< Yeremiya 51 >

1 Yehova akuti, “Taonani, ndidzadzutsa mphepo yowononga kuti iwononge Babuloni pamodzi ndi anthu a ku Lebi Kamai.
The Lord seith these thingis, Lo! Y schal reise on Babiloyne, and on the dwelleris therof, that reisiden her herte ayens me, as a wynd of pestilence.
2 Ndidzatuma alendo ku Babuloni kudzamupeta ndi kuwononga dziko lake kotheratu. Iwo adzalimbana naye ku mbali zonse pa tsiku la masautso ake.
And Y schal sende in to Babiloyne wyndeweris, and thei schulen wyndewe it, and thei schulen destrie the lond of it; for thei camen on it on ech side, in the dai of the turment therof.
3 Okoka uta musawalekerere kapena wonyadira chovala chawo chankhondo. Musawasiye anyamata ake kuti akhale ndi moyo; koma muwononge ankhondo ake kotheratu.
He that beendith his bowe, beende not, and a man clothid in haburioun, stie not; nyle ye spare the yonge men therof, sle ye al the chyualrie therof.
4 Adzavulazidwa ndi kufera mʼdziko la Babuloni lomwelo ndi mʼmisewu yawo yomwe.
And slayn men schulen falle in the lond of Caldeis, and woundid men in the cuntreis therof.
5 Pakuti Yuda ndi Israeli sanasiyidwe ngati amasiye ndi Mulungu wawo, Yehova Wamphamvuzonse, koma ngakhale dziko la Babuloni ndi lodzaza ndi machimo pamaso pa Woyerayo wa Israeli.
For whi Israel and Juda was not maad widewe fro her God, the Lord of oostis; but the lond of hem was fillid with trespas of the hooli of Israel.
6 “Thawaniko ku Babuloni! Aliyense apulumutse moyo wake! Musawonongeke naye pamodzi chifukwa cha machimo ake. Imeneyi ndi nthawi yoti Yehova amulange; Yehova adzamulipsira.
Fle ye fro the myddis of Babiloyne, that ech man saue his soule; nyle ye be stille on the wickidnesse therof, for whi tyme of veniaunce therof is to the Lord; he schal yelde while to it.
7 Babuloni anali ngati chikho cha golide mʼdzanja la Yehova; kuti aledzeretse dziko lonse lapansi. Mitundu yambiri ya anthu inamwa vinyo wake; nʼchifukwa chake tsopano inachita misala.
Babiloyne is a goldun cuppe in the hond of the Lord, and fillith al erthe; hethene men drunken of the wyn therof, and therfor thei ben mouyd.
8 Babuloni wagwa mwadzidzidzi ndi kusweka. Mulireni! Mfunireni mankhwala opha ululu wake; mwina iye nʼkuchira.”
Babiloyne felle doun sudenli, and is al to-brokun; yelle ye on it, take ye recyn to the sorewe therof, if perauenture it be heelid.
9 Ena anati, “‘Ife tinayesa kumupatsa mankhwala Babuloni, koma sanachire; tiyeni timusiye ndipo aliyense apite ku dziko la kwawo, pakuti mlandu wake wafika mpaka mlengalenga, wafika mpaka kumwamba.’
We heeliden Babiloyne, and it is not maad hool; forsake we it and go we ech in to his lond; for the doom therof cam `til to heuenes, and is reisid `til to cloudis.
10 “‘Yehova waonetsa poyera kuti ndife osalakwa; tiyeni tilengeze mu Ziyoni zimene Yehova Mulungu wathu wachita.’
The Lord hath brouyt forth oure riytfulnessis; come ye, and telle we in Sion the werk of oure Lord God.
11 “Yehova wadzutsa mitima ya mafumu a Amedi, popeza cholinga chake ndi kuwononga Babuloni. Motero adzalipsira Ababuloni chifukwa chowononga Nyumba yake. Ndiye Yehova akuti, ‘Nolani mivi, tengani zishango.’
Scharpe ye arowis, fille ye arowe caasis; the Lord reiside the spirit of the kyngis of Medeis, and his mynde is ayen Babiloyne, that he leese it, for it is the veniaunce of the Lord, the veniaunce of his temple. The kyng of Medeis is reisid of the Lord ayens Babiloyne.
12 Kwezani mbendera yankhondo kuti muwononge malinga a Babuloni! Limbitsani oteteza, ikani alonda pa malo awo, konzekerani kulalira. Pakuti Yehova watsimikiza ndipo adzachitadi zomwe ananena za anthu a ku Babuloni.
Reise ye a signe on the wallis of Babiloyne, encreesse ye kepyng, reise ye keperis, make ye redi buyschementis; for the Lord thouyte, and dide, what euer thing he spak ayens the dwelleris of Babiloyne.
13 Inu muli ndi mitsinje yambiri ndi chuma chambiri. Koma chimaliziro chanu chafika, moyo wanu watha.
A! thou Babiloyne, that dwellist on many watris, riche in thi tresours, thin ende cometh, the foote mesure of thi kittyng doun.
14 Yehova Wamphamvuzonse analumbira pali Iye mwini kuti: Ndidzakutumizira adani ochuluka ngati dzombe, kuti adzakuthire nkhondo ndipo adzafuwula kuonetsa kuti apambana.
The Lord of oostis swoor bi his soule, that Y schal fille thee with men, as with bruke, and a myry song schal be sungun on thee.
15 “Yehova analenga dziko lapansi ndi mphamvu zake; Iye anapanga dziko lonse ndi nzeru zake ndipo anayala thambo mwaluso lake.
The Lord swoor, which made erthe bi his strengthe, made redy the world bi his wisdom, and stretchide forth heuenes bi his prudence.
16 Iye akayankhula, kumamveka mkokomo wamadzi akumwamba. Iyeyo amabweretsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi. Amabweretsa mphenzi pamodzi ndi mvula ndi kutulutsa mphepo yamkuntho kumalo kumene amasungira.
Whanne he yyueth vois, watris ben multiplied in heuene; which Lord reisith cloudis fro the laste of erthe, made leitis in to reyn, and brouyt forth wynd of hise tresouris.
17 “Anthu onse ndi opusa ndiponso opanda nzeru; mmisiri aliyense wosula golide akuchita manyazi ndi mafano ake. Mafano akewo ndi abodza; alibe moyo mʼkati mwawo.
Ech man is maad a fool of kunnyng, ech wellere togidere is schent in a grauun ymage; for his wellyng togidere is fals, and a spirit is not in tho.
18 Mafanowo ndi achabechabe, zinthu zosekedwa nazo. Pamene anthuwo azidzaweruzidwa mafanowo adzawonongedwa.
The werkis ben veyn, and worthi of scorn; tho schulen perische in the tyme of her visityng.
19 Koma Yehova amene ndi Cholowa cha Yakobo sali ngati mafanowo. Iyeyu ndi Mlengi wa zinthu zonse, kuphatikizapo mtundu umene anawusankha kuti ukhale anthu ake. Dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
The part of Jacob is not as these thingis; for he that made alle thingis is the part of Jacob, and Israel is the septre of his eritage; the Lord of oostis is his name.
20 “Iwe Babuloni ndi ndodo yanga, chida changa chankhondo. Ndi iwe ndimaphwanya mitundu ya anthu, ndi iwe ndimawononga maufumu,
Thou hurtlist doun to me the instrumentis of batel, and Y schal hurtle doun folkis in thee, and Y schal leese rewmes in thee;
21 ndi iwe ndimaphwanya kavalo ndi wokwerapo, ndi iwe ndimaphwanya galeta ndi woyendetsa wake.
and Y schal hurtle doun in thee an hors, and the ridere therof; and Y schal hurtle doun in thee a chare, and the stiere therof;
22 Ndi iwe ndimaphwanya mwamuna ndi mkazi, ndi iwe ndimaphwanya nkhalamba ndi wachinyamata, ndi iwe ndimaphwanya mnyamata ndi namwali.
and Y schal hurtle doun in thee a man and womman; and Y schal hurtle doun in thee an elde man and a child; and Y schal hurtle doun in thee a yong man and a virgyn;
23 Ndi iwe ndimaphwanya mʼbusa ndi ziweto, ndi iwe ndimaphwanya mlimi ndi ngʼombe, ndi iwe ndimaphwanya abwanamkubwa ndi atsogoleri a ankhondo.
and Y schal hurtle doun in thee a scheepherde and his floc; and Y schal hurtle doun in thee an erthetiliere and his yok beestis; and Y schal hurtle doun in thee duykis and magistratis.
24 “Inu mukuona ndidzalanga Babuloni ndi onse amene amakhala mʼdziko la Babuloni chifukwa cha zolakwa zonse anachita ku Ziyoni,” akutero Yehova.
And Y schal yelde, seith the Lord, to Babiloyne, and to alle the dwelleris of Caldee, al her yuel, which thei diden in Sion, bifore youre iyen.
25 “Taonani, ndikukuzenga mlandu, iwe phiri lowononga, amene umawononga dziko lonse lapansi,” akutero Yehova. “Ndidzatambalitsa dzanja langa pofuna kukulanga, kukugubuduzira pansi kuchokera pa matanthwe ako, ndi kukusandutsa kukhala phiri lopserera.
Lo! Y, seith the Lord, to thee, thou hil berynge pestilence, which corrumpist al erthe. Y schal stretche forth myn hond on thee, and Y schal vnwlappe thee fro stoonys, and Y schal yyue thee in to an hil of brennyng.
26 Palibe ngakhale ndi mwala wako umodzi umene anthu adzawutenga kuti awugwiritse ntchito kumangira nyumba, chifukwa iwe udzakhala chipululu mpaka muyaya,” akutero Yehova.
And Y schal not take of thee a stoon in to a corner, and a stoon in to foundementis; but thou schalt be lost with outen ende, seith the Lord.
27 “Kwezani mbendera ya nkhondo mʼdziko! Lizani lipenga pakati pa mitundu ya anthu! Konzekeretsani mitundu ya anthu kuti ikamuthire nkhondo; itanani maufumu awa: Ararati, Mini ndi Asikenazi kuti adzamuthire nkhondo. Ikani mtsogoleri wankhondo kuti amenyane naye; tumizani akavalo ochuluka ngati magulu a dzombe.
Reise ye a signe in the lond, sowne ye with a clarioun in hillis; halewe ye folkis on it, telle ye to the kyngis of Ararath, of Menny, and of Ascheneth ayens it; noumbre ye Tapser ayens it, and bringe ye an hors, as a bruke hauynge a pricke.
28 Konzekeretsani mitundu ya anthu. Amenewa ndiwo mafumu a Amedi, abwanamkubwa awo, atsogoleri a ankhondo, ndiponso ankhondo a mayiko amene amawalamulira, kuti idzathire nkhondo Babuloni.
Halowe ye folkis ayens it, the kyngis of Medey, the duykis therof, and alle magistratis therof, and al the lond of his power.
29 Dziko likunjenjemera ndi kunthunthumira, chifukwa zidzachitikadi zimene Yehova wakonzera Babuloni; kusakaza dziko la Babuloni kuti musapezeke wokhalamo.
And the erthe schal be mouyd, and schal be disturblid; for the thouyt of the Lord schal fulli wake ayens Babiloyne, that he sette the lond of Babiloyne desert, and vnhabitable.
30 Ankhondo a ku Babuloni aleka kuchita nkhondo; iwo angokhala mʼmalinga awo. Mphamvu zawo zatheratu; ndipo akhala ngati akazi. Malo ake wokhala atenthedwa; mipiringidzo ya zipata zake yathyoka.
The stronge men of Babiloyne ceessiden of batel, thei dwelliden in stronge holdis; the strengthe of hem is deuourid, and thei ben maad as wymmen; the tabernaclis therof ben brent, the barris therof ben al to-brokun.
31 Othamanga akungopezanapezana, amithenga akungotsatanatsatana kudzawuza mfumu ya ku Babuloni kuti alande mzinda wake wonse.
A rennere schal come ayens a rennere, and a messanger ayens a messanger, to telle to the kyng of Babiloyne, that his citee is takun fro the toon ende `til to the tother ende;
32 Madooko onse alandidwa, malo onse obisalamo alonda atenthedwa ndi moto, ndipo ankhondo onse asokonezeka.”
and the forthis ben bifore ocupied, and the mareisis ben brent with fier, and the men werryours ben disturblid.
33 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Babuloni wokongola uja wakhala ngati malo opunthirapo tirigu pa nthawi yake yopuntha tirigu; A ku Yerusalemu akuti, Posachedwapa nthawi yake yomukolola ifika.”
For the Lord of oostis, God of Israel, seith these thingis, The douyter of Babiloyne is as a corn floor, the tyme of threischyng therof; yit a litil, and the tyme of repyng therof schal come.
34 A ku Yerusalemu akuti, “Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni watiwononga, watiphwanya, ndi kutitaya ngati mbiya yopanda kanthu. Watimeza ngati ngʼona, wakhuta ndi zakudya zathu zokoma, kenaka nʼkutilavula.”
Nabugodonosor, the kyng of Babiloyne, eet me, and deuouride me; he made me as a voide vessel, he as a dragoun swolewide me; he fillide his wombe with my tendirnesse, and he castide me out.
35 Anthu a ku Ziyoni anene kuti, “Zankhanza zimene anatichitira ife ziwabwerere Ababuloni.” Anthu okhala mu Yerusalemu anene kuti, “Magazi athu amene anakhetsedwa akhale pa amene akukhala ku Babuloni.”
Wickidnesse ayens me, and my fleisch on Babiloyne, seith the dwellyng of Sion; and my blood on the dwelleris of Caldee, seith Jerusalem.
36 Nʼchifukwa chake Yehova akuti, “Taona, ndidzakumenyera nkhondo ndi kukulipsirira; ndidzawumitsa nyanja yake ndipo akasupe ake adzaphwa.
Therfor the Lord seith these thingis, Lo! Y schal deme thi cause, and Y schal venge thi veniaunce; and Y schal make the see therof forsakun, and Y schal make drie the veyne therof.
37 Motero Babuloni adzasanduka mulu wa nyumba zogumuka, malo okhala nkhandwe, malo ochititsa mantha ndi onyozedwa, malo wopanda aliyense wokhalamo.
And Babiloyne schal be in to biriels, it schal be the dwellyng of dragouns, wondryng and hissyng, for that no dwellere is.
38 Anthu ake onse adzabangula ngati mkango, adzadzuma ngati ana amkango.
Thei schulen rore togidere as liouns, and thei schulen schake lockis, as the whelpis of liouns.
39 Ngati achita dyera ndiye ndidzawakonzera madyerero ndi kuwaledzeretsa, kotero kuti adzasangalala, kenaka nʼkugona tulo mpaka muyaya ndipo sadzadzukanso,” akutero Yehova.
In the heete of hem Y schal sette the drynkis of hem; and Y schal make hem drunkun, that thei be brouyt asleepe, and that thei slepe euerlastynge sleep, and rise not, seith the Lord.
40 “Ine ndidzawatenga kuti akaphedwe ngati ana ankhosa onenepa, ngati nkhosa zazimuna ndi mbuzi.
Y schal lede forth hem, as lambren to slayn sacrifice, and as wetheris with kidis. Hou is Sesac takun, and the noble citee of al erthe is takun?
41 “Ndithu Babuloni walandidwa, mzinda umene dziko lonse lapansi limanyadira wagwidwa! Taonani, mmene Babuloni wasandukira chinthu chochititsa mantha pakati pa mitundu ya anthu!
Hou is Babiloyne made in to wondre among hethene men?
42 Nyanja yakwera ndi kumiza Babuloni; mafunde ake okokoma aphimba Babuloni.
And the see stiede on Babiloyne, it was hilid with the multitude of hise wawis.
43 Mizinda yake yasanduka bwinja, dziko lowuma ndi lachipululu, dziko losakhalamo wina aliyense, dziko losayendamo munthu aliyense.
The citees therof ben maad in to wondryng, the lond is maad vnhabitable and forsakun; the lond wherynne no man dwellith, and the sone of man schal not passe bi it.
44 Ndidzalanga Beli mulungu wa Ababuloni, ndidzamusanzitsa zimene anameza. Mitundu ya anthu sidzapitanso kwa iye. Malinga a Babuloni agwa.
And Y schal visite on Bel in to Babiloyne, and Y schal caste out of hise mouth that, that he hadde swolewid, and folkis schulen no more flowe to it; for also the wal of Babiloyne schal falle doun.
45 “Tulukani mʼBabuloni anthu anga! Pulumutsani miyoyo yanu! Thawani mkwiyo woopsa wa Yehova.
Mi puple, go ye out fro the myddis therof, that ech man saue his soule fro the wraththe of the strong veniaunce of the Lord;
46 Musataye mtima kapena kuchita mantha pamene mphekesera zikumveka mʼdziko mwanu. Chaka ndi chaka pamabuka mphekesera za ziwawa mʼdziko lapansi, ndiponso yakuti mfumu yakuti ikuthira nkhondo mfumu ina.
and lest perauenture youre herte wexe neische, and lest ye dreden the heryng, that schal be herd in the lond; and heryng schal come in a yeer, and aftir this yeer schal come heryng and wickidnesse in the lond, and a lord on a lord.
47 Pakuti taonani, nthawi ikubwera ndithu pamene ndidzalanga mafano a ku Babuloni; dziko lake lonse lidzachita manyazi ndi ophedwa ake onse adzakhala ngundangunda pakati pake.
Therfor lo! daies comen, seith the Lord, and Y schal visite on the grauun ymagis of Babiloyne; and al the lond therof schal be schent, and alle slayn men therof schulen falle doun in the myddis therof.
48 Pamenepo kumwamba ndi dziko lapansi ndi zonse zili mʼmenemo zidzayimba mokondwa chifukwa cha kugwa kwa Babuloni. Anthu owononga ochokera kumpoto adzamuthira nkhondo,” akutero Yehova.
And heuenes, and erthis, and alle thingis that ben in tho, schulen herie on Babiloyne; for rauynours schulen come fro the north to it, seith the Lord.
49 “Babuloni anapha anthu ambiri pa dziko lapansi. Tsono, nawo anthu a ku Babuloni ayenera kuphedwa chifukwa anapha anthu a ku Yerusalemu.
And as Babiloyne dide, that slayn men felle doun in Israel, so of Babiloyne slayn men schulen falle doun and in al the lond.
50 Inu amene munapulumuka ku nkhondo ya Babuloni, chokani pano ndipo musazengereze! Kumbukirani Yehova ngakhale muli ku mayiko akutali, ganizirani za Yerusalemu.”
Come ye, that fledden the swerd, nyle ye stonde; haue ye mynde afer on the Lord, and Jerusalem stie on youre herte.
51 Inu mukuti, “Tikuchita manyazi, chifukwa tanyozedwa ndipo nkhope zathu zili ndi manyazi, chifukwa anthu achilendo alowa malo opatulika a Nyumba ya Yehova.”
We ben schent, for we herden schenschipe; schame hilide oure faces, for aliens comen on the halewyng of the hous of the Lord.
52 Nʼchifukwa chake Yehova akuti, “Masiku akubwera pamene ndidzalanga mafano ake, ndipo mʼdziko lake lonse anthu ovulala adzabuwula.
Therfor lo! daies comen, seith the Lord, and Y schal visite on the grauun ymagis of Babiloyne, and in al the lond therof a woundid man schal loowe.
53 Ngakhale Babuloni atadzikweza mpaka mlengalenga ndi kulimbitsa nsanja zake, ndidzatuma anthu owononga kudzamenyana naye,” akutero Yehova.
If Babiloyne stieth in to heuene, and makith stidfast his strengthe an hiy, distrieris therof schulen come on me, seith the Lord.
54 “Imvani mfuwu wolira kuchokera ku Babuloni. Imvani phokoso lachiwonongeko chachikulu kuchokera mʼdziko la Babuloni.
The vois of a criere of Babiloyne, and greet sorewe of the lond of Caldeis,
55 Pakuti Yehova akuwononga Babuloni, ndipo akuthetsa phokoso lake lalikulu. Mfuwu wa adani ukumveka ngati mkokomo wa madzi ambiri. Phokoso lawo likunka likwererakwerera.
for the Lord distriede Babiloyne, and lost of it a greet vois; and the wawis of hem schulen sowne as many watris. The vois of hem yaf sown,
56 Pakuti wowononga wafika kudzamenyana ndi Babuloni, ankhondo ake agwidwa, ndipo mauta awo athyoka. Paja Yehova ndi Mulungu wobwezera chilango; adzabwezera kwathunthu.
for a rauenour cam on it, that is, on Babiloyne; and the stronge men therof ben takun, and the bouwe of hem welewide, for the stronge vengere the Lord yeldynge schal yelde.
57 Ndidzaledzeretsa akuluakulu ake pamodzi ndi anzeru ake, abwanamkubwa ake, atsogoleri a ankhondo pamodzinso ndi ankhondo; adzagona kwamuyaya osadzukanso,” akutero Mfumu, amene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
And Y schal make drunkun the princis therof, and the wise men therof, the duykis therof, and the magistratis therof, and the stronge men therof; and thei schulen slepe euerlastynge sleep, and thei schulen not be awakid, seith the kyng, the Lord of oostis is name of hym.
58 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Malinga aakulu a Babuloni adzasalazidwa ndipo zipata zake zazitali zidzatenthedwa; mitundu ya anthu inangogwira ntchito pachabe. Anthu anatopa ndi kumanga zimene tsopano zikupsa ndi moto.”
The Lord God of oostis seith these thingis, Thilke brodeste wal of Babiloyne schal be mynyd with mynyng, and the hiye yatis therof schulen be brent with fier; and the trauels of puples schulen be to nouyt, and the trauels of hethene men schulen be in to fier, and schulen perische.
59 Zedekiya mfumu ya Yuda inali ndi phungu wake wamkulu amene dzina lake linali Seraya mwana wa Neriya chidzukulu cha Maseya. Mʼchaka chachinayi cha ulamuliro wake, Zedekiya anapita ndi Seraya ku Babuloni. Tsono mneneri Yeremiya anamupatsirako uthenga Serayayo.
The word which Jeremye, the profete, comaundide to Saraie, sone of Nerie, sone of Maasie, whanne he yede with Sedechie, the kyng, in to Babiloyne, in the fourthe yeer of his rewme; forsothe Saraie was prynce of profesie.
60 Yeremiya anali atalemba mʼbuku za masautso onse amene adzafike pa Babuloni ndi zina zonse zokhudza Babuloni.
And Jeremye wroot al the yuel, that was to comynge on Babiloyne, in a book, alle these wordis that weren writun ayens Babiloyne.
61 Yeremiya anawuza Seraya kuti, “Ukakafika ku Babuloni, ukaonetsetse kuti wawawerengera anthu onse mawu onsewa.
And Jeremye seide to Saraie, Whanne thou comest in to Babiloyne, and seest, and redist alle these wordis,
62 Ndipo ukanene kuti, ‘Inu Yehova, mwanena kuti mudzawononga malo ano, kotero kuti simudzatsala munthu kapena nyama mʼdziko muno; lidzakhala chipululu mpaka muyaya.’
thou schalt seie, Lord, thou spakist ayens this place, that thou schuldist leese it, that noon be that dwelle therynne, fro man `til to beeste, and that it be an euerlastynge wildirnesse.
63 Ukakatha kuwerenga bukuli, ukalimangirire ku mwala ndipo ukaliponye pakati pa mtsinje wa Yufurate.
And whanne thou hast fillid to rede this book, thou schalt bynde to it a stoon, and thou schalt caste it forth in to the myddis of Eufrates; and thou schalt seie,
64 Ndipo ukanene kuti, ‘Umu ndi mmene adzamirire Babuloni ndipo sadzadzukanso chifukwa cha masautso amene adzamugwere.’” Mawu a Yeremiya athera pamenepa.
So Babiloyne schal be drenchid, and it schal not rise fro the face of turment, which Y brynge on it, and it schal be distried. Hidurto ben the wordis of Jeremye.

< Yeremiya 51 >