< Yeremiya 25 >

1 Yehova anayankhula ndi Yeremiya za anthu onse a ku Yuda mʼchaka chachinayi cha ufumu wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya ku Yuda, chimene chinali chaka choyamba cha ufumu wa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni.
Rijeè koja doðe Jeremiji za sav narod Judin èetvrte godine Joakima sina Josijina cara Judina, a to je prva godina Navuhodonosora cara Vavilonskoga,
2 Choncho mneneri Yeremiya anawuza anthu onse a ku Yuda pamodzi ndi onse amene amakhala mu Yerusalemu kuti:
Koju reèe Jeremija prorok svemu narodu Judinu i svijem stanovnicima Jerusalimskim, govoreæi:
3 Kwa zaka 23, kuyambira chaka cha 13 cha ufumu wa Yosiya mwana wa Amoni mfumu ya ku Yuda mpaka lero lino, Yehova wakhala akundipatsa mauthenga ake ndipo ine ndakhala ndikuyankhula ndi inu kawirikawiri, koma inu simunamvere.
Od trinaeste godine Josije sina Amonova cara Judina do danas, za ove dvadeset i tri godine, dolazi mi rijeè Gospodnja i govorih vam zarana jednako, ali ne poslušaste.
4 Ndipo ngakhale Yehova kawirikawiri wakhala akukutumizirani atumiki ake onse, aneneri, inuyo simunamvere kapena kutchera khutu.
I sla vam Gospod sve sluge svoje proroke zarana jednako, ali ne poslušaste, niti prignuste uha svojega da biste èuli.
5 Aneneriwo ankanena kuti, “Ngati aliyense wa inu abwerere, kusiya njira zake zoyipa ndi machitidwe ake oyipa, ndiye kuti mudzakhala mʼdziko limene Yehova anapereka kwa makolo anu kwamuyaya.
I govorahu: vratite se svaki sa svojega puta zloga i od zloæe djela svojih, pa æete ostati u zemlji koju dade Gospod vama i ocima vašim od vijeka do vijeka.
6 Musatsatire milungu ina nʼkuyitumikira ndi kuyipembedza. Musapute mkwiyo wanga ndi mafano amene mwapanga ndi manja anu. Mukatero Ine sindidzakuwonongani.
I ne idite za drugim bogovima da im služite i da im se klanjate, i ne gnjevite me djelom ruku svojih, i neæu vam uèiniti zla.
7 “Koma inu simunandimvere,” akutero Yehova, “ndipo munaputa mkwiyo wanga ndi mafano amene munapanga ndi manja anu. Choncho munadziwononga nokha.”
Ali me ne poslušaste, govori Gospod, nego me gnjeviste djelom ruku svojih na svoje zlo.
8 Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Chifukwa simunamvere mawu anga,
Zato ovako veli Gospod nad vojskama: što ne poslušaste mojih rijeèi,
9 ndidzayitana mafuko onse akumpoto, pamodzi ndi mtumiki wanga Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni,” akutero Yehova, “ndipo adzathira nkhondo dziko lino ndi anthu ake pamodzi ndi mitundu yonse ya anthu ozungulira dzikoli. Ndidzawawononga kwathunthu ndi kuwasandutsa chinthu chochititsa mantha ndi chonyozeka, mpaka muyaya.
Evo, ja æu poslati po sve narode sjeverne, govori Gospod, i po Navuhodonosora cara Vavilonskoga slugu svojega, i dovešæu ih na tu zemlju i na stanovnike njezine, i na sve te narode okolne, koje æu zatrti, i uèiniæu da budu èudo i potsmijeh i pustoš vjeèna.
10 Ndidzathetsa mfuwu wachimwemwe ndi wachisangalalo, mawu a mkwati ndi mkwatibwi, phokoso la mphero ndi kuwala kwa nyale.
I uèiniæu da nestane meðu njima glasa radosna i glasa vesela, glasa ženikova i glasa nevjestina, lupe od žrvanja i svjetlosti od žiška.
11 Dziko lonse lidzakhala bwinja ndi chipululu, ndipo mitundu ina idzatumikira mfumu ya ku Babuloni kwa 70.
I sva æe ta zemlja biti pustoš i èudo, i ti æe narodi služiti caru Vavilonskom sedamdeset godina.
12 “Koma zaka 70 zikadzatha, ndidzalanga mfumu ya ku Babuloni pamodzi ndi anthu ake, chifukwa cha zolakwa zawo,” akutero Yehova, “ndipo dziko lawo lidzakhala chipululu mpaka muyaya.
A kad se navrši sedamdeset godina, onda æu pohoditi cara Vavilonskoga i onaj narod, govori Gospod, za bezakonje njihovo, i zemlju Haldejsku, i obratiæu je u pustoš vjeènu.
13 Ndidzachita zinthu zonse zimene ndinayankhula zotsutsa dzikolo, zonse zimene zalembedwa mʼbuku lino, ndiponso zonse zimene Yeremiya analosera zotsutsa anthu amenewa.
I pustiæu na tu zemlju sve što sam govorio o njoj, sve što je napisano u ovoj knjizi, što prorokova Jeremija za sve narode.
14 Iwo eni adzakhala akapolo a anthu a mitundu yochuluka ndi mafumu amphamvu. Ndidzawabwezera molingana ndi zochita zawo ndi ntchito za manja awo.”
Jer æe veliki narodi i silni carevi i njih pokoriti; tada æu im platiti po djelima njihovijem i po onom što su èinili rukama svojim.
15 Yehova, Mulungu wa Israeli, anandiwuza kuti, “Tenga chikho ichi chodzaza ndi vinyo wa ukali wanga, ndipo ukamwetse anthu a mitundu yonse kumene ndikukutuma.
Jer ovako mi reèe Gospod Bog Izrailjev: uzmi iz moje ruke èašu vina, ovoga gnjeva, i napoj iz nje sve narode ka kojima te ja pošljem,
16 Akadzamwa adzayamba kudzandira ndi kuchita misala chifukwa cha nkhondo imene ndikuyitumiza pakati pawo.”
Neka piju i smetu se i polude od oštroga maèa koji æu ja poslati meðu njih.
17 Choncho ine ndinatenga chikhocho mʼdzanja la Yehova ndipo ndinamwetsa mitundu yonse ya anthu kumene Iye ananditumako:
I uzeh èašu iz ruke Gospodu, i napojih sve te narode, ka kojima me posla Gospod:
18 Anandituma ku Yerusalemu ndi ku mizinda ya Yuda, kwa mafumu ake ndi nduna zake kuti ndikawasandutse ngati bwinja ndi chinthu chochititsa mantha ndi chonyozeka ndiponso chotembereredwa, monga mmene alili lero lino.
Jerusalim i gradove Judine i careve njegove i knezove njegove, da budu pustoš i èudo i potsmijeh i uklin, kao što je danas,
19 Ananditumanso kwa Farao, mfumu ya ku Igupto, kwa atumiki ake, nduna zake ndi kwa anthu ake onse,
Faraona cara Misirskoga i sluge njegove i knezove njegove i sav narod njegov,
20 ndi kwa anthu ena onse a mitundu yachilendo; mafumu onse a ku Uzi; mafumu onse a Afilisti, a ku Asikeloni, ku Gaza, ku Ekroni ndiponso kwa anthu a ku chigwa chotsala cha Asidodi;
I svu mješavinu, i sve careve zemlje Uza, sve careve zemlje Filistejske, i Askalon i Gazu i Akaron i ostatak od Azota,
21 Edomu, Mowabu ndi Amoni.
Edomce i Moavce i sinove Amonove,
22 Ananditumanso kwa mafumu onse a ku Turo ndi ku Sidoni; kwa mafumu a kutsidya la nyanja;
I sve careve Tirske i sve careve Sidonske i careve na ostrvima preko mora,
23 ku Dedani, ku Tema, ku Buzi ndi kwa onse ometa chamʼmbali.
Dedana i Temu i Vuza, i sve koji se s kraja strigu,
24 Ananditumanso kwa mafumu onse a ku Arabiya ndi mafumu onse a anthu achilendo amene amakhala mʼchipululu.
I sve careve Arapske i sve careve od mješavine koji žive u pustinji,
25 Anandituma kwa mafumu onse a ku Zimuri, Elamu ndi Mediya;
I sve careve Zimrijske, i sve careve Elamske, i sve careve Midske,
26 ndiponso kwa mafumu onse a kumpoto, akufupi ndi kutali omwe, mafumu onse a dziko lapansi. Ndipo potsiriza pake, idzamwenso ndi mfumu Sesaki.
I sve careve sjeverne, koji su blizu i koji su daleko, kako jednoga tako drugoga, i sva carstva zemaljska što su po zemlji; a car Sisaški piæe poslije njih.
27 “Ndipo uwawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Imwani, ledzerani ndipo musanze, mugwe osadzukanso chifukwa cha nkhondo imene ndikutumiza pakati panu.’
I reci im: ovako veli Gospod nad vojskama Bog Izrailjev: pijte i opijte se, i bljujte i padajte, da ne ustanete od maèa koji æu pustiti meðu vas.
28 Koma ngati akana kutenga chikhocho mʼdzanja lako ndi kumwa, uwawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti: Muyenera kumwa ndithu!’”
Ako li ne bi htjeli uzeti èaše iz ruke tvoje da piju, tada im reci: ovako veli Gospod nad vojskama: zaista æete piti.
29 Taonani, tsopano ndiyamba kulanga mzinda uno umene umadziwika ndi dzina langa. Kodi inu muganiza kuti simudzalangidwa? Ayi, simudzapulumuka chifukwa ndikutumiza nkhondo pa onse okhala pa dziko lapansi, akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Jer evo poèinjem puštati zlo na grad koji se naziva mojim imenom, a vi li æete ostati bez kara? neæete ostati bez kara, jer æu dozvati maè na sve stanovnike zemaljske, govori Gospod nad vojskama.
30 “Tsopano iwe nenera mawu owatsutsa ndipo uwawuze kuti, “‘Yehova adzabangula kumwamba; mawu ake adzamveka ngati bingu kuchokera ku malo ake opatulika. Adzabangula mwamphamvu kukalipira dziko lake. Iye adzafuwula ngati anthu oponda mphesa, kukalipira onse amene akukhala pa dziko lapansi.
Ti dakle prorokuj im sve ove rijeèi i reci im: Gospod æe s visine riknuti, i iz stana svetinje svoje pustiæe glas svoj, silno æe riknuti iz stana svojega, kao oni što gaze grožðe podignuæe viku na sve stanovnike zemaljske.
31 Phokoso lalikulu lidzamveka mpaka kumalekezero a dziko lonse lapansi, chifukwa Yehova adzazenga mlandu anthu a mitundu yonse; adzaweruza mtundu wonse wa anthu ndipo oyipa adzawapha ndi lupanga,’” akutero Yehova.
Proæi æe graja do kraja zemlje, jer raspru ima Gospod s narodima, sudi se sa svakim tijelom, bezbožnike æe dati pod maè, govori Gospod.
32 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani! Mavuto akuti akachoka pa mtundu wina akukagwa pa mtundu wina; mphepo ya mkuntho ikuyambira ku malekezero a dziko.”
Ovako veli Gospod nad vojskama: evo, nevolja æe poæi od naroda do naroda, i velik æe se vihor podignuti od krajeva zemaljskih.
33 Pa tsiku limenelo, onse ophedwa ndi Yehova adzangoti mbwee ponseponse, pa dziko lonse lapansi. Palibe amene adzawalire kapena kusonkhanitsa mitemboyo kuti ikayikidwe mʼmanda, koma idzakhala mbwee ngati ndowe.
I u onaj æe dan biti od kraja do kraja zemlje pobijeni od Gospoda, neæe biti oplakani, niti æe se pokupiti i pogrepsti, biæe gnoj po zemlji.
34 Khetsani misozi ndi kufuwula mwamphamvu, abusa inu; gubudukani pa fumbi, inu atsogoleri a nkhosa. Pakuti nthawi yanu yophedwa yafika; mudzagwa ndi kuphwanyika ngati mbiya yabwino kwambiri.
Ridajte, pastiri, i vièite i valjajte se po prahu, glavari stadu, jer se navršiše vaši dani da budete poklani, i da se razaspete, i pašæete kao skupocjen sud.
35 Abusa adzasowa kothawira, atsogoleri a nkhosa adzasowa malo opulumukira.
I neæe biti utoèišta pastirima, ni izbavljenja glavarima od stada.
36 Imvani kulira kwa abusa, atsogoleri a nkhosa akulira, chifukwa Yehova akuwononga msipu wawo.
Vikaæe pastiri i ridaæe glavari od stada, jer æe potrti Gospod pašu njihovu.
37 Makola awo a nkhosa amene anali pamtendere adzasanduka bwinja chifukwa cha mkwiyo woopsa wa Yehova.
I razvaliæe se mirni torovi od žestokoga gnjeva Gospodnjega.
38 Ngati mkango, Yehova wasiya phanga lake, pakuti dziko lawo lasanduka chipululu chifukwa cha nkhondo ya owazunza ndiponso chifukwa cha mkwiyo woopsa wa Yehova.
Kao laviæ ostavio je šator svoj, jer æe zemlja njihova opustjeti od žestine nasilnikove i od ljutoga gnjeva njegova.

< Yeremiya 25 >