< Yobu 10 >

1 “Ine ndatopa nawo moyo wanga; choncho ndidzanena zodandaula zanga momasuka ndipo ndidzayankhula mwa kuwawidwa mtima kwanga.
Moja dusza zmęczona jest życiem; dam upust swemu narzekaniu, będę mówił w goryczy swej duszy.
2 Ndidzati kwa Mulungu wanga: Musandiweruze kuti ndine wolakwa, koma mundiwuze chifukwa chimene Inu mukukanganira ndi ine.
Powiem Bogu: Nie potępiaj mnie. Oznajmij mi, czemu wiedziesz ze mną spór?
3 Kodi mumakondwera mukamandizunza, kunyoza ntchito ya manja anu, chonsecho mukusekerera ndi zochita za anthu oyipa?
Czy dobrze ci z tym, że mnie uciskasz, że odrzucasz dzieło swoich rąk i sprzyjasz radzie niegodziwych?
4 Kodi maso anu ali ngati a munthu? Kodi mumaona zinthu monga momwe amazionera munthu?
Czy masz oczy cielesne? Czy widzisz, jak człowiek widzi?
5 Kodi masiku anu ali ngati masiku a munthu, kapena zaka zanu ngati zaka za munthu,
Czy twoje dni są jak dni człowieka, a twoje lata jak lata ludzkie;
6 kuti Inu mufufuze zolakwa zanga ndi kulondola tchimo langa,
Że się wywiadujesz o moją nieprawość i dochodzisz mojego grzechu?
7 ngakhale mukudziwa kuti sindine wolakwa ndiponso kuti palibe amene angandilanditse mʼdzanja lanu?
Ty wiesz, że nie jestem niegodziwy i nikt nie wyrwie [mnie] z twoich rąk.
8 “Munandiwumba ndi kundipanga ndi manja anu. Kodi tsopano Inu mudzatembenuka ndi kundiwononga?
Twoje ręce ukształtowały mnie i uczyniły mnie całego ze wszystkich stron, lecz mnie niszczysz.
9 Kumbukirani kuti munandipanga ndi dothi, kodi tsopano mundibwezeranso ku fumbi?
Pamiętaj, proszę, że ulepiłeś mnie jak glinę; czy obrócisz mnie w proch?
10 Suja munapatsa abambo anga mphamvu zoti andibale, suja munandikuza bwino mʼmimba mwa amayi anga?
Czy nie wylałeś mnie jak mleko i nie sprawiłeś, że jak ser stężałem?
11 Munandikuta ndi khungu ndi mnofu ndi kundilumikiza pamodzi ndi mafupa ndi mitsempha?
Przyoblekłeś mnie skórą i ciałem, a kośćmi i żyłami pospinałeś mnie.
12 Munandipatsa moyo ndi kundionetsa chifundo chanu, ndipo munasamalira bwino moyo wanga.
Obdarzyłeś mnie życiem i miłosierdziem, a twoja opatrzność strzegła mego ducha.
13 “Koma izi ndi zimene munabisa mu mtima mwanu, ndipo ndikudziwa kuti zinali mʼmaganizo anu:
I chociaż ukryłeś to wszystko w swoim sercu, wiem jednak, że to jest z twojej woli.
14 Kuti ngati ndingachimwe mudzakhala mukundipenyetsetsa ndipo kuti simudzalola kuti ndisalangidwe chifukwa cha kulakwa kwanga.
Jeśli grzeszę, ty to spostrzegasz i nie uwolnisz mnie od mojej nieprawości.
15 Ngati ndili wolakwa, tsoka langa! Koma ngakhale ndili wosalakwa sindingathe kutukula mutu wanga, pakuti ndagwidwa ndi manyazi ndipo ndamizidwa mʼmavuto anga.
Jeśli jestem niegodziwy, biada mi, a [choćbym też] był sprawiedliwy, nie podniosę swojej głowy. Jestem syty hańby, zważ na moje utrapienie;
16 Ndipo ndikatukula mutu wanga, Inu mumandisaka ngati mkango ndiponso mumandiopseza ndi mphamvu yanu.
Gdyż go przybywa; gonisz mnie jak okrutny lew i zachowujesz się dziwnie wobec mnie.
17 Mumabweretsa mboni zatsopano potsutsana nane ndipo mkwiyo wanu pa ine umanka nukulirakulira ndi magulu anu olimbana nane amanka nachulukirachulukira.
Stawiasz przeciwko mnie nowych świadków i pomnażasz nade mną swój gniew; wojsko za wojskiem naciera na mnie.
18 “Chifukwa chiyani Inu munalola kuti ndibadwe? Ndi bwino ndikanafa diso lililonse lisanandione.
Czemu wyprowadziłeś mnie z łona? Obym umarł i nie widziało mnie żadne oko!
19 Ndikanapanda kubadwa, kapena akanangonditenga nditabadwa kupita nane ku manda!
Byłbym, jakby mnie nie było, od łona zanieśliby mnie do grobu!
20 Kodi masiku anga owerengeka sali pafupi kutha? Ndilekeni kuti ndipumule pangʼono pokha
Czy nie zostało mi niewiele dni? Przestań więc i odejdź ode mnie, abym nabrał trochę otuchy;
21 ndisanapite ku malo amene munthu sabwererako ku dziko la imfa ndi kwa mdima wandiweyani,
Zanim odejdę tam, skąd już nie powrócę, do ziemi ciemności i cienia śmierci;
22 ku dziko la mdima wandiweyani ndi chisokonezo, kumene kuwala kumakhala ngati mdima.”
Do ziemi ciemnej jak noc [i do] cienia śmierci i bezładu, gdzie świeci tylko ciemność.

< Yobu 10 >