< Yobu 37 >

1 “Mtima wanga ukulumphalumpha pa chimenechinso ndipo ukuchoka mʼmalo mwake.
Myn herte dredde of this thing, and is moued out of his place.
2 Tamverani! Tamverani kubangula kwa liwu lake, kugunda kumene kukuchokera mʼkamwa mwake.
It schal here an heryng in the feerdfulnesse of his vois, and a sown comynge forth of his mouth.
3 Iye amaponya chingʼaningʼani chake pansi pa thambo lonse ndipo amachitumiza ku dziko lapansi.
He biholdith ouere alle heuenes; and his liyt is ouere the termes of erthe.
4 Pambuyo pake kubangula kwake kumamveka. Iye amabangula ndi liwu lake laulemerero. Pamene wabangula, palibe chimene amalephera kuchita.
Sown schal rore aftir hym, he schal thundre with the vois of his greetnesse; and it schal not be souyt out, whanne his vois is herd.
5 Liwu la Mulungu limabangula mʼnjira zambiri zodabwitsa Iye amachita zinthu zazikulu zimene sitingathe kuzimvetsa.
God schal thundre in his vois wondurfulli, that makith grete thingis and that moun not be souyt out.
6 Amalamula chisanu chowundana kuti, ‘Igwa pa dziko lapansi,’ ndipo amalamulanso mvula yamawawa kuti, ‘Khala mvula yamphamvu.’
Which comaundith to the snow to come doun on erthe, and to the reynes of wijntir, and to the reynes of his strengthe.
7 Kuti anthu onse amene anawalenga athe kuzindikira ntchito yake. Iye amalepheretsa anthu kugwira ntchito zawo.
Which markith in the hond of alle men, that alle men knowe her werkis.
8 Zirombo zimakabisala ndipo zimakhala mʼmaenje mwawo.
An vnresonable beeste schal go in to his denne, and schal dwelle in his caue, `ethir derke place.
9 Mphepo yamkuntho imatuluka ku malo ake, kuzizira kumatuluka mʼmphepo yamkunthoyo.
Tempestis schulen go out fro the ynnere thingis, and coold fro Arturus.
10 Mpweya wa Mulungu umawunditsa madzi ndipo madzi a mʼnyanja amawuma kuti gwaa.
Whanne God makith blowyng, frost wexith togidere; and eft ful brood watris ben sched out.
11 Iye amadzaza mitambo ndi madzi a mvula, amabalalitsa zingʼaningʼani zake kuchokera mʼmitambomo.
Whete desirith cloudis, and cloudis spreeden abrood her liyt.
12 Mulungu amayendetsa mitamboyo mozungulirazungulira dziko lonse lapansi kuti ichite zonse zimene Iye akufuna pa dziko lapansi.
Whiche cloudes cumpassen alle thingis bi cumpas, whidur euere the wil of the gouernour ledith tho, to al thing which he comaundith `to tho on the face of the world;
13 Iye amagwetsa mvula kuti alange anthu, kapena kubweretsa chinyontho pa dziko lapansi kuti aonetse chikondi chake.
whether in o lynage, ethir in his lond, ether in what euer place of his merci he comaundith tho to be foundun.
14 “Abambo Yobu, tamvani izi; imani ndipo muganizire ntchito zodabwitsa za Mulungu.
Joob, herkene thou these thingis; stonde thou, and biholde the meruels of God.
15 Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayendetsera mitambo ndi kuchititsa kuti kukhale zingʼaningʼani?
Whethir thou woost, whanne God comaundide to the reynes, that tho schulen schewe the liyt of hise cloudis?
16 Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayalira mitambo, ntchito zodabwitsa za Iye amene ndi wanzeru zangwiro?
Whether thou knowist the grete weies of cloudis, and perfit kunnyngis?
17 Inu amene mʼzovala zanu mumatuluka thukuta pamene kunja kwatentha chifukwa cha mphepo yakummwera,
Whether thi cloothis ben not hoote, whanne the erthe is blowun with the south?
18 kodi mungathe kuthandizana naye kutambasula thambo limene ndi lolimba ngati chitsulo?
In hap thou madist with hym heuenes, which moost sad ben foundid, as of bras.
19 “Tiwuzeni ife zoti tikanene kwa Iye; sitingathe kufotokoza mlandu wathu chifukwa cha mdima umene uli mwa ife.
Schewe thou to vs, what we schulen seie to hym; for we ben wlappid in derknessis.
20 Kodi nʼkofunika kumudziwitsa Mulungu kuti ndili naye mawu? Kodi kutero sikuchita ngati kupempha kuti ndiwonongeke?
Who schal telle to hym, what thingis Y speke? yhe, if he spekith, a man schal be deuourid.
21 Tsopano munthu sangathe kuyangʼana dzuwa, ndi kunyezimira mlengalenga, kuwomba kwa mphepo kutachotsa mitambo yonse.
And now men seen not liyt; the eir schal be maad thicke sudenli in to cloudis, and wynd passynge schal dryue awei tho.
22 Kuwala kwake kumaonekera cha kumpoto; Mulungu amabwera ndi ulemerero woopsa.
Gold schal come fro the north, and ferdful preisyng of God.
23 Wamphamvuzonse sitingathe kumufikira pafupi ndi wa mphamvu zoposa; pa chiweruzo chake cholungama ndi mʼchilungamo chake chachikulu Iye sapondereza anthu ozunzika.
For we moun not fynde him worthili; he is greet in strengthe, and in doom, and in riytfulnesse, and may not be teld out.
24 Nʼchifukwa chake anthu amamuopa kwambiri, kodi saganizira za onse amene amaganiza kuti ndi anzeru?”
Therfor men schulen drede hym; and alle men, that semen to hem silf to be wise, schulen not be hardi to biholde.

< Yobu 37 >