< Yobu 37 >

1 “Mtima wanga ukulumphalumpha pa chimenechinso ndipo ukuchoka mʼmalo mwake.
I od toga drkæe srce moje, i otskaèe sa svojega mjesta.
2 Tamverani! Tamverani kubangula kwa liwu lake, kugunda kumene kukuchokera mʼkamwa mwake.
Slušajte dobro gromovni glas njegov i govor što izlazi iz usta njegovijeh.
3 Iye amaponya chingʼaningʼani chake pansi pa thambo lonse ndipo amachitumiza ku dziko lapansi.
Pod sva nebesa pušta ga, i svjetlost svoju do krajeva zemaljskih.
4 Pambuyo pake kubangula kwake kumamveka. Iye amabangula ndi liwu lake laulemerero. Pamene wabangula, palibe chimene amalephera kuchita.
Za njom rièe grom, grmi glasom velièanstva svojega, niti što odgaða kad se èuje glas njegov.
5 Liwu la Mulungu limabangula mʼnjira zambiri zodabwitsa Iye amachita zinthu zazikulu zimene sitingathe kuzimvetsa.
Divno Bog grmi glasom svojim, èini stvari velike, da ih ne možemo razumjeti.
6 Amalamula chisanu chowundana kuti, ‘Igwa pa dziko lapansi,’ ndipo amalamulanso mvula yamawawa kuti, ‘Khala mvula yamphamvu.’
Govori snijegu: padni na zemlju; i daždu sitnome i daždu silnome.
7 Kuti anthu onse amene anawalenga athe kuzindikira ntchito yake. Iye amalepheretsa anthu kugwira ntchito zawo.
Zapeèaæava ruku svakom èovjeku, da pozna sve poslenike svoje.
8 Zirombo zimakabisala ndipo zimakhala mʼmaenje mwawo.
Tada zvijer ulazi u jamu, i ostaje na svojoj loži.
9 Mphepo yamkuntho imatuluka ku malo ake, kuzizira kumatuluka mʼmphepo yamkunthoyo.
S juga dolazi oluja, i sa sjevera zima.
10 Mpweya wa Mulungu umawunditsa madzi ndipo madzi a mʼnyanja amawuma kuti gwaa.
Od dihanja Božijega postaje led, i široke vode stiskuju se.
11 Iye amadzaza mitambo ndi madzi a mvula, amabalalitsa zingʼaningʼani zake kuchokera mʼmitambomo.
I da se natapa zemlja, natjeruje oblak, i rasipa oblak svjetlošæu svojom.
12 Mulungu amayendetsa mitamboyo mozungulirazungulira dziko lonse lapansi kuti ichite zonse zimene Iye akufuna pa dziko lapansi.
I on se obræe i tamo i amo po volji njegovoj da èini sve što mu zapovjedi po vasiljenoj.
13 Iye amagwetsa mvula kuti alange anthu, kapena kubweretsa chinyontho pa dziko lapansi kuti aonetse chikondi chake.
Èini da se naðe ili za kar ili za zemlju ili za dobroèinstvo.
14 “Abambo Yobu, tamvani izi; imani ndipo muganizire ntchito zodabwitsa za Mulungu.
Èuj to, Jove, stani i gledaj èudesa Božija.
15 Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayendetsera mitambo ndi kuchititsa kuti kukhale zingʼaningʼani?
Znaš li kako ih Bog ureðuje i kako sija svjetlošæu iz oblaka svojega?
16 Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayalira mitambo, ntchito zodabwitsa za Iye amene ndi wanzeru zangwiro?
Znaš li kako vise oblaci? Znaš li èudesa onoga koji je savršen u svakom znanju?
17 Inu amene mʼzovala zanu mumatuluka thukuta pamene kunja kwatentha chifukwa cha mphepo yakummwera,
Kako ti se haljine ugriju kad umiri zemlju od juga?
18 kodi mungathe kuthandizana naye kutambasula thambo limene ndi lolimba ngati chitsulo?
Jesi li ti s njim razapinjao nebesa, koja stoje tvrdo kao saliveno ogledalo?
19 “Tiwuzeni ife zoti tikanene kwa Iye; sitingathe kufotokoza mlandu wathu chifukwa cha mdima umene uli mwa ife.
Nauèi nas šta æemo mu reæi; ne možemo od tame govoriti po redu.
20 Kodi nʼkofunika kumudziwitsa Mulungu kuti ndili naye mawu? Kodi kutero sikuchita ngati kupempha kuti ndiwonongeke?
Hoæe li mu ko pripovjediti što bih ja govorio? Ako li bi ko govorio, zaista, bio bih proždrt.
21 Tsopano munthu sangathe kuyangʼana dzuwa, ndi kunyezimira mlengalenga, kuwomba kwa mphepo kutachotsa mitambo yonse.
Ali sada ne mogu ljudi gledati u svjetlost kad sjaje na nebu, pošto vjetar proðe i oèisti ga;
22 Kuwala kwake kumaonekera cha kumpoto; Mulungu amabwera ndi ulemerero woopsa.
Sa sjevera dolazi kao zlato; ali je u Bogu strašnija slava.
23 Wamphamvuzonse sitingathe kumufikira pafupi ndi wa mphamvu zoposa; pa chiweruzo chake cholungama ndi mʼchilungamo chake chachikulu Iye sapondereza anthu ozunzika.
Svemoguæ je, ne možemo ga stignuti; velike je sile, ali sudom i velikom pravdom nikoga ne muèi.
24 Nʼchifukwa chake anthu amamuopa kwambiri, kodi saganizira za onse amene amaganiza kuti ndi anzeru?”
Zato ga se boje ljudi: ne može ga vidjeti nikakav mudarac.

< Yobu 37 >