< Yeremiya 33 >

1 Yeremiya akanali mʼndende mʼbwalo la alonda, Yehova anayankhula nayenso kachiwiri nati:
I doðe rijeè Gospodnja Jeremiji drugi put dok još bijaše zatvoren u trijemu od tamnice, govoreæi:
2 “Yehova amene analenga dziko lapansi, kuliwumba ndi kulikhazikitsa; amene dzina lake ndi Yehova, akuti,
Ovako veli Gospod koji èini to, Gospod koji udešava i potvrðuje to, kojemu je ime Gospod:
3 ‘Unditame mopemba ndipo ndidzakuyankha. Ndidzakuwuza zinsinsi zazikulu zimene suzidziwa.’
Zovi me, i odazvaæu ti se, i kazaæu ti velike i tajne stvari, za koje ne znaš.
4 Yehova Mulungu wa Israeli akunenapo pa za nyumba za mu mzinda muno ndiponso pa za nyumba za mafumu a Yuda. Zidzagwetsedwa, ndipo palibe chifukwa cholimbana ndi mitumbira ya nkhondo ya Ababuloni.
Jer ovako veli Gospod Bog Izrailjev za domove ovoga grada i za domove careva Judinijeh koji æe se razvaliti opkopima i maèem,
5 Ababuloni akubwera kudzawuthira nkhondo mzindawu ndipo nyumba zake zidzadzaza ndi mitembo ya anthu amene ndidzawapha mokwiya ndi mwaukali. Ndawufulatira mzinda uno chifukwa cha zoyipa zake zonse.
I za one koji doðoše da se biju s Haldejcima, ali æe ih napuniti mrtvijem tjelesima ljudi koje æu pobiti u gnjevu svom i u jarosti svojoj odvrativ lice svoje od toga grada za svu zloæu njihovu:
6 “‘Pambuyo pake mzindawu ndidzawupatsanso moyo ndi kuwuchiritsa; ndidzachiritsa anthu anga ndi kuwapatsa chitetezo ndi mtendere weniweni.
Evo, ja æu ga iscijeliti i zdravlje mu dati, iscijeliæu ih i pokazaæu im obilje mira, postojanoga mira.
7 Ndidzawakhazikanso Ayuda ndi Aisraeli ku dziko lawo, ndipo ndidzawabwezera monga mmene analili poyamba.
Jer æu povratiti roblje Judino i roblje Izrailjevo, i sazidaæu ih kao prije.
8 Ndidzawayeretsa pochotsa zoyipa zonse zimene anandichitira, ndiponso ndidzawakhululukira machimo onse amene anachita pondiwukira.
I oèistiæu ih od svakoga bezakonja njihova kojim mi sagriješiše, i oprostiæu im sva bezakonja njihova, kojima mi sagriješiše i kojima se odmetnuše od mene.
9 Mzinda wa Yerusalemu udzandipatsa chimwemwe, chiyamiko ndi ulemerero. Anthu a mitundu yonse adzanditamanda akadzamva za zabwino zonse zimene ndawuchitira mzindawu. Iwo adzachita mantha ndi kunjenjemera poona madalitso ochuluka ndi mtendere zimene ndapereka kwa mzinda umenewu.’
I biæe mi milo ime i hvala i slava u svijeh naroda na zemlji koji æe èuti za sve dobro što æu im uèiniti, i uplašiæe se i drktaæe radi svega dobra i radi svega mira što æu im ja dati.
10 “Yehova akuti, ‘Inu mumanena za malo ano kuti ndi bwinja,’ malo opandamo anthu kapena nyama. Komatu mizinda ya Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu mʼmene tsopano muli zii mudzamvekanso
Ovako veli Gospod: na ovom mjestu, za koje vi velite da je pusto i nema u njemu ni èovjeka ni živinèeta, u gradovima Judinijem i po ulicama Jerusalimskim opustjelim da nema èovjeka ni stanovnika ni živinèeta, opet æe se èuti
11 mfuwu wachimwemwe ndi mawu achisangalalo, mawu a mkwatibwi ndi mkwati. Mʼnyumba ya Mulungu mudzamvekanso nyimbo za anthu amene akudzapereka nsembe zothokoza Yehova. Azidzati, “Yamikani Yehova Wamphamvuzonse, popeza Iye ndi wabwino; pakuti chifundo chake nʼchamuyaya.” Pakuti ndidzabwezeretsa zinthu zabwino za dziko lino monga zinalili poyamba, akutero Yehova.
Glas radostan i glas veseo, glas ženikov i glas nevjestin, glas onijeh koji æe govoriti: slavite Gospoda nad vojskama, jer je dobar Gospod, jer je dovijeka milost njegova; koji æe prinositi prinose zahvalne u domu Gospodnjem; jer æu vratiti roblje ove zemlje kao što je bilo prije, govori Gospod.
12 “Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Malo ano, a chipululu ndi wopanda anthu kapena nyama, mʼmizinda yake yonse mudzakhala msipu umene abusa adzadyetserako nkhosa zawo.
Ovako veli Gospod nad vojskama: na ovom mjestu pustom, gdje nema èovjeka ni živinèeta, i u svijem gradovima njegovijem opet æe biti torovi pastirski da poèivaju stada.
13 Ku mizinda ya kumapiri, ya kuchigwa, ya ku Negevi, ya ku dera la Benjamini, ku dziko lozungulira Yerusalemu, ndi ku mizinda ya Yuda, nkhosa zidzadutsanso pamaso pa munthu woziwerenga,’ akutero Yehova.
U gradovima po gorama, u gradovima po ravnici i u gradovima južnijem i u zemlji Venijaminovoj i oko Jerusalima i po gradovima Judinijem opet æe prolaziti stada ispod ruku brojaèevijeh, veli Gospod.
14 “‘Taonani masiku akubwera,’ akutero Yehova, ‘pamene ndidzachitadi zokoma zimene ndinalonjeza Aisraeli ndi nyumba ya Yuda.
Evo, idu dani, govori Gospod, kad æu izvršiti ovu dobru rijeè koju rekoh za dom Izrailjev i za dom Judin.
15 “‘Mʼmasiku amenewo ndi pa nthawi imeneyo ndidzaphukitsa Nthambi yolungama kuchokera ku banja la Davide; munthuyo adzachita zolungama ndi zabwino mʼdziko.
U te dane i u to vrijeme uèiniæu da proklija Davidu klica prava, koja æe èiniti sud i pravdu na zemlji.
16 Mʼmasiku amenewo Yuda adzapulumuka ndipo Yerusalemu adzakhala mwamtendere. Dzina limene mzindawu udzadziwike nalo ndi ili: Yehova Chilungamo Chathu.’
U te dane spašæe se Juda, i Jerusalim æe stajati bez straha, i zvaæe se: Gospod pravda naša.
17 Yehova akunena kuti, ‘Davide sadzasowa mdzukulu wolowa mʼmalo mwake pa mpando waufumu wa Israeli,
Jer ovako veli Gospod: neæe nestati Davidu èovjeka koji bi sjedio na prijestolu doma Izrailjeva.
18 ngakhale ansembe, amene ndi Alevi, sadzasowanso munthu woyima pamaso panga nthawi zonse wopereka nsembe zopsereza, nsembe zaufa ndi nsembe zina.’”
Ni sveštenicima Levitima neæe nestati preda mnom èovjeka koji bi prinosio žrtvu paljenicu i palio dar i klao žrtvu dovijeka.
19 Yehova anawuza Yeremiya kuti:
Potom doðe rijeè Gospodnja Jeremiji govoreæi:
20 Mawu anga ndi awa. Ine ndinachita pangano ndi usana ndi usiku kuti zizibwera pa nthawi yake. Pangano limeneli inu simungaliphwanye.
Ovako veli Gospod: ako možete ukinuti zavjet moj za dan i zavjet moj za noæ da ne bude dana ni noæi na vrijeme,
21 Ndinachitanso pangano ndi Davide, mtumiki wanga kuti nthawi zonse adzakhala ndi mdzukulu wodzakhala pa mpando wake waufumu. Ndinachitanso pangano ndi Alevi kuti iwonso adzanditumikira nthawi zonse. Mapangano amenewa sadzaphwanyidwa nthawi zonse.
Onda æe se ukinuti i moj zavjet s Davidom slugom mojim, da nema sina koji bi carovao na prijestolu njegovu, i s Levitima sveštenicima slugama mojim.
22 Ndidzachulukitsa ngati nyenyezi zamlengalenga ndiponso ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja zidzukulu za mtumiki wanga Davide ndiponso za Alevi amene amanditumikira Ine.
Kao što se ne može izbrojiti vojska nebeska ni izmjeriti pijesak morski, tako æu umnožiti sjeme Davida sluge svojega i Levita sluga svojih.
23 Yehova anafunsa Yeremiya kuti,
Opet doðe rijeè Gospodnja Jeremiji govoreæi:
24 “Kodi sunamve mmene anthu ena akumanenera kuti, ‘Yehova wakana maufumu awiriwa amene Iye anawasankha.’ Kotero anthuwo akunyoza anthu anga ndipo sakuwayesanso mtundu wa anthu.
Nijesi li vidio što reèe taj narod govoreæi: dvije porodice, koje bješe izabrao Gospod, odbaci ih? I ruže moj narod kao da veæ nije narod pred njima.
25 ‘Koma Ine Yehova ndinachita pangano ndi usana ndi usiku. Ndinakhazikitsanso malamulo oyendetsa dziko lakumwamba ndi dziko lapansi,
Ovako veli Gospod: ako nijesam postavio zavjeta svojega za dan i za noæ i uredbe nebesima i zemlji,
26 monga ndachita zimenezi motsimikiza, choncho ndidzasunga pangano limene ndinachita ndi zidzukulu za Yakobo ndi Davide mtumiki wanga. Ndidzasankha mmodzi mwa ana a Davide kuti alamulire zidzukulu za Abrahamu, Isake ndi Yakobo. Komatu ndidzawamvera chifundo ndi kuwakhazikanso pabwino.’”
Onda æu i sjeme Jakovljevo i Davida sluge svojega odbaciti da ne uzimam od sjemena njegova onijeh koji æe vladati sjemenom Avramovijem, Isakovijem i Jakovljevijem; jer æu povratiti roblje njihovo i smilovaæu se na njih.

< Yeremiya 33 >