< Yeremiya 25 >

1 Yehova anayankhula ndi Yeremiya za anthu onse a ku Yuda mʼchaka chachinayi cha ufumu wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya ku Yuda, chimene chinali chaka choyamba cha ufumu wa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni.
Słowo, które doszło do Jeremiasza o całym ludzie Judy w czwartym roku Joakima, syna Jozjasza, króla Judy, a był to pierwszy rok Nabuchodonozora, króla Babilonu;
2 Choncho mneneri Yeremiya anawuza anthu onse a ku Yuda pamodzi ndi onse amene amakhala mu Yerusalemu kuti:
Które wypowiedział prorok Jeremiasz do całego ludu Judy i do wszystkich mieszkańców Jerozolimy, mówiąc:
3 Kwa zaka 23, kuyambira chaka cha 13 cha ufumu wa Yosiya mwana wa Amoni mfumu ya ku Yuda mpaka lero lino, Yehova wakhala akundipatsa mauthenga ake ndipo ine ndakhala ndikuyankhula ndi inu kawirikawiri, koma inu simunamvere.
Od trzynastego roku Jozjasza, syna Amona, króla Judy, aż do dziś, to [znaczy] już [przez] dwadzieścia trzy lata, dochodziło do mnie słowo PANA i przemawiałem do was z wczesnym wstawaniem i mówieniem, ale nie słuchaliście.
4 Ndipo ngakhale Yehova kawirikawiri wakhala akukutumizirani atumiki ake onse, aneneri, inuyo simunamvere kapena kutchera khutu.
PAN też posyłał do was wszystkie swoje sługi, proroków, z wczesnym wstawaniem i przesłaniem, ale nie usłuchaliście ani nie nakłoniliście swego ucha, aby usłyszeć.
5 Aneneriwo ankanena kuti, “Ngati aliyense wa inu abwerere, kusiya njira zake zoyipa ndi machitidwe ake oyipa, ndiye kuti mudzakhala mʼdziko limene Yehova anapereka kwa makolo anu kwamuyaya.
Oni mówili: Niech teraz każdy z was się odwróci od swojej złej drogi i od zła swoich uczynków, a będziecie mieszkać w tej ziemi, którą PAN dał wam i waszym ojcom na wieki wieków.
6 Musatsatire milungu ina nʼkuyitumikira ndi kuyipembedza. Musapute mkwiyo wanga ndi mafano amene mwapanga ndi manja anu. Mukatero Ine sindidzakuwonongani.
Nie chodźcie za innymi bogami, aby im służyć i oddawać im pokłon, i nie pobudzajcie mnie do gniewu uczynkami waszych rąk, a [ja] nie uczynię wam nic złego.
7 “Koma inu simunandimvere,” akutero Yehova, “ndipo munaputa mkwiyo wanga ndi mafano amene munapanga ndi manja anu. Choncho munadziwononga nokha.”
Ale nie usłuchaliście mnie, mówi PAN, pobudzając mnie do gniewu uczynkami swoich rąk na własne nieszczęście.
8 Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Chifukwa simunamvere mawu anga,
Dlatego tak mówi PAN zastępów: Ponieważ nie usłuchaliście moich słów;
9 ndidzayitana mafuko onse akumpoto, pamodzi ndi mtumiki wanga Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni,” akutero Yehova, “ndipo adzathira nkhondo dziko lino ndi anthu ake pamodzi ndi mitundu yonse ya anthu ozungulira dzikoli. Ndidzawawononga kwathunthu ndi kuwasandutsa chinthu chochititsa mantha ndi chonyozeka, mpaka muyaya.
Oto poślę po wszystkie rody północne i zbiorę [je], mówi PAN, i Nabuchodonozora, króla Babilonu, swego sługę, i sprowadzę ich na tę ziemię, na jej mieszkańców i na te wszystkie okoliczne narody, a doszczętnie zniszczę ich i uczynię ich [przedmiotem] zdumienia i świstania, i wiecznym spustoszeniem.
10 Ndidzathetsa mfuwu wachimwemwe ndi wachisangalalo, mawu a mkwati ndi mkwatibwi, phokoso la mphero ndi kuwala kwa nyale.
I sprawię, że zaniknie głos wesela i głos radości, głos oblubieńca i głos oblubienicy, odgłos żaren i światło pochodni.
11 Dziko lonse lidzakhala bwinja ndi chipululu, ndipo mitundu ina idzatumikira mfumu ya ku Babuloni kwa 70.
I cała ta ziemia stanie się spustoszeniem i zdumieniem, a te narody będą służyć królowi Babilonu przez siedemdziesiąt lat.
12 “Koma zaka 70 zikadzatha, ndidzalanga mfumu ya ku Babuloni pamodzi ndi anthu ake, chifukwa cha zolakwa zawo,” akutero Yehova, “ndipo dziko lawo lidzakhala chipululu mpaka muyaya.
A gdy się dopełni siedemdziesiąt lat, ukarzę króla Babilonu i ten naród, mówi PAN, za ich nieprawość, oraz ziemię Chaldejczyków, i zamienię ją w wieczne spustoszenie.
13 Ndidzachita zinthu zonse zimene ndinayankhula zotsutsa dzikolo, zonse zimene zalembedwa mʼbuku lino, ndiponso zonse zimene Yeremiya analosera zotsutsa anthu amenewa.
I sprowadzę na tę ziemię wszystkie moje słowa, które wypowiedziałem przeciw niej, [mianowicie] to wszystko, co jest napisane w tej księdze, co prorokował Jeremiasz przeciw wszystkim narodom.
14 Iwo eni adzakhala akapolo a anthu a mitundu yochuluka ndi mafumu amphamvu. Ndidzawabwezera molingana ndi zochita zawo ndi ntchito za manja awo.”
Gdyż i one będą podbite i wzięte do niewoli przez liczne narody i wielkich królów. Odpłacę im według ich czynów i według uczynków ich rąk.
15 Yehova, Mulungu wa Israeli, anandiwuza kuti, “Tenga chikho ichi chodzaza ndi vinyo wa ukali wanga, ndipo ukamwetse anthu a mitundu yonse kumene ndikukutuma.
Tak bowiem powiedział do mnie PAN, Bóg Izraela: Weź z mojej ręki kubek wina tej zapalczywości i daj z niego pić wszystkim narodom, do których cię posyłam.
16 Akadzamwa adzayamba kudzandira ndi kuchita misala chifukwa cha nkhondo imene ndikuyitumiza pakati pawo.”
Będą pić i zataczać się, a nawet szaleć przed ostrzem miecza, który posyłam między nie.
17 Choncho ine ndinatenga chikhocho mʼdzanja la Yehova ndipo ndinamwetsa mitundu yonse ya anthu kumene Iye ananditumako:
Wziąłem więc kubek z ręki PANA i napoiłem wszystkie narody, do których PAN mnie posłał:
18 Anandituma ku Yerusalemu ndi ku mizinda ya Yuda, kwa mafumu ake ndi nduna zake kuti ndikawasandutse ngati bwinja ndi chinthu chochititsa mantha ndi chonyozeka ndiponso chotembereredwa, monga mmene alili lero lino.
Jerozolimę i miasta ziemi Judy, jej królów i książąt, aby uczynić ich [przedmiotem] spustoszenia, zdumienia, świstania i przekleństwa, jak [to jest] dzisiaj;
19 Ananditumanso kwa Farao, mfumu ya ku Igupto, kwa atumiki ake, nduna zake ndi kwa anthu ake onse,
Faraona, króla Egiptu, jego sługi i książąt, oraz cały jego lud;
20 ndi kwa anthu ena onse a mitundu yachilendo; mafumu onse a ku Uzi; mafumu onse a Afilisti, a ku Asikeloni, ku Gaza, ku Ekroni ndiponso kwa anthu a ku chigwa chotsala cha Asidodi;
Całą różnorodną ludność, wszystkich królów ziemi Uz, wszystkich królów ziemi Filistynów oraz Aszkelon, Gazę, Ekron i resztkę Aszdodu;
21 Edomu, Mowabu ndi Amoni.
Edom, Moab i synów Ammona;
22 Ananditumanso kwa mafumu onse a ku Turo ndi ku Sidoni; kwa mafumu a kutsidya la nyanja;
Wszystkich królów Tyru, wszystkich królów Sydonu oraz królów zamorskich wysp;
23 ku Dedani, ku Tema, ku Buzi ndi kwa onse ometa chamʼmbali.
Dedan, Temę, Buzę i wszystkich [mieszkańców] w najdalszych zakątkach:
24 Ananditumanso kwa mafumu onse a ku Arabiya ndi mafumu onse a anthu achilendo amene amakhala mʼchipululu.
Wszystkich królów Arabii i wszystkich królów różnorodnej ludności mieszkającej na pustyni;
25 Anandituma kwa mafumu onse a ku Zimuri, Elamu ndi Mediya;
Wszystkich królów Zimri, wszystkich królów Elamu i wszystkich królów Medii;
26 ndiponso kwa mafumu onse a kumpoto, akufupi ndi kutali omwe, mafumu onse a dziko lapansi. Ndipo potsiriza pake, idzamwenso ndi mfumu Sesaki.
I wszystkich królów Północy, bliskich i dalekich, jednego po drugim; wszystkie królestwa ziemi, jakie są na powierzchni ziemi. A król Szeszak będzie po nich pił.
27 “Ndipo uwawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Imwani, ledzerani ndipo musanze, mugwe osadzukanso chifukwa cha nkhondo imene ndikutumiza pakati panu.’
I powiesz im: Tak mówi PAN zastępów, Bóg Izraela: Pijcie i upijacie się, wymiotujcie i padajcie, aby już nie powstać z powodu miecza, który ja poślę między was.
28 Koma ngati akana kutenga chikhocho mʼdzanja lako ndi kumwa, uwawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti: Muyenera kumwa ndithu!’”
A jeśli nie zechcą wziąć kubka z twojej ręki, aby pić, wtedy im powiesz: Tak mówi PAN zastępów: Koniecznie będziecie pić.
29 Taonani, tsopano ndiyamba kulanga mzinda uno umene umadziwika ndi dzina langa. Kodi inu muganiza kuti simudzalangidwa? Ayi, simudzapulumuka chifukwa ndikutumiza nkhondo pa onse okhala pa dziko lapansi, akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Oto bowiem na to miasto, nad którym jest wzywane moje imię, zaczynam sprowadzać nieszczęście, a wy mielibyście pozostać nieukarani? Nie ujdziecie karze, bo ja przyzywam miecz na wszystkich mieszkańców tej ziemi, mówi PAN zastępów.
30 “Tsopano iwe nenera mawu owatsutsa ndipo uwawuze kuti, “‘Yehova adzabangula kumwamba; mawu ake adzamveka ngati bingu kuchokera ku malo ake opatulika. Adzabangula mwamphamvu kukalipira dziko lake. Iye adzafuwula ngati anthu oponda mphesa, kukalipira onse amene akukhala pa dziko lapansi.
Dlatego ty prorokuj przeciwko nim wszystkie te słowa i powiedz im: PAN zagrzmi z wysoka i ze swego Świętego Przybytku wyda swój głos; zagrzmi nad swoim miejscem zamieszkania; wzniesie okrzyk jak tłoczący winogrona przeciwko wszystkim mieszkańcom tej ziemi.
31 Phokoso lalikulu lidzamveka mpaka kumalekezero a dziko lonse lapansi, chifukwa Yehova adzazenga mlandu anthu a mitundu yonse; adzaweruza mtundu wonse wa anthu ndipo oyipa adzawapha ndi lupanga,’” akutero Yehova.
I dojdzie wrzawa aż do krańców ziemi, bo PAN prowadzi spór z tymi narodami, sprawuje sąd nad wszelkim ciałem, bezbożnych wyda pod miecz, mówi PAN.
32 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani! Mavuto akuti akachoka pa mtundu wina akukagwa pa mtundu wina; mphepo ya mkuntho ikuyambira ku malekezero a dziko.”
Tak mówi PAN zastępów: Oto nieszczęście przejdzie z narodu na naród, a wielki wicher zerwie się od krańców ziemi.
33 Pa tsiku limenelo, onse ophedwa ndi Yehova adzangoti mbwee ponseponse, pa dziko lonse lapansi. Palibe amene adzawalire kapena kusonkhanitsa mitemboyo kuti ikayikidwe mʼmanda, koma idzakhala mbwee ngati ndowe.
I pobici przez PANA w tym dniu leżeć będą od krańca ziemi aż po kraniec ziemi; nie będą ich opłakiwać ani zbierać, ani grzebać, będą jak nawóz na polu.
34 Khetsani misozi ndi kufuwula mwamphamvu, abusa inu; gubudukani pa fumbi, inu atsogoleri a nkhosa. Pakuti nthawi yanu yophedwa yafika; mudzagwa ndi kuphwanyika ngati mbiya yabwino kwambiri.
Zawódźcie, pasterze, i wołajcie, tarzajcie się w popiele, wy, przewodnicy tej trzody! Dopełniły się bowiem dni waszej rzezi i rozproszenia i padniecie jak drogie naczynie.
35 Abusa adzasowa kothawira, atsogoleri a nkhosa adzasowa malo opulumukira.
Nie będzie ucieczki dla pasterzy ani ocalenia dla przewodników tej trzody.
36 Imvani kulira kwa abusa, atsogoleri a nkhosa akulira, chifukwa Yehova akuwononga msipu wawo.
[Będzie słychać] głos wołania pasterzy i zawodzenie przewodników tej trzody, bo PAN spustoszy ich pastwiska.
37 Makola awo a nkhosa amene anali pamtendere adzasanduka bwinja chifukwa cha mkwiyo woopsa wa Yehova.
I będą zniszczone spokojne łąki z powodu zapalczywości gniewu PANA.
38 Ngati mkango, Yehova wasiya phanga lake, pakuti dziko lawo lasanduka chipululu chifukwa cha nkhondo ya owazunza ndiponso chifukwa cha mkwiyo woopsa wa Yehova.
Opuścił jak lew swoją jaskinię, bo ich ziemia jest spustoszona z powodu zapalczywości niszczyciela i zapalczywości jego gniewu.

< Yeremiya 25 >