< Yeremiya 6 >

1 “Thawani, inu anthu a ku Benjamini! Tulukani mu Yerusalemu! Lizani lipenga ku Tekowa! Kwezani mbendera ku Beti-Hakeremu! Pakuti tsoka lalikulu likubwera kuchokera kumpoto, ndipo chiwonongekocho nʼchachikulu.
Sones of Beniamyn, be ye coumfortid in the myddil of Jerusalem, and make ye noise with a clarioun in Thecua, and reise ye a baner on Bethecarem; for whi yuel and greet sorewe is seyn fro the north.
2 Kodi mzinda wa Ziyoni suli ngati msipu wokongola kwambiri, kumene abusa amafikako ndi ziweto zawo?
Y haue licned the douytir of Sion to a fair womman and delicat.
3 Abusa ndi nkhosa zawo adzabwera kudzalimbana nawo; adzamanga matenti awo mowuzinga, ndipo aliyense adzakhazika anthu ake pamalo pake.”
Scheepherdis and her flockis schulen come to it; thei han piyt tentis in it in cumpas; ech man schal feede hem, that ben vndur his hond.
4 Adzanena kuti, “Konzekani kuwuthira nkhondo mzindawo! Nyamukani, kuti tiwuthire nkhondo mzindawu masana ano. Koma tili ndi tsoka, dzuwa lapendeka, ndipo zithunzithunzi za kumadzulo zikunka zitalika.
Halewe ye batel on it. Rise ye togidire, and stie we in myddai. Wo to vs, for the dai is bowid doun, for shadewis ben maad lengere in the euentid.
5 Tsono nyamukani kuti tiwuthire nkhondo mzindawu usiku uno ndi kuwononga malinga ake!”
Rise ye, and stie we in the niyt, and distry we the housis therof.
6 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Dulani mitengo ndipo mumange mitumbira yankhondo kulimbana ndi Yerusalemu. Mzinda umenewu uyenera kulangidwa; wadzaza ndi kuponderezana.
For the Lord of oostis seith these thingis, Kitte ye doun the tre therof, and schede ye erthe aboute Jerusalem; this is the citee of visitacioun; al fals caleng is in the myddis therof.
7 Monga momwe chitsime chimatulutsira madzi ndi mmenenso Yerusalemu amatulutsira zoyipa zake. Chiwawa ndi chiwonongeko ndi zomwe zimamveka mu mzindamo; nthenda yake ndi mabala ake ndimaziona nthawi zonse.
As a cisterne makith his water coold, so it made his malice coold; wickidnesse and distriyng schal euer be herd ther ynne bifore me, sikenesse and wounde.
8 Iwe Yerusalemu, tengapo phunziro, kuopa kuti chikondi changa pa iwe chingakuchokere ndi kusandutsa dziko lako kukhala bwinja mopanda munthu wokhalamo.”
Jerusalem, be thou tauyt, lest perauenture my soule go awei fro thee; lest perauenture Y sette thee forsakun, a loond vnhabitable.
9 Yehova Wamphamvuzonse anandiwuza kuti, “Adani adzawakunkha ndithu anthu otsala a Israeli, monga momwe amachitira populula mphesa. Tsono iwe yesetsa kupulumutsa amene ungathe monga mmene amachitira munthu wokolola mphesa.”
The Lord of oostis seith these thingis, Thei schulen gadere til to a racyn, thei schulen gadere the remenauntis of Israel as in a vyner; turne thin hond, as a gaderer of grapis to the bascat.
10 Kodi ndiyankhule ndi yani ndi kumuchenjeza? Ndinene mawu ochenjeza kwa yani kuti amve? Makutu awo ndi otsekeka kotero kuti sangathe kumva. Mawu a Yehova ndi onyansa kwa iwo; sasangalatsidwa nawo.
To whom schal Y speke, and to whom schal Y seie witnessing, that he here? Lo! the eeris of hem ben vncircumcidid, and thei moun not here; lo! the word of the Lord is maad to hem in to dispit, and thei schulen not resseiue it.
11 Koma ine ndadzazidwa ndi mkwiyo wa Yehova, ndipo ndatopa ndi kusunga mkwiyo wa Yehova. Yehova anandiwuza kuti, “Tsono ndidzawutulutsira mkwiyo umenewu pa ana oyenda mʼmisewu ndi pa achinyamata amene asonkhana pamodzi; pakutinso mwamuna ndi mkazi wake adzatengedwa, pamodzi ndi okalamba amene ali ndi zaka zochuluka.
Therfor Y am ful of the strong veniaunce of the Lord, and Y trauelide suffrynge. Schede thou out on a litil child with outforth, and on the counsel of yonge men togidere; for a man with his wijf schal be takun, and an eeld man with him that is ful of daies.
12 Nyumba zawo adzazipereka kwa ena, pamodzi ndi minda yawo ndi akazi awo. Ndidzatambasula dzanja langa kukantha anthu okhala mʼdzikomo,” akutero Yehova.
And the housis of hem, the feeldis and wyues togidere, schulen go to othere men; for Y schal stretche forth myn hond on the dwelleris of the lond, seith the Lord.
13 “Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, onse ali ndi dyera lofuna kupeza phindu mwa kuba; aneneri pamodzi ndi ansembe omwe, onse amachita zachinyengo.
For fro the lesse `til to the grettere, alle studien to auerise; and alle doon gile, fro the profete `til to the preest.
14 Amapoletsa zilonda za anthu anga pamwamba pokha. Iwo amanena kuti, ‘Mtendere, mtendere,’ pamene palibe mtendere.
And thei heeliden the sorewe of the douyter of my puple with yuel fame, seiynge, Pees, pees, and no pees was.
15 Kodi amachita manyazi akamachita zonyansazo? Ayi, sachita manyazi ndi pangʼono pomwe; sadziwa ndi kugwetsa nkhope komwe. Choncho iwo adzagwera pakati pa anzawo amene agwa kale; adzagwa pansi tsiku limene ndidzawalange,” akutero Yehova.
Thei ben schent, that diden abhomynacioun; yhe, rathere thei weren not schent bi confusioun, and thei kouden not be aschamed. Wherfor thei schulen falle doun among hem that schulen falle doun; thei schulen falle doun in the tyme of her visitacioun, seith the Lord.
16 Yehova akuti, “Imani pa mphambano ndipo mupenye; kumeneko ndiye kuli njira zakale, funsani kumene kuli njira yabwino. Yendani mʼmenemo, ndipo mudzapeza mpumulo wa miyoyo yanu. Koma inu munati, ‘Ife sitidzayenda njira imeneyo.’
The Lord seith these thingis, Stonde ye on weies, and se ye, and axe ye of elde pathis, which is the good weie; and go ye ther ynne, and ye schulen fynde refreischyng to youre soulis. And thei seiden, We schulen not go.
17 Ine ndinakupatsani alonda oti akuyangʼanireni ndipo ndinati, ‘Imvani kulira kwa lipenga!’ koma inu munati, ‘Sitidzamvera.’
And Y ordeynede aspieris on you, and Y seide, Here ye the vois of a trumpe. And thei seiden, We schulen not here.
18 Nʼchifukwa chake imvani, inu anthu a mitundu ina; yangʼanitsitsani, inu amene mwasonkhana pano, chimene chidzawachitikire anthuwo.
Therfor, hethene men, here ye, and, thou congregacioun, knowe, hou grete thingis Y schal do to hem.
19 Imvani, inu anthu okhala pa dziko lapansi, ndikubweretsa masautso pa anthu awa. Zimenezi ndi mphotho ya ntchito zawo. Iwowa sanamvere mawu anga ndipo anakana lamulo langa.
Thou erthe, here, lo! Y schal brynge yuels on this puple, the fruit of her thouytis; for thei herden not my wordis, and castiden awei my lawe.
20 Kodi pali phindu lanji ngakhale mubwere ndi lubani kuchokera ku Seba, kapena zonunkhira zina kuchokera ku dziko lakutali? Nsembe zanu zopsereza Ine sindidzalandira; nsembe zanu sizindikondweretsa.”
Wherto bryngen ye to me encense fro Saba, and a tre of spicerie smellynge swetli fro a fer lond? Youre brent sacrifices ben not acceptid, and youre slayn sacrifices plesiden not me.
21 Choncho Yehova akuti, “Ndidzayika zokhumudwitsa pamaso pa anthu awa. Abambo ndi ana awo aamuna onse adzapunthwa ndi kugwa; anansi awo ndi abwenzi awo adzawonongeka.”
Therfor the Lord God seith these thingis, Lo! Y schal yyue fallyngis in to this puple, and fadris and sones togidere, a neiybore and kynesman, schulen falle in hem, and schulen perische.
22 Yehova akunena kuti, “Taonani, gulu lankhondo likubwera kuchokera kumpoto; mtundu wa anthu amphamvu wanyamuka kuchokera kumathero a dziko lapansi.
The Lord God seith these thingis, Lo! a puple cometh fro the lond of the north, and a greet folk schal rise togidere fro the endis of erthe.
23 Atenga mauta ndi mikondo; ndi anthu ankhanza ndi opanda chifundo. Phokoso lawo lili ngati mkokomo wa nyanja. Akwera pa akavalo awo ndipo akonzekera ngati anthu ankhondo, kudzakuthirani nkhondo anthu a ku Ziyoni.”
It schal take an arowe and scheld; it is cruel, and schal not haue merci; the vois therof schal sowne as the see, and thei maad redi as a man to batel schulen stie on horsis ayens thee, thou douyter of Sion.
24 A ku Ziyoni akuti “Ife tamva mbiri yawo, ndipo manja anthu alefukiratu. Nkhawa yatigwira, ndipo tikumva ululu ngati mayi pa nthawi yake yochira.
We herden the fame therof, oure hondis ben `a clumsid; tribulacioun hath take vs, sorewis han take vs as a womman trauelinge of child.
25 Musapite ku minda kapena kuyenda mʼmisewu, pakuti mdani ali ndi lupanga, ndipo ponseponse anthu akuchita mantha.
Nyle ye go out to the feeldis, and go ye not in the weie, for the swerd of the enemye, drede in cumpas.
26 Inu anthu anga, valani ziguduli ndipo gubudukani pa phulusa; lirani mwamphamvu ngati munthu wolirira mwana wake mmodzi yekha, pakuti mwadzidzidzi wowonongayo adzabwera kudzatipha.
The douytir of my puple, be thou gird with heire, and be thou spreynt togidere with aische; make to thee mourenyng of oon aloone gendrid sone, a bitter weilyng, for whi a wastere schal come sodenli on you.
27 “Iwe Yeremiya, ndakuyika kuti ukhale choyesera zitsulo. Uwayese anthu anga monga ungayesere chitsulo kuti uwone makhalidwe awo.
I yaf thee a strong preuere in my puple, and thou schalt knowe, and preue the weie of hem.
28 Onsewo ali ndi khalidwe lokanika ndi lowukira ndipo akunka nanena zamiseche. Iwo ndi olimba ngati mkuwa ndi chitsulo. Onse amangochita zoyipa zokhazokha.
Alle these princis bowynge awei, goynge gilefuli, ben metal and irun; alle ben corrupt.
29 Moto mu mvukuto ukuyaka kwambiri; mtovu watha kusungunuka ndi moto. Koma ntchito yosungunulayo sikupindula chifukwa zoyipa sizikuchokapo.
The belu failide, leed is waastid in the fier, the wellere wellide in veyn; for the malices of hem ben not wastid.
30 Iwo ali ngati siliva wotayidwa, chifukwa Yehova wawakana.”
Clepe ye hem repreuable siluer, for the Lord hath cast hem awei.

< Yeremiya 6 >