< Yobu 41 >

1 “Kodi ungathe kukoka ngʼona ndi mbedza ya nsomba kapena kukanikiza lilime lake pansi ndi chingwe?
Whether thou schalt mowe drawe out leuyathan with an hook, and schalt bynde with a roop his tunge?
2 Kodi ungathe kumanga chingwe mʼmphuno mwake, kapena kubowola nsagwada zake ndi mbedza?
Whethir thou schalt putte a ryng in hise nosethirlis, ethir schalt perse hyse cheke with `an hook?
3 Kodi ngʼonayo idzakupempha kuti uyichitire chifundo? Kodi idzakuyankhula ndi mawu ofatsa?
Whether he schal multiplie preieris to thee, ether schal speke softe thingis to thee?
4 Kodi idzachita nawe mgwirizano kuti uyisandutse kapolo wako mpaka muyaya?
Whether he schal make couenaunt with thee, and `thou schalt take him a seruaunt euerlastinge?
5 Kodi udzasewera nayo ngati mbalame, kapena kuyimangirira kuti atsikana ako asewere nayo?
Whether thou schalt scorne hym as a brid, ethir schalt bynde hym to thin handmaidis?
6 Kodi anthu adzayitsatsa malonda? Nanga amalondawo nʼkugawanagawana nyama yake kuti akagulitse?
Schulen frendis `kerue hym, schulen marchauntis departe hym?
7 Kodi chikopa chake ungathe kuchilasa ndi zisonga, kapena kubowola mutu wake ndi nthungo zophera nsomba?
Whether thou schalt fille nettis with his skyn, and a `leep of fischis with his heed?
8 Ukayiputa udziwe kuti pali nkhondo, ndipo iweyo sudzabwereranso.
Schalt thou putte thin hond on hym? haue thou mynde of the batel, and adde no more to speke.
9 Chiyembekezo choti nʼkuyigonjetsa ndi chabodza; kungoyiona kokha, ndithu iwe kumangodzigwera wekha.
Lo! his hope schal disseyue hym; and in the siyt of alle men he schal be cast doun.
10 Palibe wolimba mtima kuti ndi kuyiputa. Ndani angalimbe mtima kulimbana ndi Ine?
I not as cruel schal reise hym; for who may ayenstonde my face?
11 Kodi ndani anandipatsa kanthu kuti ndimubwezere? Zonse za pansi pa thambo ndi zanga.
And who `yaf to me bifore, that Y yelde to hym? Alle thingis, that ben vndur heuene, ben myne.
12 “Sindidzaleka kuyankhula za ziwalo zake za chirombocho, za mphamvu zake ndiponso za maonekedwe a thupi lake.
Y schal not spare hym for myyti wordis, and maad faire to biseche.
13 Ndani angasende chikopa chake? Ndani angayiyandikire kuti abowole chikopa chake cholimbacho?
Who schal schewe the face of his clothing, and who schal entre in to the myddis of his mouth?
14 Ndani angatsekule kukamwa kwake, pakamwa pamene pazunguliridwa ndi mano ochititsa mantha?
Who schal opene the yatis of his cheer? ferdfulnesse is bi the cumpas of hise teeth.
15 Kumsana kwake kuli mizere ya mamba onga zishango zolumikizanalumikizana;
His bodi is as yotun scheldys of bras, and ioyned togidere with scalis ouerleiynge hem silf.
16 Mambawo ndi olukanalukana kotero kuti mpweya sungathe kulowa pakati pake.
Oon is ioyned to another; and sotheli brething goith not thorouy tho.
17 Ndi olumikizanalumikizana; ndi omatirirana kwambiri kotero kuti sangathe kulekana.
Oon schal cleue to anothir, and tho holdynge hem silf schulen not be departid.
18 Kuyetsemula kwake kumatulutsa mbaliwali; maso ake amawala ngati kuwala kwa mʼbandakucha.
His fnesynge is as schynynge of fier, and hise iyen ben as iyelidis of the morewtid.
19 Mʼkamwa mwake mumatuluka nsakali zamoto ndipo mumathetheka mbaliwali zamoto.
Laumpis comen forth of his mouth, as trees of fier, that ben kyndlid.
20 Mʼmphuno mwake mumatuluka utsi ngati wa mʼnkhali yowira yomwe ili pa moto wa bango.
Smoke cometh forth of hise nosethirlis, as of a pot set on the fier `and boilynge.
21 Mpweya wake umayatsa makala, ndipo malawi amoto amatuluka mʼkamwa mwake.
His breeth makith colis to brenne, and flawme goith out of his mouth.
22 Mphamvu zake zili mʼkhosi mwake; aliyense wokumana nayo amangoti njenjenje ndi mantha.
Strengthe schal dwelle in his necke, and nedynesse schal go bifor his face.
23 Minyewa ya thupi lake ndi yolumikizana ndipo ndi yokhwima kwambiri ndi yolimba.
The membris of hise fleischis ben cleuynge togidere to hem silf; God schal sende floodis ayens hym, and tho schulen not be borun to an other place.
24 Pachifuwa pake ndi powuma ngati mwala, ndi pa gwaa, ngati mwala wamphero.
His herte schal be maad hard as a stoon; and it schal be streyned togidere as the anefeld of a smith.
25 Ngʼonayo ikangovuwuka, ndi anthu amphamvu omwe amaopa; amabwerera mʼmbuyo, kuthawa.
Whanne he schal be takun awei, aungels schulen drede; and thei aferd schulen be purgid.
26 Ngakhale ikanthidwe ndi lupanga, lupangalo silichita kanthu, ngakhale mkondo, muvi ndi nthungo, zonse zimalephera.
Whanne swerd takith hym, it may not stonde, nethir spere, nether haburioun.
27 Chitsulo imachiyesa ngati phesi chabe ndi mkuwa ngati chikuni chowola.
For he schal arette irun as chaffis, and bras as rotun tre.
28 Muvi sungathe kuyithawitsa, miyala imene ayilasa nayo imangoyinyenyanyenya.
A man archere schal not dryue hym awei; stoonys of a slynge ben turned in to stobil to hym.
29 Zibonga zimakhala ngati ziputu; imangoseka pamene akuyibaya ndi nthungo.
He schal arette an hamer as stobil; and he schal scorne a florischynge spere.
30 Mamba a ku mimba kwake ali ngati chopunthira chakunthwa ndipo imasiya mkukuluzi mʼmatope ngati galeta lopunthira tirigu.
The beemys of the sunne schulen be vndur hym; and he schal strewe to hym silf gold as cley.
31 Imagadutsa madzi ozama ngati madzi a mʼnkhali, imachititsa nyanja kuti iwire ngati mbiya yoyengera mafuta.
He schal make the depe se to buyle as a pot; and he schal putte, as whanne oynementis buylen.
32 Kumbuyo kwake imasiya nthubwitubwi zambee, kotero kuti munthu angaganize kuti nyanja yachita imvi.
A path schal schyne aftir hym; he schal gesse the greet occian as wexynge eld.
33 Pa dziko lapansi palibe china chofanana nacho, nʼcholengedwa chopanda mantha.
No power is on erthe, that schal be comparisound to hym; which is maad, that he schulde drede noon.
34 Chimanyoza nyama zina zonse; icho chija ndi mfumu ya nyama zonse.”
He seeth al hiy thing; he is kyng ouer alle the sones of pride.

< Yobu 41 >