< Yobu 41 >

1 “Kodi ungathe kukoka ngʼona ndi mbedza ya nsomba kapena kukanikiza lilime lake pansi ndi chingwe?
Czy lewiatana wyciągniesz wędką? Czy za jego język [wyciągniesz go] sznurem opuszczonym?
2 Kodi ungathe kumanga chingwe mʼmphuno mwake, kapena kubowola nsagwada zake ndi mbedza?
Czy przewleczesz hak przez jego nozdrza? Czy kolcem przebijesz mu szczęki?
3 Kodi ngʼonayo idzakupempha kuti uyichitire chifundo? Kodi idzakuyankhula ndi mawu ofatsa?
Czy będzie cię błagać? Czy będzie z tobą rozmawiał łagodnie?
4 Kodi idzachita nawe mgwirizano kuti uyisandutse kapolo wako mpaka muyaya?
Czy zawrze z tobą przymierze? Czy przyjmiesz go za sługę na zawsze?
5 Kodi udzasewera nayo ngati mbalame, kapena kuyimangirira kuti atsikana ako asewere nayo?
Czy będziesz z nim igrał jak z ptaszkiem? Czy uwiążesz go dla swoich córek?
6 Kodi anthu adzayitsatsa malonda? Nanga amalondawo nʼkugawanagawana nyama yake kuti akagulitse?
Czy [twoi] towarzysze wyprawią sobie z niego ucztę? Czy podzielą go między siebie kupcy?
7 Kodi chikopa chake ungathe kuchilasa ndi zisonga, kapena kubowola mutu wake ndi nthungo zophera nsomba?
Czy poprzebijasz jego skórę grotami albo jego głowę harpunami?
8 Ukayiputa udziwe kuti pali nkhondo, ndipo iweyo sudzabwereranso.
Połóż tylko rękę na niego i wspomnij o walce, więcej tego nie zrobisz.
9 Chiyembekezo choti nʼkuyigonjetsa ndi chabodza; kungoyiona kokha, ndithu iwe kumangodzigwera wekha.
Oto nadzieja pojmania go jest złudna. Czy na sam jego widok nie zostanie człowiek powalony?
10 Palibe wolimba mtima kuti ndi kuyiputa. Ndani angalimbe mtima kulimbana ndi Ine?
Nikt nie odważy się go obudzić. Kto zdoła więc stanąć przede mną?
11 Kodi ndani anandipatsa kanthu kuti ndimubwezere? Zonse za pansi pa thambo ndi zanga.
Kto mi coś dał, abym mu odpłacił? [Cokolwiek znajduje się] pod całym niebem należy do mnie.
12 “Sindidzaleka kuyankhula za ziwalo zake za chirombocho, za mphamvu zake ndiponso za maonekedwe a thupi lake.
Nie będę milczał o jego członkach ani o jego potędze, ani o jego wspaniałej budowie.
13 Ndani angasende chikopa chake? Ndani angayiyandikire kuti abowole chikopa chake cholimbacho?
Kto odkryje wierzch jego szaty? Kto przystąpi [do niego] z podwójnym wędzidłem?
14 Ndani angatsekule kukamwa kwake, pakamwa pamene pazunguliridwa ndi mano ochititsa mantha?
Kto otworzy wrota jego paszczy? Groza roztacza się wokół jego zębów.
15 Kumsana kwake kuli mizere ya mamba onga zishango zolumikizanalumikizana;
[Jego] łuski to jego pycha, ściśle spięte razem [jakby] pieczęcią.
16 Mambawo ndi olukanalukana kotero kuti mpweya sungathe kulowa pakati pake.
Jedna do drugiej tak przylega, że powietrze nie wejdzie między nie.
17 Ndi olumikizanalumikizana; ndi omatirirana kwambiri kotero kuti sangathe kulekana.
Jedna z drugą jest spojona, są tak złączone, że nie można ich rozdzielić.
18 Kuyetsemula kwake kumatulutsa mbaliwali; maso ake amawala ngati kuwala kwa mʼbandakucha.
Przez jego kichanie błyszczy światło, a jego oczy [są] jak powieki zorzy.
19 Mʼkamwa mwake mumatuluka nsakali zamoto ndipo mumathetheka mbaliwali zamoto.
Z jego paszczy wychodzą pochodnie, tryskają iskry ognia.
20 Mʼmphuno mwake mumatuluka utsi ngati wa mʼnkhali yowira yomwe ili pa moto wa bango.
Z jego nozdrzy wychodzi dym jak z wrzącego garnca lub kotła.
21 Mpweya wake umayatsa makala, ndipo malawi amoto amatuluka mʼkamwa mwake.
Jego oddech rozpala węgle, z jego paszczy wychodzi płomień.
22 Mphamvu zake zili mʼkhosi mwake; aliyense wokumana nayo amangoti njenjenje ndi mantha.
W jego szyi spoczywa moc i przed nim ucieka smutek.
23 Minyewa ya thupi lake ndi yolumikizana ndipo ndi yokhwima kwambiri ndi yolimba.
Warstwy jego ciała są spojone, tak twarde, że się nie poruszają.
24 Pachifuwa pake ndi powuma ngati mwala, ndi pa gwaa, ngati mwala wamphero.
Jego serce jest twarde jak kamień, tak twarde jak część dolnego kamienia młyńskiego.
25 Ngʼonayo ikangovuwuka, ndi anthu amphamvu omwe amaopa; amabwerera mʼmbuyo, kuthawa.
Gdy się podnosi, drżą mocarze, a od strachu oczyszczają się.
26 Ngakhale ikanthidwe ndi lupanga, lupangalo silichita kanthu, ngakhale mkondo, muvi ndi nthungo, zonse zimalephera.
Miecz, który go dosięga, nie ostaje się, podobnie drzewce, strzała i pancerz.
27 Chitsulo imachiyesa ngati phesi chabe ndi mkuwa ngati chikuni chowola.
Żelazo uważa za słomę, a miedź za zbutwiałe drewno.
28 Muvi sungathe kuyithawitsa, miyala imene ayilasa nayo imangoyinyenyanyenya.
Strzała nie spłoszy go, a kamienie z procy są dla niego jak źdźbło.
29 Zibonga zimakhala ngati ziputu; imangoseka pamene akuyibaya ndi nthungo.
Oszczep uważa za słomę, a drwi sobie z szarpania włócznią.
30 Mamba a ku mimba kwake ali ngati chopunthira chakunthwa ndipo imasiya mkukuluzi mʼmatope ngati galeta lopunthira tirigu.
Pod nim [są] ostre skorupy; w błocie ścieli [sobie wszelkimi] ostrymi rzeczami.
31 Imagadutsa madzi ozama ngati madzi a mʼnkhali, imachititsa nyanja kuti iwire ngati mbiya yoyengera mafuta.
Sprawia, że głębiny wrą jak kocioł, a morze mąci jak w moździerzu.
32 Kumbuyo kwake imasiya nthubwitubwi zambee, kotero kuti munthu angaganize kuti nyanja yachita imvi.
Zostawia za sobą błyszczącą ścieżkę, tak że się wydaje, że głębiny mają siwiznę.
33 Pa dziko lapansi palibe china chofanana nacho, nʼcholengedwa chopanda mantha.
Nie ma na ziemi jemu podobnego, który został tak stworzony, że niczego się nie boi.
34 Chimanyoza nyama zina zonse; icho chija ndi mfumu ya nyama zonse.”
Lekceważy wszelką wysoką rzecz. On jest królem nad wszystkimi synami pychy.

< Yobu 41 >