< Yobu 41 >

1 “Kodi ungathe kukoka ngʼona ndi mbedza ya nsomba kapena kukanikiza lilime lake pansi ndi chingwe?
an extrahere poteris Leviathan hamo et fune ligabis linguam eius
2 Kodi ungathe kumanga chingwe mʼmphuno mwake, kapena kubowola nsagwada zake ndi mbedza?
numquid pones circulum in naribus eius et armilla perforabis maxillam eius
3 Kodi ngʼonayo idzakupempha kuti uyichitire chifundo? Kodi idzakuyankhula ndi mawu ofatsa?
numquid multiplicabit ad te preces aut loquetur tibi mollia
4 Kodi idzachita nawe mgwirizano kuti uyisandutse kapolo wako mpaka muyaya?
numquid feriet tecum pactum et accipies eum servum sempiternum
5 Kodi udzasewera nayo ngati mbalame, kapena kuyimangirira kuti atsikana ako asewere nayo?
numquid inludes ei quasi avi aut ligabis illum ancillis tuis
6 Kodi anthu adzayitsatsa malonda? Nanga amalondawo nʼkugawanagawana nyama yake kuti akagulitse?
concident eum amici divident illum negotiatores
7 Kodi chikopa chake ungathe kuchilasa ndi zisonga, kapena kubowola mutu wake ndi nthungo zophera nsomba?
numquid implebis sagenas pelle eius et gurgustium piscium capite illius
8 Ukayiputa udziwe kuti pali nkhondo, ndipo iweyo sudzabwereranso.
pone super eum manum tuam memento belli nec ultra addas loqui
9 Chiyembekezo choti nʼkuyigonjetsa ndi chabodza; kungoyiona kokha, ndithu iwe kumangodzigwera wekha.
ecce spes eius frustrabitur eum et videntibus cunctis praecipitabitur
10 Palibe wolimba mtima kuti ndi kuyiputa. Ndani angalimbe mtima kulimbana ndi Ine?
non quasi crudelis suscitabo eum quis enim resistere potest vultui meo
11 Kodi ndani anandipatsa kanthu kuti ndimubwezere? Zonse za pansi pa thambo ndi zanga.
quis ante dedit mihi ut reddam ei omnia quae sub caelo sunt mea sunt
12 “Sindidzaleka kuyankhula za ziwalo zake za chirombocho, za mphamvu zake ndiponso za maonekedwe a thupi lake.
non parcam ei et verbis potentibus et ad deprecandum conpositis
13 Ndani angasende chikopa chake? Ndani angayiyandikire kuti abowole chikopa chake cholimbacho?
quis revelavit faciem indumenti eius et in medium oris eius quis intrabit
14 Ndani angatsekule kukamwa kwake, pakamwa pamene pazunguliridwa ndi mano ochititsa mantha?
portas vultus eius quis aperiet per gyrum dentium eius formido
15 Kumsana kwake kuli mizere ya mamba onga zishango zolumikizanalumikizana;
corpus illius quasi scuta fusilia et conpactum squamis se prementibus
16 Mambawo ndi olukanalukana kotero kuti mpweya sungathe kulowa pakati pake.
una uni coniungitur et ne spiraculum quidem incedit per eas
17 Ndi olumikizanalumikizana; ndi omatirirana kwambiri kotero kuti sangathe kulekana.
una alteri adherebunt et tenentes se nequaquam separabuntur
18 Kuyetsemula kwake kumatulutsa mbaliwali; maso ake amawala ngati kuwala kwa mʼbandakucha.
sternutatio eius splendor ignis et oculi eius ut palpebrae diluculi
19 Mʼkamwa mwake mumatuluka nsakali zamoto ndipo mumathetheka mbaliwali zamoto.
de ore eius lampades procedunt sicut taedae ignis accensae
20 Mʼmphuno mwake mumatuluka utsi ngati wa mʼnkhali yowira yomwe ili pa moto wa bango.
de naribus eius procedit fumus sicut ollae succensae atque ferventis
21 Mpweya wake umayatsa makala, ndipo malawi amoto amatuluka mʼkamwa mwake.
halitus eius prunas ardere facit et flamma de ore eius egreditur
22 Mphamvu zake zili mʼkhosi mwake; aliyense wokumana nayo amangoti njenjenje ndi mantha.
in collo eius morabitur fortitudo et faciem eius praecedet egestas
23 Minyewa ya thupi lake ndi yolumikizana ndipo ndi yokhwima kwambiri ndi yolimba.
membra carnium eius coherentia sibi mittet contra eum fulmina et ad locum alium non ferentur
24 Pachifuwa pake ndi powuma ngati mwala, ndi pa gwaa, ngati mwala wamphero.
cor eius indurabitur quasi lapis et stringetur quasi malleatoris incus
25 Ngʼonayo ikangovuwuka, ndi anthu amphamvu omwe amaopa; amabwerera mʼmbuyo, kuthawa.
cum sublatus fuerit timebunt angeli et territi purgabuntur
26 Ngakhale ikanthidwe ndi lupanga, lupangalo silichita kanthu, ngakhale mkondo, muvi ndi nthungo, zonse zimalephera.
cum adprehenderit eum gladius subsistere non poterit neque hasta neque torax
27 Chitsulo imachiyesa ngati phesi chabe ndi mkuwa ngati chikuni chowola.
reputabit enim quasi paleas ferrum et quasi lignum putridum aes
28 Muvi sungathe kuyithawitsa, miyala imene ayilasa nayo imangoyinyenyanyenya.
non fugabit eum vir sagittarius in stipulam versi sunt ei lapides fundae
29 Zibonga zimakhala ngati ziputu; imangoseka pamene akuyibaya ndi nthungo.
quasi stipulam aestimabit malleum et deridebit vibrantem hastam
30 Mamba a ku mimba kwake ali ngati chopunthira chakunthwa ndipo imasiya mkukuluzi mʼmatope ngati galeta lopunthira tirigu.
sub ipso erunt radii solis sternet sibi aurum quasi lutum
31 Imagadutsa madzi ozama ngati madzi a mʼnkhali, imachititsa nyanja kuti iwire ngati mbiya yoyengera mafuta.
fervescere faciet quasi ollam profundum mare ponet quasi cum unguenta bulliunt
32 Kumbuyo kwake imasiya nthubwitubwi zambee, kotero kuti munthu angaganize kuti nyanja yachita imvi.
post eum lucebit semita aestimabit abyssum quasi senescentem
33 Pa dziko lapansi palibe china chofanana nacho, nʼcholengedwa chopanda mantha.
non est super terram potestas quae conparetur ei qui factus est ut nullum timeret
34 Chimanyoza nyama zina zonse; icho chija ndi mfumu ya nyama zonse.”
omne sublime videt ipse est rex super universos filios superbiae

< Yobu 41 >