< Yobu 12 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Sotheli Joob answeride, and seide,
2 “Ndithudi inuyo ndinu anthu ndipo nzeru zanu zidzafera nanu pamodzi!
Therfor ben ye men aloone, that wisdom dwelle with you?
3 Koma inenso ndili nazo nzeru ngati inu; ineyo sindine munthu wamba kwa inu. Ndani amene sadziwa zonse zimene mwanenazi?
And to me is an herte, as and to you, and Y am not lowere than ye; for who knowith not these thingis, whiche ye knowen?
4 “Ndasanduka chinthu choseketsa kwa abwenzi anga, ngakhale ndinkapemphera kwa Mulungu ndipo Iye ankandiyankha. Ine ndasanduka chinthu chongoseketsa, ngakhale ndili wolungama ndi wosalakwa!
He that is scorned of his frend, as Y am, schal inwardli clepe God, and God schal here hym; for the symplenesse of a iust man is scorned.
5 Anthu amene ali pabwino amanyoza anzawo amene ali pa tsoka. Tsokalo limagwa pa amene wayamba kale kugwa.
A laumpe is dispisid at the thouytis of riche men, and the laumpe is maad redi to a tyme ordeyned.
6 Nyumba za anthu achifwamba zimakhala pa mtendere, ndipo anthu amene amaputa Mulungu amakhala pabwino, amene amanyamula milungu yawo mʼmanja.
The tabernaclis of robberis ben plenteuouse, `ether ful of goodis; and boldli thei terren God to wraththe, whanne he hath youe alle thingis in to her hondis.
7 “Koma funsa nyama zakuthengo ndipo zidzakuphunzitsa, kapena mbalame zamumlengalenga ndipo zidzakuwuza;
No wondur, ax thou beestis, and tho schulen teche thee; and axe thou volatilis of the eir, and tho schulen schewe to thee.
8 kapena uyankhule ndi dziko lapansi ndipo lidzakuphunzitsa, kapena ulole nsomba zamʼnyanja kuti zikufotokozere.
Speke thou to the erthe, and it schal answere thee; and the fischis of the see schulen telle tho thingis.
9 Kodi mwa zonsezi ndi chiti chimene sichidziwa kuti lachita zimenezi ndi dzanja la Yehova?
Who knowith not that the hond of the Lord made alle these thingis?
10 Mʼmanja mwake ndi mʼmene muli moyo wa cholengedwa chilichonse, ndiponso moyo wa anthu a mitundu yonse.
In whos hond the soule is of ech lyuynge thing, and the spirit, `that is, resonable soule, of ech fleisch of man.
11 Kodi khutu sindiye limene limamva mawu monga mmene lilime limalawira chakudya?
Whether the eere demeth not wordis, and the chekis of the etere demen sauour?
12 Kodi nzeru sipezeka pakati pa anthu okalamba? Kodi moyo wautali sumabweretsa nzeru zomvetsa zinthu?
Wisdom is in elde men, and prudence is in myche tyme.
13 “Kwa Mulungu ndiye kuli nzeru ndi mphamvu; uphungu ndi kumvetsa zinthu ndi zake.
Wisdom and strengthe is at God; he hath counsel and vndurstondyng.
14 Chimene Iye wapasula palibe angachimangenso. Akatsekera munthu mʼndende palibe angamutulutse.
If he distrieth, no man is that bildith; if he schittith in a man, `noon is that openith.
15 Iyeyo akamanga mvula dziko limawuma; akamasula mvulayo, madzi amasefukira pa dziko.
If he holdith togidere watris, alle thingis schulen be maad drie; if he sendith out tho watris, tho schulen distrie the erthe.
16 Kwa Iye kuli mphamvu ndi kupambana; munthu wopusitsidwa ndiponso wopusitsa onse ali mu ulamuliro wake.
Strengthe and wisdom is at God; he knowith bothe hym that disseyueth and hym that is disseyued.
17 Iye amalanda aphungu nzeru zawo ndipo amapusitsa oweruza.
And he bryngith conselours in to a fonned eende, and iugis in to wondryng, ethir astonying.
18 Iye amachotsa zingwe zimene mafumu anawamanga nazo ndipo amawamanga lamba mʼchiwuno mwawo.
He vnbindith the girdil of kyngis, and girdith her reynes with a coorde.
19 Iye amasocheretsa ansembe atawalanda nzeru zawo ndipo amagonjetsa anthu amphamvu amene ndi okhazikika.
He ledith her prestis with out glorie, and he disseyueth the principal men, `ethir counselours;
20 Iye amakhalitsa chete aphungu odalirika ndipo amalanda chidziwitso cha anthu akuluakulu.
and he chaungith the lippis of sothefast men, and takith awei the doctrine of elde men.
21 Iye amanyoza anthu otchuka ndipo anthu anyonga amawatha mphamvu.
He schedith out dispisyng on princes, and releeueth hem, that weren oppressid.
22 Iye amatulutsira poyera zinthu zozama za mu mdima ndipo mdima wandiweyaniwo amawusandutsa kuwala.
Which schewith depe thingis fro derknessis; and bryngith forth in to liyt the schadewe of deeth.
23 Iye amakuza mitundu ya anthu ndipo amayiwononganso; amachulukitsa mitundu ya anthu ndipo amayimwazanso.
Which multiplieth folkis, and leesith hem, and restorith hem destried in to the hool.
24 Iye amalanda nzeru za atsogoleri a dziko lapansi; amawayendetsa mʼthengo mopanda njira.
Which chaungith the herte of princes of the puple of erthe; and disseyueth hem, that thei go in veyn out of the weie.
25 Iwo amafufuzafufuza njira mu mdima wopanda chowunikira; Iye amawayendetsa dzandidzandi ngati oledzera.
Thei schulen grope, as in derknessis, and not in liyt; and he schal make hem to erre as drunken men.

< Yobu 12 >