< Yobu 31 >

1 “Ndinachita pangano ndi maso anga kuti sindidzapenya namwali momusirira.
I made couenaunt with myn iyen, that Y schulde not thenke of a virgyn.
2 Kodi Mulungu kumwambako wandisungira zotani? Kodi cholowa changa chochokera kwa Wamphamvuzonse kumwambako nʼchotani?
For what part schulde God aboue haue in me, and eritage Almyyti God of hiye thingis?
3 Kodi si chiwonongeko kwa anthu oyipa, tsoka kwa iwo amene amachita zolakwa?
Whether perdicioun is not to a wickid man, and alienacioun of God is to men worchynge wickidnesse?
4 Kodi Mulungu saona zochita zanga, ndi kudziwa mayendedwe anga?
Whether he biholdith not my weies, and noumbrith alle my goyngis?
5 “Ngati ndachita zinthu mwachiphamaso, kapena kufulumira kukachita zachinyengo,
If Y yede in vanyte, and my foot hastide in gile,
6 Mulungu andiyeze ndi muyeso wake wolungama ndipo Iye adzadziwa kuti ine ndine wosalakwa,
God weie me in a iust balaunce, and knowe my symplenesse.
7 ngati mayendedwe anga asempha njira, ngati mtima wanga wakhumbira zimene maso anga aona, kapena ngati ndachita choyipa chilichonse.
If my step bowide fro the weie; if myn iye suede myn herte, and a spotte cleuede to myn hondis;
8 Pamenepo ena adye zimene ndinadzala, ndipo zomera zanga zizulidwe.
sowe Y, and another ete, and my generacioun be drawun out bi the root.
9 “Ngati mtima wanga unakopekapo ndi mkazi, ndipo ngati ndinalakalaka mkazi wa mnansi wanga,
If myn herte was disseyued on a womman, and if Y settide aspies at the dore of my frend; my wijf be the hoore of anothir man,
10 pamenepo mkazi wanga aphikire mwamuna wina chakudya, ndipo amuna ena azigona naye.
and othir men be bowid doun on hir.
11 Pakuti zimenezo zikanakhala zochititsa manyazi, tchimo loyenera kulangidwa nalo.
For this is vnleueful, and the moost wickidnesse.
12 Ndi moto umene umayaka mpaka chiwonongeko; ukanapsereza zokolola zanga.
Fier is deourynge `til to wastyng, and drawynge vp bi the roote alle generaciouns.
13 “Ngati ndinkapondereza mlandu wa akapolo anga aamuna kapena aakazi, pamene ankabwera kwa ine ndi milandu yawo,
If Y dispiside to take doom with my seruaunt and myn hand mayde, whanne thei stryueden ayens me.
14 ndidzatani pamene Mulungu adzanditsutsa? Nanga ndidzayankha chiyani akadzandifunsa?
What sotheli schal Y do, whanne God schal rise to deme? and whanne he schal axe, what schal Y answere to hym?
15 Kodi amene anapanga ine mʼmimba mwa amayi anga si yemwe anapanganso iwo? Kodi si mmodzi yemweyo amene anatipanga tonsefe mʼmimba mwa amayi athu?
Whether he, that wrouyte also hym, made not me in the wombe, and o God formede me in the wombe?
16 “Ngati ndinawamana aumphawi zinthu zimene ankazikhumba, kapena kuwagwiritsa fuwa lamoto akazi amasiye amene amafuna thandizo kwa ine,
If Y denyede to pore men that, that thei wolden, and if Y made the iyen of a wydewe to abide;
17 ngati chakudya changa ndinadya ndekha, wosagawirako mwana wamasiye,
if Y aloone eet my mussel, and a faderles child eet not therof;
18 chonsechotu kuyambira unyamata wanga ndinamulera monga abambo ake, ndipo moyo wanga wonse ndakhala ndikusamalira akazi amasiye,
for merciful doyng encreesside with me fro my yong childhed, and yede out of my modris wombe with me;
19 ngati ndinaona wina aliyense akuzunzika ndi usiwa, kapena munthu wosauka alibe chofunda,
if Y dispiside a man passynge forth, for he hadde not a cloth, and a pore man with out hilyng;
20 ndipo ngati iyeyo sananditamandepo chifukwa chomufunditsa ndi nsalu ya ubweya wankhosa,
if hise sidis blessiden not me, and was not maad hoot of the fleeces of my scheep;
21 ngati ndinaopsezapo mwana wamasiye, poganiza kuti ndinali ndi mphamvu mʼbwalo la milandu,
if Y reiside myn hond on a fadirles child, yhe, whanne Y siy me the hiyere in the yate;
22 pamenepo phewa langa lipokonyeke, mkono wanga ukonyoke polumikizira pake.
my schuldre falle fro his ioynt, and myn arm with hise boonys be al to-brokun.
23 Popeza ine ndinaopa kwambiri chiwonongeko chochokera kwa Mulungu, ndinachitanso mantha ndi ulemerero wake, sindikanatha kuchita zinthu zimenezi.
For euere Y dredde God, as wawis wexynge gret on me; and `Y myyte not bere his birthun.
24 “Ngati ndinayika mtima wanga pa chuma kapena kunena kwa golide wabwino kwambiri kuti, ‘Iwe ndiye chitetezo changa,’
If Y gesside gold my strengthe, and if Y seide to purid gold, Thou art my trist;
25 ngati ndinakondwera chifukwa choti chuma changa chinali chambiri, zinthu zimene manja anga anazipeza,
if Y was glad on my many ritchessis, and for myn hond foond ful many thingis;
26 ngati pamene ndinaona dzuwa likuwala, kapena mwezi ukuyenda mwa ulemerero wake,
if Y siy the sunne, whanne it schynede, and the moone goynge clereli;
27 ndipo kuti mtima wanga unakopeka nazo nʼkuyika dzanja langa pakamwa mozilemekeza,
and if myn herte was glad in priuyte, and if Y kisside myn hond with my mouth;
28 pamenepo zimenezinso zikanakhala machimo oti ndilangidwe nawo, chifukwa ndikanakhala wosakhulupirika kwa Mulungu wakumwamba.
which is the moost wickidnesse, and deniyng ayens hiyeste God;
29 “Ngati ndinasangalala ndi kuwonongeka kwa mdani wanga, kapena kusekera mavuto pamene mavuto anamugwera,
if Y hadde ioye at the fallyng of hym, that hatide me, and if Y ioide fulli, that yuel hadde founde hym;
30 ine sindinachimwe ndi pakamwa panga potulutsa matemberero a mdani wanga kuti awonongeke,
for Y yaf not my throte to do synne, that Y schulde asaile and curse his soule;
31 ngati anthu amene ndimakhala nawo mʼnyumba mwanga sananenepo kuti, ‘Kodi ndani amene sakhuta ndi chakudya cha Yobu?’
if the men of my tabernacle seiden not, Who yyueth, that we be fillid of hise fleischis? a pilgryme dwellide not with outforth;
32 Komatu mlendo sindinamusiye pa msewu usiku wonse, pakuti khomo langa linali lotsekuka nthawi zonse kwa alendo,
my dore was opyn to a weiegoere;
33 ngati ndinabisa tchimo langa monga amachitira anthu ena, kubisa kulakwa mu mtima mwanga
if Y as man hidde my synne, and helide my wickidnesse in my bosum;
34 chifukwa choopa gulu la anthu, ndi kuchita mantha ndi mnyozo wa mafuko kotero ndinakhala chete ndipo sindinatuluke panja.
if Y dredde at ful greet multitude, and if dispisyng of neyyboris made me aferd; and not more Y was stille, and yede not out of the dore;
35 “Aa, pakanakhala wina wondimva! Tsopano ndikutsiriza mawu anga odzitetezera. Wamphamvuzonse andiyankhe; mdani wanga achite kulemba pa kalata mawu ake ondineneza.
who yyueth an helpere to me, that Almyyti God here my desire? that he that demeth,
36 Ndithu ine ndikanakoleka kalatayo pa phewa langa, ndikanayivala kumutu ngati chipewa chaufumu.
write a book, that Y bere it in my schuldre, and cumpasse it as a coroun to me?
37 Ndikanamufotokozera zonse zimene ndinachita; ndikanafika pamaso pake ngati kalonga.
Bi alle my degrees Y schal pronounce it, and Y schal as offre it to the prynce.
38 “Ngati minda yanga ikulira monditsutsa ine ndipo malo ake onse osalimidwa anyowa ndi misozi,
If my lond crieth ayens me, and hise forewis wepen with it;
39 ngati ndinadya za mʼminda mwake osapereka ndalama kapena kukhumudwitsa anthu olima mʼmindamo,
if Y eet fruytis therof with out money, and Y turmentide the soule of erthetileris of it;
40 pamenepo mʼmindamo mumere namsongole mʼmalo mwa tirigu ndi udzu mʼmalo mwa barele.” Mawu a Yobu athera pano.
a brere growe to me for wheete, and a thorn for barli.

< Yobu 31 >