< Yobu 15 >

1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
A Elifas Temanac odgovori i reèe:
2 “Kodi munthu wanzeru angayankhe ndi mawu achabechabe otere, kapena angakhutitse mimba yake ndi mphepo yotentha yochokera kummawa?
Hoæe li mudar èovjek kazivati prazne misli i puniti trbuh svoj vjetrom istoènijem,
3 Kodi angathe kutsutsa ndi mawu opanda pake, kapena kuyankhula mawu opanda phindu?
Prepiruæi se govorom koji ne pomaže i rijeèima koje nijesu ni na što?
4 Koma iwe ukuchepetsa zoopa Mulungu ndipo ukutchinga zodzikhuthulira kwa Mulungu.
A ti uništavaš strah Božji i ukidaš molitve k Bogu.
5 Tchimo lako ndiye likuyankhulitsa pakamwa pakopo; ndipo watengera mayankhulidwe a atambwali.
Jer bezakonje tvoje pokazuju usta tvoja, ako i jesi izabrao jezik lukav.
6 Pakamwa pakopo ndiye pakukutsutsa osati pakamwa panga; milomo yakoyo ikukutsutsa.
Osuðuju te usta tvoja, a ne ja; i usne tvoje svjedoèe na te.
7 “Kodi ndiwe munthu woyamba kubadwa? Kodi unalengedwa mapiri asanalengedwe?
Jesi li se ti prvi èovjek rodio? ili si prije humova sazdan?
8 Kodi unali mʼgulu la alangizi a Mulungu? Kodi ukudziyesa wanzeru ndiwe wekha?
Jesi li tajnu Božiju èuo i pokupio u sebe mudrost?
9 Kodi iwe umadziwa chiyani chimene ife sitichidziwa? Kodi iwe uli ndi chidziwitso chanji chimene ife tilibe?
Šta ti znaš što mi ne bismo znali? šta ti razumiješ što ne bi bilo u nas?
10 Anthu a imvi ndi okalamba ali mbali yathu, anthu amvulazakale kupambana abambo ako.
I sijedijeh i starijeh ljudi ima meðu nama, starijih od oca tvojega.
11 Kodi mawu otonthoza mtima ochokera kwa Mulungu sakukukwanira, mawu oyankhula mofatsawa kwa iwe?
Male li su ti utjehe Božije? ili imaš što sakriveno u sebi?
12 Chifukwa chiyani ukupsa mtima, ndipo chifukwa chiyani ukutuzula maso ako,
Što te je zanijelo srce tvoje? i što sijevaju oèi tvoje,
13 moti ukupsera mtima Mulungu ndi kuyankhula mawu otero pakamwa pako?
Te obraæaš protiv Boga duh svoj i puštaš iz usta svojih take rijeèi?
14 “Kodi munthu nʼchiyani kuti nʼkukhala woyera mtima kapena wobadwa mwa amayi nʼchiyani kuti nʼkukhala wolungama mtima?
Šta je èovjek, da bi bio èist, i roðeni od žene, da bi bio prav?
15 Ngati Mulungu sakhulupirira ngakhale angelo ake, ngakhale zakumwamba sizoyera pamaso pake,
Gle, ne vjeruje svecima svojim, i nebesa nijesu èista pred oèima njegovijem;
16 nanga kuli bwanji munthu amene ndi wonyansa ndi wa njira zokhotakhota, amene kuchita zoyipa kuli ngati kumwa madzi.
Akamoli gadni i smrdljivi èovjek, koji pije nepravdu kao vodu?
17 “Mvetsera kwa ine ndipo ndidzakufotokozera; ndilole ndikuwuze zimene ndaziona,
Ja æu ti kazati, poslušaj me, i pripovjediæu ti što sam vidio,
18 zimene anandiphunzitsa anthu anzeru, sanandibisire kalikonse kamene anamva kuchokera kwa makolo awo.
Što mudarci kazaše i ne zatajiše, što primiše od otaca svojih,
19 (Ndi kwa iwowa kumene dziko lino linaperekedwa pamene panalibe mlendo wokhala pakati pawo).
Kojima samijem dana bi zemlja, i tuðin ne proðe kroz nju.
20 Munthu woyipa amavutika ndi masautso masiku onse a moyo wake, munthu wankhanza adzavutika zaka zake zonse.
Bezbožnik se muèi svega vijeka svojega, i nasilniku je malo godina ostavljeno.
21 Amamva mawu owopsa mʼmakutu mwake, pamene zonse zikuoneka ngati zili bwino, anthu achifwamba amamuthira nkhondo.
Strah mu zuji u ušima, u mirno doba napada pustošnik na nj.
22 Iye sakhulupirira kuti angathe kupulumuka ku mdima wa imfa; iyeyo ndi woyenera kuphedwa.
Ne vjeruje da æe se vratiti iz tame, otsvuda priviða maè.
23 Amangoyendayenda pali ponse kunka nafuna chakudya; amadziwa kuti tsiku la mdima lili pafupi.
Tumara za hljebom govoreæi: gdje je? Zna da je za nj spremljen dan tamni.
24 Masautso ndi nthumanzi zimamuchititsa mantha kwambiri; zimamugonjetsa iye monga imachitira mfumu yokonzekera kukathira nkhondo,
Tuga i nevolja straše ga, i navaljuju na nj kao car gotov na boj.
25 chifukwa iye amatambasula dzanja lake kuyambana ndi Mulungu ndipo amadzitama yekha polimbana ndi Wamphamvuzonse.
Jer je zamahnuo na Boga rukom svojom, i svemoguæemu se opro.
26 Amapita mwa mwano kukalimbana naye atanyamula chishango chochindikala ndi cholimba.
Trèi ispravljena vrata na nj s mnogim visokim štitovima svojim.
27 “Ngakhale nkhope yake ndi yonenepa ndipo mʼchiwuno mwake muli mnofu wambiri,
Jer je pokrio lice svoje pretilinom, i navaljao salo na bokove svoje.
28 munthuyo adzakhala mʼmizinda yowonongeka ndi mʼnyumba zosayenera kukhalamo anthu, nyumba zimene zikugwa ndi kuwonongeka.
I sjedio je u gradovima raskopanijem i u kuæama pustijem, obraæenijem u gomilu kamenja.
29 Iye sadzalemeranso ndipo chuma chake sichidzakhalitsa, ngakhale minda yake sidzabala zipatso pa dziko lapansi.
Neæe se obratiti niti æe ostati blago njegovo, i neæe se raširiti po zemlji dobro njegovo.
30 Iyeyo sadzapulumuka mu mdimamo; lawi lamoto lidzawumitsa nthambi zake, ndipo mpweya wochokera mʼkamwa mwa Mulungu udzamusesa.
Neæe izaæi iz mraka, ogranke njegove osušiæe plamen, odnijeæe ga duh usta njegovijeh.
31 Asadzinyenge yekha podalira zinthu zachabechabe, pakuti pa mapeto pake sadzaphulapo kanthu.
Neka se ne uzda u taštinu prevareni, jer æe mu taština biti plata.
32 Iye adzalandira malipiro ake nthawi yake isanakwane, ndipo nthambi zake sizidzaphukanso.
Prije svojega vremena svršiæe se, i grana njegova neæe zelenjeti.
33 Iye adzakhala ngati mtengo wamphesa wopululidwa zipatso zake zisanapse, adzakhala ngati mtengo wa olivi umene wayoyola maluwa ake.
Otkinuæe se kao s loze nezreo grozd njegov i pupci æe se njegovi kao s masline pobacati.
34 Pakuti anthu osapembedza Mulungu adzakhala osabala ndipo moto udzapsereza nyumba za onse okonda ziphuphu.
Jer æe opustjeti zbor licemjerski, i oganj æe spaliti šatore onijeh koji primaju poklone.
35 Iwo amalingalira zaupandu ndipo amachita zoyipa; mtima wawo umakonzekera zachinyengo.”
Zaèinju nevolju i raðaju muku, i trbuh njihov sastavlja prijevaru.

< Yobu 15 >