< Yeremiya 46 >

1 Yehova anamupatsa Yeremiya uthenga wonena za anthu a mitundu ina.
Rijeè Gospodnja koja doðe Jeremiji proroku za narode:
2 Kunena za Igupto: Yehova ananena za gulu lankhondo la Farao Neko mfumu ya ku Igupto limene Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni analigonjetsa ku Karikemesi ku mtsinje wa Yufurate mʼchaka cha chinayi cha Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda,
Za Misirce, za vojsku Faraona Nehaona cara Misirskoga, koja bijaše na reci Efratu kod Harkemisa, i razbi je Navuhodonosor car Vavilonski èetvrte godine Joakima sina Josijina cara Judina.
3 anati, “Konzani zishango zanu ndi malihawo, ndipo yambanipo kupita ku nkhondo!
Pripravite štite i štitiæe, i idite u boj;
4 Mangani akavalo, ndipo kwerani inu okwerapo! Khalani pa mzere mutavala zipewa! Nolani mikondo yanu, valani malaya anu ankhondo!
Prežite konje, i pojašite, konjici; postavite se sa šljemovima; utrite koplja, oblaèite se u oklope.
5 Yeremiya anati: Kodi ndikuona chiyani? Achita mantha akubwerera, ankhondo awo agonjetsedwa. Akuthawa mofulumirapo osayangʼananso mʼmbuyo, ndipo agwidwa ndi mantha ponseponse,” akutero Yehova.
Zašto ih vidim gdje se poplašiše, vraæaju se natrag, junaci njihovi polomiše se i bježe bez obzira? Strah je otsvuda, govori Gospod.
6 Waliwiro sangathe kuthawa ngakhale wankhondo wamphamvu sangathe kupulumuka. Akunka napunthwa ndi kugwa kumpoto kwa mtsinje wa Yufurate.
Da ne uteèe laki, niti se izbavi jaki; da se na sjeveru na brijegu rijeke Efrata spotaknu i padnu.
7 “Kodi ndani amene akukwera ngati Nailo, ngati mtsinje wa madzi amkokomo?
Ko je to što se diže kao potok, i vode mu se kolebaju kao rijeke?
8 Igupto akusefukira ngati Nailo, ngati mitsinje ya madzi amkokomo. Iye akunena kuti, ‘Ndidzadzuka ndi kuphimba dziko lapansi; ndidzawononga mizinda ndi anthu ake.’
Misir se diže kao potok i njegove se vode kolebaju kao rijeke; i veli: idem, pokriæu zemlju, zatræu grad i one koji žive u njemu.
9 Tiyeni, inu akavalo! Thamangani inu magaleta! Tulukani, inu ankhondo, ankhondo a ku Kusi ndi Puti amene mumanyamula zishango, ankhondo a ku Ludi amene mumaponya uta.
Izlazite, konji, bjesnite, kola; i neka izaðu junaci, Husi i Fudi, koji nose štitove, i Ludeji, koji nose i natežu luk.
10 Koma tsikulo ndi la Ambuye Yehova Wamphamvuzonse; tsiku lolipsira, lolipsira adani ake. Lupanga lake lidzawononga ndi kukhuta magazi, lidzaledzera ndi magazi. Pakuti Yehova, Yehova Wamphamvuzonse, adzapereka adani ake ngati nsembe mʼdziko la kumpoto mʼmbali mwa mtsinje wa Yufurate.
Jer je ovaj dan Gospodu Gospodu nad vojskama dan osvete, da se osveti neprijateljima svojim; maè æe ih proždrijeti i nasitiæe se i opiæe se krvlju njihovom; jer æe biti žrtva Gospoda Gospoda nad vojskama u zemlji sjevernoj na rijeci Efratu.
11 “Pita ku Giliyadi ukatenge mankhwala iwe namwali Igupto. Wayesayesa mankhwala ambiri koma osachira; palibe mankhwala okuchiritsa.
Izidi u Galad i uzmi balsama, djevojko kæeri Misirska; zaludu su ti mnogi lijekovi, neæeš se izlijeèiti.
12 Anthu a mitundu ina amva za manyazi ako; kulira kwako kwadzaza dziko lapansi. Ankhondo akunka nagwetsanagwetsana, onse awiri agwa pansi limodzi.”
Narodi èuše sramotu tvoju, i vike tvoje puna je zemlja, jer se spotièu junak o junaka, te obojica padaju.
13 Uthenga umene Yehova anapatsa mneneri Yeremiya wonena za kubwera kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni kudzathira nkhondo Igupto ndi uwu:
Rijeè koju reèe Gospod Jeremiji proroku o dolasku Navuhodonosora cara Vavilonskoga da potre zemlju Misirsku:
14 “Mulengeze ku Igupto. Mulengeze ku Migidoli. Mulengezenso ku Mefisi ndi ku Tapanesi. Muwawuze anthu akumeneko kuti, ‘Imani pamalo panu ndi kukhala okonzeka kudziteteza, chifukwa lupanga lidzawononga zonse zimene muli nazo.’
Javite u Misiru, i oglasite u Migdolu, oglasite i u Nofu i u Tafnesu, i recite: stani i pripravi se, jer maè proždrije što je oko tebe.
15 Chifukwa chiyani mulungu wanu wamphamvu uja Apisi wathawa? Iye sakanatha kulimba chifukwa Yehova anamugwetsa.
Zašto se povaljaše junaci tvoji? Ne stoje, jer ih Gospod obara.
16 Ankhondo anu apunthwa ndi kugwa. Aliyense akuwuza mnzake kuti, ‘Tiyeni tibwerere kwathu, ku dziko kumene tinabadwira, tithawe lupanga la adani athu.’
Èini, te se mnogi spotièu i padaju jedan na drugoga, i govore: ustani da se vratimo k narodu svojemu i na postojbinu svoju ispred maèa nasilnikova.
17 Kumeneku iwo adzafuwula kuti, ‘Farao, mfumu ya ku Igupto mupatseni dzina lakuti, Waphokoso, Wotaya mwayi wake.’
Vièu ondje: Faraon car Misirski propade, proðe mu rok.
18 “Pali Ine wamoyo,” ikutero Mfumu, imene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse, “wina adzabwera amene ali ngati Tabori phiri lopambana mapiri ena, ngati phiri la Karimeli loti njoo mʼmbali mwa nyanja.
Tako da sam ja živ, govori car, kojemu je ime Gospod nad vojskama; kao Tavor meðu gorama i kao Karmil na moru doæi æe.
19 Konzani katundu wanu wopita naye ku ukapolo inu anthu a ku Igupto, pakuti Mefisi adzasanduka chipululu ndipo adzakhala bwinja mopanda wokhalamo.
Spremi što ti treba da se seliš, stanovnice, kæeri Misirska; jer æe Nof opustjeti i spaliæe se da neæe niko živjeti u njemu.
20 “Igupto ali ngati mwana wangʼombe wokongola, koma chimphanga chikubwera kuchokera kumpoto kudzalimbana naye.
Misir je lijepa junica; ali pogibao ide, ide sa sjevera.
21 Ngakhale ankhondo aganyu amene ali naye ali ngati ana angʼombe onenepa. Nawonso abwerera mʼmbuyo, nathawa pamodzi. Palibe amene wachirimika. Ndithu, tsiku la tsoka lawafikira; ndiyo nthawi yowalanga.
I najamnici su njegovi usred njega kao teoci ugojeni, ali se i oni obrnuše i pobjegoše, ne ostaše, jer doðe na njih dan nesreæe njihove, vrijeme pohoðenja njihova.
22 Aigupto akuthawa ndi liwu lawo lili ngati la njoka yothawa pamene adani abwera ndi zida zawo, abwera ndi nkhwangwa ngati anthu odula mitengo.
Glas æe njihov iæi kao zmijinji, jer oni idu s vojskom i doæi æe sa sjekirama na nj kao oni koji sijeku drva.
23 Iwo adzadula nkhalango ya Igupto,” akutero Yehova, “ngakhale kuti ndi yowirira. Anthuwo ndi ochuluka kupambana dzombe, moti sangatheke kuwerengeka.
I oni æe posjeæi šumu njegovu, govori Gospod, ako joj i nema mjere, jer ih je više nego skakavaca i nema im broja.
24 Anthu a ku Igupto achita manyazi atengedwa ukapolo ndi anthu a kumpoto.”
Posrami se kæi Misirska, predana je u ruke narodu sjevernom.
25 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akunena kuti, “Ndili pafupi kulanga Amoni mulungu wa Tebesi. Ndidzalanganso Farao ndi Igupto pamodzi ndi milungu yake yonse, mafumu ake ndi onse amene amamukhulupirira.
Govori Gospod nad vojskama Bog Izrailjev: evo, ja æu pohoditi ljudstvo u Noji, i Faraona i Misir i bogove njegove i careve njegove, Faraona i sve koji se uzdaju u nj.
26 Ndidzawapereka kwa amene akufuna kuwapha, ndiye kuti kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni ndi atsogoleri ake ankhondo. Komabe, mʼtsogolomo Igupto adzakhalanso ndi anthu monga kale,” akutero Yehova.
I daæu ih u ruke onima koji traže dušu njihovu, u ruke Navuhodonosoru caru Vavilonskom i u ruke slugama njegovijem; a poslije æe biti naseljen kao prije, govori Gospod.
27 “Iwe mtumiki wanga Yakobo, usachite mantha; usataye mtima, iwe Israeli. Ndithu Ine ndidzakupulumutsa kuchokera ku mayiko akutali, ndidzapulumutsanso zidzukulu zako kuchokera ku mayiko kumene anapita nazo ku ukapolo. Yakobo adzabwerera ndipo adzakhala motakasuka ndi pa mtendere, ndipo palibenso wina amene adzamuopsa.
A ti se ne boj, slugo moj Jakove, i ne plaši se, Izrailju, jer evo ja æu te izbaviti iz daljne zemlje i sjeme tvoje iz zemlje ropstva njegova; i Jakov æe se vratiti i poèivaæe, i biæe miran i niko ga neæe plašiti.
28 Iwe mtumiki wanga Yakobo, usachite mantha, pakuti Ine ndili nawe,” akutero Yehova. “Ndidzawonongeratu mitundu yonse ya anthu a ku mayiko kumene ndakupirikitsira, Koma iwe sindidzakuwononga kotheratu. Ndidzakulanga iwe ndithu koma moyenerera; sindidzakulekerera osakulanga.”
Ti se ne boj, slugo moj Jakove, govori Gospod, jer sam ja s tobom; jer æu uèiniti kraj svijem narodima, u koje te prognah, ali tebi neæu uèiniti kraja, nego æu te pokarati s mjerom, a neæu te ostaviti sasvijem bez kara.

< Yeremiya 46 >