< Yeremiya 44 >

1 Uthenga umene Yeremiya analandira wonena za Ayuda onse amene ankakhala ku Igupto, ku mizinda ya Migidoli, Tapanesi ndi Mefisi, ndiponso ku Patirosi ndi uwu:
The word came to Jeremiah concerning all the Judeans who lived in the land of Egypt, the ones staying in Migdol, Tahpanhes, Memphis, and in Upper Egypt:
2 “Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Inu mwaona mavuto aakulu amene ndinawabweretsa pa Yerusalemu ndi mizinda yonse ya Yuda. Lero mizinda yonseyo yasanduka mabwinja, yopanda munthu wokhalamo.
“Yahweh of hosts, God of Israel, says, 'You yourselves have seen all the disasters that I brought on Jerusalem and all the cities of Judah. See, they are ruins today. There is no one to live in them.
3 Zimenezi zinachitika chifukwa cha zoyipa zomwe anachita. Iwo anaputa mkwiyo wanga pofukiza lubani ndi potumikira milungu ina imene iwo kapena inu ngakhalenso makolo anu sanayidziwe.
This is because of the wicked things they did to offend me by going to burn incense and to worship other gods. These were gods that neither they themselves, nor you, nor your ancestors knew.'
4 Kawirikawiri Ine ndakhala ndikutuma atumiki anga, aneneri, amene anati, ‘Musachite chinthu chonyansachi chimene Ine ndimadana nacho!’
So I repeatedly sent all of my servants the prophets to them. I sent them to say, 'Stop doing these abominable things that I hate.'
5 Koma iwo sanamvere kapena kulabadira; sanatembenuke kusiya zoyipa zawo kapena kuleka kufukiza lubani kwa milungu ina.
But they did not listen. They refused to pay attention or turn from their wickedness in burning incense to other gods.
6 Nʼchifukwa chake mkwiyo wanga unayaka ngati moto kutentha mizinda ya ku Yuda ndi misewu ya mu Yerusalemu ndi kuyisandutsa bwinja mpaka lero.
So my fury and my wrath were poured out and kindled a fire in the cities of Judah and the streets of Jerusalem. So they became ruins and devastations, as at this present day.'
7 “Ndiye tsopano Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akunena kuti, ‘Chifukwa chiyani mukufuna kudziwononga chotere? Kodi mukufuna kuti amuna, akazi, ana ndi makanda onse aphedwe ndi kuti mu Yuda musatsale ndi munthu mmodzi yemwe?
So now Yahweh, the God of hosts and the God of Israel, says this, 'Why are you doing great wickedness against yourselves? Why are you causing yourselves to be cut off from among Judah—men and women, children and babies? No remnant of you will be left.
8 Chifukwa chiyani mukuputa mkwiyo wanga popembedza mafano pofukiza lubani kwa milungu ina mʼdziko lino la Igupto mʼmene mukukhalamo. Kodi mukuchita zimenezi kuti mudziwononge nokha ndi kuti mudzisandutse chinthu choseketsa ndi chonyozeka pakati pa mitundu yonse ya dziko lapansi?
By your wickedness you have offended me with the deeds of your hands, by burning incense to other gods in the land of Egypt, where you have gone to live. You have gone there so that you will be destroyed, so that you will be a curse and a reproach among all the nations of the earth.
9 Kodi mwayiwala zoyipa zimene anachita makolo anu, mafumu a ku Yuda ndi akazi awo, ndiponso zoyipa zimene munachita inuyo ndi akazi anu mʼdziko la Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu?
Have you forgotten the wickedness committed by your ancestors and the wickedness committed by the kings of Judah and their wives? Have you forgotten the evil committed by yourselves and your wives in the land of Judah and the streets of Jerusalem?
10 Koma mpaka lero simunalape. Simunandilemekeze kapena kumvera malamulo anga amene ndinayikira inuyo ndi makolo anu.
To this day, they still are not humbled. They do not honor my law or decrees that I placed before them and their ancestors, nor do they walk in them.'
11 “Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akunena kuti, ‘Ine ndatsimikiza zobweretsa mavuto pa inu ndi kuwatheratu anthu a ku Yuda.
Therefore Yahweh of hosts, God of Israel, says this, 'See, I am about to set my face against you to bring disaster to you and to destroy all of Judah.
12 Ndidzatenga anthu otsala a ku Yuda amene atsimikiza zopita ku Igupto ndi kukakhala kumeneko. Onse adzathera ku Igupto. Adzaphedwa ndi lupanga kapena kufa ndi njala. Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, adzaphedwa ndi lupanga kapena kufa ndi njala. Adzasanduka chinthu chotembereredwa ndi chochititsa mantha, chinthu choseketsa ndi chonyozeka.
For I will take the remnant of Judah that has set out to go to the land of Egypt to live there. I will do this so that they will all perish in the land of Egypt. They will fall by sword and famine. From the least to the greatest they will perish by sword and famine. They will die and will become an object of swearing, cursing, reproaching, and a horrible thing.
13 Ndidzalanga Ayuda okhala ku Igupto ndi lupanga, njala ndi mliri, ngati mmene ndinalangira anthu a ku Yerusalemu.
For I will punish the people inhabiting the land of Egypt just as I punished Jerusalem with the sword, with famine, and with the plague,
14 Motero mwa anthu amene anapita ku Igupto palibe ndi mmodzi yemwe adzapulumuke, kapena kukhala ndi moyo, kapena kubwerera ku Yuda. Palibe amene adzabwerere kupatula othawa nkhondo.’”
so that none of the remnant of Judah who have gone to live in the land of Egypt will escape or survive or return to the land of Judah, to which they desire to return and live; and none of them will return except a few who escaped from there.'”
15 Tsono amuna onse amene anadziwa kuti akazi awo ankafukiza lubani kwa milungu ina, ndiponso akazi onse amene anali pamenepo, gulu lalikulu la anthu, pamodzi ndi anthu onse amene amakhala ku Patirosi mʼdziko la Igupto, anati kwa Yeremiya,
Then all the men who knew that their wives were burning incense to other gods, and all the women who were in the great assembly, and all the people who were living in Lower and Upper Egypt, answered Jeremiah.
16 “Ife sitimvera uthenga umene watiwuza mʼdzina la Yehova!
They said, “About the word that you have told us in Yahweh's name—we will not listen to you.
17 Koma tidzachitadi chilichonse chimene tinanena kuti tidzachita: Tidzafukiza lubani kwa mfumukazi yakumwamba ndipo tidzayipatsa nsembe yachakumwa ngati mmene tinkachitira ifeyo ndi makolo athu, mafumu athu ndi akuluakulu mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu. Nthawi imeneyo ife tinali ndi chakudya chochuluka ndipo tinali pabwino, sitimapeza mavuto.
For we will certainly do all the things that we said we would do—burn incense to the queen of heaven and pour out drink offerings to her just as we, our ancestors, our kings, and our leaders did in the cities of Judah and the streets of Jerusalem. Then we will be filled with food and will prosper, without experiencing any disaster.
18 Koma kuchokera nthawi imene tinasiya kufukiza lubani ndi kupereka chopereka cha chakumwa kwa mfumukazi yakumwamba, ifeyo takhala tikusowa zinthu ndipo takhala tikuphedwa ndi lupanga ndi kufa ndi njala.”
When we refrained from doing these things, not offering incense to the queen of heaven and not pouring out drink offerings to her, we were all suffering poverty and were dying by sword and famine.”
19 Akazi anawonjezera kunena kuti, “Pamene tinkafukiza lubani kwa mfumukazi yakumwamba ndi kuyipatsa chopereka cha chakumwa, kodi suja amuna athu ankavomereza mmene timayipangira mfumukazi yakumwambayo makeke abwino olembapo chinthunzi chake ndi kuyipatsa chopereka cha chakumwa?”
The women said, “When we were making incense offerings before the queen of heaven and pouring out drink offerings to her, was it against our husbands that we did these things, making cakes in her image and pouring out drink offerings to her?”
20 Yeremiya atamva kuyankha kumeneku anawawuza kuti,
Then Jeremiah said to all the people—to the men and women, and all the people who answered him—he proclaimed and said,
21 “Kodi mukuganiza kuti Yehova nʼkuyiwala kuti inuyo ndi makolo anu, mafumu anu ndi akuluakulu anu, ndiponso anthu onse, munkafukiza lubani kwa mafano a mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu?
“Did not Yahweh remember the incense that you burned in the cities of Judah and the streets of Jerusalem—you and your ancestors, your kings and leaders, and the people of the land? For Yahweh calls this to mind; it comes to his thoughts.
22 Ndiye Yehova sakanathanso kupirira ndi machitidwe anu ndi zonyansa zimene munkachita. Nʼchifukwa chake dziko lanu linasanduka chipululu, chinthu choopsa ndi chotembereredwa. Dziko lopandamo anthu monga zilili lero lino.
Then he was no longer able to bear it because of your wicked practices, because of the abominations that you did. Then your land became a desolation, a horror, and a curse so there was no longer an inhabitant as at this present day.
23 Mavuto awa akugwerani chifukwa munkafukiza lubani ndipo munkachimwira Yehova pokana kumvera mawu ake ndi kutsatira malamulo ndi malangizo ake.”
Because you burned incense and sinned against Yahweh, and because you would not listen to his voice, his law, his statutes, or his covenant decrees, this disaster against you has happened as at this present day.”
24 Kenaka Yeremiya anawuza anthu onse, makamaka akazi kuti, “Imvani mawu a Yehova, anthu onse a ku Yuda amene muli mu Igupto.
Then Jeremiah said to all the people and all the women, “Hear the word of Yahweh, all of Judah who are in the land of Egypt.
25 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Inu ndi akazi anu munalonjeza ndi pakamwa panu, ndipo malonjezowo mwakwaniritsa. Inu munanena kuti, ‘Tidzachita zimene tinalonjeza, kufukizira lubani mfumukazi yakumwamba ndi kuyipatsa chopereka cha zakumwa.’ Tsopano chitanitu zimene munalonjezazo! Kwaniritsani malumbiro anu. “Yambani, chitani zimene munalonjeza! Kwaniritsani malumbiro anu!
Yahweh of hosts, God of Israel, says this, 'You and your wives both have said with your mouths and carried out with your hands what you said, “We will certainly carry out the vows that we made to worship the queen of heaven, to pour out drink offerings to her.” Now fulfill your vows; carry them out.'
26 Koma imvani mawu a Yehova, inu Ayuda nonse amene mukukhala mu Igupto: Yehova akuti, ‘Ine ndikulumbira mʼdzina langa lopambana kuti palibe wochokera ku Yuda amene akukhala mu Igupto amene adzatchule dzina langa polumbira kuti, ‘Pali Ambuye Yehova wamoyo.’
So then, hear the word of Yahweh, all of Judah who are staying in the land of Egypt, 'See, I have sworn by my great name—says Yahweh. My name will no longer be called upon by the mouths of any of the men of Judah in all the land of Egypt, you who now say, “As the Lord Yahweh lives.”
27 Pakuti ndionetsetsa kuti ndiwachitire choyipa, osati chabwino. Anthu a ku Yuda amene akukhala ku Igupto adzaphedwa pa nkhondo. Ena adzafa ndi njala mpaka onse atatheratu.
See, I am watching over them for disaster and not for good. Every person of Judah in the land of Egypt will perish by sword and famine until they are all finished.
28 Amene adzapulumuke ku lupanga ndi kubwerera ku dziko la Yuda kuchokera ku Igupto adzakhala ochepa kwambiri. Choncho otsala onse a ku Yuda amene anapita kukakhala ku Igupto adzadziwa kuti mawu woona ndi ati, anga kapena awo.
Then the survivors of the sword will return from the land of Egypt to the land of Judah, only a small number of them. So all the remnant of Judah who went to the land of Egypt to live there will know whose word will stand—mine or theirs.
29 “Ine Yehova ndikukupatsani chizindikiro chakuti ndidzakulangani ku malo ano. Motero mudzadziwa kuti mawu anga akuti ndidzakulangani ndi woona.
This will be the sign for you—this is Yahweh's declaration—that I am setting against you in this place, so that you will know that my words will certainly attack you with disaster.'
30 Yehova akuti, ‘Ine ndidzamupereka Farao Hofira mfumu ya Igupto kwa adani ake amene akufuna kumupha, monga momwe ndinaperekera Zedekiya mfumu ya Yuda kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, mdani wake amene ankafuna kumupha.’”
Yahweh says this, 'Look, I am about to give Pharaoh Hophra king of Egypt into the hand of his enemies and into the hand of those who seek to kill him. It will the same as when I gave Zedekiah king of Judah into the hand of Nebuchadnezzar king of Babylon, his enemy who sought his life.'”

< Yeremiya 44 >