< Yobu 21 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Wtedy Hiob odpowiedział:
2 “Mvetserani bwino mawu anga; ichi chikhale chitonthozo changa chochokera kwa inu.
Słuchajcie uważnie moich słów, a to będzie dla mnie wasza pociecha.
3 Ndiloleni ndiyankhule ndipo ndikatha kuyankhula munditonzetonze.
Pozwólcie mi mówić, a potem, gdy powiem, naśmiewajcie się ze mnie.
4 “Kodi ine ndikudandaulira munthu? Tsono ndilekerenji kupsa mtima?
Czy swoją skargę kieruję do człowieka? A jeśli tak, to dlaczego mój duch nie miałby być wzburzony?
5 Ndipenyeni ndipo mudabwe; mugwire dzanja pakamwa.
Spójrzcie na mnie, zdumiewajcie się i połóżcie rękę na swoje usta.
6 Ndikamaganiza zimenezi ndimachita mantha kwambiri; thupi langa limanjenjemera.
Gdy tylko sobie przypomnę, jestem przerażony i strach ogarnia moje ciało.
7 Chifukwa chiyani anthu oyipa amakhalabe ndi moyo, amakalamba ndi kusanduka amphamvu?
Czemu niegodziwi żyją, starzeją się, a nawet wzrastają w bogactwie?
8 Amaona ana awo akukhazikika pamodzi nawo, zidzukulu zawo zikukula bwino iwo akuona.
Ich potomstwo utrwala się przed nimi, a ich rodzina [wzrasta] na ich oczach.
9 Mabanja awo amakhala pa mtendere ndipo sakhala ndi mantha; mkwapulo wa Mulungu suwakhudza nʼkomwe.
Ich domy są bezpieczne, bez strachu i nie dotyka ich rózga Boga.
10 Ngʼombe zawo zazimuna sizilephera kubereketsa; ngʼombe zawo zazikazi sizipoloza.
Ich byk zapładnia i nie zawodzi, ich krowa cieli się i nie roni.
11 Amatulutsa ana awo ngati gulu la nkhosa; makanda awo amavinavina pabwalo.
Wypuszczają swe malutkie [dzieci] jak trzodę, a ich synowie podskakują.
12 Amayimba nyimbo pogwiritsa ntchito matambolini ndi azeze; amakondwa pakumva kulira kwa chitoliro.
Chwytają za bęben i harfę i weselą się przy dźwięku fletu.
13 Zaka zawo zimatha ali mu ulemerero ndipo amatsikira ku manda mwamtendere. (Sheol h7585)
Spędzają swoje dni w dobrobycie, a w mgnieniu oka zstępują do grobu. (Sheol h7585)
14 Koma anthuwo amawuza Mulungu kuti, ‘Tichokereni!’ Ife tilibe chikhumbokhumbo chofuna kudziwa njira zanu.
Dlatego mówią do Boga: Odejdź od nas, bo nie chcemy poznać twoich dróg.
15 Kodi Wamphamvuzonseyo ndani kuti timutumikire? Ife tipindula chiyani tikamapemphera kwa Iyeyo?
Kim jest Wszechmocny, abyśmy mieli mu służyć? Cóż nam pomoże [to], że będziemy się modlić do niego?
16 Komatu ulemerero wawo suli mʼmanja mwawo, koma ine ndimakhala patali ndi uphungu wa anthu oyipa.
Oto ich dobra nie są w ich rękach. Rada niegodziwych daleka [jest] ode mnie.
17 “Koma nʼkangati kamene nyale ya anthu oyipa imazimitsidwa? Nʼkangati kamene tsoka limawagwera? Nʼkangati kamene Mulungu amawakwiyira ndi kuwalanga?
Jak często gaśnie pochodnia niegodziwych? [Jak często] przychodzi na nich zguba? [Bóg] im wydziela cierpienie w swoim gniewie.
18 Nʼkangati kamene iwo amakhala ngati phesi lowuluka ndi mphepo, ngati mungu wowuluzika ndi kamvuluvulu?
Są jak słoma na wietrze i jak plewa, którą wicher porywa.
19 Paja amati, ‘Mulungu amalanga ana chifukwa cha machimo abambo awo.’ Koma Mulungu amabwezera chilango munthuyo, kuti adziwe kuti Mulungu amalangadi.
Bóg zachowuje jego nieprawość dla jego synów; odpłaca mu, aby to poczuł.
20 Mulole kuti adzionere yekha chilango chake, kuti alawe ukali wa Wamphamvuzonse.
Jego oczy ujrzą jego nieszczęście i będzie pił z gniewu Wszechmocnego.
21 Nanga kodi amalabadira chiyani zabanja lake limene walisiya mʼmbuyo, pamene chiwerengero cha masiku ake chatha?
Jaką bowiem ma on rozkosz w swoim domu, po swojej [śmierci], gdy liczba jego miesięcy zostanie skrócona?
22 “Kodi alipo wina amene angaphunzitse Mulungu nzeru, poti Iye amaweruza ngakhale anthu apamwamba?
Czy [ktoś] może uczyć Boga wiedzy, wiedząc, że on sam sądzi najwyższych?
23 Munthu wina amamwalira ali ndi mphamvu zonse, ali pa mtendere ndi pa mpumulo,
Jeden umiera w pełni swoich sił, bezpieczny ze wszystkich stron i spokojny;
24 thupi lake lili lonenepa, mafupa ake ali odzaza ndi mafuta.
Jego piersi są pełne mleka, a jego kości zwilża szpik.
25 Munthu wina amamwalira ali wowawidwa mtima, wosalawapo chinthu chabwino chilichonse.
Drugi zaś umiera w goryczy ducha i nigdy nie jadał z uciechą.
26 Olemera ndi osauka omwe amamwalira ndi kuyikidwa mʼmanda ndipo onse amatuluka mphutsi.
Razem będą leżeć w prochu i okryją ich robaki.
27 “Ndikudziwa bwino zimene mukuganiza, ziwembu zanu zomwe mukuti mundichitire.
Oto znam wasze myśli i zamiary, [jakie] przeciwko mnie złośliwie obmyślacie.
28 Inu mukuti, ‘Kodi nyumba ya mkulu uja ili kuti, matenti amene munkakhala anthu oyipa aja ali kuti?’
Mówicie bowiem: Gdzie [jest] dom księcia? A gdzie mieszkanie niegodziwych?
29 Kodi munawafunsapo anthu amene ali pa ulendo? Kodi munaganizirapo zimene iwo amanena?
Czy nie pytaliście podróżnych? Czy nie chcecie poznać ich znaków;
30 Zakuti munthu woyipa amasungidwa chifukwa cha tsiku la tsoka, kuti amapulumutsidwa chifukwa cha tsiku la ukali wa Mulungu?
Że niegodziwy jest zachowany na dzień zatracenia? Zostanie przyprowadzony na dzień gniewu.
31 Kodi ndani amadzudzula munthu wochimwayo? Ndani amamubwezera zoyipa zimene anachita?
Któż mu wypomni w oczy jego drogę? A kto mu odpłaci za to, co uczynił?
32 Iye amanyamulidwa kupita ku manda ndipo anthu amachezera pa manda ake.
Zaprowadzą go do grobu i zostanie w grobowcu.
33 Dothi la ku chigwa limamukomera; anthu onse amatsatira mtembo wake, ndipo anthu osawerengeka amakhala patsogolo pa chitanda chakecho.
Słodkie mu będą bryły ziemi z doliny i pociągnie za sobą wszystkich ludzi; a ci, którzy szli przed nim, są niezliczeni.
34 “Nanga inu mudzanditonthoza bwanji ine ndi mawu anu opandapakewo palibe chimene chatsala kuti muyankhe koma mabodza basi!”
Czemu więc daremnie mnie pocieszacie, skoro w waszych odpowiedziach pozostaje fałsz?

< Yobu 21 >