< Yesaya 65 >

1 “Ndinali wokonzeka kumva mapemphero a amene sankandipempha kanthu; ndipo ndinalola kuti anthu amene ankandifunafuna kuti andipeze. Kwa mtundu wa anthu umene sunkapempha chithandizo kwa Ine, ndinati, ‘Ine ndili pano, Ine ndili pano.’
Objawiłem się tym, którzy o mnie nie pytali, zostałem znaleziony przez tych, którzy mnie nie szukali. Do narodu, który się nie nazywał moim imieniem, mówiłem: Oto jestem, oto jestem.
2 Tsiku lonse ndatambasulira manja anga anthu owukira aja, amene amachita zoyipa, natsatira zokhumba zawo.
Cały dzień wyciągałem swoje ręce do ludu buntowniczego, który kroczy drogą niedobrą, za własnymi myślami;
3 Ndatambasulira manja anga anthu aja amene nthawi zonse amandikwiyitsa mopanda manyazi. Iwo amapereka nsembe mʼminda ndi kufukiza lubani pa maguwa ansembe a njerwa.
Do ludu, który stale i zuchwale pobudza mnie do gniewu, składając ofiary w ogrodach i paląc kadzidło na cegłach;
4 Amakatandala ku manda ndipo amakachezera usiku wonse kumalo obisika. Amadya nyama ya nkhumba, ndipo mʼmiphika mwawo muli msunzi wa nyama yodetsedwa.
Który przesiaduje na grobach i nocuje przy swoich bożkach, który je mięso wieprzowe, a obrzydliwa polewka [jest] w jego naczyniach;
5 Amawuza ena kuti, ‘Khala patali usandiyandikire, chifukwa ungatengere kupatulika kwanga!’ Ukali wanga pa anthu otere uli ngati utsi mphuno zanga, ngati moto umene umayaka tsiku lonse.
I mówi: Odsuń się, nie zbliżaj się do mnie, bo jestem świętszy od ciebie. On jest dymem w moich nozdrzach i ogniem płonącym przez cały dzień.
6 “Taonani, ndatsimikiza kale mlandu ndi chilango chawo; sindidzakhala chete koma ndidzawalanga kwathunthu chifukwa cha machimo awo
Oto zapisano to przede mną. Nie zamilknę, ale oddam i odpłacę im w zanadrzu;
7 ndi a makolo awo,” akutero Yehova. “Chifukwa anapereka nsembe zopsereza pa mapiri ndi kundinyoza Ine pa zitunda zawo, Ine ndidzawalanga kwathunthu potsata zimene anachita kale.”
Za wasze nieprawości i nieprawości waszych ojców, mówi PAN, którzy palili kadzidło na górach i hańbili mnie na pagórkach; dlatego wymierzę im w zanadrze za ich dawne czyny.
8 Yehova akuti, “Pamene madzi akanapezeka mu phava la mphesa ndipo anthu amati, ‘Musawononge phavalo, popeza madzi ena abwino akanalimobe mʼphavalo,’ Inenso chifukwa cha mtumiki wanga; sindidzawononga onse.
Tak mówi PAN: Jak wtedy, gdy znajduje się wino w kiści i mówi się: Nie psuj go, bo w nim jest błogosławieństwo, tak i ja uczynię przez wzgląd na moje sługi – nie zniszczę ich wszystkich.
9 Ndidzatulutsa zidzukulu mʼbanja la Yakobo, ndipo a banja la Yuda adzalandira mapiri anga ngati cholowa chawo. Anthu anga osankhidwa adzalandira zimenezi, ndipo atumiki anga adzakhala kumeneko.
Bo wywiodę z Jakuba potomstwo, a z Judy dziedzica moich gór. Moi wybrani posiądą je i moi słudzy będą tam mieszkać.
10 Chigwa cha Saroni chidzakhala kodyetserako nkhosa, ndipo chigwa cha Akori chidzakhala malo opumirako ngʼombe kwa anthu anga ondifunafuna Ine.
A Szaron stanie się pastwiskiem dla owiec, a dolina Akor legowiskiem dla wołów – to dla mojego ludu, który mnie szukał.
11 “Koma inu amene mumasiya Yehova ndi kuyiwala phiri langa lopatulika, amene munamukonzera Gadi chakudya ndi kuthirira Meni chakumwa,
Ale was, którzy opuściliście PANA, którzy zapominacie o mojej świętej górze, którzy zastawiacie stół dla tego wojska i składacie ofiary z płynów temu mnóstwu;
12 ndidzakuperekani ku lupanga ngati nsembe, ndipo nonse mudzaphedwa; chifukwa simunayankhe pamene ndinakuyitanani, ndinayankhula koma simunamvere. Munachita zoyipa pamaso panga ndipo munasankha kuchita zoyipa zomwe sindikondwera nazo.”
Was przeznaczę pod miecz i wy wszyscy schylicie się na rzeź, ponieważ wołałem, a nie odezwaliście się, mówiłem, a nie słyszeliście, ale czyniliście to, co złe w moich oczach, i wybraliście to, co mi się nie podobało.
13 Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, “Atumiki anga adzadya, koma inu mudzakhala ndi njala; atumiki anga adzamwa, koma inu mudzakhala ndi ludzu; atumiki anga adzakondwa, koma inu mudzakhala ndi manyazi.
Dlatego tak mówi Pan BÓG: Oto moi słudzy będą jeść, a wy będziecie głodni. Oto moi słudzy będą pić, a wy będziecie spragnieni. Oto moi słudzy będą się radować, a wy będziecie zawstydzeni.
14 Atumiki anga adzayimba mosangalala, koma inu mudzalira kwambiri chifukwa chovutika mu mtima ndipo mudzalira mofuwula chifukwa mudzamva kuwawa mu mtima.
Oto moi słudzy będą śpiewać z radości serca, a wy będziecie krzyczeć z boleści serca i zawodzić z powodu zrozpaczonego ducha.
15 Anthu anga osankhidwa adzatchula dzina lanu potemberera. Ambuye Yehova adzakuphani, koma atumiki ake adzawapatsa dzina lina.
I zostawicie swoje imię moim wybranym na przekleństwo, gdyż Pan BÓG zabije was, a swoje sługi nazwie innym imieniem.
16 Aliyense wopempha dalitso mʼdzikomo adzachita zimenezo kwa Mulungu woona; ndipo aliyense wochita malumbiro mʼdzikomo adzalumbira mwa Mulungu woona. Pakuti mavuto akale adzayiwalika ndipo adzachotsedwa pamaso panga.
Ten, który będzie sobie błogosławił na ziemi, będzie sobie błogosławił w Bogu prawdziwym, a kto będzie przysięgał na ziemi, będzie przysięgał na Boga prawdziwego, bo dawne uciski pójdą w zapomnienie i będą zakryte przed moimi oczami.
17 “Taonani, ndikulenga mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano. Zinthu zakale sizidzakumbukika, zidzayiwalika kotheratu.
Oto bowiem stworzę nowe niebiosa i nową ziemię i nie będą wspominane pierwsze rzeczy ani nie przyjdą na myśl.
18 Koma inu mukhale osangalala ndi okondwa mpaka muyaya chifukwa cha zimene ndikulenga, pakuti ndikulenga Yerusalemu kukhala malo wosangalatsa ndipo anthu ake adzakhala achimwemwe.
Lecz weselcie się i radujcie na wieki wieków z tego, co ja stworzę, bo oto stworzę Jerozolimę radością i jej lud weselem.
19 Ine ndidzakondwa chifuwa cha Yerusalemu ndipo ndidzasangalala chifukwa cha anthu anga. Kumeneko sikudzamvekanso kulira ndi mfuwu wodandaula.
I będę się radować z powodu Jerozolimy i weselić z powodu mojego ludu, a nie będzie już słychać w nim głosu płaczu ani narzekania.
20 “Ana sadzafa ali akhanda ndipo nkhalamba zonse zidzakwaniritsa zaka zawo zonse. Wamngʼono mwa iwo adzafa ali ndi zaka 100. Amene adzalephere kufika zaka 100 adzatengedwa kukhala wotembereredwa.
Nie będzie tam już ani niemowlęcia [żyjącego] tylko kilka dni, ani starca, który by nie dożył swoich dni, bo dziecko umrze jako stuletni, ale grzesznik, choćby miał i sto lat, będzie przeklęty.
21 Anthu adzamanga nyumba ndi kukhalamo, adzadzala mpesa ndipo adzadya zipatso zake.
Pobudują też domy i będą w nich mieszkać, zasadzą winnice i będą jeść z nich owoce.
22 Sadzamanganso nyumba anthu ena nʼkukhalamo, kapena kudzala ndi ena nʼkudya. Pakuti anthu anga adzakhala ndi moyo wautali ngati mitengo. Osankhidwa anga adzakondwera ndi ntchito ya manja awo nthawi yayitali.
Nie będą budować, by ktoś inny tam mieszkał, nie będą sadzić, by ktoś inny jadł, bo dni mojego ludu będą jak dni drzewa i moi wybrani długo będą korzystać z dzieła swoich rąk.
23 Sadzagwira ntchito pachabe kapena kubereka ana kuti aone tsoka; chifukwa adzakhala anthu odalitsidwa ndi Yehova, iwowo pamodzi ndi adzukulu awo omwe.
Nie będą trudzić się na próżno ani rodzić, aby się bać, gdyż są potomstwem błogosławionym przez PANA, oni i ich potomkowie wraz z nimi.
24 Ndidzawayankha ngakhale asanathe nʼkupempha komwe. Pamene akuyankhula kumene Ine ndidzakhala nditamva kale.
I będzie tak, że zanim zawołają, ja się odezwę, gdy jeszcze będą mówić, ja wysłucham.
25 Mʼmbulu ndi mwana wankhosa wamkazi zidzadyera pamodzi. Mkango udzadya udzu monga ngʼombe, koma fumbi ndiye chidzakhale chakudya cha njoka. Pa phiri langa lopatulika sipadzakhala chinthu chopweteka kapena chowononga,” akutero Yehova.
Wilk z barankiem paść się będą razem, lew jak wół będzie jeść słomę i proch będzie pokarmem węża. Nie będą szkodzić ani niszczyć na całej mojej świętej górze, mówi PAN.

< Yesaya 65 >