< Yeremiya 51 >

1 Yehova akuti, “Taonani, ndidzadzutsa mphepo yowononga kuti iwononge Babuloni pamodzi ndi anthu a ku Lebi Kamai.
Tak mówi PAN: Oto wzbudzę niszczący wiatr przeciwko Babilonowi i przeciwko tym, którzy mieszkają pośród powstających przeciwko mnie;
2 Ndidzatuma alendo ku Babuloni kudzamupeta ndi kuwononga dziko lake kotheratu. Iwo adzalimbana naye ku mbali zonse pa tsiku la masautso ake.
I poślę do Babilonu obcych, którzy będą go przewiewać, i opróżnią jego ziemię, gdyż zewsząd zwrócą się przeciwko niemu w dniu ucisku.
3 Okoka uta musawalekerere kapena wonyadira chovala chawo chankhondo. Musawasiye anyamata ake kuti akhale ndi moyo; koma muwononge ankhondo ake kotheratu.
Niech łucznik napina swój łuk przeciwko niemu i przeciwko stającym do walki w swoich pancerzach. Nie oszczędzajcie jego młodzieńców, zgładźcie całe jego wojsko.
4 Adzavulazidwa ndi kufera mʼdziko la Babuloni lomwelo ndi mʼmisewu yawo yomwe.
Tak padną zabici w ziemi Chaldejczyków i przebici na jego ulicach.
5 Pakuti Yuda ndi Israeli sanasiyidwe ngati amasiye ndi Mulungu wawo, Yehova Wamphamvuzonse, koma ngakhale dziko la Babuloni ndi lodzaza ndi machimo pamaso pa Woyerayo wa Israeli.
Nie są bowiem opuszczone Izrael ani Juda przez swego Boga, PANA zastępów, choć ich ziemia była pełna grzechu przeciwko Świętemu Izraela.
6 “Thawaniko ku Babuloni! Aliyense apulumutse moyo wake! Musawonongeke naye pamodzi chifukwa cha machimo ake. Imeneyi ndi nthawi yoti Yehova amulange; Yehova adzamulipsira.
Uciekajcie ze środka Babilonu i niech każdy ratuje swoją duszę. Nie gińcie w jego nieprawości, bo jest to czas zemsty PANA, on oddaje mu zapłatę.
7 Babuloni anali ngati chikho cha golide mʼdzanja la Yehova; kuti aledzeretse dziko lonse lapansi. Mitundu yambiri ya anthu inamwa vinyo wake; nʼchifukwa chake tsopano inachita misala.
Babilon był złotym kielichem w ręce PANA, upajającym całą ziemię. Z jego wina piły narody, dlatego narody szaleją.
8 Babuloni wagwa mwadzidzidzi ndi kusweka. Mulireni! Mfunireni mankhwala opha ululu wake; mwina iye nʼkuchira.”
Nagle upadł Babilon i został rozbity. Zawódźcie nad nim, weźcie balsam na jego ból, może da się go wyleczyć.
9 Ena anati, “‘Ife tinayesa kumupatsa mankhwala Babuloni, koma sanachire; tiyeni timusiye ndipo aliyense apite ku dziko la kwawo, pakuti mlandu wake wafika mpaka mlengalenga, wafika mpaka kumwamba.’
Leczyliśmy Babilon, ale nie został uleczony. Opuśćmy go i niech każdy pójdzie do swojej ziemi, bo jego sąd aż do nieba sięga i wznosi się aż po obłoki.
10 “‘Yehova waonetsa poyera kuti ndife osalakwa; tiyeni tilengeze mu Ziyoni zimene Yehova Mulungu wathu wachita.’
PAN ujawnił naszą sprawiedliwość. Chodźcie, głośmy na Syjonie dzieło PANA, naszego Boga.
11 “Yehova wadzutsa mitima ya mafumu a Amedi, popeza cholinga chake ndi kuwononga Babuloni. Motero adzalipsira Ababuloni chifukwa chowononga Nyumba yake. Ndiye Yehova akuti, ‘Nolani mivi, tengani zishango.’
Wyostrzcie strzały, przygotujcie tarcze. PAN wzbudził ducha królów Medii, bo jego zamiar jest przeciwko Babilonowi, aby go zniszczyć. Jest to bowiem pomsta PANA, pomsta za jego świątynię.
12 Kwezani mbendera yankhondo kuti muwononge malinga a Babuloni! Limbitsani oteteza, ikani alonda pa malo awo, konzekerani kulalira. Pakuti Yehova watsimikiza ndipo adzachitadi zomwe ananena za anthu a ku Babuloni.
Podnieście sztandar na murach Babilonu, wzmocnijcie straże, postawcie stróżów, przygotujcie zasadzki. PAN bowiem obmyślił i wykonał to, co wypowiedział przeciwko mieszkańcom Babilonu.
13 Inu muli ndi mitsinje yambiri ndi chuma chambiri. Koma chimaliziro chanu chafika, moyo wanu watha.
Ty, który mieszkasz nad wieloma wodami, bogaty w skarby! Nadszedł twój koniec, kres twojej chciwości.
14 Yehova Wamphamvuzonse analumbira pali Iye mwini kuti: Ndidzakutumizira adani ochuluka ngati dzombe, kuti adzakuthire nkhondo ndipo adzafuwula kuonetsa kuti apambana.
PAN zastępów przysiągł na siebie samego: Zaprawdę, napełnię cię ludźmi jak szarańczą, wzniosą nad tobą okrzyk wojenny.
15 “Yehova analenga dziko lapansi ndi mphamvu zake; Iye anapanga dziko lonse ndi nzeru zake ndipo anayala thambo mwaluso lake.
On uczynił ziemię swoją mocą, utwierdził świat swoją mądrością i rozpostarł niebiosa swoją roztropnością.
16 Iye akayankhula, kumamveka mkokomo wamadzi akumwamba. Iyeyo amabweretsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi. Amabweretsa mphenzi pamodzi ndi mvula ndi kutulutsa mphepo yamkuntho kumalo kumene amasungira.
Gdy on wydaje głos, huczą wody w niebiosach, on sprawia, że chmury wznoszą się z krańców ziemi. I czyni błyskawice z deszczem, a wywodzi wiatr ze swoich skarbców.
17 “Anthu onse ndi opusa ndiponso opanda nzeru; mmisiri aliyense wosula golide akuchita manyazi ndi mafano ake. Mafano akewo ndi abodza; alibe moyo mʼkati mwawo.
Głupi jest każdy człowiek, kto tego nie zna, każdy złotnik jest zawstydzony z powodu posągu, bo jego odlany posąg jest fałszem i nie ma w nich ducha.
18 Mafanowo ndi achabechabe, zinthu zosekedwa nazo. Pamene anthuwo azidzaweruzidwa mafanowo adzawonongedwa.
Są marnością i dziełem błędów; zginą w czasie swego nawiedzenia.
19 Koma Yehova amene ndi Cholowa cha Yakobo sali ngati mafanowo. Iyeyu ndi Mlengi wa zinthu zonse, kuphatikizapo mtundu umene anawusankha kuti ukhale anthu ake. Dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
Nie takim jak one jest dział Jakuba, bo on jest Stwórcą wszystkiego, a [Izrael] jest szczepem jego dziedzictwa. PAN zastępów – to jego imię.
20 “Iwe Babuloni ndi ndodo yanga, chida changa chankhondo. Ndi iwe ndimaphwanya mitundu ya anthu, ndi iwe ndimawononga maufumu,
Jesteś moim młotem i orężem wojennym. Tobą zmiażdżę narody, tobą zniszczę królestwa;
21 ndi iwe ndimaphwanya kavalo ndi wokwerapo, ndi iwe ndimaphwanya galeta ndi woyendetsa wake.
Tobą zmiażdżę konia i jeźdźca, tobą zmiażdżę rydwan i jego woźnicę;
22 Ndi iwe ndimaphwanya mwamuna ndi mkazi, ndi iwe ndimaphwanya nkhalamba ndi wachinyamata, ndi iwe ndimaphwanya mnyamata ndi namwali.
Tobą zmiażdżę mężczyznę i kobietę, tobą zmiażdżę starca i dziecko, tobą zmiażdżę młodzieńca i pannę;
23 Ndi iwe ndimaphwanya mʼbusa ndi ziweto, ndi iwe ndimaphwanya mlimi ndi ngʼombe, ndi iwe ndimaphwanya abwanamkubwa ndi atsogoleri a ankhondo.
Tobą zmiażdżę pasterza i jego trzodę, tobą zmiażdżę oracza i jego zaprzęg, tobą zmiażdżę dowódców i rządców.
24 “Inu mukuona ndidzalanga Babuloni ndi onse amene amakhala mʼdziko la Babuloni chifukwa cha zolakwa zonse anachita ku Ziyoni,” akutero Yehova.
Ale odpłacę Babilonowi i wszystkim mieszkańcom Chaldei za całe ich zło, które czynili na Syjonie na waszych oczach, mówi PAN.
25 “Taonani, ndikukuzenga mlandu, iwe phiri lowononga, amene umawononga dziko lonse lapansi,” akutero Yehova. “Ndidzatambalitsa dzanja langa pofuna kukulanga, kukugubuduzira pansi kuchokera pa matanthwe ako, ndi kukusandutsa kukhala phiri lopserera.
Oto jestem przeciwko tobie, góro niszczycielska, mówi PAN, która niszczysz całą ziemię. Wyciągnę swoją rękę przeciwko tobie i strącę cię ze skał, i uczynię cię górą wypaloną.
26 Palibe ngakhale ndi mwala wako umodzi umene anthu adzawutenga kuti awugwiritse ntchito kumangira nyumba, chifukwa iwe udzakhala chipululu mpaka muyaya,” akutero Yehova.
A nie wezmą z ciebie kamienia węgielnego ani kamienia na fundamenty, bo staniesz się wiecznym pustkowiem, mówi PAN.
27 “Kwezani mbendera ya nkhondo mʼdziko! Lizani lipenga pakati pa mitundu ya anthu! Konzekeretsani mitundu ya anthu kuti ikamuthire nkhondo; itanani maufumu awa: Ararati, Mini ndi Asikenazi kuti adzamuthire nkhondo. Ikani mtsogoleri wankhondo kuti amenyane naye; tumizani akavalo ochuluka ngati magulu a dzombe.
Podnieście sztandar w ziemi, zadmijcie w trąbę wśród narodów, przygotujcie przeciwko niemu narody, zwołajcie przeciwko niemu królestwa Ararat, Minni i Aszkenaz; ustanówcie przeciwko niemu dowódcę, sprowadźcie konie jak najeżone szarańcze.
28 Konzekeretsani mitundu ya anthu. Amenewa ndiwo mafumu a Amedi, abwanamkubwa awo, atsogoleri a ankhondo, ndiponso ankhondo a mayiko amene amawalamulira, kuti idzathire nkhondo Babuloni.
Przygotujcie przeciwko niemu narody, królów Medii, ich dowódców i wszystkich ich rządców, oraz całą ziemię pod ich władzą;
29 Dziko likunjenjemera ndi kunthunthumira, chifukwa zidzachitikadi zimene Yehova wakonzera Babuloni; kusakaza dziko la Babuloni kuti musapezeke wokhalamo.
Wtedy ziemia zadrży i będzie w bólach, gdyż spełnią się przeciwko Babilonowi zamiary PANA, [aby] zamienić ziemię Babilonu w pustkowie, bez mieszkańców.
30 Ankhondo a ku Babuloni aleka kuchita nkhondo; iwo angokhala mʼmalinga awo. Mphamvu zawo zatheratu; ndipo akhala ngati akazi. Malo ake wokhala atenthedwa; mipiringidzo ya zipata zake yathyoka.
Mocarze Babilonu przestali walczyć, siedzą w warowniach, osłabło ich męstwo, stali się jak kobiety. Spalono jego mieszkania, wyłamano jego rygle.
31 Othamanga akungopezanapezana, amithenga akungotsatanatsatana kudzawuza mfumu ya ku Babuloni kuti alande mzinda wake wonse.
Goniec wybiegnie na spotkanie gońca, posłaniec – na spotkanie posłańca, aby opowiedzieć królowi Babilonu, że wzięto jego miasto z jednej strony;
32 Madooko onse alandidwa, malo onse obisalamo alonda atenthedwa ndi moto, ndipo ankhondo onse asokonezeka.”
[Że] brody są zajęte, sitowia spalone ogniem, a wojownicy przerażeni.
33 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Babuloni wokongola uja wakhala ngati malo opunthirapo tirigu pa nthawi yake yopuntha tirigu; A ku Yerusalemu akuti, Posachedwapa nthawi yake yomukolola ifika.”
Tak bowiem mówi PAN zastępów, Bóg Izraela: Córka Babilonu [jest] jak klepisko, [nadszedł] czas, gdy się je udeptuje; jeszcze chwila, a przyjdzie czas jej żniwa.
34 A ku Yerusalemu akuti, “Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni watiwononga, watiphwanya, ndi kutitaya ngati mbiya yopanda kanthu. Watimeza ngati ngʼona, wakhuta ndi zakudya zathu zokoma, kenaka nʼkutilavula.”
Pożarł mnie i zmiażdżył Nabuchodonozor, król Babilonu, uczynił mnie pustym naczyniem, połknął mnie jak smok, napełnił swój brzuch moimi rozkoszami i wypędził mnie.
35 Anthu a ku Ziyoni anene kuti, “Zankhanza zimene anatichitira ife ziwabwerere Ababuloni.” Anthu okhala mu Yerusalemu anene kuti, “Magazi athu amene anakhetsedwa akhale pa amene akukhala ku Babuloni.”
Krzywda zadana mi i memu ciału [niech spadnie] na Babilon, powie mieszkanka Syjonu, a moja krew – na mieszkańców Chaldei, powie Jerozolima.
36 Nʼchifukwa chake Yehova akuti, “Taona, ndidzakumenyera nkhondo ndi kukulipsirira; ndidzawumitsa nyanja yake ndipo akasupe ake adzaphwa.
Dlatego tak mówi PAN: Oto będę bronił twojej sprawy i pomszczę cię; wysuszę jego morze i sprawię, że wyschną jego źródła.
37 Motero Babuloni adzasanduka mulu wa nyumba zogumuka, malo okhala nkhandwe, malo ochititsa mantha ndi onyozedwa, malo wopanda aliyense wokhalamo.
I Babilon stanie się rumowiskiem, legowiskiem smoków, zdumieniem i świstaniem, pozbawionym mieszkańców.
38 Anthu ake onse adzabangula ngati mkango, adzadzuma ngati ana amkango.
Będą ryczeć razem jak lwy, warczeć jak lwie szczenięta.
39 Ngati achita dyera ndiye ndidzawakonzera madyerero ndi kuwaledzeretsa, kotero kuti adzasangalala, kenaka nʼkugona tulo mpaka muyaya ndipo sadzadzukanso,” akutero Yehova.
Gdy się rozpalą, uczynię im ucztę i upoję ich tak, aby weselili się i zasnęli wiecznym snem, by już się nie obudzili, mówi PAN.
40 “Ine ndidzawatenga kuti akaphedwe ngati ana ankhosa onenepa, ngati nkhosa zazimuna ndi mbuzi.
Sprowadzę ich jak baranki na rzeź, jak barany wraz z kozłami.
41 “Ndithu Babuloni walandidwa, mzinda umene dziko lonse lapansi limanyadira wagwidwa! Taonani, mmene Babuloni wasandukira chinthu chochititsa mantha pakati pa mitundu ya anthu!
Jakże został zdobyty Szeszak! Jakże została wzięta chwała całej ziemi! Jakże Babilon stał się spustoszeniem wśród narodów!
42 Nyanja yakwera ndi kumiza Babuloni; mafunde ake okokoma aphimba Babuloni.
Wystąpiło morze przeciwko Babilonowi, został przykryty mnóstwem jego fal.
43 Mizinda yake yasanduka bwinja, dziko lowuma ndi lachipululu, dziko losakhalamo wina aliyense, dziko losayendamo munthu aliyense.
Jego miasta stały się spustoszeniem, ziemią suchą i pustynną, ziemią, w której nikt nie mieszka, i przez którą nie przechodzi [żaden] syn człowieczy.
44 Ndidzalanga Beli mulungu wa Ababuloni, ndidzamusanzitsa zimene anameza. Mitundu ya anthu sidzapitanso kwa iye. Malinga a Babuloni agwa.
Nawiedzę też Bela w Babilonie i wyrwę mu z paszczy to, co pochłonął. Narody już nie będą napływać do niego; upadnie też mur Babilonu.
45 “Tulukani mʼBabuloni anthu anga! Pulumutsani miyoyo yanu! Thawani mkwiyo woopsa wa Yehova.
Wyjdźcie spośród niego, mój ludu, i niech każdy ratuje swoją duszę przed zapalczywością gniewu PANA.
46 Musataye mtima kapena kuchita mantha pamene mphekesera zikumveka mʼdziko mwanu. Chaka ndi chaka pamabuka mphekesera za ziwawa mʼdziko lapansi, ndiponso yakuti mfumu yakuti ikuthira nkhondo mfumu ina.
A niech wasze serce nie omdlewa ani się nie lękajcie wieści, którą będzie słychać w tej ziemi, gdy przyjdzie [jednego] roku wieść, potem drugiego roku wieść, ucisk w ziemi, władca przeciwko władcy.
47 Pakuti taonani, nthawi ikubwera ndithu pamene ndidzalanga mafano a ku Babuloni; dziko lake lonse lidzachita manyazi ndi ophedwa ake onse adzakhala ngundangunda pakati pake.
Dlatego oto nadchodzą dni, gdy nawiedzę rzeźbione obrazy Babilonu. Cała jego ziemia zostanie pohańbiona i wszyscy jego zabici padną pośród niego.
48 Pamenepo kumwamba ndi dziko lapansi ndi zonse zili mʼmenemo zidzayimba mokondwa chifukwa cha kugwa kwa Babuloni. Anthu owononga ochokera kumpoto adzamuthira nkhondo,” akutero Yehova.
Wtedy niebo, ziemia i wszystko, co w nich jest, będą śpiewać nad Babilonem. Z północy bowiem przyjdą na niego niszczyciele, mówi PAN.
49 “Babuloni anapha anthu ambiri pa dziko lapansi. Tsono, nawo anthu a ku Babuloni ayenera kuphedwa chifukwa anapha anthu a ku Yerusalemu.
Jak przez Babilon padli zabici Izraela, tak w Babilonie padną zabici całej ziemi.
50 Inu amene munapulumuka ku nkhondo ya Babuloni, chokani pano ndipo musazengereze! Kumbukirani Yehova ngakhale muli ku mayiko akutali, ganizirani za Yerusalemu.”
Wy, którzy uszliście spod miecza, idźcie, nie zatrzymujcie się! Wspominajcie PANA z daleka i niech przyjdzie wam na myśl Jerozolima.
51 Inu mukuti, “Tikuchita manyazi, chifukwa tanyozedwa ndipo nkhope zathu zili ndi manyazi, chifukwa anthu achilendo alowa malo opatulika a Nyumba ya Yehova.”
[Powiedzcie]: Wstydzimy się, że słyszymy zniewagi, hańba okryła nasze twarze. Weszli bowiem cudzoziemcy do świętych miejsc domu PANA.
52 Nʼchifukwa chake Yehova akuti, “Masiku akubwera pamene ndidzalanga mafano ake, ndipo mʼdziko lake lonse anthu ovulala adzabuwula.
Dlatego oto nadchodzą dni, mówi PAN, że nawiedzę jego rzeźbione obrazy, a po całej jego ziemi będą jęczeć jego zranieni.
53 Ngakhale Babuloni atadzikweza mpaka mlengalenga ndi kulimbitsa nsanja zake, ndidzatuma anthu owononga kudzamenyana naye,” akutero Yehova.
Choćby Babilon wstąpił do nieba i obwarował szczyty swojej potęgi, mimo to wyjdą ode mnie jego niszczyciele, mówi PAN.
54 “Imvani mfuwu wolira kuchokera ku Babuloni. Imvani phokoso lachiwonongeko chachikulu kuchokera mʼdziko la Babuloni.
[Słychać] głos krzyku z Babilonu i wielkie zniszczenie z ziemi Chaldejczyków;
55 Pakuti Yehova akuwononga Babuloni, ndipo akuthetsa phokoso lake lalikulu. Mfuwu wa adani ukumveka ngati mkokomo wa madzi ambiri. Phokoso lawo likunka likwererakwerera.
Bo PAN pustoszy Babilon i wytraci z niego wielki głos, choćby ich fale huczały jak wielkie wody [i] rozlegał się szum ich głosu.
56 Pakuti wowononga wafika kudzamenyana ndi Babuloni, ankhondo ake agwidwa, ndipo mauta awo athyoka. Paja Yehova ndi Mulungu wobwezera chilango; adzabwezera kwathunthu.
Niszczyciel bowiem nadciąga na niego, na Babilon, i jego mocarze zostaną pojmani, ich łuki będą połamane. PAN bowiem, Bóg odpłaty, odpłaci im niezawodnie;
57 Ndidzaledzeretsa akuluakulu ake pamodzi ndi anzeru ake, abwanamkubwa ake, atsogoleri a ankhondo pamodzinso ndi ankhondo; adzagona kwamuyaya osadzukanso,” akutero Mfumu, amene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
Upiję jego książąt i mędrców, jego dowódców i rządców oraz jego mocarzy, aby zasnęli wiecznym snem i już się nie obudzili, mówi Król, PAN zastępów to jego imię.
58 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Malinga aakulu a Babuloni adzasalazidwa ndipo zipata zake zazitali zidzatenthedwa; mitundu ya anthu inangogwira ntchito pachabe. Anthu anatopa ndi kumanga zimene tsopano zikupsa ndi moto.”
Tak mówi PAN zastępów: Szerokie mury Babilonu będą doszczętnie zniszczone i jego wysokie bramy zostaną spalone ogniem; ludzie będą trudzić się na darmo i narody – przy ogniu, a osłabną.
59 Zedekiya mfumu ya Yuda inali ndi phungu wake wamkulu amene dzina lake linali Seraya mwana wa Neriya chidzukulu cha Maseya. Mʼchaka chachinayi cha ulamuliro wake, Zedekiya anapita ndi Seraya ku Babuloni. Tsono mneneri Yeremiya anamupatsirako uthenga Serayayo.
Słowo, które prorok Jeremiasz polecił Serajaszowi, synowi Neriasza, syna Machsejasza, gdy [ten] udał się z Sedekiaszem, królem Judy, do Babilonu, w czwartym roku jego królowania. A Serajasz był spokojnym księciem.
60 Yeremiya anali atalemba mʼbuku za masautso onse amene adzafike pa Babuloni ndi zina zonse zokhudza Babuloni.
Jeremiasz więc spisał w jednej księdze całe nieszczęście, które miało spaść na Babilon, wszystkie słowa, które zostały napisane przeciwko Babilonowi.
61 Yeremiya anawuza Seraya kuti, “Ukakafika ku Babuloni, ukaonetsetse kuti wawawerengera anthu onse mawu onsewa.
I Jeremiasz powiedział do Serajasza: Gdy przybędziesz do Babilonu i zobaczysz go, i przeczytasz wszystkie te słowa;
62 Ndipo ukanene kuti, ‘Inu Yehova, mwanena kuti mudzawononga malo ano, kotero kuti simudzatsala munthu kapena nyama mʼdziko muno; lidzakhala chipululu mpaka muyaya.’
Powiesz: PANIE, ty mówiłeś przeciwko temu miejscu, że je wyniszczysz, aby nikt w nim nie mieszkał, ani człowiek, ani zwierzę, ale żeby było wiecznym pustkowiem.
63 Ukakatha kuwerenga bukuli, ukalimangirire ku mwala ndipo ukaliponye pakati pa mtsinje wa Yufurate.
A gdy dokończysz czytanie tej księgi, przywiążesz do niej kamień i wrzucisz ją w środek Eufratu;
64 Ndipo ukanene kuti, ‘Umu ndi mmene adzamirire Babuloni ndipo sadzadzukanso chifukwa cha masautso amene adzamugwere.’” Mawu a Yeremiya athera pamenepa.
I powiesz: Tak utonie Babilon i już nie powstanie z tego nieszczęścia, które na niego sprowadzę, i osłabną. Dotąd słowa Jeremiasza.

< Yeremiya 51 >