< Yeremiya 23 >

1 “Tsoka kwa abusa amene akuwononga ndi kubalalitsa nkhosa za pabusa panga!” akutero Yehova.
Teško pastirima koji potiru i razmeæu stado paše moje! govori Gospod.
2 Nʼchifukwa chake Yehova, Mulungu wa Israeli, ponena za abusa amene akuweta anthu anga akuti, “Mwabalalitsa ndi kumwaza nkhosa zanga. Komanso simunazisamale bwino. Choncho ndidzakulangani chifukwa cha machimo anu,” akutero Yehova.
Zato ovako veli Gospod Bog Izrailjev za pastire koji pasu narod moj: vi razmetnuste ovce moje i razagnaste ih, i ne obilaziste ih; evo, ja æu vas obiæi za zloæu djela vaših, govori Gospod.
3 “Pambuyo pake Ine mwini wakene ndidzasonkhanitsa nkhosa zanga zotsala, kuzichotsa ku mayiko onse kumene ndinazibalalitsira ndi kuzibweretsanso ku msipu wawo. Kumeneko zidzaswana ndi kuchulukana.
I ostatak ovaca svojih ja æu skupiti iz svijeh zemalja, u koje ih razagnah, i vratiæu ih u torove njihove, gdje æe se naploditi i umnožiti.
4 Ndidzazipatsa abusa amene adzaziweta, ndipo sizidzaopanso kapena kuchita mantha, ndipo palibe imene idzasochera,” akutero Yehova.
I postaviæu im pastire, koji æe ih pasti, da se ne boje više i ne plaše i da ne pogine nijedna, govori Gospod.
5 Yehova akuti, “Masiku akubwera, pamene ndidzaphukitsira Davide Nthambi yowongoka. Imeneyi ndiye mfumu imene idzalamulira mwanzeru, mwachilungamo ndi mosakondera mʼdziko.
Gle, idu dani, govori Gospod, u koje æu podignuti Davidu klicu pravednu, koja æe carovati i biti sreæna i èiniti sud i pravdu na zemlji.
6 Pa masiku a ulamuliro wake Yuda adzapulumuka ndipo Israeli adzakhala pamtendere. Dzina limene adzamutcha ndi ili: Yehova ndiye Chilungamo Chathu.
U njegove dane spašæe se Juda, i Izrailj æe stanovati u miru, i ovo mu je ime kojim æe se zvati: Gospod pravda naša.
7 Choncho, masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene anthu sadzanenanso polumbira kuti, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa Aisraeli ku Igupto,’
Zato, evo, idu dani, govori Gospod, u koje se neæe više govoriti: tako da je živ Gospod, koji je izveo sinove Izrailjeve iz zemlje Misirske;
8 koma adzanena kuti, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa zidzukulu za Israeli ku dziko lakumpoto ndi ku mayiko konse kumene anawabalalitsira.’ Ndipo iwo adzawabweretsa ku dziko lawolawo.”
Nego: tako da je živ Gospod, koji je izveo i doveo sjeme doma Izrailjeva iz sjeverne zemlje i iz svijeh zemalja, u koje ih bijah razagnao. I oni æe sjedjeti u svojoj zemlji.
9 Kunena za aneneri awa: Mtima wanga wasweka; mʼnkhongono mwati zii. Ndakhala ngati munthu woledzera, ngati munthu amene wasokonezeka ndi vinyo, chifukwa cha Yehova ndi mawu ake opatulika.
Radi proroka puca srce u meni, trepeæu sve kosti moje, kao pijan sam i kao èovjek kojega je osvojilo vino, Gospoda radi i njegovijeh radi svetijeh rijeèi.
10 Dziko ladzaza ndi anthu achigololo; lili pansi pa matemberero. Dziko lasanduka chipululu ndipo msipu wawuma. Aneneri akuchita zoyipa ndipo akugwiritsa ntchito mphamvu zawo molakwika.
Jer je zemlja puna preljuboèinaca, i s kletava tuži zemlja, posušiše se paše u pustinji; trk je njihov zao i moæ njihova neprava.
11 “Mneneri ngakhale wansembe onse sapembedza Yehova. Amachita zoyipa ngakhale mʼnyumba yanga,” akutero Yehova.
Jer i prorok i sveštenik skvrne je, nalazim i u domu svom zloæu njihovu, govori Gospod.
12 “Nʼchifukwa chake njira zawo zidzakhala zoterera; adzawapirikitsira ku mdima ndipo adzagwera kumeneko. Adzaona zosaona mʼnthawi ya chilango chawo,” akutero Yehova.
Zato æe put njihov biti kao klizavica po tami, gdje æe popuznuti i pasti; jer æu pustiti na njih zlo godine pohoðenja njihova, govori Gospod.
13 “Pakati pa aneneri a ku Samariya ndinaona chonyansa ichi: Ankanenera mʼdzina la Baala ndipo anasocheretsa anthu anga, Aisraeli.
U proroka Samarijskih vidio sam bezumlje, prorokovahu Valom, prelašæivahu narod moj Izrailja;
14 Ndipo pakati pa aneneri a ku Yerusalemu ndaonapo chinthu choopsa kwambiri: amachita chigololo, amanena bodza ndipo amalimbitsa mtima anthu ochita zoyipa. Choncho palibe amene amasiya zoyipa zake. Kwa Ine anthu onsewa ali ngati a ku Sodomu ndi Gomora.”
Ali u proroka Jerusalimskih vidim strahotu: èine preljubu i hode u laži, ukrjepljuju ruke zlikovcima da se niko ne vrati od svoje zloæe; svi su mi kao Sodom, i stanovnici njegovi kao Gomor.
15 Choncho ponena za aneneriwa Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ndidzawadyetsa zakudya zowawa ndi kuwamwetsa madzi a ndulu, chifukwa uchimo umene wafalikira mʼdziko lonse ndi wochokera kwa aneneri a ku Yerusalemuwa.”
Zato ovako veli Gospod nad vojskama o tijem prorocima: evo, ja æu ih nahraniti pelenom i napojiæu ih žuèi; jer od proroka Jerusalimskih izide oskvrnjenje po svoj zemlji.
16 Koma Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Musamvere zimene aneneri amenewa akulosera kwa inu; zomwe aloserazo nʼzachabechabe. Iwo akungoyankhula za masomphenya a mʼmitima mwawo basi, osati zochokera kwa Yehova.
Ovako veli Gospod nad vojskama: ne slušajte što govore proroci koji vam prorokuju; varaju vas, govore utvare svojega srca, ne iz usta Gospodnjih.
17 Iwo amapita ndi kumakawuza amene amandinyoza Ine kuti, ‘zinthu zidzakuyenderani bwino.’ Kwa iwo amene amawumirira kutsata zofuna za mitima yawo amakawawuza kuti, ‘palibe choyipa chimene chidzakugwereni.’”
Jednako govore onima koji ne mare za me: Gospod je rekao: imaæete mir; i svakome koji ide po misli srca svojega govore: neæe doæi na vas zlo.
18 Ine ndikuti, “Koma ndani wa iwo amene anakhalapo mu msonkhano wa Yehova? Ndani anaonapo kapena kumvapo mawu ake? Ndani mwa iwo analabadirako za mawu ake ndi kuwamvera?
Jer ko je stajao u vijeæu Gospodnjem, i vidio ili èuo rijeè njegovu? ko je pazio na rijeè njegovu i èuo?
19 Taonani ukali wa Yehova uli ngati chimphepo chamkuntho, inde ngati namondwe. Ndipo adzakantha mitu ya anthu oyipa.
Evo, vihor Gospodnji, gnjev, iziæi æe vihor, koji ne prestaje, pašæe na glavu bezbožnicima.
20 Mkwiyo wa Yehova sudzaleka mpaka atachita zonse zimene anatsimikiza mu mtima mwake. Mudzazizindikira bwino zimenezi masiku akubwerawa.”
Neæe se odvratiti gnjev Gospodnji dokle ne uèini i izvrši što je u srcu naumio; najposlije æete razumjeti to sasvijem.
21 Yehova anati, “Ine sindinatume aneneri amenewa, komabe iwo athamanga uku ndi uku kulalikira uthenga wawo; Ine sindinawayankhule, komabe iwo ananenera.
Ne slah tijeh proroka, a oni trèaše; ne govorih im, a oni prorokovaše.
22 Iwo akanakhala pa msonkhano wanga ndiye kuti akanamayankhula mawu anga kwa anthu anga. Komanso bwenzi atawachotsa anthu anga mʼnjira zawo zoyipa kuti aleke machimo awo.”
Da su stajali u mom vijeæu, tada bi kazivali moje rijeèi narodu mojemu, i odvraæali bi ih s puta njihova zloga i od zloæe djela njihovijeh.
23 Yehova akuti, “Kodi ndimakhala Mulungu pokhapokha ndikakhala pafupi, ndiye sindine Mulungu?
Jesam li ja Bog izbliza, govori Gospod, a nijesam Bog i izdaleka?
24 Kodi wina angathe kubisala Ine osamuona?” “Kodi Ine sindili ponseponse kumwamba ndi dziko lapansi?” Akutero Yehova.
Može li se ko sakriti na tajno mjesto da ga ja ne vidim? govori Gospod; ne ispunjam li ja nebo i zemlju? govori Gospod.
25 “Ndamva zimene aneneri akuyankhula. Iwo amalosera zabodza mʼdzina langa nʼkumati, ‘Ndalota! Ndalota!’
Èujem što govore ti proroci koji u ime moje prorokuju laž govoreæi: snio sam, snio sam.
26 Kodi zabodzazi zidzakhalabe mʼmitima ya aneneriwa mpaka liti? Iwotu amalosera zonyenga za mʼmitima yawo.
Dokle æe to biti u srcu prorocima koji prorokuju laž, i prijevaru srca svojega prorokuju?
27 Aneneriwa amakhulupirira kuti anthu anga adzayiwala mawu anga akamamva za maloto awo amene amayankhulana ngati mmene anachitira makolo awo popembedza Baala.
Koji misle da æe uèiniti da narod moj zaboravi ime moje uza sne njihove, koje pripovijedaju jedan drugomu, kao što zaboraviše oci njihovi ime moje uz Vala.
28 Mneneri amene ali ndi maloto afotokoze malotowo. Koma iye amene ali ndi mawu anga alalikire mawuwo mokhulupirika. Kodi phesi lingafanane ndi chimanga?
Prorok koji sni, neka pripovijeda san; a u koga je rijeè moja, neka govori rijeè moju istinito; šta æe pljeva sa pšenicom? govori Gospod.
29 Kodi suja mawu anga amatentha ngati moto? Suja mawu anga amaphwanya monga ichitira nyundo kuphwanya miyala?” Akutero Yehova.
Nije li rijeè moja kao oganj, govori Gospod, i kao malj koji razbija kamen?
30 Yehova akuti, “Nʼchifukwa chake, Ine ndikudana nawo aneneri amene amaberana okhaokha mawu nʼkumati mawuwo ndi a Yehova.”
Zato, evo me na te proroke, govori Gospod, koji kradu moje rijeèi jedan od drugoga.
31 Yehova akuti, “Inde, Ine ndikudana ndi aneneri amene amakonda kuyankhula zabodza nʼkumanena kuti, ‘Amenewa ndi mawu a Yehova.’”
Evo me na te proroke, veli Gospod, koji dižu jezik svoj i govore: on veli.
32 Yehova akuti, “Ndithudi, Ine ndikudana ndi aneneri a maloto abodzawa. Iwo amafotokoza malotowo nʼkumasocheretsa anthu anga ndi bodza lawo losachita nalo manyazilo, chonsecho Ine sindinawatume kapena kuwalamula. Iwo sathandiza anthuwa ndi pangʼono pomwe,” akutero Yehova.
Evo me na one koji prorokuju lažne sne, veli Gospod, i pripovijedajuæi ih zavode narod moj lažima svojim i hitrinom svojom; a ja ih nijesam poslao niti sam im zapovjedio; i neæe ništa pomoæi tome narodu, govori Gospod.
33 Yehova anawuza Yeremiya kuti, “Anthu awa, kapena mneneri, kapenanso wansembe, akakufunsa kuti, ‘Kodi uthenga wolemetsa wa Yehova ukuti chiyani?’ uwawuze kuti, ‘Inuyo ndinu katundu wolemetsa Yehova, ndipo adzakutayani.’
Ako te zapita ovaj narod ili koji prorok ili sveštenik govoreæi: kako je breme Gospodnje? tada im reci: kako breme? ostaviæu vas, govori Gospod.
34 Ngati mneneri kapena wansembe kapenanso munthu wina aliyense anena kuti, ‘Uthenga wolemetsa wa Yehova ndi uwu,’ Ine ndidzalanga munthu ameneyo pamodzi ndi banja lake.
A proroka i sveštenika i narod koji reèe: breme Gospodnje, ja æu pokarati toga èovjeka i dom njegov.
35 Koma chimene aliyense wa inu azifunsa kwa mnzake kapena mʼbale wake ndi ichi: ‘Kodi Yehova wayankha chiyani?’ kapena ‘Yehova wayankhula chiyani?’
Nego ovako govorite svaki bližnjemu svojemu i svaki bratu svojemu: šta odgovori Gospod? i: šta reèe Gospod?
36 Koma musanenenso kuti ‘nawu uthenga wolemetsa wa Yehova,’ chifukwa mawu a munthu aliyense ndiwo uthenga wa iye mwini, kotero kuti inu mumakhotetsa mawu a Mulungu wamoyo, Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wathu.
A bremena Gospodnjega ne pominjite više, jer æe svakome biti breme rijeè njegova, jer izvræete rijeèi Boga živoga, Gospoda nad vojskama, Boga našega.
37 Tsono iwe Yeremiya udzamufunse mneneri kuti, ‘Kodi Yehova wakuyankha chiyani?’ kapena, ‘Kodi Yehova wayankhula chiyani?’
Ovako reci proroku: šta ti odgovori Gospod? i: šta ti reèe Gospod?
38 Ngati mudzanena kuti, ‘Nawu uthenga wolemetsa wa Yehova,’ ndiye tsono Yehova akuti, ‘Popeza mwagwiritsa ntchito mawu akuti: Nawu uthenga wolemetsa wa Yehova, mawu amene ndinakuletsani kuti musawatchule,
Ali kad kažete: breme Gospodnje, zato ovako veli Gospod: šta govorite tu rijeè: breme Gospodnje, a ja slah k vama da vam kažu: ne govorite: breme Gospodnje,
39 ndiye kuti Ine ndidzakunyamulani ngati katundu nʼkukuponyani kutali. Ndidzakuchotsani pamaso panga, inuyo pamodzi ndi mzinda umene ndinakupatsani inu ndi makolo anu.
Zato evo me, ja æu vas zaboraviti sasvijem i odbaciæu od sebe vas i grad koji sam dao vama i ocima vašim.
40 Ndidzakunyozani mpaka muyaya. Ndidzakuchititsani manyazi osayiwalika.’”
I navaliæu na vas porugu vjeènu i sramotu vjeènu koja se neæe zaboraviti.

< Yeremiya 23 >