< Yeremiya 38 >

1 Sefatiya mwana wa Matani, Gedaliya mwana wa Pasi-Huri, Yukali mwana wa Selemiya, ndi Pasi-Huri mwana wa Malikiya anamva zimene Yeremiya ankawuza anthu onse kuti,
A Sefatija sin Matanov i Godolija sin Pashorov i Juhal sin Selemijin i Pashor sin Malhijin èuše rijeèi koje govori Jeremija svemu narodu rekavši:
2 “Yehova akuti, ‘Aliyense amene akhale mu mzinda muno adzafa ndi nkhondo njala kapena mliri. Koma aliyense amene atatuluke kukadzipereka kwa Ababuloni adzapulumutsa moyo wake; iyeyo adzakhala ndi moyo.
Ovako veli Gospod: ko ostane u tom gradu, poginuæe od maèa, od gladi ili od pomora; a ko otide ka Haldejcima, ostaæe živ, i duša æe mu njegova biti mjesto plijena, i biæe živ.
3 Mzinda uno udzaperekedwa ndithu kwa gulu lankhondo la mfumu ya ku Babuloni, amene adzawulande.’”
Ovako veli Gospod: doista æe taj grad biti predan u ruke vojsci cara Vavilonskoga, i uzeæe ga.
4 Tsono akuluakuluwo anawuza mfumu kuti, “Munthu uyu ayenera kuphedwa. Iye akutayitsa mtima asilikali pamodzi ndi anthu onse amene atsala mu mzinda muno, chifukwa cha zimene akuwawuza. Munthu ameneyu sakufunira zabwino anthuwa koma chiwonongeko chawo.”
I rekoše knezovi caru: da se pogubi taj èovjek, jer on oslabljava ruke vojnicima koji ostaše u ovom gradu, i ruke svemu narodu govoreæi im take rijeèi, jer taj èovjek ne traži dobra ovom narodu nego zlo.
5 Mfumu Zedekiya anayankha kuti, “Munthuyu ali mʼmanja mwanu. Ine sindingakuletseni chimene mukufuna kumuchitira.”
A car Sedekija reèe: eto, u vašim je rukama; jer car ne može ništa suprot vama.
6 Choncho iwo anatenga Yeremiya nakamuponya mʼchitsime cha Malikiya, mwana wa mfumu, chimene chinali mʼbwalo la alonda. Iwo anamutsitsira mʼdzenjemo ndi chingwe. Munalibe madzi koma matope okhaokha, ndipo Yeremiya anamira mʼmatopewo.
Tada uzeše Jeremiju i baciše ga u jamu Malhije sina Amelehova, koja bijaše u trijemu od tamnice, i spustiše Jeremiju o užima; a u jami ne bješe vode, nego glib, i Jeremija se uvali u glib.
7 Koma Ebedi-Meleki, Mkusi, mmodzi mwa anthu ofulidwa ogwira ntchito mʼnyumba ya mfumu, anamva kuti Yeremiya anamuponya mʼchitsime. Nthawi imeneyo nʼkuti mfumu ili ku chipata cha Benjamini.
Ali kad èu Avdemeleh Etiopljanin, dvoranin, koji bijaše u dvoru carevu, da su metnuli Jeremiju u onu jamu, a car sjeðaše na vratima Venijaminovijem,
8 Ebedi-Meleki anatuluka ku nyumba ya mfumu kukayiwuza kuti,
Izide Avdemeleh iz dvora careva i reèe caru govoreæi:
9 “Mbuye wanga mfumu, zimene anthu awa amuchitira mneneri Yeremiya ndi zoyipa kwambiri. Iwo amuponya mʼchitsime, ndipo adzafa ndi njala chifukwa buledi watha mu mzinda muno.”
Care gospodaru moj, zlo uèiniše ti ljudi u svemu što uèiniše Jeremiji proroku bacivši ga u jamu, jer bi i ondje gdje je bio od gladi umro, jer nema više hljeba u gradu.
10 Tsono mfumu inalamula Ebedi-Meleki, Mkusi, kuti, “Tenga anthu makumi atatu, ndipo mukamutulutse mʼchitsimemo mneneri Yeremiya asanafe.”
Zato car zapovjedi Avdemelehu Etiopljaninu govoreæi: uzmi odavde trideset ljudi i izvadi Jeremiju proroka iz jame dok nije umro.
11 Pamenepo Ebedi-Meleki anatenga anthuwo, napita nawo ku nyumba ya mfumu ya pansi pa chipinda chosungiramo chuma. Kumeneko anakatengako sanza ndipo anatsitsira sanzazo ndi chingwe mʼchitsime mʼmene munali Yeremiya.
Tada uze Avdemeleh ljude, i doðe u dom carev pod riznicu, i uze odande iznošenijeh haljina i starijeh rita, i spusti ih Jeremiji u jamu o užima.
12 Ebedi-Meleki, Mkusi, anawuza Yeremiya kuti, “Ika sanzazo mkwapa mwako kuti zingwe zingakupweteke.” Yeremiya anachitadi zimenezi,
I reèe Avdemeleh Etiopljanin Jeremiji: podmetni te stare haljine i rite pod pazuha ispod uža. I uèini Jeremija tako.
13 ndipo anamukoka ndi zingwe ndi kumutulutsa mʼchitsimecho. Ndipo Yeremiya anakhalabe ku bwalo la alonda.
I izvukoše Jeremiju na užima i izvadiše ga iz jame; i osta Jeremija u trijemu od tamnice.
14 Tsiku lina Mfumu Zedekiya anayitana mneneri Yeremiya ndipo anabwera naye ku chipata chachitatu cha Nyumba ya Yehova. Mfumu inawuza Yeremiya kuti, “Ndikufuna kukufunsa kanthu kena, ndipo usandibisire chilichonse.”
Potom car Sedekija posla po Jeremiju proroka, te ga dovedoše preda nj u treæi ulazak koji bijaše u domu Gospodnjem; i reèe car Jeremiji: zapitaæu te nešto, nemoj mi zatajiti.
15 Yeremiya anati kwa Zedekiya, “Ndikakuyankhani, kodi simundipha? Ngakhaletu ine nditakulangizani, inu simudzandimvera.”
A Jeremija reèe Sedekiji: da ti kažem, neæeš li me pogubiti? a da te svjetujem, neæeš me poslušati.
16 Koma Mfumu Zedekiya mwachinsinsi inalumbira kwa Yeremiya kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene amatipatsa moyo, sindidzakupha ngakhalenso kukupereka kwa amene akufuna kukuphawa.”
Tada se car Sedekija zakle Jeremiji nasamo govoreæi: tako da je živ Gospod, koji nam je stvorio ovu dušu, neæu te pogubiti niti æu te dati u ruke ljudima koji traže dušu tvoju.
17 Pamenepo Yeremiya anati kwa Zedekiya, “Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ngati mutuluka kukadzipereka kwa ankhondo a mfumu ya ku Babuloni, mudzakhala ndi moyo ndipo mzinda uno sadzawutentha, inu pamodzi ndi banja lanu mudzakhala ndi moyo.
Tada Jeremija reèe Sedekiji: ovako veli Gospod Bog nad vojskama, Bog Izrailjev: ako otideš ka knezovima cara Vavilonskoga, živa æe ostati duša tvoja, i grad ovaj neæe izgorjeti ognjem, i tako æeš ostati u životu ti i dom tvoj.
18 Koma ngati simutuluka kukadzipereka kwa ankhondo a mfumu ya ku Babuloni, mzinda uno udzaperekedwa kwa Ababuloni ndipo adzawutentha; inuyo simudzapulumuka mʼdzanja mwawo.’”
Ako li ne otideš ka knezovima cara Vavilonskoga, ovaj æe grad biti predan u ruke Haldejcima, koji æe ga spaliti ognjem, i ti neæeš uteæi iz ruku njihovijeh.
19 Mfumu Zedekiya inati kwa Yeremiya, “Ine ndikuopa Ayuda amene anathawira kale kwa Ababuloni, pakuti mwina Ababuloniwo adzandipereka kwa Ayudawo ndipo iwowo adzandizunza.”
A car Sedekija reèe Jeremiji: ja se bojim Judejaca koji su prebjegli ka Haldejcima, da me ne predadu u njihove ruke, te æe mi se narugati.
20 Yeremiya anayankha kuti, “Ngati mumvera Yehova ndi kuchita zimene ndakuwuzani, ndiye kuti zinthu zidzakuyenderani bwino. Inu simudzaphedwa.
A Jeremija reèe: neæe te predati; poslušaj glas Gospodnji, koji ti ja govorim, i dobro æe ti biti i živa æe biti tvoja duša.
21 Koma mukakana kudzipereka, chimene Yehova wandiwululira ndi ichi:
Ako li neæeš da izideš, ovo je što mi pokaza Gospod:
22 Akazi onse amene atsala mʼnyumba ya mfumu ya Yuda adzaperekedwa kwa akuluakulu a mfumu ya ku Babuloni. Akazi amenewo adzakuwuzani kuti, “‘Abwenzi ako okhulupirika aja anakusokeretsa, ndipo anakugonjetsa. Poti tsopano miyendo yako yazama mʼmatope; abwenzi ako aja akusiya.’
Gle, sve žene koje su ostale u domu cara Judina, odvešæe se ka knezovima cara Vavilonskoga, i one æe reæi: nagovoriše te i prevariše te prijatelji tvoji; noge ti se uvališe u glib, a oni se povukoše natrag.
23 “Akazi pamodzi ndi ana anu adzaperekedwa kwa Ababuloni. Inuyo simudzapulumuka mʼmanja mwawo koma mfumu ya ku Babuloni idzakugwirani; mzinda uno adzawutentha.”
Sve žene tvoje i sinovi tvoji odvešæe se Haldejcima, i ti neæeš uteæi iz ruku njihovijeh; nego æeš dopasti u ruke caru Vavilonskom, i ovaj æe grad izgorjeti ognjem.
24 Pamenepo Zedekiya anati kwa Yeremiya, “Usawuze munthu wina aliyense zimene takambiranazi, ukatero udzaphedwa.
Tada reèe Sedekija Jeremiji: niko da ne dozna za te rijeèi, da ne pogineš.
25 Akuluakulu akamva kuti ndinayankhula nawe ndipo akabwera kwa iwe nʼkudzakufunsa kuti, ‘Tiwuze zimene unanena kwa mfumu ndi zimene mfumu inanena kwa iwe; usatibisire, ukatero tidzakupha,’
Ako li knezovi èuvši da sam govorio s tobom doðu k tebi i reku ti: kaži nam šta si govorio caru, nemoj tajiti od nas, pa te neæemo pogubiti, i šta je car tebi govorio?
26 udzawawuze kuti, ‘Ine ndimapempha mfumu kuti isandibwezerenso ku nyumba ya Yonatani kuti ndikafere kumeneko.’”
Reci im: ja pripadoh k caru moleæi se da me ne pošlje natrag u dom Jonatanov da umrem ondje.
27 Akuluakulu onse anabweradi kwa Yeremiya kudzamufunsa. Iye anawayankha monga momwe mfumu inamulamula. Choncho palibe amene ananenanso kanthu, pakuti palibe amene anamva zomwe anakambirana ndi mfumu.
I doðoše svi knezovi k Jeremiji i pitaše ga; a on im odgovori sasvijem kako mu zapovjedi car. I okaniše ga se, jer ne doznaše ništa od toga.
28 Ndipo Yeremiya anakhalabe mʼbwalo la alonda mpaka tsiku limene mzinda wa Yerusalemu unalandidwa.
A Jeremija osta u trijemu od tamnice do dana kad uzeše Jerusalim; i on bijaše ondje kad uzeše Jerusalim.

< Yeremiya 38 >