< Yeremiya 7 >

1 Mawu amene Yehova anayankhula kwa Yeremiya ndi awa,
Rijeè koja doðe Jeremiji od Gospoda govoreæi:
2 “Ima pa chipata cha Nyumba ya Yehova ndipo kumeneko ukalalikire uthenga uwu: “‘Imvani mawu a Yehova, inu nonse anthu a ku Yuda amene mumalowa pa chipata ichi kudzapembedza Yehova.
Stani na vratima doma Gospodnjega, i oglasi ondje ovu rijeè, i reci: èujte rijeè Gospodnju, svi Judejci, koji ulazite na ova vrata da se poklonite Gospodu.
3 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Konzani makhalidwe anu ndi zochita zanu, ndipo ndidzakulolani kukhala pa malo ano.
Ovako govori Gospod nad vojskama, Bog Izrailjev: popravite svoje putove i djela svoja, pa æu uèiniti da stanujete na ovom mjestu.
4 Musamakhulupirire mawu anu achinyengo onena kuti, ‘Ino ndi Nyumba ya Yehova, Nyumba ya Yehova, Nyumba ya Yehova!’
Ne uzdajte se u lažne rijeèi govoreæi: crkva Gospodnja, crkva Gospodnja, crkva Gospodnja ovo je.
5 Ngati mutasinthadi makhalidwe anu ndi zochita zanu, ndi kumachitirana zolungama,
Nego doista popravite svoje putove i djela svoja, i sudite pravo izmeðu èovjeka i bližnjega njegova.
6 ngati mutaleka kuzunza mlendo, ana amasiye kapena akazi amasiye ndi kuleka kupha anthu osalakwa pa malo ano, ndipo ngati muleka kutsatira milungu ina, kuti ingakuwonongeni,
Inostrancu, siroti i udovici ne èinite krivo, i krvi prave ne proljevajte na ovom mjestu, i ne idite za drugim bogovima na svoje zlo.
7 Ine ndidzakulolani kukhala pa malo ano, mʼdziko limene ndinapatsa makolo anu mpaka muyaya.
Tada æu uèiniti da stanujete od vijeka do vijeka na ovom mjestu, u zemlji koju sam dao ocima vašim.
8 Koma onani, inu mukudalira mawu abodza amene alibe phindu.
Eto, vi se uzdate u rijeèi lažne, koje ne pomažu.
9 “Kodi inu muziba ndi kupha, kuchita chigololo ndi kulumbira monama, kufukiza lubani kwa Baala ndi kutsatira milungu ina imene simunayidziwe,
Kradete, ubijate i èinite preljubu, kunete se krivo, i kadite Valima, i idete za drugim bogovima, kojih ne znate;
10 ndipo kenaka nʼkubwera kudzayima pamaso panga mʼNyumba ino, Nyumba imene imadziwika ndi Dzina langa, inu nʼkumati, ‘Tapulumuka.’ Mwapulumuka kuti muzichitabe zonyansazi?
Pa onda dohodite i stajete preda mnom u ovom domu, koji se zove mojim imenom, i govorite: izbavismo se, da èinite sve ove gadove.
11 Kodi Nyumba ino imene imadziwika ndi Dzina langa, yasanduka phanga la anthu olanda zinthu anzawo mwachifwamba inu mukuona? Komatu ndakhala ndi kuziona zonsezi! akutero Yehova.”
Je li ovaj dom, koji se zove mojim imenom, u vašim oèima peæina hajduèka? Gle, i ja vidim, veli Gospod.
12 “‘Pitani tsopano ku malo anga ku Silo, malo amene poyamba ankadziwika ndi Dzina langa, ndipo mukaone zimene ndinachita kumeneko chifukwa cha kuyipa kwa anthu anga Aisraeli.
Nego idite sada na moje mjesto, koje je bilo u Silomu, gdje namjestih ime svoje ispoèetka, i vidite što sam mu uèinio za zloæu naroda svojega Izrailja.
13 Tsono popeza munkachita zonsezi, ngakhale Ine kukuyankhulani koma inu osamvera, kukuyitanani koma inu osayankha,
Zato sada, što èinite sva ona djela, veli Gospod, i što vam govorim zarana jednako, a vi ne slušate, i kad vas zovem, a vi se ne odzivate,
14 choncho ndidzachita pa Nyumba imene imadziwika ndi Dzina langayi, Nyumba ya Yehova imene mumayidalira, malo amene ndinapereka kwa inu ndi makolo anu, zomwe ndinachita ku Silo.
Zato æu uèiniti tomu domu, koji se zove mojim imenom, u koji se vi uzdate, i ovomu mjestu, koje dadoh vama i ocima vašim, kao što sam uèinio Silomu.
15 Ndidzakuthamangitsani pamaso panga, ngati momwe ndinachitira abale anu onse, anthu a Efereimu.’”
I odbaciæu vas od lica svojega, kao što sam odbacio svu braæu vašu, sve sjeme Jefremovo.
16 “Choncho iwe Yeremiya usawapempherere anthu awa ngakhale kuwapepesera kapenanso kuwapembedzera; usandidandaulire, chifukwa Ine sindidzakumvera.
Ti se dakle ne moli za taj narod, i ne podiži vike ni molbe za njih, i ne govori mi za njih; jer te neæu uslišiti.
17 Kodi sukuona zimene akuchita mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya ku Yerusalemu?
Zar ne vidiš šta èine po gradovima Judinijem i po ulicama Jerusalimskim?
18 Ana akutorera nkhuni, abambo akusonkha moto, ndipo amayi akukanda ufa kuti aphike makeke oti akapereke nsembe kwa mfumukazi yazakumwamba. Iwo amathira nsembe ya zakumwa kwa milungu ina kuti andipsetse mtima.
Sinovi kupe drva, a ocevi lože oganj, i žene mijese tijesto, da peku kolaèe carici nebeskoj, i da ljevaju naljeve drugim bogovima, da bi mene dražili.
19 Koma kodi akuvutitsa Ine? Kodi sakungodzivuta okha, ndi kudzichititsa manyazi? akutero Yehova.”
Mene li draže? govori Gospod; eda li ne sebe, na sramotu licu svojemu?
20 “Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Ndidzatsanulira mkwiyo wanga pa Nyumba yangayi, anthu, nyama, mitengo ndi zipatso zomwe. Mkwiyowo udzakhala ngati moto wosazimitsika.
Zato ovako govori Gospod Gospod: gle, gnjev moj i jarost moja izliæe se na ovo mjesto, na ljude i na stoku i na drveta poljska i na rod zemaljski, i raspaliæe se, i neæe se ugasiti.
21 “Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Wonjezerani nsembe zanu zopsereza pa nsembe zanu zinazo ndipo mudye nyama yakeyo!
Ovako veli Gospod nad vojskama Bog Izrailjev: žrtve svoje paljenice sastavite sa prinosima svojim, i jedite meso.
22 Pakuti pamene ndinatulutsa makolo anu ku Igupto ndi kuyankhula nawo, sindinawalamulire kuti azipereka nsembe zopsereza kapena nsembe zinazo,
Jer ne govorih ocima vašim, niti im zapovjedih, kad ih izvedoh iz zemlje Misirske, za žrtve paljenice ni za prinose.
23 koma ndinawalamula kuti: Mverani Ine, ndipo ndidzakhala Mulungu wanu ndipo inu mudzakhala anthu anga. Muzitsata zonse zimene ndakulamulirani, ndipo zinthu zidzakuyenderani bwino.
Nego im ovo zapovjedih govoreæi: slušajte glas moj i biæu vam Bog i vi æete mi biti narod, i idite svijem putovima koje vam zapovjedih, da bi vam dobro bilo.
24 Koma anthuwo sanamvere kapena kulabadira; mʼmalo mwake anapitirira kusamvera ndi mitima yawo yoyipa. Iwo anabwerera mʼmbuyo mʼmalo mopita patsogolo.
Ali ne poslušaše, niti uha svojega prignuše, nego idoše po savjetima i mislima zloga srca svojega, i otidoše natrag a ne naprijed.
25 Kuyambira tsiku limene makolo awo anachoka ku Igupto mpaka lero lino, ndakhala ndikuwatumizira atumiki anga, aneneri.
Otkad iziðoše oci vaši iz zemlje Misiriske do danas, slah k vama sve sluge svoje proroke svaki dan zarana i bez prestanka.
26 Koma anthuwo sanandimvere kapena kusamalira. Anawumitsa mitima yawo ndi kuchita zoyipa kuposa makolo awo.
Ali ne poslušaše me, niti uha svojega prignuše, nego bijahu tvrdovrati i èiniše gore nego oci njihovi.
27 “Ngakhale iwe uwawuze zonsezi koma sadzakumvera. Ngakhale uwayitane koma sadzakuyankha.
Govoriæeš im sve ove rijeèi, ali te neæe poslušati; i zvaæeš ih, ali ti se neæe odazvati.
28 Nʼchifukwa chake udzawawuze kuti, ‘Uwu ndi mtundu wa anthu umene sunamvere Yehova Mulungu wake, wosalola kulangizidwa. Choonadi chatha; chazimirira pa milomo yawo.’
Zato im reci: ovo je narod koji ne sluša glasa Gospoda Boga svojega, niti prima nauke; propade vjera i nesta je iz usta njihovijeh.
29 “Tsono meta tsitsi lako ndi kulitaya. Ulire kwambiri pa zitunda zopanda zomera, pakuti Yehova waukana ndi kuwusiya mʼbado umene wamukwiyitsawu.”
Ostrizi kosu svoju i baci je, i zaridaj iza glasa na visokim mjestima, jer odbaci Gospod i ostavi rod, na koji se razgnjevi.
30 “Anthu a ku Yuda achita zoyipa pamaso panga, akutero Yehova. Ayimika mafano awo onyansa mʼnyumba imene imadziwika ndi Dzina langa ndipo ayipitsa.
Jer sinovi Judini uèiniše što je zlo preda mnom, govori Gospod, metnuše gadove svoje u dom koji se zove mojim imenom, da bi ga oskvrnili.
31 Amanga nsanja yopembedzera Tofeti mʼChigwa cha Hinomu kuti apserezereko ana awo aamuna ndi aakazi. Zimenezi Ine sindinawalamulire ngakhale kuziganizira nʼkomwe.
I sagradiše visine Tofetu, koji je u dolini sina Enomova, da sažižu sinove svoje i kæeri svoje ognjem, što nijesam zapovjedio niti mi je došlo na um.
32 Nʼchifukwa chake masiku akubwera, akutero Yehova, pamene anthu sadzawatchulanso malowo Tofeti kapena Chigwa cha Hinomu, koma adzawatchula Chigwa cha Imfa, chifukwa adzakwirira anthu akufa ku Tofeti mpaka osapezekanso malo owayika.
Zato evo, idu dani, veli Gospod, kad se više neæe zvati Tofet ni dolina sina Enomova, nego dolina krvna, i pogrebavaæe se u Tofetu, jer neæe biti mjesta.
33 Ndipo mitembo ya anthu amenewa idzakhala chakudya cha mbalame zamlengalenga ndi zirombo zakuthengo, ndipo palibe wina amene adzazipirikitse.
I mrtva æe tjelesa naroda ovoga biti hrana pticama nebeskim i zvijerju zemaljskom, i neæe biti nikoga da ih plaši.
34 Ndidzathetsa nyimbo zonse zachisangalalo ndi zachikondwerero mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya ku Yerusalemu. Sikudzamvekanso mawu a chikondwerero a mkwatibwi ndi mkwati pakuti dzikolo lidzasanduka chipululu.”
I uèiniæu, te æe iz gradova Judinijeh i s ulica Jerusalimskih nestati glasa radosna i glasa vesela, glasa ženikova i glasa nevjestina; jer æe zemlja opustjeti.

< Yeremiya 7 >