< Yobu 19 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
A Jov odgovori i reèe:
2 “Kodi mudzakhala mukundizunza mpaka liti, ndi kundilasa ndi mawu anuwo?
Dokle æete muèiti dušu moju i satirati me rijeèima?
3 Inuyo mwandinyoza kwambiri; mwanditsutsa mopanda manyazi.
Veæ ste me deset puta naružili; nije vas stid što tako navaljujete na me?
4 Ngati ndi zoona kuti ine ndasochera, cholakwachotu nʼchanga.
Ali ako sam doista pogriješio, pogrješka æe moja ostati kod mene.
5 Ngati ndithudi mukudziyika nokha pamwamba panga, ndi kugwiritsa ntchito kunyozedwa kwanga polimbana nane,
Ako li se još hoæete da dižete na me i da me korite mojom sramotom,
6 pamenepa dziwani kuti Mulungu wandilakwira ndipo wandizinga ukonde wake.
Onda znajte da me je Bog oborio i mrežu svoju razapeo oko mene.
7 “Ngakhale ndifuwule kuti, ‘Akundizunza!’ Palibe wondiyankha; ngakhale ndipemphe thandizo, palibe wondichitira zolungama.
Eto, vièem na nepravdu, ali se ne slušam; vapijem, ali nema suda.
8 Mulungu wanditsekera njira yanga kotero sindingathe kudutsa; waphimba njira zanga ndi mdima.
Zagradio je put moj da ne mogu proæi; na staze moje metnuo je mrak.
9 Iye wandilanda ulemu wanga ndipo wandivula chipewa chaufumu pamutu panga.
Svukao je s mene slavu moju i skinuo vijenac s glave moje.
10 Wandiphwanyaphwanya mbali zonse ndipo ndatheratu; Iye wazula chiyembekezo changa ngati mtengo.
Porušio me je otsvuda, da me nema; i kao drvo išèupao je nadanje moje.
11 Wandikwiyira ndipo akundiyesa mmodzi mwa adani ake.
Raspalio se na me gnjev njegov, i uzeo me je meðu neprijatelje svoje.
12 Ankhondo ake akubwera kwa ine mwamphamvu, akonzekera zodzalimbana nane ndipo azungulira nyumba yanga.
Vojske njegove doðoše sve zajedno i nasuše sebi put k meni, i stadoše u oko okolo šatora mojega.
13 “Mulungu wandisiyanitsa ndi abale anga; wasandutsa odziwana nane kukhala achilendo kwa ine.
Braæu moju udaljio je od mene, i znanci moji tuðe se od mene.
14 Abale anga andithawa; abwenzi anga andiyiwala.
Bližnji moji ostaviše me, i znanci moji zaboraviše me.
15 Anthu odzacheza ku nyumba kwanga ndiponso antchito anga aakazi andisandutsa mlendo; ndasanduka mlendo mʼmaso mwawo.
Domašnji moji i moje sluškinje gledaju me kao tuðina; stranac sam u oèima njihovijem.
16 Ndikayitana wa ntchito wanga, iye sandiyankha, ngakhale ndikapempha ndi pakamwa panga sandichitira kanthu.
Zovem slugu svojega, a on se ne odziva, a molim ga ustima svojim.
17 Mpweya wanga umamunyansa mkazi wanga; ndine chinthu chonyansa kwa abale anga a mimba imodzi.
Dah je moj mrzak ženi mojoj, a preklinjem je sinovima utrobe svoje.
18 Inde, ngakhale ana amandinyoza; akandiona amandinyodola.
Ni djeca ne haju za me; kad ustanem, ruže me.
19 Anzanga onse apamtima amanyansidwa nane; iwo amene ndinkawakonda andiwukira.
Mrzak sam svjema najvjernijim svojim, i koje ljubljah postaše mi protivnici.
20 Ndangotsala khungu ndi mafupa okhaokha; ndapulumuka lokumbakumba.
Za kožu moju kao za meso moje prionuše kosti moje; jedva osta koža oko zuba mojih.
21 “Mvereni chisoni, inu abwenzi anga, mvereni chisoni, pakuti dzanja la Mulungu landikantha.
Smilujte se na me, smilujte se na me, prijatelji moji, jer se ruka Božija dotakla mene.
22 Chifukwa chiyani mukundilondola ngati Mulungu? Kodi simunatope nalo thupi langa?
Zašto me gonite kao Bog, i mesa mojega ne možete da se nasitite?
23 “Aa, achikhala mawu anga analembedwa, achikhala analembedwa mʼbuku,
O kad bi se napisale rijeèi moje! kad bi se stavile u knjigu!
24 akanalembedwa pa mwala ndi chitsulo, akanalembedwa pa thanthwe kuti sangathe kufufutidwa!
Pisaljkom gvozdenom i olovom na kamenu za vjeèni spomen kad bi se urezale!
25 Koma ndikudziwa kuti mpulumutsi wanga ali ndi moyo, ndipo pa nthawi yomaliza adzabwera kudzanditeteza.
Ali znam da je živ moj iskupitelj, i na pošljedak da æe stati nad prahom.
26 Ndipo khungu langa litatha nʼkuwonongeka, mʼthupi langa lomweli ndidzamuona Mulungu.
I ako se ova koža moja i rašèini, opet æu u tijelu svom vidjeti Boga.
27 Ine ndemwe ndidzamuona Iye ndi maso angawa, ineyo, osati wina ayi. Ndithu mtima wanga ukufunitsitsadi!
Ja isti vidjeæu ga, i oèi moje gledaæe ga, a ne drugi. A bubrega mojih nestaje u meni.
28 “Koma inu mukuti, ‘Haa! Tingamuzunze bwanji, popeza kuti zonsezi zaoneka chifukwa cha iye yemweyo?’
Nego bi trebalo da reèete: zašto ga gonimo? kad je korijen besjede u meni.
29 Inu muyenera kuopa lupanga; pakuti mkwiyo wake umalangadi ndi lupanga; zikadzatero muzadziwa kuti chiweruzo chilipo ndithu.”
Bojte se maèa; jer je maè osveta za bezakonje; i znajte da ima sud.

< Yobu 19 >