< Yobu 40 >

1 Yehova anati kwa Yobu:
L’Eterno continuò a rispondere a Giobbe e disse:
2 “Kodi iwe ufuna kukangana ndi Wamphamvuzonse? Iwe amene unatsutsana ndi Mulungu umuyankhe Iyeyo!”
“Il censore dell’Onnipotente vuole ancora contendere con lui? Colui che censura Iddio ha egli una risposta a tutto questo?”
3 Pamenepo Yobu anayankha Yehova:
Allora Giobbe rispose all’Eterno e disse:
4 “Ine sindili kanthu konse, kodi ndingathe kukuyankhani chiyani? Ndagwira pakamwa panga.
“Ecco, io son troppo meschino; che ti risponderei? Io mi metto la mano sulla bocca.
5 Ndinayankhula kamodzi, koma pano ndilibe yankho, ndinayankha kawiri, koma sindiwonjezeranso mawu ena.”
Ho parlato una volta, ma non riprenderò la parola, due volte… ma non lo farò più”.
6 Ndipo Yehova anayankha Yobu mʼkamvuluvulu kuti,
L’Eterno allora rispose a Giobbe dal seno della tempesta, e disse:
7 “Tsopano vala dzilimbe ngati mwamuna; ndikufunsa mafunso ndipo iwe undiyankhe.
“Orsù, cingiti i lombi come un prode; ti farò delle domande e tu insegnami!
8 “Kodi iwe unganyoze chiweruzo changa cholungama? Kodi ungandidzudzule kuti iweyo ukhale wolungama?
Vuoi tu proprio annullare il mio giudizio? condannar me per giustificar te stesso?
9 Kodi uli ndi dzanja monga la Mulungu, ndipo mawu ako angagunde ngati mphenzi monga a Mulungu?
Hai tu un braccio pari a quello di Dio? o una voce che tuoni come la sua?
10 Ngati zili choncho udzikometsere ndi ulemerero ndi kukongola, ndipo udziveke ulemu ndi ulemerero waufumu.
Su via, adornati di maestà, di grandezza, rivestiti di splendore, di magnificenza!
11 Tsanula ukali wako wosefukirawo, uyangʼane aliyense wodzikuza ndipo umuchepetse,
Da’ libero corso ai furori dell’ira tua; mira tutti i superbi e abbassali!
12 Uyangʼane aliyense wodzikweza ndipo umutsitse, uwapondereze oyipa onse pamalo pomwe alilipo.
Mira tutti i superbi e umiliali! e schiaccia gli empi dovunque stanno!
13 Onsewo uwakwirire pamodzi mfumbi; ukulunge nkhope zawo mʼmanda.
Seppelliscili tutti assieme nella polvere, copri di bende la lor faccia nel buio della tomba!
14 Ukatero Ine ndidzakuvomereza kuti dzanja lako lamanja lakupulumutsadi.
Allora, anch’io ti loderò, perché la tua destra t’avrà dato la vittoria.
15 “Taganiza za mvuwu, imene ndinayipanga monga momwe ndinapangira iwe, ndipo imadya udzu ngati ngʼombe.
Guarda l’ippopotamo che ho fatto al par di te; esso mangia l’erba come il bove.
16 Mphamvu zake ndi zazikulu kwambiri, thupi lake ndi lanyonga kwambiri!
Ecco la sua forza è nei suoi lombi, e il vigor suo nei muscoli del ventre.
17 Mchira wake umayima tolotolo ngati mtengo wamkungudza; mitsempha ya ntchafu zake ndi yogwirana bwino.
Stende rigida come un cedro la coda; i nervi delle sue cosce sono intrecciati insieme.
18 Mafupa ake ali ngati mapayipi amkuwa, nthiti zake zili ngati mipiringidzo yachitsulo.
Le sue ossa sono tubi di rame; le sue membra, sbarre di ferro.
19 Mvuwuyo ndi yayikulu mwa zolengedwa za Mulungu, komatu mlengi wake amatha kuyiopseza ndi lupanga lake.
Esso è il capolavoro di Dio; colui che lo fece l’ha fornito di falce,
20 Imapeza chakudya chake ku mtunda ndipo nyama zakuthengo zonse zimasewera pambali pake.
perché i monti gli producon la pastura; e là tutte le bestie de’ campi gli scherzano intorno.
21 Imagona pa tsinde pa zitsamba za mipeta, imabisala mʼbango ndiponso pa thawale.
Si giace sotto i loti, nel folto de’ canneti, in mezzo alle paludi.
22 Imaphimbika ndi mthunzi wazitsamba za mipeta; imazunguliridwa ndi misondozi ya mu mtsinje.
I loti lo copron dell’ombra loro, i salci del torrente lo circondano.
23 Madzi a mu mtsinje akakokoma, sichita mantha, iyo sitekeseka, ngakhale madzi a mu Yorodani afike mʼkhosi mwake.
Straripi pure il fiume, ei non trema; rimane calmo, anche se avesse un Giordano alla gola.
24 Kodi alipo amene angathe kukola mvuwu ndi mbedza kapena kuyikola mu msampha?
Potrebbe alcuno impadronirsene assalendolo di fronte? o prenderlo colle reti per forargli il naso?

< Yobu 40 >