< Yesaya 7 >

1 Pamene Ahazi mwana wa Yotamu, mdzukulu wa Uziya anali mfumu ya Yuda, Rezini mfumu ya Siriya ndi Peka mwana wa Remaliya, mfumu ya Israeli anabwera kudzathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu, koma sanathe kuwugonjetsa.
Il arriva du temps d'Achaz, fils de Joatham, fils d'Ozias, roi de Juda, que Rasin, roi de Syrie, avec Phacée, fils de Romélie, roi d'Israël, monta contre Jérusalem pour l'attaquer; mais il ne put s'en emparer.
2 Tsono nyumba ya Davide inawuzidwa kuti, “Dziko la Siriya lagwirizana ndi Efereimu.” Choncho mfumu Ahazi ndi anthu ake ananjenjemera, monga momwe mitengo ya mʼnkhalango imagwedezekera ndi mphepo.
On annonça à la maison de David cette nouvelle: " La Syrie est campée en Ephraïm. " Alors le cœur du roi et le cœur de son peuple furent agités comme les arbres de la forêt sont agités par le vent.
3 Pamenepo Yehova anawuza Yesaya kuti, “Tuluka, iwe ndi mwana wako Seariyasubu, mupite mukakumane ndi Ahazi kumapeto kwa ngalande yamadzi yochokera ku Dziwe Lakumtunda, pa msewu wopita ku Munda wa mmisiri wochapa nsalu.
Et Yahweh dit à Isaïe: " Sors à la rencontre d'Achaz, toi et Schéar-Jasub, ton fils, vers l'extrémité du canal de l'étang supérieur, sur le chemin du champ du foulon.
4 Ukamuwuze kuti, ‘Chenjera, khala phee ndipo usaope. Usataye mtima chifukwa cha zitsa ziwiri zomwe zikufuka, chifukwa cha ukali woopsa wa Rezini ndi Siriya, ndiponso wa Peka mwana wa Remaliya.
Et tu lui diras: Prends garde, tiens-toi tranquille, ne crains point, et que ton cœur ne défaille point devant ces deux bouts de tisons fumants, à cause de la fureur de Rasin et de la Syrie, et du fils de Romélie.
5 Mfumu ya Siriya, Efereimu ndi mwana wa Remaliya apangana kuti akuchitire choyipa. Akunena kuti,
Parce que la Syrie a médité le mal contre toi ainsi qu'Ephraïm et le fils de Romélie, en disant:
6 ‘Tiyeni tikalimbane ndi Yuda. Tiyeni tiliwononge ndi kuligawa; tiligawane pakati pathu, ndipo tilonge ufumu mwana wa Tabeeli kumeneko.’
" Montons contre Juda, jetons-le dans l'épouvante, envahissons-le, et établissons-y pour roi le fils de Tabéel;
7 Komabe zimene akunena Ambuye Yehova ndi izi: “‘Zimenezo sizidzatheka, sizidzachitika konse,
ainsi parle le Seigneur Yahweh: Cela n'aura pas d'effet, cela ne sera pas!
8 pakuti Siriya amadalira Damasiko, ndipo Damasiko amadalira mfumu Rezini basi. Zisanathe zaka 65 Efereimu adzawonongedwa kotheratu, sadzakhalanso mtundu wa anthu.
Car la tête de la Syrie, c'est Damas, et la tête de Damas, c'est Rasin; et encore soixante-cinq ans, et Ephraïm aura cessé d'être un peuple.
9 Dziko la Efereimu limadalira Samariya ndipo Samariya amadalira mwana wa Remaliya basi. Mukapanda kulimbika pa chikhulupiriro chanu, ndithu simudzalimba konse.’”
Et la tête d'Ephraïm, c'est Samarie, et la tête de Samarie, c'est le fils de Romélie. Si vous ne croyez pas, vous ne subsisterez pas! "
10 Yehova anayankhulanso ndi Ahazi,
Yahweh parla encore à Achaz, en disant:
11 “Pempha chizindikiro kwa Yehova Mulungu wako, chikhale chozama ngati manda kapena chachitali ngati mlengalenga.” (Sheol h7585)
" Demande un signe à Yahweh, ton Dieu, demande-le dans les profondeurs du schéol ou dans les hauteurs du ciel. " (Sheol h7585)
12 Koma Ahazi anati, “Ine sindipempha; sindikufuna kuyesa Yehova.”
Mais Achaz dit: " Je ne le demanderai pas, je ne tenterai pas Yahweh. "
13 Apo Yesaya anati, “Imva tsopano, iwe nyumba ya Davide! Kodi sikokwanira kutopetsa anthu? Kodi mudzayeseranso kutopetsa Mulungu wanga?
Et Isaïe dit: " Ecoutez, maison de David: Est-ce trop peu pour vous de fatiguer les hommes, que vous fatiguiez aussi mon Dieu?
14 Nʼchifukwa chake Ambuye mwini adzakupatsani chizindikiro: Onani, namwali adzakhala woyembekezera ndipo adzabala mwana wamwamuna, ndipo mwanayo adzamutcha Imanueli.
C'est pourquoi le Seigneur lui-même vous donnera un signe: Voici que la Vierge a conçu, et elle enfante un fils, et elle lui donne le nom d'Emmanuel.
15 Azidzadya chambiko ndi uchi, mpaka atadziwa kukana choyipa ndi kusankha chabwino.
Il mangera de la crème et du miel, jusqu'à ce qu'il sache rejeter le mal et choisir le bien.
16 Koma nthawi yokana choyipa ndi kusankha chabwino kwa mwanayo isanafike, mayiko a mafumu awiri amene amakuopsaniwo adzakhala atasanduka bwinja.
Car avant que l'enfant sache rejeter le mal et choisir le bien, le pays dont tu redoutes les deux rois sera dévasté.
17 Yehova adzabweretsa pa inu, pa anthu anu ndiponso pa nyumba ya bambo wanu masiku a mavuto woti sanakhalepo kuyambira tsiku limene Efereimu anapatukana ndi Yuda. Yehova adzabweretsa mfumu ya ku Asiriya.”
Yahweh fera venir sur toi et sur ton peuple, et sur la maison de ton père, des jours tels qu'il n'en est pas venu depuis le jour où Ephraïm s'est séparé de Juda, — le roi d'Assyrie. "
18 Tsiku limenelo Yehova adzalizira likhweru ntchentche zochokera ku mitsinje yakutali ku Igupto, ndiponso njuchi zochokera ku dziko la Asiriya.
En ce jour-là, Yahweh sifflera la mouche qui est à l'extrémité des fleuves d'Egypte, et l'abeille qui est au pays d'Assyrie.
19 Onsewo adzafika ndi kudzakhazikika mu zigwa zozama, mʼmingʼalu ya matanthwe ndi mʼzitsamba zonse zaminga ndiponso ponse pamene pali malo omwetsera ziweto.
Elles viendront et se poseront toutes dans les vallées escarpées et dans les fentes des rochers, sur tous les buissons et sur tous les pâturages.
20 Tsiku limenelo Ambuye adzalemba ganyu ometa ochokera kutsidya kwa Mtsinje, ndiye mfumu ya ku Asiriya, kudzameta tsitsi lanu la ku mutu ndi la mʼmiyendo ndi ndevu zomwe.
En ce jour-là, le Seigneur rasera avec un rasoir qu'il aura loué au delà du Fleuve — avec le roi d'Assyrie, — la tête et le poil des pieds, et il enlèvera aussi la barbe.
21 Tsiku limenelo adzangosunga ngʼombe yayikazi yayingʼono ndi mbuzi ziwiri.
En ce jour-là, un homme nourrira une vache et deux brebis,
22 Ndipo chifukwa cha kuchuluka kwa mkaka umene ziwetozi zidzapereka, munthuyo azidzadya chambiko. Aliyense amene adzatsalire mʼdzikomo azidzadya chambiko ndi uchi.
et, à cause de l'abondance du lait qu'elles donneront, on ne mangera plus que de la crème; car c'est de la crème et du miel que mangeront tous ceux qui seront restés dans le pays.
23 Tsiku limenelo, paliponse pamene panali mitengo ya mpesa 1,000 ndipo mtengo wake ndi wokwana masekeli asiliva 1,000, padzamera mkandankhuku ndi minga.
En ce jour-là, tout endroit où il y avait mille ceps de vigne, valant mille pièces d'argent, sera couvert de ronces et d'épines.
24 Anthu adzapita kumeneko kukachita uzimba ali ndi uta ndi mivi, popeza kuti mʼdziko monsemo mudzakhala mkandankhuku ndi minga.
On y entrera avec des flèches et avec l'arc, car tout le pays ne sera que ronces et épines.
25 Ndipo mʼmapiri monse mʼmene kale munkalimidwa ndi khasu, simudzapitamo kuopa mkandankhuku ndi minga; malowo adzasanduka odyetserako ngʼombe ndi nkhosa.
Et sur toutes les montagnes que l'on cultivait avec le sarcloir, tu n'iras plus, par crainte des ronces et des épines, elles seront un pâturage de bœufs, et une terre foulée par les brebis.

< Yesaya 7 >