< Yeremiya 16 >

1 Kenaka Yehova anandiwuza kuti,
Potom doðe mi rijeè Gospodnja govoreæi:
2 “Usadzakwatire ndi kubereka ana aamuna kapena aakazi malo ano
Nemoj se ženiti, i da nemaš sinova ni kæeri na tom mjestu.
3 pakuti ana aamuna ndi ana aakazi obadwira mʼdziko muno, komanso amayi awo ndi abambo awo amene anabereka anawo mʼdziko muno,
Jer ovako govori Gospod za sinove i kæeri što se rode na tom mjestu i za matere njihove koje ih rode, i za oce njihove koji ih rode u toj zemlji:
4 adzafa ndi nthenda zoopsa. Sadzawalira maliro kapena kuyikidwa mʼmanda koma adzakhala ngati ndowe zotayikira pansi. Ena adzaphedwa ku nkhondo ndipo ena adzafa ndi njala. Mitembo yawo idzakhala chakudya cha mbalame zamlengalenga ndi zirombo zakuthengo.”
Ljutom æe smræu pomrijeti, neæe biti oplakani niti æe se pogrepsti, biæe gnoj po zemlji, i od maèa i od gladi izginuæe, i mrtva æe tjelesa njihova biti hrana pticama nebeskim i zvijerima zemaljskim.
5 Yehova akuti, “Usalowe mʼnyumba ya maliro; usapite kukalira maliro kapena kukapepesa, chifukwa Ine ndawachotsera madalitso anga, chikondi changa ndi chifundo changa.”
Jer ovako govori Gospod: ne ulazi u kuæu u kojoj je žalost, i ne idi da plaèeš niti ih žali; jer sam uzeo mir svoj od toga naroda, govori Gospod, milost i žaljenje.
6 Akuluakulu ndi angʼonoangʼono omwe adzafa mʼdziko muno. Sadzayikidwa mʼmanda kapena kuliridwa, ndipo palibe amene adzaonetse chisoni podzichekacheka kapena kumeta tsitsi lake chifukwa cha iwo.
Pomrijeæe mali i veliki u ovoj zemlji, neæe biti pogrebeni niti æe se oplakati, niti æe se ko rezati ni glave striæi za njima.
7 Palibe amene adzapereka chakudya kutonthoza amene akulira maliro, ngakhale kuti womwalirayo ndi abambo ake kapena amayi ake.
Neæe im se dati hljeba u žalosti da se potješe za mrtvijem, niti æe ih napojiti iz èaše radi utjehe za ocem ili za materom.
8 “Ndipo usalowe mʼnyumba mmene muli madyerero, nʼkukhala pansi ndi kudya ndi kumwa nawo.
Tako ne ulazi u kuæu u kojoj je žalost da sjedeš s njima da jedeš i piješ.
9 Pakuti Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akunena kuti, ‘Pa nthawi yanu, inu mukuona ndidzathetsa mawu achimwemwe ndi achisangalalo ndiponso mawu a mkwati ndi mkwatibwi pa malo ano.’
Jer ovako veli Gospod nad vojskama Bog Izrailjev: evo, ja æu uèiniti da na ovom mjestu pred vašim oèima i za vaših dana ne bude glasa radosna ni glasa vesela, glasa ženikova ni glasa nevjestina.
10 “Ukawawuza anthu awa zinthu zonsezi akakufunsa kuti, ‘Chifukwa chiyani Yehova wanena kuti tsoka lalikulu lotere lidzatigwere? Kodi talakwa chiyani? Kodi tamuchimwira tchimo lotani Yehova Mulungu wathu?’
A kad kažeš tome narodu sve ove rijeèi, ako ti reku: zašto izreèe Gospod sve to veliko zlo na nas? i kako je bezakonje naše ili kaki je grijeh naš, kojim zgriješismo Gospodu Bogu svojemu?
11 Pamenepo ukawawuze kuti, ‘Nʼchifukwa chakuti makolo anu anandisiya Ine,’ akutero Yehova, ‘ndi kutsatira milungu ina, kuyitumikira ndi kuyipembedza. Iwo anandisiya Ine ndipo sanasunge lamulo langa.
Tada im reci: jer oci vaši ostaviše mene, govori Gospod, i idoše za drugim bogovima i služiše im i klanjaše im se, a mene ostaviše i zakona mojega ne držaše;
12 Komanso inu munachimwa kwambiri kupambana makolo anu. Aliyense wa inu akutsatira zoyipa ndi mtima wake wokanikawo mʼmalo mondimvera Ine.
A vi još gore èinite nego oci vaši, jer eto idete svaki po misli srca svojega zloga ne slušajuæi mene.
13 Choncho Ine ndidzakubalalitsani mʼdziko muno ndi kukulowetsani mʼdziko limene inu ndi makolo anu simunalidziwe. Kumeneko mukatumikira milungu ina usana ndi usiku, ndipo sadzakuchitirani chifundo.’”
Zato æu vas izbaciti iz ove zemlje u zemlju koje ne poznaste ni vi ni oci vaši, i ondje æete služiti drugim bogovima dan i noæ dokle vam ne uèinim milost.
14 Yehova akuti, “Komabe masiku akubwera pamene anthu polumbira sadzatinso, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto,’
Zato, evo, idu dani, govori Gospod, kad se neæe više govoriti: tako da je živ Gospod koji je izveo sinove Izrailjeve iz zemlje Misirske;
15 koma adzanena kuti, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa Aisraeli ku dziko lakumpoto, ndi ku mayiko onse kumene anawabalalitsirako.’ Pakuti ndidzawabwezera ku dziko limene ndinalipereka kwa makolo awo.”
Nego: tako da je živ Gospod koji je izveo sinove Izrailjeve iz zemlje sjeverne i iz svijeh zemalja u koje ih bješe razagnao! Jer æu ih opet dovesti u zemlju njihovu koju sam dao ocima njihovijem.
16 Yehova akuti, “Koma tsopano ndidzayitana adani okhala ngati asodzi ambiri, ndipo adzawagwira ngati nsomba. Izi zitatha adani enanso okhala ngati alenje ambiri, adzawasaka pa phiri lililonse, pa chitunda chilichonse ndiponso mʼmapanga onse a mʼmatanthwe.
Gle, ja æu poslati mnoge ribare, govori Gospod, da ih love, i poslije æu poslati mnoge lovce da ih love po svakoj gori i po svakom humu i po rasjelinama kamenijem.
17 Maso anga akuona makhalidwe awo onse; sanabisike pamaso panga. Palibe tchimo limene sindikulidziwa.
Jer oèi moje paze na sve putove njihove, nijesu sakriveni od mene, niti je bezakonje njihovo zaklonjeno od mojih oèiju.
18 Ndidzawalanga mowirikiza chifukwa cha kuyipa kwawo ndi tchimo lawo. Ndidzatero chifukwa ayipitsa dziko langa ndi mafano awo amene ali ngati mitembo, ndiponso adzaza cholowa changa ndi mafano awo onyansa.”
I platiæu im prvo dvojinom za bezakonje njihovo i za grijeh njihov, što oskvrniše zemlju moju strvima gadova svojih, i našljedstvo moje napuniše gnusobama svojim.
19 Inu Yehova, ndinu mphamvu yanga ndi linga langa, pothawirapo panga nthawi ya masautso, anthu a mitundu yonse adzabwera kwa Inu kuchokera ku mathero onse a dziko lapansi ndipo adzanena kuti, “Makolo anthu anali ndi milungu yonama, anali ndi mafano achabechabe amene sanawathandize.
Gospode, krjeposti moja i grade moj i utoèište moje u nevolji, k tebi æe doæi narodi od krajeva zemaljskih, i reæi æe: doista oci naši imaše laž, i taštinu i što nimalo ne pomaže.
20 Kodi anthu nʼkudzipangira milungu? Atati atero ndiye kuti imeneyo ikhala milungu yachabechabe.”
Eda li æe èovjek naèiniti sebi bogove, koji ipak nijesu bogovi?
21 “Choncho Ine ndidzawaphunzitsa, kokha kano kuti adziwe za mphamvu yanga ndi za nyonga zanga. Pamenepo adzadziwa kuti dzina langa ndi Yehova.
Zato, evo, ja æu ih nauèiti sada, pokazaæu im ruku svoju i silu svoju, da poznadu da mi je ime Gospod.

< Yeremiya 16 >