< Yobu 18 >

1 Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
A Vildad Sušanin odgovori i reèe:
2 “Kodi iwe Yobu utsiriza liti zoyankhula zakozi? Khala munthu wozindikira zinthu ndipo ukatero ife tidzayankhula.
Kad æete svršiti razgovor? Orazumite se, pa æemo onda govoriti.
3 Chifukwa chiyani ukutiyesa ngati ngʼombe ndi kuoneka ngati opusa mʼmaso mwako?
Zašto se misli da smo kao stoka? zašto smo gadni u vašim oèima?
4 Iwe amene ukudzipweteka wekha ndi mkwiyo wako, kodi dziko lapansi lisanduke bwinja chifukwa cha iweyo? Kodi kapena thanthwe lisunthidwe kuchoka pa malo ake?
Koji rastržeš dušu svoju u jarosti svojoj, hoæe li se tebe radi ostaviti zemlja i stijena se premjestiti sa svojega mjesta?
5 “Nyale ya munthu woyipa yazimitsidwa; malawi a moto wake sakuwalanso.
Da, vidjelo bezbožnijeh ugasiæe se, i iskra ognja njihova neæe sijati.
6 Kuwala kwa mʼnyumba mwake kwasanduka mdima; nyale ya pambali pake yazima.
Vidjelo æe pomrknuti u šatoru njegovu, i žižak æe se njegov ugasiti u njemu.
7 Mayendedwe ake amgugu azilala; fundo zake zomwe zamugwetsa.
Silni koraci njegovi stegnuæe se, i oboriæe ga njegova namjera.
8 Mapazi ake amulowetsa mu ukonde ndipo akungoyendayenda mu ukondewo.
Jer æe se uvaliti u zamku nogama svojim i naiæi æe na mrežu;
9 Msampha wamkola mwendo; khwekhwe lamugwiritsitsa.
Uhvatiæe ga zamka za petu i svladaæe ga lupež.
10 Amutchera msampha pansi mobisika; atchera diwa pa njira yake.
Sakriveno mu je pruglo na zemlji, i klopka na stazi.
11 Zoopsa zikumuchititsa mantha kumbali zonse, zikutsatira mayendedwe ake onse.
Otsvuda æe ga strahote strašiti i tjeraæe ga ustopce.
12 Mphamvu zake zatha chifukwa cha njala, tsoka likumudikira.
Izgladnjeæe sila njegova, i nevolja æe biti gotova uza nj.
13 Wagwidwa nthenda yoopsa thupi lonse; miyendo yake, manja ake, zonse zawola.
Poješæe žile kože njegove, poješæe žile njegove prvenac smrti.
14 Wachotsedwa mʼnyumba imene ankadalira, ndipo amukokera ku imfa, mfumu ya zoopsa zonse.
Išèupaæe se iz stana njegova uzdanica njegova, i to æe ga odvesti k caru strašnom.
15 Mʼnyumba mwake zonse zachotsedwamo; awazamo sulufule kuti aphe tizirombo ta matenda.
Nastavaæe se u šatoru njegovu, koji neæe biti njegov, posuæe se sumporom stan njegov.
16 Mizu yake ikuwuma pansi ndipo nthambi zake zikufota
Žile æe se njegove posušiti ozdo, i ozgo æe se sasjeæi grane njegove.
17 Sadzakumbukiridwanso pa dziko lapansi; sadzakhalanso ndi chinthu chomutchukitsa mʼdziko.
Spomen æe njegov poginuti na zemlji, niti æe mu imena biti po ulicama.
18 Amuchotsa pa malo owala ndi kumuponya ku mdima, ndipo amupirikitsa pa dziko lonse.
Odagnaæe se iz svjetlosti u mrak, i izbaciæe se iz svijeta.
19 Iye alibe ana kapena zidzukulu pakati pa anthu ake, kulibe wotsala kumene iye ankakhala.
Ni sina ni unuka neæe mu biti u narodu njegovu, niti kakoga ostatka u stanovima njegovijem.
20 Anthu akumadzulo adabwa kwambiri ndi tsoka lake; anthu akummawa agwidwa ndi mantha aakulu.
Èudiæe se danu njegovu koji budu poslije njega, a koji su bili prije obuzeæe ih strah.
21 Ndithudi, izi ndiye zimagwera munthu woyipa; amenewa ndiye mathero a munthu amene sadziwa Mulungu.”
Taki su stanovi bezakonikovi, i tako je mjesto onoga koji ne zna za Boga.

< Yobu 18 >