< Yobu 11 >

1 Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti,
Then Zophar the Naamathite answered and said,
2 “Kodi mawu ambirimbiriwa nʼkukhala osayankhidwa? Kodi munthu woyankhulayankhulayu nʼkulungamitsidwa?
“Should not such a multitude of words be answered? Should this man, so full of talk, be believed?
3 Kodi anthu nʼkukhala chete atamva kubwebweta kwakoku? Kodi palibe wina amene adzakudzudzule pamene ukuyankhula zonyoza?
Should your boasting make others remain silent? When you mock, will no one make you feel ashamed?
4 Iwe ukunena kwa Mulungu kuti, ‘Zikhulupiriro zanga ndi zopanda zolakwika ndipo ndine wangwiro pamaso panu.’
For you say to God, 'My beliefs are pure, I am blameless in your eyes.'
5 Aa, nʼkanakonda Mulungu akanayankhula kuti Iye atsekule pakamwa pake kutsutsana nawe
But, oh, that God would speak and open his lips against you;
6 ndi kukuwululira chinsinsi cha nzeru yake, pakuti nzeru yeniyeni ili ndi mbali ziwiri. Dziwa izi: Mulungu wayiwala machimo ako ena.
that he would show you the secrets of wisdom! For he is great in understanding. Know then that God demands from you less than your iniquity deserves.
7 “Kodi iwe ungathe kumvetsa zinsinsi za Mulungu? Kodi ungafufuze malire a nzeru za Wamphamvuzonse?
Can you understand God by searching for him? Can you comprehend the Almighty perfectly?
8 Zili kutali kupambana mayiko akumwamba, nanga ungachite chiyani? Ndi zakuya kupambana kuya kwa manda, nanga ungadziwe chiyani? (Sheol h7585)
The matter is as high as heaven; what can you do? It is deeper than Sheol; what can you know? (Sheol h7585)
9 Muyeso wa nzeru zake ndi wautali kupambana dziko lapansi ndipo ndi wopingasa kupambana nyanja.
Its measure is longer than the earth, and wider than the sea.
10 “Ngati Iye atabwera ndi kukutsekera mʼndende nakutengera ku bwalo la milandu, ndani angathe kumuletsa?
If he passes through and shuts anyone up, if he calls anyone to judgment, then who can stop him?
11 Ndithudi, Mulungu amazindikira anthu achinyengo; akaona choyipa, kodi sachizindikira?
For he knows false people; when he sees iniquity, does he not notice it?
12 Munthu wopanda nzeru sizingatheke kukhala wanzeru monganso mwana wa bulu wakuthengo sangasanduke munthu.
But foolish people have no understanding; they will get it when a wild donkey gives birth to a man.
13 “Koma ngati upereka mtima wako kwa Iye ndi kutambasulira manja ako kwa Iyeyo,
But suppose that you had set your heart right and had reached out with your hands toward God;
14 ngati utaya tchimo limene lili mʼdzanja lako ndi kusalola choyipa kuti chikhale mʼmoyo mwako,
suppose that iniquity were in your hand, but that then you put it far away from you, and did not let unrighteousness live in your tents.
15 udzatukula mutu wako wosachita manyazi; udzayima chilili ndipo sudzachita mantha.
Then you would certainly lift up your face without a sign of shame; indeed, you would be steadfast and would not fear.
16 Udzayiwala ndithu zowawa zako, zidzakhala ngati madzi amene apita kale.
You would forget your misery; you would remember it only like waters that have flowed away.
17 Moyo wako udzawala kupambana usana, ndipo mdima udzakhala ngati mmawa.
Your life would be brighter than the noonday; though there were darkness, it would become like the morning.
18 Udzalimba mtima popeza pali chiyembekezo; ndipo udzayangʼana mbali zonse ndi kugona mosatekeseka.
You would be secure because there is hope; indeed, you would find safety about you and would take your rest in safety.
19 Udzagona pansi, popanda wina wokuopseza ndipo ambiri adzakupempha kuti uwachitire chifundo.
Also you would lie down in rest, and none would make you afraid; indeed, many would seek your favor.
20 Koma anthu oyipa adzafuna thandizo osalipeza, ndipo adzasowa njira yothawirapo; chiyembekezo chawo chidzakhala imfa basi.”
But the eyes of wicked people will fail; they will have no way to flee; their only hope will be a last gasp of life.”

< Yobu 11 >