< Yesaya 62 >

1 Chifukwa chokonda Ziyoni sindidzakhala chete, chifukwa chokonda Yerusalemu sindidzakhala chete, mpaka chilungamo chake chitaoneka poyera ngati kuwala, ndi chipulumutso chake chitaoneka ngati sakali yoyaka.
Siona radi neæu umuknuti, i Jerusalima radi neæu se umiriti, dokle ne izaðe kao svjetlost pravda njegova i spasenje se njegovo razgori kao svijeæa.
2 Mitundu ya anthu idzaona iwe utapambana pa nkhondo ndipo mafumu onse adzaona ulemerero wako. Adzakuyitanira dzina latsopano limene adzakupatse ndi Yehova.
Tada æe vidjeti narodi pravdu tvoju i svi carevi slavu tvoju, i prozvaæeš se novijem imenom, koje æe usta Gospodnja izreæi.
3 Udzakhala ngati chipewa chaulemerero mʼdzanja la Yehova, ndi ngati nduwira yaufumu mʼdzanja la Mulungu wako.
I biæeš krasan vijenac u ruci Gospodnjoj i carska kruna u ruci Boga svojega.
4 Sadzakutchanso “Wosiyidwa,” ndipo dziko lako silidzatchedwanso “Chipululu.” Koma dzina lako latsopano lidzakhala “Ndakondwera naye.” Ndipo dziko lako lidzatchedwa “Wokwatiwa.” Chifukwa Yehova akukondwera nawe, ndipo adzakhala ngati mwamuna wa dziko lako.
Neæeš se više zvati ostavljena, niti æe se zemlja tvoja zvati pustoš, nego æeš se zvati milina moja i zemlja tvoja udata, jer æeš biti mio Gospodu i zemlja æe tvoja biti udata.
5 Monga mnyamata amakwatira namwali, momwenso mmisiri wodzakumanga adzakukwatira; monga mkwati amakondwera ndi mkwatibwi, chonchonso Mulungu adzakondwera nawe.
Jer kao što se momak ženi djevojkom, tako æe se sinovi tvoji oženiti tobom; i kako se raduje ženik nevjesti, tako æe se tebi radovati Bog tvoj.
6 Iwe Yerusalemu, pa malinga ako ndayikapo alonda; sadzakhala chete usana kapena usiku. Inu amene mumakumbutsa Yehova za malonjezo ake musapumule.
Na zidovima tvojim, Jerusalime, postavih stražare, koji neæe umuknuti nigda, ni danju ni noæu. Koji pominjete Gospoda, nemojte muèati.
7 Musamupatse mpata wopuma mpaka atakhazikitsa Yerusalemu kukhala mzinda umene dziko lapansi lidzawutamande.
I ne dajte da se umukne o njemu dokle ne utvrdi i uèini Jerusalim slavom na zemlji.
8 Yehova analumbira atakweza dzanja lake. Anati, “Sindidzaperekanso tirigu wako kuti akhale chakudya cha adani ako, ndipo alendo sadzamwanso vinyo wako watsopano pakuti unamuvutikira.
Zakle se Gospod desnicom svojom i krjepkom mišicom svojom: neæu više dati žita tvojega neprijateljima tvojim da jedu, niti æe tuðini piti vina tvojega, oko kojega si se trudio;
9 Koma amene amakakolola ndiwo amene adzadye buledi ndi kutamanda Yehova, ndipo amene amasonkhanitsa pamodzi mphesa ndiwo amene adzamwe vinyo mʼmabwalo a Nyumba yanga.”
Nego koji ga žanju, oni æe ga jesti i hvaliti Gospoda, i koji ga beru oni æe ga piti u trijemovima svetinje moje.
10 Tulukani, dutsani pa zipata! Konzerani anthu njira. Lambulani, lambulani msewu waukulu! Chotsani miyala. Kwezani mbendera kuti mitundu ya anthu izione.
Proðite, proðite kroz vrata, pripravite put narodu; poravnite, poravnite put, uklonite kamenje, podignite zastavu narodima.
11 Yehova walengeza ku dziko lonse lapansi kuti, Awuzeni anthu a ku Yerusalemu kuti, “Taonani, chipulumutso chanu chikubwera; Yehova akubwera ndi mphotho yake akubwera nazo zokuyenerani.”
Evo, Gospod oglasi do krajeva zemaljskih; recite kæeri Sionskoj: evo, spasitelj tvoj ide; evo, plata je njegova kod njega i djelo njegovo pred njim.
12 Iwo adzatchedwa Anthu Opatulika, owomboledwa a Yehova; ndipo adzakutchani “Okondwa a Yehova” “Mzinda umene Yehova sanawusiye.”
I oni æe se prozvati narod sveti, iskupljenici Gospodnji; a ti æeš se prozvati: traženi, grad neostavljeni.

< Yesaya 62 >