< Yeremiya 43 >

1 Yeremiya atatsiriza kuwawuza anthuwo mawu onse a Yehova Mulungu wawo, amene Yehova anamutuma kuti akawawuze,
Forsothe it was don, whanne Jeremye spekinge to the puple hadde fillid alle the wordis of the Lord God of hem, for whiche the Lord God of hem sente hym to hem, alle these wordis,
2 Azariya mwana wa Hosayia ndi Yohanani mwana wa Kareya pamodzi ndi anthu onse odzikuza anawuza Yeremiya kuti, “Ukunama iwe! Yehova Mulungu wathu sanakutume kuti unene kuti, ‘Musapite ku Igupto kukakhala kumeneko.’
Azarie, the sone of Josie, seide, and Johanna, the sone of Caree, and alle proude men, seiynge to Jeremye, Thou spekist a leesyng; oure Lord God sente not thee, and seide, Entre ye not in to Egipt, to dwelle there;
3 Koma ndi Baruki mwana wa Neriya amene akukulimbikitsa kuti utiletse zopita ku Igupto ndi kuti mʼmalo mwake tidzipereke mʼmanja mwa Ababuloni, kuti iwo atiphe kapena kutitenga ukapolo ku Babuloni.”
but Baruc, the sone of Nerie, stirith thee ayens vs, that he bitake vs in the hondis of Caldeis, that he sle vs, and make to be led ouer in to Babiloyne.
4 Motero Yohanani mwana wa Kareya ndi atsogoleri onse a ankhondo pamodzi ndi anthu onse sanamvere lamulo la Yehova loti akhale mʼdziko la Yuda.
And Johanna, the sone of Caree, and alle the princes of werriours, and al the puple, herden not the vois of the Lord, that thei dwellen in the lond of Juda.
5 Mʼmalo mwake, Yohanani mwana wa Kareya ndi atsogoleri onse a ankhondo anatenga anthu onse otsala a ku Yuda amene anabwera kudzakhala mʼdziko la Yuda kuchokera ku mayiko onse kumene anabalakirako.
But Johanna, the sone of Caree, and alle the princes of werriours, token alle of the remenauntis of Juda, that turneden ayen fro alle folkis, to whiche thei weren scatered bifore, that thei schulden dwelle in the lond of Juda;
6 Mʼgulu la anthu otengedwalo munali amuna onse, akazi ndi ana, ana aakazi a mfumu, ndiponso anthu amene Nebuzaradani mtsogoleri wa asilikali olonda mfumu anawasiya kwa Gedaliya mwana wa Ahikamu, mdzukulu wa Safani pamodzinso ndi mneneri Yeremiya ndi Baruki mwana wa Neriya.
thei token men, and wymmen, and litle children, and the douytris of the kyng, and ech persoone, whom Nabusardan, the prince of chyualrie, hadde left with Godolie, the sone of Aicham, sone of Saphan. And thei token Jeremye, the profete, and Baruc, the sone of Nerie,
7 Kotero anthuwo analowa mʼdziko la Igupto chifukwa anakana kumvera Yehova, nakafika ku Tapanesi.
and thei entriden in to the lond of Egipt; for thei obeieden not to the vois of the Lord, and thei camen `til to Taphnys.
8 Ndipo Yehova anayankhula ndi Yeremiya ku Tapanesi kuti,
And the word of the Lord was maad to Jeremye in Taphnys,
9 “Tenga miyala inayi yayikulu ndipo uyikwirire mʼdothi pa chiwundo cha polowera ku nyumba yaufumu ya Farao ku Tapanesi. Uchite zimenezi Ayuda onse akuona.
and seide, Take in thin hond grete stoonys, and hide thou tho in a denne, which is vndur the wal of tiil stoon, in the yate of the hous of Farao, in Taphnys, while alle Jewis seen.
10 Ndipo uwawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Ndidzayitana mtumiki wanga Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, ndipo adzakhazika mpando wake waufumu pa miyala imene ndayikwirira apayi. Iye adzafunyulula tenti yake yaufumu pa miyala imeneyi.
And thou schalt seie to hem, The Lord of oostis, God of Israel, seith these thingis, Lo! Y schal sende, and Y schal take Nabugodonosor, my seruaunt, the kyng of Babiloyne; and Y schal sette his trone on these stoonys, whiche Y hidde; and he schal sette his seete on tho stoonys.
11 Iye adzabwera kudzathira nkhondo Igupto. Iwo oyenera kufa ndi mliri adzafa ndi mliri, iwo oyenera kutengedwa ukapolo adzatengedwa ukapolo, ndipo iwo oyenera kufa ndi lupanga adzafa ndi lupanga.
And he schal come, and smyte the lond of Egipt, whiche in deth in to deth, and whiche in caitiftee in to caitiftee, and whiche in swerd in to swerd.
12 Adzayatsa moto mʼnyumba zopembedzera milungu ya Igupto. Adzayeretsa dziko la Igupto monga momwe mʼbusa amayeretsera chovala chake pochotsamo nsabwe. Pambuyo pake adzachoka mʼdziko la Igupto mwa mtendere.
And he schal kindle fier in the templis of goddis of Egipt, and he schal brenne tho templis, and schal lede hem prisoneris; and the lond of Egipt schal be wlappid, as a scheepherd is wlappid in his mentil; and he schal go out fro thennus in pees.
13 Ku Iguptoko adzagwetsa zipilala zachipembedzo za ku nyumba yopembedzera mulungu wa dzuwa. Adzatentha ndi moto nyumba za milungu ya ku Igupto.’”
And he schal al to-breke the ymagis of the hous of the sunne, that ben in the lond of Egipt; and he schal brenne in fier the templis of the goddis of Egipt.

< Yeremiya 43 >