< Yeremiya 49 >

1 Yehova ananena izi: Amoni, “Kodi Israeli alibe ana aamuna? Kapena alibe mlowamʼmalo? Tsono nʼchifukwa chiyani anthu opembedza Moleki alanda dziko la Gadi? Nʼchifukwa chiyani anthu ake akukhala mʼmizinda ya Gadi?
Za sinove Amonove: ovako veli Gospod: zar Izrailj nema sinova? zar nema našljednika? zašto Malhom naslijedi zemlju Gadovu? i zašto se narod njegov naseli u njegovijem gradovima?
2 Koma nthawi ikubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzamveketse mfuwu wankhondo ku Raba, likulu la Amoni; ndipo malo awo opembedzera milungu yawo adzatenthedwa ndi moto. Choncho Aisraeli adzalandanso dziko lawo kuchokera kwa amene anawalanda poyamba dzikolo,” akutero Yehova.
Zato evo idu dani, govori Gospod, kad æu uèiniti da se èuje vika ubojna u Ravi sinova Amonovijeh, i ona da bude gomila razvalina, i sela njezina popaljena ognjem; i Izrailj æe obladati onima koji bjehu njim obladali, govori Gospod.
3 “Lirani, inu anthu a ku Hesiboni chifukwa wowononga uja wafika! Fuwulani, inu anthu okhala ku Raba! Valani ziguduli ndi kulira mwamphamvu; thamangani uku ndi uku mʼkati mwa malinga, chifukwa mulungu wanu Moleki adzapita ku ukapolo, pamodzi ndi ansembe ake ndiponso akuluakulu ake.
Ridaj Esevone, jer je Gaj opustošen; vièite sela Ravska; pripašite oko sebe kostrijet, narièite i trèite oko plotova; jer æe Malhom otiæi u ropstvo, sveštenici njegovi i knezovi njegovi skupa.
4 Chifukwa chiyani mukunyadira chigwa chanu, inu anthu osakhulupirika amene munadalira chuma chanu nʼkumati: ‘Ndani angandithire nkhondo?’
Što se hvališ dolinama? Rastopila se dolina tvoja, kæeri odmetnico! koja se uzdaš u blago svoje: ko bi udario na me?
5 Ndidzabweretsa zoopsa pa iwe zochokera kwa onse amene akuzungulira,” akutero Ambuye, Mulungu Wamphamvuzonse. “Mudzathawa, ndipo aliyense adzathawitsa moyo wake. Sipadzapezeka munthu wosonkhanitsanso othawawo.
Evo ja æu pustiti na te strah otsvuda unaokolo, govori Gospod Gospod nad vojskama, i raspršaæete se svi, i neæe biti nikoga da sakupi bježan.
6 “Komabe pambuyo pake, ndidzabwezera kwawo Aamoni,” akutero Yehova.
Ali æu poslije povratiti roblje sinova Amonovijeh, govori Gospod.
7 Yehova Wamphamvuzonse ananena izi za Edomu: “Kodi nzeru sizikupezekanso ku Temani? Kodi anzeru analeka kupereka uphungu? Kodi nzeru zawo zinatheratu?
Za Edoma, ovako veli Gospod nad vojskama: zar nema više mudrosti u Temanu? nesta li svjeta razumnima? išèilje li mudrost njihova?
8 Inu anthu a ku Dedani, thawani, bwererani ndi kukabisala ku makwalala chifukwa ndidzagwetsa mavuto pa zidzukulu za Esau popeza nthawi yawo ya chiweruzo yafika.
Bježite, obratite pleæi, zavrite se duboko, stanovnici Dedanski, jer æu pustiti na Isava pogibao njegovu u vrijeme kad æu ga pohoditi.
9 Kodi anthu othyola mphesa akanafika kwa inu akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha? Anthu akuba akanafika usiku akanangotengako zimene akuzifuna zokha?
Da ti doðu beraèi, ne bi li ti ostavili pabiraka? da doðu lupeži noæu, ne bi li odnijeli koliko im je dosta?
10 Koma ine ndazivula zidzukulu za Esau. Ndaonetsa poyera malo awo obisalamo, kotero kuti sadzathanso kubisala. Ana ake, abale ake pamodzi ndi anansi ake awonongeka. Palibe wonena kuti,
Ali ja ogoluznih Isava, otkrih potaje njegove da se ne može sakriti; propade sjeme njegovo, braæa njegova i susjedi njegovi, niko ne osta.
11 ‘Siyani ana anu amasiye; Ine ndidzawateteza. Amayi anu amasiye akhoza kudalira Ine.’”
Ostavi sirote svoje, ja æu im život saèuvati, i udovice tvoje neka se uzdaju u me.
12 Yehova akuti, “Ngati iwo amene sanali oyenera kulangidwa adzamwa chikho cha chiweruzo, ndiye muyesa kuti inuyo simudzalangidwa? Ayi ndithu simudzakhala osalangidwa. Mudzamwa ndithu chikhocho.
Jer ovako veli Gospod: evo, koji ne bi trebalo da piju iz èaše, doista æe piti; a ti li æeš ostati bez kara? neæeš ostati bez kara, nego æeš zacijelo piti.
13 Ine ndikulumbira, akutero Yehova, kuti mzinda wa Bozira udzasanduka bwinja, chinthu chochititsa mantha, chomachiseka ndiponso chotembereredwa. Mizinda yake yonse idzakhala mabwinja mpaka muyaya.”
Jer sobom se zaklinjem, govori Gospod, da æe Vosora biti pustoš, rug, èudo i prokletstvo, i svi æe gradovi njezini biti pustinja vjeèna.
14 Ndamva uthenga wochokera kwa Yehova: Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu ina kukanena kuti, “Sonkhanani pamodzi kuti muthire nkhondo Edomu! Konzekerani nkhondo!”
Èuh glas od Gospoda, i glasnik bi poslan k narodima da reèe: skupite se i idite na nju, i dignite se u boj.
15 “Ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina. Mudzakhala anthu onyozeka pakati pa anthu.
Jer gle, uèiniæu te da budeš mali meðu narodima i prezren meðu ljudima.
16 Kuopseza kwako kwakunyenga; kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa, iwe amene umakhala mʼmapanga a mʼmatanthwe ndi mʼmapiri. Ngakhale utamanga chisa chako pamwamba kwambiri ngati chiwombankhanga, ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,” akutero Yehova.
Obijest tvoja i ponositost srca tvojega prevari tebe, koji živiš u rasjelinama kamenijem i držiš se visokih humova; da naèiniš sebi gnijezdo visoko kao orao, i odande æu te svaliti, govori Gospod.
17 “Dziko la Edomu lidzasanduka chinthu chochititsa mantha. Onse odutsamo adzadabwa ndi kupukusa mitu yawo chifukwa cha kuwonongeka kwake.
I zemlja æe Edomska biti pustinja, ko proðe mimo nju, svak æe se èuditi i zviždati radi svijeh rana njezinijeh.
18 Monga momwe anawonongekera Sodomu ndi Gomora, pamodzi ndi mizinda yake yozungulira,” akutero Yehova, “motero palibe munthu amene adzakhala mu Edomu.
Kao kad se zatr Sodom i Gomor i susjedstvo njihovo, veli Gospod, neæe se naseliti ondje niko niti æe se baviti ondje sin èovjeèji.
19 “Monga mkango wotuluka ku nkhalango za ku Yorodani kupita ku malo a msipu wobiriwira, Ine ndidzapirikitsa anthu a ku Edomu mwadzidzidzi kuchoka mʼdziko lawo. Pambuyo pake ndidzawayikira owalamulira amene ndamufuna Ine. Kodi ndani wofanana nane, ndipo angatsutsane nane ndani? Ndipo ndi mʼbusa uti amene angalimbane nane?”
Gle, kao lav izaæi æe podižuæi se više nego Jordan na stan silnoga; ali æu ga brzo otjerati iz te zemlje, i postaviæu nad njom onoga ko je izabran; jer ko je kao ja? i ko æe se preti sa mnom? i koji æe mi pastir odoljeti?
20 Nʼchifukwa chake imvani. Izi ndi zimene Ine Yehova ndakonza zolangira anthu a ku Edomu ndi a ku Temani. Ngakhale ana omwe adzatengedwa ukapolo ndipo aliyense adzachita mantha chifukwa cha iwo.
Zato èujte namjeru Gospodnju što je naumio za Edomce i misli njegove što je smislio za stanovnike Temanske: zaista najmanji iz stada razvlaèiæe ih, zaista æe opustjeti stan s njima.
21 Akadzagwa Edomu padzakhala mfuwu waukulu ndipo dziko lapansi lidzanjenjemera; kulira kwawo kudzamveka mpaka ku Nyanja Yofiira.
Od praske padanja njihova zemlja æe se tresti, i vika æe se njihova èuti na Crvenom Moru.
22 Taonani, mtundu wina udzachita kuwuluka nʼkudzatera pa Bozira ngati chiwombankhanga chimene chatambalitsa mapiko ake. Pa tsiku limenelo mitima ya ankhondo a ku Edomu idzagunda ngati mtima wa mayi pa nthawi yake yochira.
Gle, doæi æe i doletjeæe kao orao i raširiæe krila svoja nad Vosorom, i biæe srce u junaka Edomskih kao srce u žene koja se poraða.
23 Mawu a Yehova onena za Damasiko ndi awa: “Anthu a ku Hamati ndi a ku Aripadi akuchita mantha chifukwa amva nkhani yoyipa. Mitima yawo yagwidwa ndi mantha ndipo ali ngati muja ichitira nyanja yosakhazikika.
Za Damasak. Posrami se Emat i Arfad, jer èu zle glase; rastopiše se, strah je na moru, ne može se umiriti.
24 Anthu a ku Damasiko alefuka. Abwerera mʼmbuyo kufuna kuthawa chifukwa agwidwa ndi mantha aakulu. Ali ndi nkhawa komanso mantha ngati za mayi pa nthawi yake yochira.
Damasak klonu, obrati se da bježi, drhat ga poduze, tuga i bolovi osvojiše ga kao porodilju.
25 Mzinda wotchuka ndi wachikondwerero uja wasiyidwa!
Kako se ne ostavi slavni grad? grad radosti moje?
26 Nʼchifukwa chake anyamata ake adzagwa mʼmisewu ndi kufa; ankhondo ake onse adzawonongedwa tsiku limenelo,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Zato æe popadati mladiæi njegovi na ulicama njegovijem, i svi æe vojnici njegovi izginuti u onaj dan, govori Gospod nad vojskama.
27 “Ndidzatentha malinga a Damasiko; moto udzanyeketsa nyumba zaufumu za Beni-Hadadi.”
I raspaliæu oganj u zidovima Damaštanskim, i proždrijeæe dvore Ven-Adadove.
28 Mawu a Yehova onena za Kedara ndi maufumu a ku Hazori, amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawagonjetsa ndi awa: “Nyamukani mukathire nkhondo ku Kedara. Kawonongeni anthu a kummawako.
Za Kidar i za carstva Asorska, koja razbi Navuhodonosor car Vavilonski, ovako veli Gospod: ustanite, idite na Kidar, i zatrite sinove istoène.
29 Landani matenti awo ndi nkhosa zawo, ndiye kuti, mutenge nsalu zawo ndi katundu wawo. Mutengenso ngamira zawo. Anthu adzafuwula kwa iwo kuti, ‘Kuli zoopsa mbali zonse!’
Uzeæe im šatore i stada, zavjese njihove i sudove njihove i kamile njihove oteæe, i vikaæe na njih strašno otsvuda.
30 “Thawani mofulumira! Kabisaleni mʼmakhwawa, inu anthu ku Hazori,” akutero Yehova. “Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni wakukonzerani chiwembu; wakonzekera zoti alimbane nanu.
Bježite, selite se daleko, zavrite se duboko, stanovnici Asorski, govori Gospod, jer je Navuhodonosor car Vavilonski namjerio namjeru protiv vas, i smislio misao protiv vas.
31 “Nyamukani kathireni nkhondo mtundu wa anthu umene uli pamtendere, umene ukukhala mosatekeseka,” akutero Yehova, “mzindawo ulibe zipata ngakhalenso mipiringidzo; anthu ake amakhala pa okha.
Ustanite, idite k narodu mirnome, koji živi bez straha, govori Gospod, koji nema vrata ni prijevornica, žive sami.
32 Ngamira zawo zidzafunkhidwa, ndipo makola a ngʼombe zawo adzalandidwa. Ndidzabalalitsira ku mphepo zinayi onse amene amameta tsitsi lawo chamʼmbali. Ndidzawagwetsera mavuto kuchokera ku mbali zonse,” akutero Yehova.
I kamile æe njihove biti plijen, i mnoštvo stoke njihove grabež, i rasijaæu ih u sve vjetrove, one što se s kraja strigu; i dovešæu pogibao na njih sa svijeh strana, govori Gospod.
33 “Hazori adzasanduka bwinja, malo okhalamo nkhandwe mpaka muyaya. Palibe munthu amene adzayendemo.”
I Asor æe biti stan zmajevski, pustinja dovijeka: niko se neæe ondje naseliti, niti æe se baviti u njemu sin èovjeèji.
34 Uthenga umene Yehova anapatsa mneneri Yeremiya wonena za Elamu, Zedekiya mfumu ya Yuda atangoyamba kulamulira ndi uwu:
Rijeè Gospodnja koja doðe Jeremiji proroku za Elam, u poèetku carovanja Sedekije cara Judina, govoreæi:
35 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani, ndidzathyola uta wa Elamu, umene uli chida chawo champhamvu.
Ovako veli Gospod nad vojskama: evo, ja æu slomiti luk Elamu, glavnu silu njegovu;
36 Ndidzabweretsa mphepo zinayi pa Elamu kuchokera ku zigawo zinayi zamlengalenga; ndidzawabalalitsira ku mphepo zinayi, ndipo sipadzakhala dziko limene anthu a ku Elamu sadzafikako.
I dovešæu na Elam èetiri vjetra s èetiri kraja nebesa, i u sve te vjetrove rasijaæu ih, tako da neæe biti naroda kuda neæe otiæi prognanici Elamski.
37 A ku Elamuwo ndidzachititsa mantha pamaso pa adani awo komanso pamaso pa iwo amene akufuna kuwononga moyo wawo. Ndidzawagwetsera mkwiyo wanga ndipo adzakhala pa mavuto,” akutero Yehova. “Ndidzawapirikitsa ndi lupanga mpaka nditawatheratu.
I uplašiæu Elamce pred neprijateljima njihovijem, i pred onima koji traže dušu njihovu; i pustiæu zlo na njih, žestinu gnjeva svojega, govori Gospod, i pustiæu za njima maè dokle ih ne zatrem.
38 Ndidzakhazika mpando wanga waufumu ku Elamu ndipo ndidzawononga mfumu yake pamodzi ndi akuluakulu ake,” akutero Yehova.
I namjestiæu prijesto svoj u Elamu, i istrijebiæu odande cara i knezove, govori Gospod.
39 “Komabe mʼtsogolomo ndidzabwezera anthu a ku Elamu dziko lawo,” akutero Yehova.
Ali u pošljednje vrijeme povratiæu roblje Elamsko, govori Gospod.

< Yeremiya 49 >