< Yobu 31 >

1 “Ndinachita pangano ndi maso anga kuti sindidzapenya namwali momusirira.
Zawarłem przymierze ze swoimi oczami; jak mógłbym więc myśleć o pannie?
2 Kodi Mulungu kumwambako wandisungira zotani? Kodi cholowa changa chochokera kwa Wamphamvuzonse kumwambako nʼchotani?
Jaki bowiem byłby dział od Boga z góry? I jakie byłoby dziedzictwo od Wszechmocnego z wysoka?
3 Kodi si chiwonongeko kwa anthu oyipa, tsoka kwa iwo amene amachita zolakwa?
Czy zatracenie nie jest [przygotowane] dla niegodziwych i sroga pomsta dla czyniących nieprawość?
4 Kodi Mulungu saona zochita zanga, ndi kudziwa mayendedwe anga?
Czyż on nie widzi moich dróg i nie liczy wszystkich moich kroków?
5 “Ngati ndachita zinthu mwachiphamaso, kapena kufulumira kukachita zachinyengo,
Jeśli postępowałem kłamliwie, jeśli moja noga spieszyła się do oszustwa;
6 Mulungu andiyeze ndi muyeso wake wolungama ndipo Iye adzadziwa kuti ine ndine wosalakwa,
To niech zważy mnie na wadze sprawiedliwej i niech Bóg pozna moją prawość.
7 ngati mayendedwe anga asempha njira, ngati mtima wanga wakhumbira zimene maso anga aona, kapena ngati ndachita choyipa chilichonse.
Jeśli moja noga zboczyła z drogi i moje serce poszło za moimi oczami, i jeśli jakaś zmaza przylgnęła do moich rąk;
8 Pamenepo ena adye zimene ndinadzala, ndipo zomera zanga zizulidwe.
Wtedy niech ja sieję, a inny spożywa, niech moje latorośle będą wykorzenione.
9 “Ngati mtima wanga unakopekapo ndi mkazi, ndipo ngati ndinalakalaka mkazi wa mnansi wanga,
Jeśli moje serce uwiodła kobieta i jeśli czyhałem pod drzwiami swego bliźniego;
10 pamenepo mkazi wanga aphikire mwamuna wina chakudya, ndipo amuna ena azigona naye.
To niech moja żona mieli innemu i niech inni się nad nią schylają.
11 Pakuti zimenezo zikanakhala zochititsa manyazi, tchimo loyenera kulangidwa nalo.
[Jest] to bowiem haniebny czyn, karygodna nieprawość;
12 Ndi moto umene umayaka mpaka chiwonongeko; ukanapsereza zokolola zanga.
To jest ogień, który pożera aż do zatracenia i może wykorzenić cały mój dobytek.
13 “Ngati ndinkapondereza mlandu wa akapolo anga aamuna kapena aakazi, pamene ankabwera kwa ine ndi milandu yawo,
Jeśli zlekceważyłem sprawę swojego sługi albo swojej służącej, gdy wiedli spór ze mną;
14 ndidzatani pamene Mulungu adzanditsutsa? Nanga ndidzayankha chiyani akadzandifunsa?
Co zrobię, gdy Bóg powstanie? Gdy mnie nawiedzi, co mu odpowiem?
15 Kodi amene anapanga ine mʼmimba mwa amayi anga si yemwe anapanganso iwo? Kodi si mmodzi yemweyo amene anatipanga tonsefe mʼmimba mwa amayi athu?
Czy ten, który mnie stworzył w łonie, nie stworzył też jego? Czy nie on jeden ukształtował nas w łonie?
16 “Ngati ndinawamana aumphawi zinthu zimene ankazikhumba, kapena kuwagwiritsa fuwa lamoto akazi amasiye amene amafuna thandizo kwa ine,
Jeśli odmówiłem prośbie ubogich i jeśli zasmuciłem oczy wdowy;
17 ngati chakudya changa ndinadya ndekha, wosagawirako mwana wamasiye,
Jeśli sam jadłem swoją kromkę [i] nie jadła z niej sierota;
18 chonsechotu kuyambira unyamata wanga ndinamulera monga abambo ake, ndipo moyo wanga wonse ndakhala ndikusamalira akazi amasiye,
(Od swojej młodości bowiem wychowywałem ją jak ojciec, a od łona swojej matki prowadziłem [wdowę]);
19 ngati ndinaona wina aliyense akuzunzika ndi usiwa, kapena munthu wosauka alibe chofunda,
Jeśli widziałem ginącego z powodu braku ubrania albo biedaka bez okrycia;
20 ndipo ngati iyeyo sananditamandepo chifukwa chomufunditsa ndi nsalu ya ubweya wankhosa,
Jeśli jego biodra nie błogosławiły mi dlatego, że się zagrzał wełną moich owiec;
21 ngati ndinaopsezapo mwana wamasiye, poganiza kuti ndinali ndi mphamvu mʼbwalo la milandu,
Jeśli podniosłem rękę przeciwko sierocie, gdy widziałem w bramie swoją pomoc;
22 pamenepo phewa langa lipokonyeke, mkono wanga ukonyoke polumikizira pake.
Wtedy niech odpadnie mój bark od karku, a niech moje ramię wyjdzie ze stawu.
23 Popeza ine ndinaopa kwambiri chiwonongeko chochokera kwa Mulungu, ndinachitanso mantha ndi ulemerero wake, sindikanatha kuchita zinthu zimenezi.
Bałem się bowiem klęski od Boga, a przed jego majestatem nie mógłbym [się ostać].
24 “Ngati ndinayika mtima wanga pa chuma kapena kunena kwa golide wabwino kwambiri kuti, ‘Iwe ndiye chitetezo changa,’
Jeśli pokładałem w złocie swoją nadzieję, a do czystego złota mówiłem: [Ty jesteś] moją ufnością;
25 ngati ndinakondwera chifukwa choti chuma changa chinali chambiri, zinthu zimene manja anga anazipeza,
Jeśli radowałem się ze swojego wielkiego bogactwa i [tego], że moja ręka nabyła wiele;
26 ngati pamene ndinaona dzuwa likuwala, kapena mwezi ukuyenda mwa ulemerero wake,
Jeśli patrzyłem na słońce, gdy świeciło, i na księżyc, gdy sunął wspaniale;
27 ndipo kuti mtima wanga unakopeka nazo nʼkuyika dzanja langa pakamwa mozilemekeza,
A moje serce dało się uwieść potajemnie i moje usta całowały moją rękę;
28 pamenepo zimenezinso zikanakhala machimo oti ndilangidwe nawo, chifukwa ndikanakhala wosakhulupirika kwa Mulungu wakumwamba.
I to byłaby nieprawość karygodna, bo zaparłbym się Boga z wysoka.
29 “Ngati ndinasangalala ndi kuwonongeka kwa mdani wanga, kapena kusekera mavuto pamene mavuto anamugwera,
Jeśli cieszyłem się z upadku tego, który mnie nienawidzi, jeśli wyniosłem się, gdy mu się źle wiodło;
30 ine sindinachimwe ndi pakamwa panga potulutsa matemberero a mdani wanga kuti awonongeke,
(Nawet nie pozwoliłem zgrzeszyć swoim ustom, pragnąc przekleństwa na jego duszy);
31 ngati anthu amene ndimakhala nawo mʼnyumba mwanga sananenepo kuti, ‘Kodi ndani amene sakhuta ndi chakudya cha Yobu?’
Czy ludzie z mojego namiotu nie mówili: Obyśmy mieli z jego mięsa! Nie możemy się najeść.
32 Komatu mlendo sindinamusiye pa msewu usiku wonse, pakuti khomo langa linali lotsekuka nthawi zonse kwa alendo,
Obcy nie nocował na dworze, swoje drzwi otwierałem podróżnemu.
33 ngati ndinabisa tchimo langa monga amachitira anthu ena, kubisa kulakwa mu mtima mwanga
Jeśli ukrywałem swoje przestępstwa jak Adam i chowałem w zanadrzu swoją nieprawość;
34 chifukwa choopa gulu la anthu, ndi kuchita mantha ndi mnyozo wa mafuko kotero ndinakhala chete ndipo sindinatuluke panja.
Czy strach przed wielką zgrają albo pogarda bliskich przeraziły mnie, abym milczał i nie wychodził [za] drzwi?
35 “Aa, pakanakhala wina wondimva! Tsopano ndikutsiriza mawu anga odzitetezera. Wamphamvuzonse andiyankhe; mdani wanga achite kulemba pa kalata mawu ake ondineneza.
Obym miał kogoś, kto by mnie wysłuchał! Oto moja prośba, [aby] Wszechmogący odpowiedział mi i aby mój wróg napisał księgę.
36 Ndithu ine ndikanakoleka kalatayo pa phewa langa, ndikanayivala kumutu ngati chipewa chaufumu.
Czy nie nosiłbym jej na swoim ramieniu i nie przywiązałbym jej sobie [jak] koronę?
37 Ndikanamufotokozera zonse zimene ndinachita; ndikanafika pamaso pake ngati kalonga.
Oznajmiłbym mu liczbę swoich kroków; zbliżyłbym się do niego jak książę.
38 “Ngati minda yanga ikulira monditsutsa ine ndipo malo ake onse osalimidwa anyowa ndi misozi,
Jeśli moja ziemia wołała przeciwko mnie, jeśli razem z nią płakały jej bruzdy;
39 ngati ndinadya za mʼminda mwake osapereka ndalama kapena kukhumudwitsa anthu olima mʼmindamo,
Jeśli spożywałem z jej plonów bez zapłaty, jeśli jej właścicieli pozbawiłem życia;
40 pamenepo mʼmindamo mumere namsongole mʼmalo mwa tirigu ndi udzu mʼmalo mwa barele.” Mawu a Yobu athera pano.
Niech rosną ciernie zamiast pszenicy i sam kąkol zamiast jęczmienia. Skończyły się słowa Hioba.

< Yobu 31 >