< Yobu 34 >

1 Pamenepo Elihu anapitiriza kuyankhula kuti,
Još govori Elijuj i reèe:
2 “Imvani mawu anga, inu anthu anzeru; tcherani khutu inu anthu ophunzira.
Èujte, mudri, besjedu moju, i razumni poslušajte me.
3 Pakuti khutu limayesa mawu monga momwe mʼkamwa mumalawira chakudya.
Jer uho poznaje besjedu kao što grlo kuša jelo.
4 Tsono tiyeni tizindikire chomwe chili choyenera; tiphunzire pamodzi chomwe chili chabwino.
Razberimo što je pravo, izvidimo meðu sobom što je dobro.
5 “Yobu akunena kuti, ‘Ndine wosalakwa, koma Mulungu akukana kundiweruza molungama.
Jer Jov reèe: pravedan sam, a Bog odbaci moju pravdu.
6 Ngakhale ndine wolungama mtima, akundiyesa wabodza; ngakhale ndine wosachimwa, mivi yake ikundichititsa mabala osachiritsidwa.’
Hoæu li lagati za svoju pravdu? strijela je moja smrtna, a bez krivice.
7 Kodi munthu wofanana ndi Yobu ndani, amene amayankhula zamwano ngati akumwa madzi?
Koji je èovjek kao Jov da kao vodu pije potsmijeh?
8 Iye amayenda ndi anthu ochita zoyipa; amayanjana ndi anthu oyipa mtima.
I da se druži s onima koji èine bezakonje, i da hodi s bezbožnijem ljudima?
9 Paja iye amanena kuti, ‘Munthu sapindula kanthu poyesetsa kukondweretsa Mulungu.’
Jer reèe: ne pomaže èovjeku da ugaða Bogu.
10 “Tsono mverani ine, inu anthu anzeru zomvetsa zinthu. Mulungu sangachite choyipa ndi pangʼono pomwe, Wamphamvuzonse sangathe kuchita cholakwa.
Zato, ljudi razumni, poslušajte me; daleko je od Boga zloæa i nepravda od svemoguæega.
11 Iye amamubwezera munthu molingana ndi ntchito zake; Mulungu amabweretsa pa munthu molingana ndi zomwe amachita.
Jer po djelu plaæa èovjeku i daje svakome da naðe prema putu svojemu.
12 Nʼchosayembekezeka kuti Mulungu achite cholakwa, kuti Wamphamvuzonse apotoze chilungamo.
Doista Bog ne radi zlo i svemoguæi ne izvræe pravde.
13 Kodi anapatsa Mulungu udindo wolamulira dziko lapansi ndani? Ndani anayika Mulungu kuti azilamulira dziko lonse?
Ko mu je predao zemlju? i ko je uredio vasiljenu?
14 Mulungu akanakhala ndi maganizo oti achotse mzimu wake ndi mpweya wake,
Kad bi na nj okrenuo srce svoje, uzeo bi k sebi duh njegov i dihanje njegovo;
15 zamoyo zonse zikanawonongekeratu ndipo munthu akanabwerera ku fumbi.
Izginulo bi svako tijelo, i èovjek bi se povratio u prah.
16 “Ngati ndinu omvetsa zinthu, imvani izi; mvetserani zimene ndikunena.
Ako si dakle razuman, èuj ovo: slušaj glas rijeèi mojih.
17 Kodi Mulungu wodana ndi chilungamo angathe kukhala wolamulira? Kodi iwe ungathe kuweruza Wolungama ndi Wamphamvuyo?
Može li vladati onaj koji mrzi na pravdu? hoæeš li osuditi onoga koji je najpravedniji?
18 Kodi si Iye amene amanena kwa mafumu kuti, ‘Ndinu opanda pake,’ ndipo amawuza anthu otchuka, ‘Ndinu oyipa,’
Kaže li se caru: nitkove! i knezovima: bezbožnici?
19 Iye sakondera akalonga ndipo salemekeza anthu olemera kupambana osauka, pakuti onsewa ndi ntchito ya manja ake?
Akamoli onomu koji ne gleda knezovima ko su, niti u njega vrijedi više bogati od siromaha, jer su svi djelo ruku njegovijeh.
20 Iwo amafa mwadzidzidzi, pakati pa usiku; anthu amachita mantha ndipo amamwalira; munthu wamphamvu amachotsedwa popanda dzanja la munthu.
Umiru zaèas, i u po noæi uskoleba se narod i propadne, i odnese se jaki bez ruke ljudske.
21 “Maso a Mulungu amapenya njira za munthu; amaona mayendedwe ake onse.
Jer su oèi njegove obraæene na putove èovjeèije i vidi sve korake njegove.
22 Palibe malo obisika kapena a mdima wandiweyani kumene anthu ochita zoyipa angabisaleko.
Nema mraka ni sjena smrtnoga gdje bi se sakrili koji èine bezakonje.
23 Mulungu sasowa kuti apitirizebe kufufuza munthu, kuti abwere pamaso pake kudzaweruzidwa.
Jer nikome ne odgaða kad doðe da se sudi s Bogom.
24 Popanda kufufuza, Iye amawononga anthu amphamvu ndipo mʼmalo mwawo amayikamo ena.
Satire jake nedokuèljivo, i postavlja druge na njihovo mjesto.
25 Pakuti Iyeyo amadziwa bwino ntchito zawo amawagubuduza usiku ndipo amatswanyika.
Jer zna djela njihova, i dok obrati noæ, satru se.
26 Iye amawalanga chifukwa cha kuyipa kwawo, pamalo pamene aliyense akuwaona;
Kao bezbožne razbija ih na vidiku.
27 Chifukwa anasiya kumutsata ndipo sasamaliranso njira zake zonse.
Jer otstupiše od njega i ne gledaše ni na koje putove njegove;
28 Anachititsa amphawi kuti kulira kwawo kufike pamaso pake, kotero Iyeyo anamva kulira kwa amphawiwo.
Te doðe do njega vika siromahova, i èu viku nevoljnijeh.
29 Koma ngati Mulungu akhala chete, ndani angamunene kuti walakwa? Akabisa nkhope yake, ndani angathe kumupenyabe? Komatu ndiye amene amayangʼana za munthu komanso mtundu wa anthu,
Kad on umiri, ko æe uznemiriti? i kad on sakrije lice, ko æe ga vidjeti? i to biva i narodu i èovjeku,
30 kuti asalamuliridwe ndi anthu osapembedza, kuti asatchere anthu misampha.
Da ne bi carovao licemjer, da ne bi bilo zamke narodu.
31 “Mwina munthu atanena kwa Mulungu kuti, ‘Ndine wolakwa koma sindidzachimwanso,
Zaista, treba kazati Bogu: podnosio sam, neæu više griješiti.
32 ndiphunzitseni zimene sindikuziona ngati ndachita choyipa, sindidzachitanso.’
A što ne vidim, ti me nauèi; ako sam èinio nepravdu, neæu više.
33 Kodi Mulungu akuweruzeni potsata mmene inuyo mukuganizira, pamene inu mukukana kulapa? Chisankho nʼchanu, osati changa; tsono ndiwuzeni zomwe mukudziwa.
Eda li æe po tebi plaæati, jer tebi nije po volji, jer ti biraš a ne on? Ako znaš što, govori.
34 “Anthu omvetsa zinthu adzakambirana, anthu anzeru amene akundimva adzandiwuza kuti,
Ljudi æe razumni sa mnom kazati, i mudar æe èovjek pristati,
35 ‘Yobu akuyankhula mopanda nzeru; mawu ake ndi opanda fundo.’
Da Jov ne govori razumno, i da rijeèi njegove nijesu mudre.
36 Aa, kunali bwino Yobu akanayesedwa mpaka kumapeto chifukwa choyankha ngati munthu woyipa!
Oèe moj, neka se Jov iskuša do kraja, što odgovara kao zli ljudi.
37 Pa tchimo lake amawonjezerapo kuwukira; amawomba mʼmanja mwake monyoza pakati pathu, ndipo amachulukitsa mawu otsutsana ndi Mulungu.”
Jer domeæe na grijeh svoj bezakonje, pljeska rukama meðu nama, i mnogo govori na Boga.

< Yobu 34 >