< Yobu 10 >

1 “Ine ndatopa nawo moyo wanga; choncho ndidzanena zodandaula zanga momasuka ndipo ndidzayankhula mwa kuwawidwa mtima kwanga.
My soul is weary of my life; I will leave my complaint upon myself; I will speak in the bitterness of my soul.
2 Ndidzati kwa Mulungu wanga: Musandiweruze kuti ndine wolakwa, koma mundiwuze chifukwa chimene Inu mukukanganira ndi ine.
I will say to God, Do not condemn me; show me why thou contendest with me.
3 Kodi mumakondwera mukamandizunza, kunyoza ntchito ya manja anu, chonsecho mukusekerera ndi zochita za anthu oyipa?
Is it good to thee that thou shouldest oppress, that thou shouldest despise the work of thy hands, and shine upon the counsel of the wicked?
4 Kodi maso anu ali ngati a munthu? Kodi mumaona zinthu monga momwe amazionera munthu?
Hast thou eyes of flesh? or seest thou as man seeth?
5 Kodi masiku anu ali ngati masiku a munthu, kapena zaka zanu ngati zaka za munthu,
Are thy days as the days of man? are thy years as man’s days,
6 kuti Inu mufufuze zolakwa zanga ndi kulondola tchimo langa,
That thou enquirest after my iniquity, and searchest after my sin?
7 ngakhale mukudziwa kuti sindine wolakwa ndiponso kuti palibe amene angandilanditse mʼdzanja lanu?
Thou knowest that I am not wicked; and there is none that can deliver out of thy hand.
8 “Munandiwumba ndi kundipanga ndi manja anu. Kodi tsopano Inu mudzatembenuka ndi kundiwononga?
Thy hands have made me and fashioned me in all my parts; yet thou dost destroy me.
9 Kumbukirani kuti munandipanga ndi dothi, kodi tsopano mundibwezeranso ku fumbi?
Remember, I beseech thee, that thou hast made me as the clay; and wilt thou bring me into dust again?
10 Suja munapatsa abambo anga mphamvu zoti andibale, suja munandikuza bwino mʼmimba mwa amayi anga?
Hast thou not poured me out as milk, and curdled me like cheese?
11 Munandikuta ndi khungu ndi mnofu ndi kundilumikiza pamodzi ndi mafupa ndi mitsempha?
Thou hast clothed me with skin and flesh, and hast fenced me with bones and sinews.
12 Munandipatsa moyo ndi kundionetsa chifundo chanu, ndipo munasamalira bwino moyo wanga.
Thou hast granted me life and favour, and thy care hath preserved my spirit.
13 “Koma izi ndi zimene munabisa mu mtima mwanu, ndipo ndikudziwa kuti zinali mʼmaganizo anu:
And these things hast thou hid in thy heart: I know that this is with thee.
14 Kuti ngati ndingachimwe mudzakhala mukundipenyetsetsa ndipo kuti simudzalola kuti ndisalangidwe chifukwa cha kulakwa kwanga.
If I sin, then thou markest me, and thou wilt not acquit me from my iniquity.
15 Ngati ndili wolakwa, tsoka langa! Koma ngakhale ndili wosalakwa sindingathe kutukula mutu wanga, pakuti ndagwidwa ndi manyazi ndipo ndamizidwa mʼmavuto anga.
If I be wicked, woe to me; and if I be righteous, yet will I not lift up my head. I am full of confusion; therefore see thou my affliction;
16 Ndipo ndikatukula mutu wanga, Inu mumandisaka ngati mkango ndiponso mumandiopseza ndi mphamvu yanu.
For it increaseth. Thou huntest me as a fierce lion: and again thou showest thyself marvellous upon me.
17 Mumabweretsa mboni zatsopano potsutsana nane ndipo mkwiyo wanu pa ine umanka nukulirakulira ndi magulu anu olimbana nane amanka nachulukirachulukira.
Thou renewest thy witnesses against me, and increasest thy indignation upon me; changes and war are against me.
18 “Chifukwa chiyani Inu munalola kuti ndibadwe? Ndi bwino ndikanafa diso lililonse lisanandione.
Why then hast thou brought me forth from the womb? O that I had given up the ghost, and no eye had seen me!
19 Ndikanapanda kubadwa, kapena akanangonditenga nditabadwa kupita nane ku manda!
I should have been as though I had not been; I should have been carried from the womb to the grave.
20 Kodi masiku anga owerengeka sali pafupi kutha? Ndilekeni kuti ndipumule pangʼono pokha
Are not my days few? cease then, and let me alone, that I may take comfort a little,
21 ndisanapite ku malo amene munthu sabwererako ku dziko la imfa ndi kwa mdima wandiweyani,
Before I go to the place from which I shall not return, even to the land of darkness and the shadow of death;
22 ku dziko la mdima wandiweyani ndi chisokonezo, kumene kuwala kumakhala ngati mdima.”
A land of darkness, as darkness itself; and of the shadow of death, without any order, and where the light is as darkness.

< Yobu 10 >