< Yesaya 55 >

1 “Bwerani, inu nonse amene muli ndi ludzu, bwerani madzi alipo; ndipo inu amene mulibe ndalama bwerani, mudzagule chakudya kuti mudye! Bwerani mudzagule vinyo ndi mkaka osalipira ndalama, osalipira chilichonse.
Ho, euery one that thirsteth, come ye to the waters, and ye that haue no siluer, come, bye and eate: come, I say, bye wine and milke without siluer and without money.
2 Chifukwa chiyani ndalama zanu mukuwonongera zinthu zimene samadya, ndipo mukuwononga malipiro anu pa zinthu zimene sizikhutitsa? Tamverani, mvetsetsani zimene ndikunena kuti mudye zimene zili zabwino; ndipo mudzisangalatse.
Wherefore doe ye lay out siluer and not for bread? and your labour without being satisfied? hearken diligently vnto me, and eate that which is good, and let your soule delite in fatnes.
3 Tcherani makutu ndipo mubwere kwa Ine; mvereni Ine, kuti mukhale ndi moyo. Ndidzachita nanu pangano losatha, chikondi changa chija chosasinthika ndi chodalirika ndinalonjeza Davide.
Encline your eares, and come vnto me: heare, and your soule shall liue, and I will make an euerlasting couenant with you, euen the sure mercies of Dauid.
4 Taonani, ine ndamusankha kuti akhale mboni yanga kwa mitundu ya anthu, kuti akhale mtsogoleri ndi wolamulira mitundu ya anthu.
Beholde, I gaue him for a witnes to the people, for a prince and a master vnto the people.
5 Ndithu inu mudzayitanitsa mitundu ya anthu imene simuyidziwa, ndipo mitundu ya anthu imene sikudziwani idzabwera ndi liwiro kwa inu. Izi zidzatero chifukwa Yehova Mulungu wanu, Woyerayo wa Israeli, wakuvekani ulemerero.”
Beholde, thou shalt call a nation that thou knowest not, and a nation that knew not thee, shall runne vnto thee, because of the Lord thy God, and the holy one of Israel: for hee hath glorified thee.
6 Funafunani Yehova pamene Iye akupezeka. Mupemphere kwa Iye pamene ali pafupi.
Seeke ye the Lord while he may be found: call ye vpon him while he is neere.
7 Woyipa asiye makhalidwe ake oyipa, ndipo wosalungama asinthe maganizo ake oyipa. Abwerere kwa Yehova, ndipo adzamuchitira chifundo, ndi kwa Mulungu wathu, pakuti adzamukhululukira koposa.
Let the wicked forsake his wayes, and the vnrighteous his owne imaginations, and returne vnto the Lord, and he wil haue mercy vpon him: and to our God, for hee is very ready to forgiue.
8 “Pakuti maganizo anga siwofanana ndi maganizo anu, ngakhale njira zanu si njira zanga,” akutero Yehova.
For my thoughtes are not your thoughts, neither are your wayes my wayes, sayth the Lord.
9 “Monga momwe mlengalenga muli kutali ndi dziko lapansi, momwemonso zochita zanga nʼzolekana kutali ndi zochita zanu, ndipo maganizo anga ndi osiyana kutali ndi maganizo anu.
For as ye heauens are higher then the earth, so are my wayes higher then your wayes, and my thoughtes aboue your thoughts.
10 Monga mvula ndi chisanu chowundana zimatsika kuchokera kumwamba, ndipo sizibwerera komweko koma zimathirira dziko lapansi. Ndipo zimameretsa ndi kukulitsa zomera kenaka nʼkupatsa mlimi mbewu ndi chakudya.
Surely as the raine commeth downe and the snow from heauen, and returneth not thither, but watereth the earth and maketh it to bring forth and bud, that it may giue seede to the sower, and bread vnto him that eateth,
11 Ndi mmenenso amachitira mawu ochokera mʼkamwa mwanga. Sadzabwerera kwa Ine kopanda phindu lake, koma adzachita zonse zimene ndifuna, ndipo adzakwaniritsa cholinga chimene ndinawatumira.
So shall my worde be, that goeth out of my mouth: it shall not returne vnto me voyde, but it shall accomplish that which I will, and it shall prosper in the thing whereto I sent it.
12 Inu mudzatuluka mu mzindawo mwachimwemwe ndipo adzakutsogolerani mwamtendere; mapiri ndi zitunda zidzakuyimbirani nyimbo, ndipo mitengo yonse yamʼthengo idzakuwombereni mʼmanja.
Therefore ye shall go out with ioy, and be led forth with peace: the mountaines and the hilles shall breake foorth before you into ioye, and all the trees of the fielde shall clap their handes.
13 Mʼmalo mʼmene tsopano muli mitengo ya minga mudzamera mitengo ya payini, ndipo kumene kuli mkandankhuku kudzamera mchisu. Zimenezi zidzakhala chikumbutso cha Yehova, ngati chizindikiro chamuyaya, chimene sichidzafafanizika konse.”
For thornes there shall grow firre trees: for nettles shall growe the myrrhe tree, and it shalbe to the Lord for a name, and for an euerlasting signe that shall not be taken away.

< Yesaya 55 >