< Yeremiya 15 >

1 Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Ngakhale Mose ndi Samueli akanayima pamaso panga kupempherera anthu awa, Ine sindikanawachitira chisoni. Achotseni ndipo ndisawaonenso! Aleke apite!
I reèe mi Gospod: da stane Mojsije i Samuilo preda me, ne bi se duša moja obratila k tome narodu; otjeraj ih ispred mene, i neka odlaze.
2 Ndipo ngati akufunsa iwe kuti, ‘Kodi tipite kuti?’ uwawuze kuti, ‘Yehova akuti, “‘Oyenera kufa adzafa; oyenera kufa ndi lupanga adzafa ndi lupanga; oyenera kufa ndi njala adzafa ndi njala; oyenera kupita ku ukapolo adzapita ku ukapolo.’
I ako ti reku: kuda æemo iæi? tada im reci: ovako veli Gospod: ko je za smrt, na smrt; ko je za maè, pod maè; ko za glad, na glad; ko za ropstvo, u ropstvo.
3 “Ine ndidzawatumizira mitundu inayi ya zinthu zowononga,” akutero Yehova, “lupanga lowapha, agalu owaluma, mbalame zamumlengalenga ndiponso zirombo zoti ziwadye ndi kuwawononga.
I pustiæu na njih èetvoro, govori Gospod: maè, da ih ubija, i pse, da ih razvlaèe, i ptice nebeske i zvijeri zemaljske, da ih jedu i istrijebe.
4 Ndidzawasandutsa kukhala chinthu chonyansa kwa anthu a maufumu onse a dziko lapansi chifukwa cha zimene Manase mwana wa Hezekiya mfumu ya Yuda anachita mu Yerusalemu.
I daæu ih da se potucaju po svijem carstvima zemaljskim radi Manasije sina Jezekijina cara Judina za ono što je uèinio u Jerusalimu.
5 “Kodi adzakumvera chisoni ndani, Yerusalemu? Kodi adzakulira ndani? Kodi ndani amene adzapatuka kufunsa za moyo wako?
Jer ko bi se smilovao na tebe, Jerusalime? ko li bi te požalio? ko li bi došao da zapita kako ti je?
6 Inu mwandikana Ine,” akutero Yehova. “Inu mukubwererabe mʼmbuyo. Choncho Ine ndidzakukanthani. Ndatopa ndi kukuchitirani chifundo.
Ti si me ostavio, govori Gospod, otišao si natrag; zato æu mahnuti rukom svojom na te i pogubiæu te; dosadi mi žaliti.
7 Ine ndidzakubalalitsani kukuchotsani mʼmizinda ya mʼdzikomo monga mmene amachitira ndi mankhusu popeta ndi lichero. Anthu anga ndinawaliritsa ndi kuwawononga chifukwa sanasinthe makhalidwe awo oyipa.
Zato æu ih izvijati vijaèom na vratima zemaljskim, uèiniæu ih sirotima, potræu narod svoj, jer se ne vraæaju s putova svojih.
8 Ndinachulukitsa amayi awo amasiye kupambana mchenga wa kunyanja. Amayiwo ndinawawonongera ana awo aamuna dzuwa lili pamutu. Mwadzidzidzi ndinawagwetsera kuwawa mtima ndi mantha.
Više æe mi biti udovica njegovijeh nego pijeska morskoga, dovešæu im na majke momaèke zatiraèe u podne, i pustiæu iznenada na njih smetnju i strahotu.
9 Mayi wa ana asanu ndi awiri wakomoka ndipo akupuma wefuwefu. Dzuwa lake lalowa ukanali usana; anamuchititsa manyazi ndipo wathedwa nzeru. Otsala ndidzawapereka mʼmanja mwa adani awo kuti awaphe ndi lupanga,” akutero Yehova.
Iznemoæi æe koja je rodila sedmoro i ispustiæe dušu, sunce æe joj zaæi još za dana, sramiæe se i stidjeæe se, a ostatak æu njihov dati pod maè pred neprijateljima njihovijem, govori Gospod.
10 Kalanga ine, amayi pakuti munandibereka ine, munthu amene ndikutsutsana ndi kulimbana ndi anthu pa dziko lonse! Ine sindinakongoze kapena kukongola kanthu, komatu aliyense akunditemberera.
Teško meni, majko moja, što si me rodila da se sa mnom prepire i da se sa mnom svaða sva zemlja; ne davah u zajam niti mi davaše u zajam, i opet me svi proklinju.
11 Yehova anati, “Ndithudi, Ine ndidzakulanditsa kuti upeze bwino. Ndithudi, adani ako adzakupempha pa nthawi ya tsoka ndi ya mavuto awo.
Gospod reèe: doista, ostatku æe tvojemu biti dobro, i braniæu te od neprijatelja, kad budeš u nevolji i u tjeskobi.
12 “Palibe munthu amene angathe kudula chitsulo, makamaka chitsulo chochokera kumpoto chosakaniza ndi mkuwa.
Eda li æe gvožðe slomiti gvožðe sjeverno i mjed?
13 Anthu ako ndi chuma chako ndidzazipereka kwa ofunkha popanda malipiro, chifukwa cha machimo anu onse a mʼdziko lanu lonse.
Imanje tvoje i blago tvoje daæu da se razgrabi bez cijene po svijem meðama tvojim, i to za sve grijehe tvoje.
14 Ndidzakusandutsani akapolo a adani anu mʼdziko limene inu simulidziwa, chifukwa mkwiyo wanga wayaka ngati moto umene udzakutenthani.”
I odvešæu te s neprijateljima tvojim u zemlju koje ne poznaješ, jer se raspalio oganj od gnjeva mojega, i gorjeæe nad vama.
15 Ine ndinati, “Inu Yehova, mumadziwa zonse; kumbukireni ndi kundisamalira. Ndilipsireni anthu ondizunza. Ndilezereni mtima musandilande moyo wanga. Onani momwe ndi kuvutikira chifukwa cha Inu.
Ti znaš, Gospode, opomeni me se i pohodi me i osveti me od onijeh koji me gone; nemoj me zgrabiti dokle se ustežeš od gnjeva; znaj da podnosim rug tebe radi.
16 Munandiyankhula ndipo mawu anu ndinawalandira bwino. Mawu anu anandipatsa chimwemwe ndipo mtima wanga unasangalala. Paja ine, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, ndimadziwika ndi dzina lanu.
Kad se naðoše rijeèi tvoje, pojedoh ih, i rijeè tvoja bi mi radost i veselje srcu mojemu, jer je ime tvoje prizvano na me, Gospode Bože nad vojskama.
17 Sindinakhale nawo mʼgulu la anthu amadyera, sindinasangalale nawo anthu amenewo. Ndinakhala ndekha chifukwa choti dzanja lanu linali pa ine ndipo munadzaza mu mtima mwanga ndi mkwiyo.
Ne sjedim u vijeæu potsmjevaèkom niti se s njima veselim; sjedim sam radi ruke tvoje, jer si me napunio srdnje.
18 Nanga nʼchifukwa chiyani mavuto anga sakutha? Bwanji chilonda changa sichikupola? Kodi inu mudzakhala ngati mtsinje wowuma nthawi yachilimwe, kapena ngati kasupe wopanda madzi?”
Zašto bol moj jednako traje? i zašto je rana moja smrtna, te neæe da se iscijeli? Hoæeš li mi biti kao varalica, kao voda nepostojana?
19 Tsono Yehova anandiyankha kuti, “Ukabwerera kwa Ine, ndidzakulandiranso ndipo udzakhalanso mtumiki wanga. Ngati udzayankhula mawu oyenera osati achabechabe, udzakhalanso mneneri wanga. Anthu adzabwera kwa iwe ndipo sipadzafunika kuti iwe upite kwa iwo.
Zato ovako veli Gospod: ako se obratiš, ja æu te opet postaviti da stojiš preda mnom, ako odvojiš što je dragocjeno od rðavoga, biæeš kao usta moja; oni neka se obrate k tebi, a ti se ne obraæaj k njima.
20 Ndidzakusandutsa ngati khoma lolimba ngati mkuwa kwa anthu awa. Adzalimbana nawe koma sadzakugonjetsa, pakuti Ine ndili nawe kukulanditsa ndi kukupulumutsa,” akutero Yehova.
I uèiniæu da budeš tome narodu kao jak zid mjeden, i udaraæe na te, ali te neæe nadvladati; jer sam ja s tobom da te èuvam i izbavljam, govori Gospod.
21 “Ndidzakupulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa ndipo ndidzakuwombola kwa anthu ankhanza.”
I izbaviæu te iz ruku zlijeh ljudi, i iskupiæu te iz ruku nasilnièkih.

< Yeremiya 15 >