< Yobu 28 >

1 Pali mgodi wa siliva ndiponso malo oyengerapo golide.
Siluer hath bigynnyngis of his veynes; and a place is to gold, in which it is wellid togidere.
2 Chitsulo amachikumba pansi, ndipo mkuwa amawusungunula ku miyala yamkuwa.
Irun is takun fro erthe, and a stoon resolued, `ethir meltid, bi heete, is turned in to money.
3 Munthu amalowa mu mdima atatenga nyale, amafunafuna miyala mpaka ku malire a mgodiwo, kufuna mkuwa mu mdima wandiweyani.
God hath set tyme to derknessis, and he biholdith the ende of alle thingis.
4 Amakumba njira zapansi mu mgodimo, kutali ndi kumene kumakhala anthu, kumalo kumene phazi la munthu silinapondeko; iye amakhala ali lende pansipo namazungulira uku ndi uku.
Also a stronde departith a stoon of derknesse, and the schadewe of deth, fro the puple goynge in pilgrymage; it departith tho hillis, whiche the foot of a nedi man foryat, and hillis with out weie.
5 Nthaka, imene imatulutsa zakudya, kunsi kwake kumachita ngati kwasandulizika ndi moto;
The erthe, wher of breed cam forth in his place, is destried bi fier.
6 miyala ya safiro imachokera mʼmatanthwe ake, ndipo mʼfumbi lake mumakhala miyala yagolide.
The place of saphir ben stoonys therof, and the clottis therof ben gold.
7 Palibe mbalame yodya zinzake imene imadziwa njira yobisikayi, palibe kamtema amene anayiona.
A brid knewe not the weie, and the iye of a vultur, ethir rauenouse brid, bihelde it not.
8 Zirombo zolusa sizipondamo mʼnjiramo, ndipo mkango sudzeranso mʼmenemo.
The sones of marchauntis tretiden not on it, and a lyonesse passide not therbi.
9 Munthu amaphwanya matanthwe olimba, ndipo amagubuduza mapiri kuyambira mʼtsinde.
God stretchide forth his hond to a flynt; he distriede hillis fro the rootis.
10 Amabowola njira mʼmatanthwewo; ndipo amaona chuma chonse cha mʼphirimo.
He hewide doun ryuers in stoonys; and his iye siy al precious thing.
11 Amaletsa mitsinje ya pansipo kuti isayendenso, motero amatulutsira poyera zinthu zobisika.
And he souyte out the depthis of floodis; and he brouyte forth hid thingis in to liyt.
12 “Koma nzeru zingapezeke kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
But where is wisdom foundun, and which is the place of vndurstondyng?
13 Munthu sadziwa kufunika kwake kwa nzeruzo; nzeruyo sipezeka pa dziko lino la anthu amoyo.
A man noot the prijs therof, nether it is foundun in the lond of men lyuynge swetli, `ether delicatli.
14 Phompho likuti, ‘Sizipezeka mwa ine muno.’ Nyanja ikuti, ‘Mwa ine munonso ayi.’
The depthe of watris seith, It is not in me; and the see spekith, It is not with me.
15 Nzeru sungazigule ndi golide wabwino kwambiri, mtengo wake sungawuyerekeze ndi siliva wambiri.
Gold ful cleene schal not be youun for wisdom, nether siluer schal be weied in the chaungyng therof.
16 Nzeru singagulidwe ndi golide wa ku Ofiri, kapena ndi miyala ya onikisi kapena ya safiro.
It schal not be comparysound to the died colours of Iynde, not to the moost preciouse stoon of sardius, nether to saphir.
17 Nzeru sungayiyerekeze ndi golide kapena mwala wa galasi, sungayigule ndi zokometsera zagolide.
Nether gold, nether glas schal be maad euene worth therto;
18 Miyala ya korali ndi krisitali siyoyeneranso ndi kuyitchula nʼkomwe; mtengo wa nzeru ndi woposa miyala ya rubi.
and hiye and fer apperynge vessels of gold schulen not be chaungid for wisdom, nether schulen be had in mynde in comparisoun therof. Forsothe wisdom is drawun of pryuy thingis;
19 Nzeru sungayiyerekeze ndi miyala ya topazi ya ku Kusi; nzeru singagulidwe ndi golide wabwino kwambiri.
topasie of Ethiope schal not be maad euene worth to wisdom, and moost preciouse diyngis schulen not be set togidere in prijs, `ether comparisound, therto.
20 “Kodi tsono nzeru zimachokera kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
Therfor wherof cometh wisdom, and which is the place of vndurstondyng?
21 Malo ake ndi obisika kwa zamoyo zonse, ndi obisika ngakhale kwa mbalame zamlengalenga.
It is hid fro the iyen of alle lyuynge men; also it is hid fro briddis of heuene.
22 Chiwonongeko ndi imfa zikuti, ‘Tangomva mphekesera chabe ya zimenezo!’
Perdicioun and deeth seiden, With oure eeris we herden the fame therof.
23 Mulungu yekha ndiye amadziwa njira yake yopita kumeneko, ndipo Iye yekha amadziwa kumene nzeru imakhala,
God vndurstondith the weye therof, and he knowith the place therof.
24 pakuti Iye amayangʼana mpaka ku malekezero a dziko lapansi ndipo amaona zonse za kunsi kwa thambo.
For he biholdith the endis of the world, and biholdith alle thingis that ben vndur heuene.
25 Iye atapatsa mphepo mphamvu zake, nayeza kuzama kwa nyanja,
`Which God made weiyte to wyndis, and weiede watris in mesure.
26 atakhazikitsa lamulo loti mvula izigwa ndi kukonza njira ya chingʼaningʼani cha bingu,
Whanne he settide lawe to reyn, and weie to tempestis sownynge;
27 pamenepo ndi pamene anayangʼana nzeruzo naziyeza mtengo wake; nazikhazikitsa ndi kuzisanthula bwino lomwe.
thanne he siy wisdom, and telde out, and made redi, and souyte out.
28 Ndipo Iye anati kwa munthu, ‘Taonani, kuopa Ambuye, ndiye nzeru zimenezo ndipo kuthawa zoyipa ndiye kumvetsa zinthu kumeneko.’”
And he seide to man, Lo! the drede of the Lord, thilke is wisdom; and to go awei fro yuel, is vndurstondyng.

< Yobu 28 >