< Yeremiya 11 >

1 Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
Rijeè koja doðe Jeremiji od Gospoda govoreæi:
2 “Imvani mawu a pangano ili, ndipo uwawuze anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu.
Slušajte rijeèi ovoga zavjeta, i kazujte ljudima Judinijem i stanovnicima Jerusalimskim.
3 Awuze kuti Yehova, Mulungu wa Israeli akuti ‘adzakhala wotembereredwa munthu amene samvera mawu a pangano ili.
I reci im: ovako veli Gospod Bog Izrailjev: proklet da je ko ne posluša rijeèi ovoga zavjeta,
4 Awa anali mawu amene ndinalamulira makolo anu nditawatulutsa mu Igupto, kuchoka mʼngʼanjo yamoto.’ Ine ndinati, ‘Mverani Ine ndi kuchita chilichonse chimene ndakulamulirani. Mukatero mudzakhala anthu anga ndi Ine ndidzakhala Mulungu wanu.
Koji zapovjedih ocima vašim kad ih izvedoh iz zemlje Misirske iz peæi gvozdene govoreæi: slušajte glas moj i tvorite ovo sve kako vam zapovijedam, pa æete mi biti narod i ja æu vam biti Bog,
5 Tsono Ine ndidzakwaniritsa lumbiro lomwe ndinalumbira kwa makolo anu kuti ndidzawapatsa dziko loyenda mkaka ndi uchi,’ dziko lomwe inu lero mukukhalamo.” Tsono Ine ndinayankha kuti, “Ameni, Yehova.”
Da bih ispunio zakletvu kojom se zakleh ocima vašim da æu im dati zemlju u kojoj teèe mlijeko i med, kako se vidi danas. A ja odgovorih i rekoh: amin, Gospode.
6 Yehova anandiwuza kuti, “Lengeza mawu onsewa mʼmizinda yonse ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu: ‘Mverani mawu a pangano ili ndi kuzitsatira.
Potom reèe mi Gospod: kazuj sve ove rijeèi po gradovima Judinijem i po ulicama Jerusalimskim govoreæi: slušajte rijeèi ovoga zavjeta, i izvršujte ih.
7 Kuyambira nthawi imene ndinatulutsa makolo anu ku Igupto mpaka lero, ndakhala ndi kuwachenjeza kawirikawiri kuti, ‘Mverani Ine.’
Jer tvrdo zasvjedoèavah ocima vašim otkad ih izvedoh iz zemlje Misirske do danas, zarana jednako govoreæi: slušajte glas moj.
8 Koma sanamvere kapena kulabadirako. Aliyense anawumirira kuchita zoyipa za mʼmitima yawo. Ngakhale ndinawalamulira kuti asunge pangano langa koma iwo sanasunge. Choncho ndinawalanga monga ndinaneneramo.’”
Ali ne poslušaše i ne prignuše uha svojega, nego hodiše svaki za mislima zloga srca svojega; zato pustih na njih sve rijeèi ovoga zavjeta, koji zapovjedih da vrše a oni ne vršiše.
9 Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Anthu a ku Yuda ndi ku Yerusalemu andiwukira.
Tada mi reèe Gospod: buna je meðu ljudima Judinijem i stanovnicima Jerusalimskim.
10 Abwereranso ku machimo a makolo awo, amene anakana kumvera mawu anga. Akutsata milungu ina ndi kumayitumikira. Aisraeli ndi Ayuda aphwanya pangano limene ndinachita ndi makolo awo.
Vratili su se na bezakonja starijeh svojih, koji ne htješe slušati mojih rijeèi, i idu za drugim bogovima, te im služe; dom Izrailjev i dom Judin pokvariše zavjet moj, koji uèinih s ocima njihovijem.
11 Choncho Yehova akuti, ‘Ndidzawagwetsera mavuto amene sadzatha kuwalewa. Ngakhale adzandilirire, sindidzawamvera.
Zato ovako veli Gospod: evo, ja æu pustiti na njih zlo, iz kojega neæe moæi izaæi, i vapiæe k meni, ali ih neæu uslišiti.
12 Anthu a mʼmizinda ya Yuda ndi anthu a ku Yerusalemu adzapita ndi kukalirira milungu imene ankayifukizira lubani, koma milunguyo sidzawathandiza ndi pangʼono pomwe mavuto akadzafika.
Tada æe gradovi Judini i stanovnici Jerusalimski iæi i vapiti k bogovima kojima kade, ali im neæe pomoæi u nevolji njihovoj.
13 Iwe Yuda, uli ndi milungu yochuluka ngati chiwerengero cha mizinda yako; chiwerengero cha maguwa ansembe amene umafukizirapo lubani kwa Baala chili ngati misewu ya mu Yerusalemu.’
Jer imaš bogova, Judo, koliko gradova, i koliko ima ulica u Jerusalimu, toliko podigoste oltara sramotnijeh, oltara, da kadite Valu.
14 “Tsono iwe Yeremiya usawapempherere anthu amenewa ngakhale kuwadandaulira kapena kuwapepesera, chifukwa sindidzawamvera akadzandiyitana pa nthawi ya mavuto awo.
Ti se dakle ne moli za taj narod, i ne podiži vike ni molbe za njih, jer ih neæu uslišiti kad zavapiju k meni u nevolji svojoj.
15 “Kodi anthu anga okondedwa akudzachita chiyani mʼNyumba yanga? Kodi suja iwowa amachita zoyipa zambiri? Kodi mungathe kupulumuka, tsoka osakugwerani chifukwa cha nsembe zanuzo?”
Što æe mili moj u domu mom, kad èini grdilo s mnogima, i sveto meso otide od tebe, i veseliš se kad zlo èiniš?
16 Kale Yehova ankakutchani mtengo wa olivi wa masamba obiriwira, wokhala ndi zipatso zokongola. Koma tsopano adzawutentha ndi mkuntho wamkokomo ndipo nthambi zake zidzapserera.
Gospod te nazva maslinom zelenom, lijepom radi dobroga roda; ali s hukom velikoga vjetra raspali oganj oko nje, i grane joj se polomiše.
17 Yehova Wamphamvuzonse, amene anakudzalani, walamula kuti mavuto akugwereni. Inu a banja la Yuda ndi a banja la Israeli munachitira Yehova zoyipa ndi kumukwiyitsa pamene munkapereka nsembe zanu kwa Baala.
Jer Gospod nad vojskama, koji te je posadio, izreèe zlo po te, za zloæu doma Izrailjeva i doma Judina, koju èiniše meðu sobom da bi me razgnjevili kadeæi Valu.
18 Yehova anandiwululira ndipo ndinadziwa. Iye anatsekula maso anga kuti ndione chiwembu chawocho.
Gospod mi objavi, te znam; ti mi pokaza djela njihova.
19 Ndinali ngati mwana wankhosa wofatsa amene akupita naye kukamupha; sindinkadziwa kuti chiwembu chimene ankakonzekeracho chinkaloza ine. Iwo amati: “Tiyeni timuphe munthu ameneyu kuti dzina lake lisadzakumbukiridwenso.”
A ja bijah kao jagnje i tele koje se vodi na klanje, jer ne znadijah da se dogovaraju na me: oborimo drvo s rodom njegovijem, i istrijebimo ga iz zemlje živijeh, da mu se ime ne spominje više.
20 Koma, Inu Yehova Wamphamvuzonse, Inu amene mumaweruza molungama ndi kuyesa mitima ndi maganizo, lolani kuti ine ndione kuti mwawalipsira, pakuti mlandu wanga ndawupereka mʼmanja mwanu.
Ali, Gospode nad vojskama, sudijo pravedni, koji ispituješ bubrege i srce, daj da vidim osvetu tvoju na njima, jer tebi kazah parbu svoju.
21 “Nʼchifukwa chake Yehova akunena za anthu a ku Anatoti amene akufuna kuwononga moyo wako namanena kuti, ‘Usanenere mʼdzina la Yehova, ukatero ife tidzakupha ndi manja athu,’
Zato ovako veli Gospod za Anatoæane, koji traže dušu tvoju govoreæi: ne prorokuj u ime Gospodnje, da ne pogineš od naših ruku;
22 koma Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Ine ndidzawalanga. Achinyamata awo adzaphedwa ndi lupanga, ana awo aamuna ndi aakazi adzafa ndi njala.
Zato ovako veli Gospod nad vojskama: evo, ja æu ih pohoditi; mladiæi æe njihovi izginuti od maèa, sinovi njihovi i kæeri njihove izginuæe od gladi.
23 Sipadzakhala otsala ndi mmodzi yemwe, chifukwa ndidzalanga anthu a ku Anatoti chikadzafika chaka chawo cha chilango.’”
I neæe biti od njih ostatka; jer æu pustiti zlo na Anatoæane kad ih pohodim.

< Yeremiya 11 >