Kodi ndiwe yani amene ukufuna kusokoneza uphungu wanga ndi mawu opanda nzeru? Zoonadi ndinayankhula zimene sindinazimvetse, zinthu zodabwitsa kwambiri kwa ine zimene sindinazidziwe.
Ko je to što zamraèuje savjet nerazumno? Zato kažem da nijesam razumijevao; èudesno je to za me, te ne mogu znati.
4 “Inu munandiwuza kuti, ‘Mvetsetsa tsopano ndipo ndidzayankhula; ndidzakufunsa ndipo iwe udzandiyankhe.’
Slušaj kad uzgovorim, i kad zapitam, kaži mi.
5 Ndinkangomva za Inu ndi makutu anga, koma tsopanonso ndakuonani ndi maso anga.
Ušima slušah o tebi, a sada te oko moje vidi.
6 Nʼchifukwa chake ndi kuchita manyazi, ndikulapa podzithira fumbi ndi phulusa.”
Zato porièem, i kajem se u prahu i pepelu.
7 Yehova atayankhula ndi Yobu mawu amenewa anawuza Elifazi wa ku Temani kuti, “Ine ndakukwiyira pamodzi ndi abwenzi ako awiri, chifukwa simunayankhule zabwino za Ine, monga mmene wayankhulira mtumiki wanga Yobu.
A kad Gospod izgovori one rijeèi Jovu, reèe Gospod Elifasu Temancu: raspalio se gnjev moj na tebe i na dva prijatelja tvoja što ne govoriste o meni pravo kao sluga moj Jov.
8 Kotero tsopano mutenge ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi kupita nazo kwa mtumiki wanga Yobu kuti mukapereke nsembe zopsereza. Mtumiki wanga Yobu adzakupemphererani, ndipo Ine ndidzalandira pemphero lake. Sindidzakuchitirani kanthu molingana ndi uchitsiru wanu. Inu simunayankhule zabwino za Ine, monga anayankhulira Yobu mtumiki wanga.”
Zato sada uzmite sedam telaca i sedam ovnova, i idite k sluzi mojemu Jovu i prinesite žrtve paljenice za se, i sluga moj Jov neka se pomoli za vas, jer æu doista pogledati na nj da ne uèinim s vama po vašoj ludosti, jer ne govoriste o meni pravo kao sluga moj Jov.
9 Motero Elifazi wa ku Temani, Bilidadi wa ku Suki ndi Zofari wa ku Naama anachita zimene Yehova anawawuza ndipo Yehova anamvera pemphero la Yobu.
I tako otide Elifas Temanac i Vildad Sušanin i Sofar Namaæanin, i uèiniše kako im zapovjedi Gospod. I pogleda Gospod na Jova.
10 Yobu atawapempherera abwenzi ake aja, Yehova anamubwezera chuma chake ndipo anamupatsa mowirikiza kuposa zomwe anali nazo kale.
I Gospod povrati što bješe uzeto Jovu pošto se pomoli za prijatelje svoje; i umnoži Gospod Jovu dvojinom sve što bješe imao.
11 Abale ake ndi alongo ake onse, kuphatikizapo onse amene ankamudziwa kale, amabwera kwa iye nʼkudzadya naye chakudya mʼnyumba mwake. Iwo anamutonthoza ndi kumupepesa chifukwa cha mavuto onse amene Yehova analola kuti amugwere. Aliyense wa iwowa anamupatsa ndalama ndi mphete yagolide.
I doðoše k njemu sva braæa njegova i sve sestre njegove i svi preðašnji znanci njegovi, i jedoše s njim u njegovoj kuæi i žaleæi ga tješiše ga za sve zlo što bješe Gospod pustio na nj, i dadoše mu svaki po novac i po grivnu zlatnu.
12 Yehova anadalitsa Yobu pa masiku ake otsirizawa kupambana poyamba paja. Iye anali ndi nkhosa 14,000, ngamira 6,000, ngʼombe zantchito 2,000 ndi abulu aakazi 1,000.
I Gospod blagoslovi pošljedak Jovov više nego poèetak, te imaše èetrnaest tisuæa ovaca i šest tisuæa kamila i tisuæu jarmova volova i tisuæu magarica.
13 Anaberekanso ana aamuna asanu ndi awiri ndi ana aakazi atatu.
I imaše sedam sinova i tri kæeri.
14 Mwana wake wamkazi woyamba anamutcha Yemima, wachiwiri anamutcha Keziya, wachitatu anamutcha Kereni Hapuki.
I prvoj nadje ime Jemima, a drugoj Kesija a treæoj Keren-apuha.
15 Mʼdziko monsemo munalibe akazi okongola ngati ana a Yobu, ndipo abambo awo anawapatsa cholowa pamodzi ndi alongo awo.
I ne nahoðaše se u svoj zemlji tako lijepijeh djevojaka kao kæeri Jovove, i otac im dade našljedstvo meðu braæom njihovom.
16 Zitachitika zimenezi, Yobu anakhala ndi moyo zaka 140. Iye anaona zidzukulu zake mpaka mʼbado wachinayi.
I poslije poživje Jov sto i èetrdeset godina, i vidje sinove i unuke do èetvrtoga koljena.
17 Potsiriza, Yobu anamwalira ali nkhalamba ya zaka zochuluka kwambiri.
I umrije Jov star i sit života.

< Yobu 42 >