< Yeremiya 22 >

1 Yehova anandiwuza kuti, “Pita ku nyumba ya mfumu ya ku Yuda ndipo ukayiwuze kuti,
The Lord seith these thingis, Go thou doun in to the hous of the kyng of Juda, and thou schalt speke there this word, and schalt seie,
2 ‘Imva mawu a Yehova, iwe mfumu ya ku Yuda, amene umakhala pa mpando waufumu wa Davide; iwe, nduna zako pamodzi ndi anthu ako amene amalowera pa zipata izi.
Thou kyng of Juda, that sittist on the seete of Dauid, here the word of the Lord, thou, and thi seruauntis, and thi puple, that entren bi these yatis.
3 Yehova akuti, uziweruza molungama ndi mosakondera. Uzipulumutsa munthu amene walandidwa katundu mʼdzanja la womuzunza. Usazunze kapena kupondereza mlendo, ana amasiye kapena akazi amasiye. Usaphe munthu wosalakwa pa malo pano.
The Lord seith these thingis, Do ye doom, and riytfulnesse, and delyuere ye hym that is oppressid bi violence fro the hond of the fals chalenger; and nyle ye make sori, nether oppresse ye wickidli a comelyng, and a fadirles child, and a widewe, and schede ye not out innocent blood in this place.
4 Pakuti ngati udzamvera malamulo awa, ndiye kuti mafumu onse okhala pa mpando waufumu wa Davide azidzalowabe pa zipata za nyumba yaufumu ino, atakwera magaleta ndi akavalo, iwowo pamodzi ndi nduna zawo ndi anthu awo.
For if ye doynge don this word, kyngis of the kyn of Dauid sittynge on his trone schulen entre bi the yatis of this hous, and schulen stie on charis and horsis, thei, and the seruauntis, and the puple of hem.
5 Koma ngati sumvera malamulo awa, akutero Yehova, ndikulumbira pali Ine ndemwe kuti nyumba ino yaufumu idzasanduka bwinja.’”
That if ye heren not these wordis, Y swoore in my silf, seith the Lord, that this hous schal be in to wildirnesse.
6 Pakuti zimene Yehova akunena za nyumba yaufumu ya mfumu ya ku Yuda ndi izi: “Ngakhale iwe uli ngati Giliyadi kwa Ine, ngati msonga ya phiri la Lebanoni, komabe ndidzakusandutsa chipululu, ngati mizinda yopanda anthu.
For the Lord seith these thingis on the hous of the kyng of Juda, Galaad, thou art to me the heed of the Liban; credence be not youun to me, if Y sette not thee a wildirnesse, citees vnhabitable.
7 Ndidzatuma anthu oti adzakuwononge, munthu aliyense ali ndi zida zake, ndipo adzadula mikungudza yako yokongola nadzayiponya pa moto.
And Y schal halewe on thee a man sleynge, and hise armuris; and thei schulen kitte doun thi chosun cedris, and schulen caste doun in to fier.
8 “Pamene anthu a mitundu ina adzadutsa pa mzinda umenewu adzafunsana kuti, ‘Chifukwa chiyani Yehova wachita chinthu chotere pa mzinda waukuluwu?’
And many folkis schulen passe bi this citee, and ech man schal seie to his neiybore, Whi dide the Lord thus to this greet citee?
9 Ndipo yankho lake lidzakhala lakuti, ‘Chifukwa anasiya pangano limene anapangana ndi Yehova Mulungu wawo ndipo anapembedza ndi kutumikira milungu ina.’”
And thei schulen answere, For thei forsoken the couenaunt of her Lord God, and worschipiden alien goddis, and serueden hem.
10 Musayilire mfumu Yosiya, musamuyimbire nyimbo womwalirayo; mʼmalo mwake, mulire kwambiri chifukwa cha Yehowahazi amene wapita ku ukapolo, chifukwa sadzabwereranso kapena kuonanso dziko lake lobadwira.
Nyle ye biwepe hym that is deed, nether weile ye on hym bi wepyng; biweile ye hym that goith out, for he schal no more turne ayen, nether he schal se the lond of his birthe.
11 Pakuti zimene Yehova akunena za Yehowahazi mwana wa Yosiya, amene anatenga mpando waufumu wa Yuda mʼmalo mwa abambo ake koma nʼkuwusiya ndi izi: “Iye sadzabwereranso.
For the Lord seith these thingis to Sellum, the sone of Josie, the kyng of Juda, that regnede for Josye, his fadir, He that yede out of this place, schal no more turne ayen hidur;
12 Iyeyo adzafera ku ukapoloko. Sadzalionanso dziko lino.”
but in the place to which Y translatide him, there he schal die, and he schal no more se this lond.
13 “Tsoka kwa munthu womanga nyumba yake mopanda chilungamo, womanga zipinda zake zosanja monyenga, pogwiritsa ntchito abale ake mwathangata, osawapatsa malipiro a ntchito yawo.
Wo to him that bildith his hous in vnriytfulnesse, and his soleris not in doom; he schal oppresse his freend in veyn, and he schal not yelde his hire to hym.
14 Munthuyo amati, ‘Ndidzadzimangira nyumba yayikulu ya zipinda zikuluzikulu zamʼmwamba.’ Kotero ndidzapanga mazenera akuluakulu, ndi kukhomamo matabwa a mkungudza ndi kukongoletsa ndi makaka ofiira.
Which seith, Y schal bilde to me a large hous, and wide soleris; which openeth wyndows to hym silf, and makith couplis of cedre, and peyntith with reed colour.
15 “Kodi kukhala ndi nyumba ya mkungudza wambiri zingachititse iwe kukhala mfumu? Ganiza za abambo ako. Suja anali ndi zonse zakudya ndi zakumwa. Abambo ako ankaweruza molungama ndi mosakondera, ndipo zonse zinkawayendera bwino.
Whether thou schalt regne, for thou comparisonest thee to a cedre? whether thi fadir eet not, and drank, and dide doom and riytfulnesse thanne, whanne it was wel to hym?
16 Iye ankateteza anthu osauka ndi osowa, ndipo zonse zinkamuyendera bwino. Kodi zimenezi sindiye tanthauzo la kudziwa Ine?” akutero Yehova.
He demyde the cause of a pore man, and nedi, in to his good; whether not therfor for he knew me? seith the Lord.
17 “Koma maso ako ndi mtima sizili penanso, koma zili pa phindu lachinyengo, pa zopha anthu osalakwa ndi pa kuzunza ndi pakulamulira mwankhanza.”
Forsothe thin iyen and herte ben to aueryce, and to schede innocent blood, and to fals caleng, and to the perfourmyng of yuel werk.
18 Nʼchifukwa chake Yehova ponena za Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya ku Yuda akuti, “Anthu sadzamulira maliro kapena kunena kuti, ‘Kalanga ine, mʼbale wanga! Kalanga ine mlongo wanga! Anthu ake sadzamulira maliro kuti, Kalanga ine, mbuye wathu! Taonani ulemerero wake wapita!’
Therfor the Lord seith these thingis to Joachym, the sone of Josie, the kyng of Juda, Thei schulen not biweile hym, Wo brother! and wo sistir! thei schulen not sowne togidere to hym, Wo lord! and wo noble man!
19 Adzayikidwa ngati bulu, kuchita kumuguguza ndi kukamutaya kunja kwa zipata za Yerusalemu.”
He schal be biried with the biriyng of an asse, he schal be rotun, and cast forth without the yatis of Jerusalem.
20 “Tsono inu anthu a ku Yerusalemu, pitani ku mapiri a Lebanoni kuti mukalire mofuwula kumeneko, mawu anu akamveke mpaka ku Basani. Mulire mofuwula muli ku Abarimu chifukwa abwenzi ako onse awonongeka.
Stie thou on the Liban, and cry thou, and yyue thi vois in Basan, and cry to hem that passen forth, for alle thi louyeris ben al to-brokun.
21 Ndinakuchenjezani pamene munali pa mtendere. Koma inu munati, ‘Sindidzamvera.’ Umu ndi mmene mwakhala mukuchitira kuyambira mukali aangʼono. Simunandimvere Ine.
Y spak to thee in thi plentee, and thou seidist, Y schal not here; this is thi weie fro thi yongthe, for thou herdist not my vois.
22 Mphepo idzakuchotserani abusa anu onse, ndipo abwenzi anu adzatengedwa ku ukapolo. Pamenepo mudzachita manyazi ndi kunyozedwa chifukwa cha zoyipa zanu zonse.
Wynd schal feede alle thi scheepherdis, and thi louyeris schulen go in to caitifte;
23 Inu amene mumakhala mʼnyumba ya ku Lebanoni, amene munamanga nyumba zanu pakati pa mikungudza, mudzabuwula kwambiri pamene zowawa zidzakugwerani, zonga za mkazi pa nthawi yake yochira!
and thanne thou that sittist in the Liban, and makist nest in cedris, schalt be schent, and be aschamed of al thi malice. Hou weilidist thou, whanne sorewis weren comun to thee, as the sorew of a womman trauelynge of child?
24 “Pali Ine wamoyo, akutero Yehova, ngakhale iwe, Yehoyakini mwana wa Yehoyakimu mfumu ya ku Yuda, ukanakhala ngati mphete ya ku dzanja langa lamanja, ndikanakuvula nʼkukutaya.
I lyue, seith the Lord, for thouy Jeconye, the sone of Joachym, kyng of Juda, were a ring in my riyt hond, fro thennus Y schal drawe awei hym.
25 Ndidzakupereka kwa amene akufuna kukupha, amene iwe umawaopa. Ndidzakupereka kwa Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni ndi anthu ake.
And Y schal yyue thee in the hond of hem that seken thi lijf, and in the hond of hem whos face thou dredist, and in the hond of Nabugodonosor, kyng of Babiloyne, and in the hond of Caldeis.
26 Iwe pamodzi ndi amayi ako amene anakubereka ndidzakupititsani ku dziko lachilendo. Ngakhale inu simunabadwire kumeneko, komabe mudzafera komweko.
And Y schal sende thee, and thi moder that gendride thee, in to an alien lond, in which ye weren not borun, and there ye schulen die;
27 Simudzabwereranso ku dziko limene mudzafuna kubwerera.”
and thei schulen not turne ayen in to the lond, to which thei reisen her soule, that thei turne ayen thidur.
28 Kodi Yehoyakini wakhala ngati mbiya yonyozeka, yosweka imene anthu sakuyifunanso? Kodi nʼchifukwa chake iye pamodzi ndi ana ake, achotsedwa nʼkutayidwa ku dziko limene iwo sakulidziwa?
Whether this man Jeconye is an erthene vessel, and al to-brokun? whether a vessel withouten al likyng? Whi ben he and his seed cast awei, and cast forth in to a lond which thei knewen not?
29 Iwe dziko, dziko, dziko, Imva mawu a Yehova!
Erthe, erthe, erthe, here thou the word of the Lord.
30 Yehova akuti, “Munthu ameneyu mumutenge ngati wopanda ana, munthu amene sadzakhala wochita bwino pamoyo wake wonse, pakuti palibe ndi mmodzi yemwe mwa zidzukulu zake zomwe zidzachita bwino. Palibe amene adzathe kukhala pa mpando waufumu wa Davide ndi kulamulira Yuda.”
The Lord seith these thingis, Write thou this man bareyn, a man that schal not haue prosperite in hise daies; for of his seed schal be no man, that schal sitte on the seete of Dauid, and haue powere ferthere in Juda.

< Yeremiya 22 >