< Yobu 32 >

1 Tsono anthu atatuwa analeka kumuyankha Yobu, chifukwa chakuti iyeyo ankadziona kuti ndi wolungama.
Tada prestaše ona tri èovjeka odgovarati Jovu, jer se èinjaše da je pravedan.
2 Koma Elihu, mwana wa Barakeli, wa fuko la Buzi, wa banja la Ramu, anapsera mtima kwambiri Yobu chifukwa choti Yobuyo anakana kuvomera kuti anachimwa ndi kuti Mulungu anakhoza pomulanga.
A Elijuj sin Varahilov od Vuza, roda Ramova, razgnjevi se na Jova što se sam graðaše pravedniji od Boga;
3 Anapseranso mtima abwenzi ake atatu aja chifukwa sanapeze njira yomutsutsira Yobu, ngakhale iwo anamupeza kuti anali wolakwa.
I na tri prijatelja njegova razgnjevi se što ne naðoše odgovora i opet osuðivahu Jova.
4 Tsono Elihu anadikira kuti ayankhule ndi Yobu chifukwa choti abwenziwo anali akuluakulu kupambana iyeyo.
Jer Elijuj èekaše dokle oni govorahu s Jovom, jer bijahu stariji od njega.
5 Koma Elihu ataona kuti anthu atatuwo analibe mawu oti ayankhulenso, iye anapsa mtima.
Pa kad vidje Elijuj da nema odgovora u ustima ona tri èovjeka, raspali se gnjev njegov.
6 Choncho Elihu mwana wa Barakeli wa fuko la Buzi anati: “Ine ndine wamngʼono, inuyo ndinu akuluakulu, nʼchifukwa chake ndimaopa, ndimachita mantha kuti ndikuwuzeni zimene ndimadziwa.
I progovori Elijuj sin Varahilov od Vuza, i reèe: ja sam najmlaði, a vi ste starci, zato se bojah i ne smijah vam kazati što mislim.
7 Ndimaganiza kuti, ‘Ayambe ndi akuluakulu kuyankhula; anthu amvulazakale ndiwo amaphunzitsa nzeru.’
Mišljah: neka govori starost, i mnoge godine neka objave mudrost.
8 Koma mzimu wa Mulungu mwa munthu, mpweya wa Wamphamvuzonse, ndi umene umapereka nzeru zomvetsa zinthu.
Ali je duh u ljudima, i duh svemoguæega urazumljuje ih.
9 Si okalamba amene ali ndi nzeru, si amvulazakale okha amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu zimene zili zoyenera.
Veliki nijesu svagda mudri, i starci ne znaju svagda šta je pravo.
10 “Nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Mvereni; inenso ndikukuwuzani zimene ndikuzidziwa.’
Zato velim: poslušaj me da kažem i ja kako mislim.
11 Ndadikira nthawi yonseyi, ndimamvetsera mwachidwi zimene mumayankhula, pamene mumafunafuna mawu oti muyankhule,
Eto, èekao sam da vi izgovorite, slušao sam razloge vaše dokle izviðaste besjedu.
12 ineyo ndinakumvetseranidi. Koma palibe ndi mmodzi yemwe wa inu amene anatsutsa Yobu; palibe aliyense wa inu amene anamuyankha mawu ake.
Pazio sam, ali gle, nijedan od vas ne sapre Jova, ne odgovori na njegove rijeèi.
13 Musanene kuti, ‘Ife tapeza nzeru; Mulungu ndiye amutsutse, osati munthu.’
Može biti da æete reæi: naðosmo mudrost, Bog æe ga oboriti, ne èovjek.
14 Koma Yobu sanayankhule motsutsana ndi ine, ndipo ine sindimuyankha monga mmene inu mwamuyankhira.
Nije na me upravio besjede, ni ja mu neæu odgovarati vašim rijeèima.
15 “Iwo asokonezeka ndipo alibe choti ayankhulenso; mawu awathera.
Smeli su se, ne odgovaraju više, nestalo im je rijeèi.
16 Kodi ine ndidikire chifukwa iwo sakuyankhula tsopano, pakuti angoyima phee wopanda yankho?
Èekao sam, ali ne govore, stadoše, i više ne odgovaraju.
17 Inenso ndiyankhulapo tsopano; nanenso ndinena zimene ndikudziwa.
Odgovoriæu i ja za se, kazaæu i ja kako mislim.
18 Pakuti ndili nawo mawu ambiri, ndipo mtima wanga ukundikakamiza;
Jer sam pun rijeèi, tijesno je duhu u meni.
19 mʼkati mwanga ndili ngati botolo lodzaza ndi vinyo, ngati matumba a vinyo watsopano amene ali pafupi kuphulika.
Gle, trbuh je moj kao vino bez oduške, i raspukao bi se kao nov mijeh.
20 Ndiyenera kuyankhula kuti mtima utsike; ndiyenera kutsekula pakamwa panga ndi kuyankha.
Govoriæu da odahnem, otvoriæu usne svoje, i odgovoriæu.
21 Sindidzakondera munthu wina aliyense, kapena kuyankhula zoshashalika,
Neæu gledati ko je ko, i èovjeku æu govoriti bez laskanja.
22 pakuti ndikanakhala wa luso loyankhula moshashalika, Mlengi wanga akanandilanga msanga.”
Jer ne umijem laskati; odmah bi me uzeo tvorac moj.

< Yobu 32 >