< Yesaya 8 >

1 Yehova anati kwa ine, “Tenga cholembapo chachikulu ndipo ulembepo malemba odziwika bwino: Kusakaza-Kwamsanga Kufunkha-Kofulumira.
I reèe mi Gospod: uzmi knjigu veliku i napiši u njoj pismom èovjeèijim: brz na plijen, hitar na grabež.
2 Ndipo ndidzayitana wansembe Uriya ndi Zekariya mwana wa Yeberekiya kuti akhale mboni zanga zodalirika.”
I uzeh vjerne svjedoke, Uriju sveštenika i Zahariju sina Jeverehijina.
3 Ndipo ine ndinapita kwa mneneri wamkazi, ndipo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna. Ndipo Yehova anati kwa ine, “Umutche dzina lakuti, ‘Kusakaza-Kwamsanga Kufunkha-Kofulumira.’
Potom pristupih k proroèici, i ona zatrudnje i rodi sina. A Gospod mi reèe: nadjeni mu ime: brz na plijen, hitar na grabež.
4 Mwanayo asanayambe kudziwa kuyitana kuti, ‘Ababa’ kapena ‘Amama’ chuma cha Damasiko ndi zofunkha za Samariya zidzatengedwa ndi mfumu ya ku Asiriya.”
Jer prije nego dijete nauèi vikati: oèe moj i majko moja, odnijeæe se blago Damaštansko i plijen Samarijski pred carem Asirskim.
5 Yehova anayankhulanso ndi Ine;
I još mi reèe Gospod govoreæi:
6 “Popeza anthu a dziko ili akana madzi anga oyenda mwachifatse a ku Siloamu, ndipo akukondwerera Rezini ndi mwana wa Remaliya,
Što ovaj narod ne mari za vodu Siloamsku koja teèe tiho, i raduje se Resinu i sinu Remalijinu,
7 nʼchifukwa chake Ambuye ali pafupi kubweretsa madzi amkokomo a mtsinje wa Yufurate kudzalimbana nawo; mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lake lonse lankhondo. Madziwo adzasefukira mʼngalande zake zonse ndi mʼmagombe ake onse.
Zato, evo, Gospod æe navesti na njih vodu iz rijeke silnu i veliku, cara Asirskoga i svu slavu njegovu, te æe izaæi iz svijeh potoka svojih, i teæi æe povrh svijeh bregova svojih,
8 Ndipo adzalowa mwamphamvu mʼdziko la Yuda, adzasefukira, adzapitirira mpaka kumuyesa mʼkhosi. Mapiko ake otambasuka adzaphimba dziko lako lonse, iwe Imanueli!”
I navaliæe preko Jude, plaviæe i razlivaæe se i doæi do grla, i krila æe joj se raširiti preko svekolike zemlje tvoje, Emanuilo!
9 Chitani phokoso lankhondo, inu mitundu ya anthu, ndipo munjenjemere! Tamverani, inu mayiko onse akutali. Konzekerani nkhondo ndipo munjenjemere! Konzekerani nkhondo ndipo munjenjemere!
Združujte se, narodi, ali æete se potrti; èujte svi koji ste u daljnoj zemlji: oružajte se, ali æete se potrti; oružajte se, ali æete se potrti.
10 Konzani kachitidwe kanu kankhondo, koma simudzaphula kanthu, kambiranani zochita, koma zidzalephereka, pakuti Mulungu ali nafe.
Dogovarajte se, dogovor æe vam se razbiti: recite rijeè, neæe biti od nje ništa, jer je s nama Bog.
11 Yehova anandiyankhula ine mwamphamvu, ndipo anandichenjeza kuti ndisamayende mʼnjira za anthuwa. Iye anati:
Jer mi ovako reèe Gospod uhvativši me za ruku i opomenuvši me da ne idem putem ovoga naroda, govoreæi:
12 “Usamanene kuti ndi chiwembu, chilichonse chimene anthuwa amati ndi chiwembu usamaope zimene anthuwa amaziopa, ndipo usamachite nazo mantha.
Ne govorite buna, kad god ovaj narod kaže buna, i ne bojte se èega se on boji, i ne plašite se.
13 Yehova Wamphamvuzonse ndiye amene uyenera kumuona kuti ndi woyera, ndiye amene uyenera kumuopa, ndiye amene uyenera kuchita naye mantha,
Gospoda nad vojskama svetite; i on neka vam je strah i bojazan.
14 ndipo ndiye amene adzakhala malo opatulika; koma kwa anthu a ku Yuda ndi kwa anthu a ku Israeli adzakhala mwala wopunthwitsa, mwala umene umapunthwitsa anthu, thanthwe limene limagwetsa anthu. Ndipo kwa anthu a mu Yerusalemu adzakhala ngati msampha ndi khwekhwe.
I biæe vam svetinja, a kamen za spoticanje i stijena za sablazan objema domovima Izrailjevijem, zamka i mreža stanovnicima Jerusalimskim.
15 Anthu ambiri adzapunthwapo adzagwa ndi kuthyokathyoka, adzakodwa ndi kugwidwa.”
I spotaknuæe se mnogi i pašæe i satræe se, zaplešæe se i uhvatiæe se.
16 Manga umboniwu ndipo umate malamulowa pamaso pa ophunzira anga.
Sveži svjedoèanstvo, zapeèati zakon mojim uèenicima.
17 Ndidzayembekezera Yehova, amene akubisira nkhope yake nyumba ya Yakobo. Ine ndidzakhulupirira Iyeyo.
Èekaæu dakle Gospoda, koji je sakrio lice svoje od doma Jakovljeva, i uzdaæu se u nj.
18 Onani, ine ndili pano pamodzi ndi ana amene Yehova wandipatsa, ndife zizindikiro ndi zodabwitsa kwa Aisraeli zochokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, amene amakhala pa Phiri la Ziyoni.
Evo ja i djeca koju mi je dao Gospod jesmo znak i èudo Izrailju od Gospoda nad vojskama, koji nastava na gori Sionu.
19 Anthu akakuwuza kuti kafunsire kwa oyankhula ndi mizimu, amene amayankhula monongʼona ndi mongʼungʼudza, kodi anthu sayenera kukafunsira kwa Mulungu wawo? Chifukwa chiyani amafunsira kwa anthu akufa mʼmalo mwa kwa anthu amoyo,
I ako vam reku: pitajte vraèe i gatare, koji šapæu i mrmljaju; recite: ne treba li narod da pita Boga svojega? ili æe pitati mrtve mjesto živijeh?
20 kuti akalandireko mawu enieni ndi malangizo? Ngati anthuwo sayankhula monga mwa mawu awa, mwa iwo mulibe kuwala.
Zakon i svjedoèanstvo tražite. Ako li ko ne govori tako, njemu nema zore.
21 Anthu adzayendayenda mʼdziko movutika kwambiri ali ndi njala; pamene afowokeratu ndi njala, iwo adzakwiya kwambiri ndipo adzayangʼana kumwamba ndi kutemberera mfumu yawo ndi Mulungu wawo.
I hodiæe po zemlji potucajuæi se i gladujuæi; i kad bude gladan, ljutiæe se i psovati cara svojega i Boga svojega gore.
22 Ndipo akadzayangʼana pa dziko lapansi adzangoona mavuto okhaokha ndi mdima woopsa ndi wodetsa nkhawa, ndipo adzaponyedwa mu mdima wandiweyani.
A kad pogleda na zemlju, a to nevolja i mrak i teška muka, i on zagnan u tamu.

< Yesaya 8 >