< Yesaya 57 >

1 Anthu olungama amafa, ndipo palibe amene amalingalira mu mtima mwake; anthu odzipereka amatengedwa, ndipo palibe amene amamvetsa chifukwa chake. Anthu olungama amatengedwa kuti tsoka lisawagwere.
Sprawiedliwy ginie, a nikt nie bierze sobie tego do serca. Ludzie pobożni odchodzą, a nikt nie zważa na to, że sprawiedliwy jest zabierany przed nadejściem zła.
2 Iwo amene amakhala moyo wolungama amafa mwamtendere; amapeza mpumulo pamene agona mu imfa.
Dostąpi pokoju i odpocznie na swoim łożu każdy, kto postępuje uczciwie.
3 “Bwerani kuno, anthu ochita zoyipa, inu muli ngati zidzukulu za mkazi wachigololo ndi wadama!
Ale wy zbliżcie się tutaj, synowie czarownicy, potomstwo cudzołożnika i nierządnicy.
4 Kodi inu mukuseka yani? Kodi mukumunena ndani ndi kupotoza pakamwa panu? Kodi inu si ana owukira, zidzukulu za anthu abodza?
Z kogo się naigrawacie? Na kogo rozdziawiacie usta i wywieszacie język? Czy nie jesteście synami nierządu, potomstwem fałszu;
5 Inu mumapembedza mafano pamene mumalobodoka ndi zilakolako zanu pakati pa mitengo ya thundu, ndiponso pa tsinde pa mtengo uliwonse wa nthambi zambiri. Mumapereka ana anu ngati nsembe mu zigwa ndiponso mʼmingʼalu ya mʼmatanthwe.
[Wy], którzy uprawiacie nierząd z posągami pod każdym zielonym drzewem, zabijając swoje dzieci przy potokach, pod wysokimi skałami?
6 Mafano a pakati pa miyala yosalala ya mu zigwa ndiye chuma chanu. Inde, ndiye gawo lanu. Mumapereka chopereka cha chakumwa kwa mafanowo, ndipo mumaperekanso chopereka cha chakudya. Kodi zimenezi zingandichititse kuti ndikukomereni mtima?
Wśród gładkich kamieni potoku jest twój dział. Właśnie one są twoim losem, na nie wylewasz ofiarę z płynów i ofiarowujesz ofiarę z pokarmów. Czyż w tym miałbym mieć upodobanie?
7 Inu munayiwala bedi lanu pa phiri lalitali ndi looneka kutali. Mumapita kumeneko kukapereka nsembe zanu.
Na górze wysokiej i wyniosłej postawiłaś swoje łoże i tam wstępowałaś, aby składać ofiary.
8 Mʼnyumba mwanu mwayika mafano kuseri kwa zitseko ndiponso pa mphuthu. Mwandisiya Ine, mwavula zovala zanu. Bedi lanu mwalikulitsa ndipo mwakwera ndi zibwenzi zanu, ndiye mwazilipira kuti mugone nazo. Kumene mwakwaniritsa zilakolako zanu zoyipa.
A za drzwiami i za odrzwiami postawiłaś swoją pamiątkę, gdyż odchodząc ode mnie, odkrywałaś się [innym], wstąpiłaś i rozszerzyłaś swoje łoże, czyniąc z nimi przymierze; kochałaś ich łoże w każdym miejscu, gdzie [je] widziałaś.
9 Mumapita kukapembedza fano la Moleki mutatenga mafuta ndi zonunkhira zochuluka. Munachita kutumiza akazembe anu kutali; inu ngakhale munapita ku manda kwenikweniko! (Sheol h7585)
Chodziłaś także do króla z olejkiem i mnożyłaś swoje wonności; posłałaś daleko swoich posłańców, a poniżałaś się aż do grobu. (Sheol h7585)
10 Inu mumatopa ndi maulendo anu, koma simunathe kunena kuti, ‘Nʼzopanda phindu.’ Munapezako kumeneko zokhumba zanu nʼchifukwa chake simunalefuke.
Zmęczyłaś się licznymi swymi drogami, ale nie powiedziałaś: Na próżno. Znalazłaś pomoc w swojej ręce, dlatego nie osłabłaś.
11 “Kodi ndani amene mwachita naye mantha ndi kumuopa, kotero kuti mwakhala mukundinamiza, ndipo Ine simundikumbukira nʼkomwe, kapena kuganizirapo mʼmitima yanu za Ine? Kodi mwaleka kundiopa chifukwa choti ndakhala chete nthawi yayitali?
Kogo się bałaś i lękałaś, że skłamałaś, i nie pamiętałaś o mnie ani nie wzięłaś sobie tego do serca? Czy ja nie milczałem, i to od dawna, a ty mnie się nie boisz?
12 Koma ndaonetsa poyera ntchito zanu zomwe mumati nʼzolungama, ndi mafano anu kuti nʼzosathandiza.
Opowiem twoją sprawiedliwość i twoje uczynki, które nic ci nie pomogą.
13 Pamene mufuwula kupempha thandizo, mafano anu amene munasonkhanitsawo ndiyetu akupulumutseni! Mphepo idzanyamula mafano anu onsewo, mpweya chabe udzawulutsa mafanowo. Koma munthu amene amadalira ine adzalandira dziko lokhalamo. Phiri langa lopatulika lidzakhala lakelake.”
Gdy zawołasz, niech wybawi cię twoja zgraja; ale wszystkich ich wiatr rozniesie i pochwyci marność. Lecz ten, który mi zaufa, odziedziczy ziemię i posiądzie moją świętą górę.
14 Ndipo panamveka mawu akuti, “Undani, undani, konzani msewu! Chotsani zotchinga pa njira yoyendamo anthu anga.”
I powiedzą: Wyrównajcie, wyrównajcie, przygotujcie drogę, usuńcie przeszkody z drogi mojego ludu.
15 Pakuti Iye amene ali Wamkulu ndi Wopambanazonse, amene alipo nthawi zonse, amene dzina lake ndi Woyerayo, akunena kuti, “Ndimakhala pamalo aulemu ndi opatulika, koma ndimakhalanso ndi munthu wodzichepetsa ndi wosweka mtima kuti odzichepetsawo ndiwalimbitse ndi kuwachotsa mantha osweka mtima.
Tak bowiem mówi Wysoki i Wyniosły, który zamieszkuje wieczność, którego imię to Święty: Ja, który mieszkam na wysokościach, na miejscu świętym, mieszkam i z tym, który jest skruszony i uniżony w duchu, aby ożywić ducha pokornych i ożywić serce skruszonych.
16 Sindidzawatsutsa anthu mpaka muyaya kapena kuwapsera mtima nthawi zonse, popeza kuti ndinalenga anthu anga ndi kuwapatsa mpweya wamoyo.
Nie będę się spierał na wieki ani nie będę wiecznie się gniewał, bo zemdlałby przede mną duch i dusze, które uczyniłem.
17 Ine ndinakwiya kwambiri chifukwa cha tchimo lawo ladyera; ndinawalanga ndi kuwafulatira mokwiya, koma iwo anapitirirabe kuchita ntchito zawo zoyipa.
Z powodu jego niegodziwej chciwości rozgniewałem się i uderzyłem go. Ukryłem się i rozgniewałem, on jednak był uparty i poszedł drogą swego serca.
18 Ndaona zochita zawo, komabe ndidzawachiritsa; kuwapumulitsa ndi kuwapatsa mtendere,
Widziałem jego drogi, lecz uzdrowię go. Poprowadzę go i przywrócę mu pociechę, również tym, którzy z nim płaczą.
19 anthu olira a mu Israeli adzanditamanda ndi milomo yawo. Anthu amene ali kutali ndi apafupi pomwe ndidzawapatsa mtendere,” “Ndipo ndidzawachiritsa.” Akutero Yehova.
Stworzę owoc warg: Pokój, pokój dalekiemu i bliskiemu, mówi PAN; i tak uzdrowię go.
20 Koma anthu oyipa ali ngati nyanja yowinduka, yosatha kukhala bata, mafunde ake amaponya matope ndi ndere.
Lecz bezbożni będą jak wzburzone morze niemogące się uspokoić, którego wody wyrzucają muł i błoto.
21 “Palibe mtendere kwa oyipa,” akutero Mulungu wanga.
Nie ma pokoju dla bezbożnych, mówi mój Bóg.

< Yesaya 57 >