< Yobu 20 >

1 Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti
Et Tsophar, le Naamathite, répondit et dit:
2 “Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe chifukwa ndasautsidwa kwambiri.
C’est pourquoi mes pensées m’inspirent une réponse, et à cause de ceci l’ardeur de mon esprit [agit] en moi:
3 Ndikumva kudzudzula kondinyoza, ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe.
J’entends une réprimande qui me couvre de honte, et mon esprit me répond par mon intelligence.
4 “Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale, kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi,
Sais-tu bien que, de tout temps, depuis que l’homme a été mis sur la terre,
5 kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha, chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa.
L’exultation des méchants est courte, et la joie de l’impie n’est que pour un moment?
6 Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba ndipo mutu wake uli nengʼaa,
Si sa hauteur s’élève jusqu’aux cieux, et que sa tête touche les nuées,
7 iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe; iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’
Il périra pour toujours comme ses ordures; ceux qui l’ont vu diront: Où est-il?
8 Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso, adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku.
Il s’envole comme un songe, et on ne le trouve pas; il s’enfuit comme une vision de la nuit.
9 Diso limene linamuona silidzamuonanso; sadzapezekanso pamalo pake.
L’œil l’a regardé et ne l’aperçoit plus, et son lieu ne le revoit plus.
10 Ana ake adzabwezera zonse zimene iyeyo analanda anthu osauka;
Ses fils rechercheront la faveur des pauvres, et ses mains restitueront [ce que] sa violence [a ravi].
11 Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake zidzagona naye limodzi mʼfumbi.
Ses os étaient pleins de sa jeunesse: elle se couchera avec lui sur la poussière.
12 “Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake,
Si le mal est doux dans sa bouche, [et] qu’il le cache sous sa langue,
13 ngakhale salola kuzilavula, ndipo amazisunga mʼkamwa mwake,
S’il l’épargne et ne l’abandonne pas, mais qu’il le retienne dans sa bouche,
14 koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake; chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo.
Son pain sera changé dans ses entrailles en un fiel d’aspic au-dedans de lui.
15 Adzachisanza chuma chimene anachimeza; Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo.
Il a avalé les richesses, et il les vomira; Dieu les chassera de son ventre.
16 Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo ululu wa mphiri udzamupha.
Il sucera le venin des aspics, la langue de la vipère le tuera.
17 Sadzasangalala ndi timitsinje, mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta.
Il ne verra pas des ruisseaux, des rivières, des torrents de miel et de beurre.
18 Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya; sadzasangalala ndi phindu la malonda ake.
Il rendra le fruit de son travail, et ne l’avalera pas; il le restituera selon sa valeur, et ne s’en réjouira pas.
19 Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo; iyeyo analanda nyumba zimene sanamange.
Car il a opprimé, délaissé les pauvres; il a pillé une maison qu’il n’avait pas bâtie.
20 “Chifukwa choti umbombo wake sutha, sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho.
Parce qu’il n’a pas connu de repos dans son désir, il ne sauvera rien de ce qu’il a de plus cher.
21 Palibe chatsala kuti iye adye; chuma chake sichidzachedwa kutha.
Rien n’a échappé à sa voracité: c’est pourquoi son bien-être ne durera pas.
22 Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera; mavuto aakulu adzamugwera.
Dans la plénitude de son abondance, il sera dans la détresse; toutes les mains des malheureux viendront sur lui.
23 Akadya nʼkukhuta, Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto ngati mvula yosalekeza.
Il arrivera que, pour remplir son ventre, [Dieu] enverra sur lui l’ardeur de sa colère, et la fera pleuvoir sur lui dans sa chair.
24 Ngakhale athawe mkondo wachitsulo, muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa.
S’il fuit devant les armes de fer, un arc d’airain le transpercera.
25 Muviwo adzawutulutsira ku msana, songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake. Adzagwidwa ndi mantha aakulu;
Il arrache [la flèche] et elle sort de son corps, et le fer étincelant de son fiel: les terreurs sont sur lui.
26 mdima wandiweyani ukudikira chuma chake. Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake.
Toutes les ténèbres sont réservées pour ses trésors; un feu qu’on ne souffle pas le dévorera, [et] se repaîtra de ce qui reste dans sa tente.
27 Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake; dziko lapansi lidzamuwukira.
Les cieux révéleront son iniquité, et la terre s’élèvera contre lui.
28 Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake, katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu.
Le revenu de sa maison sera emporté; il s’écoulera au jour de Sa colère.
29 Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa, mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”
Telle est, de la part de Dieu, la portion de l’homme méchant, et l’héritage qui lui est assigné par Dieu.

< Yobu 20 >