< Yesaya 54 >

1 “Sangalala, iwe mayi wosabala, iwe amene sunabalepo mwana; imba nyimbo, ndi kufuwula mwachimwemwe, iwe amene sunamvepo ululu wa pobereka; chifukwa mkazi wosiyidwa adzakhala ndi ana ambiri kuposa mkazi wokwatiwa,” akutero Yehova.
Śpiewaj, niepłodna, która nie rodziłaś, śpiewaj głośno i krzycz, która nie zaznałaś bólów rodzenia. Więcej bowiem jest synów opuszczonej niż synów zamężnej, mówi PAN.
2 Kulitsa malo omangapo tenti yako, tambasula kwambiri nsalu zake, usaleke; talikitsa zingwe zako, limbitsa zikhomo zako.
Rozszerz miejsce swego namiotu, a niech rozciągają zasłony twoich mieszkań; nie oszczędzaj, wydłuż swoje powrozy i wzmocnij swoje kołki.
3 Pakuti udzasendeza malire ako kumanja ndi kumanzere; ndipo zidzukulu zako zidzalanda dziko la anthu a mitundu ina ndipo zidzakhala mʼmizinda yawo yosiyidwa.
Rozprzestrzenisz się bowiem na prawo i lewo, a twoje potomstwo odziedziczy narody i zaludni spustoszone miasta.
4 “Usachite mantha; sadzakunyozanso. Usakhumudwe; sudzapeputsidwanso. Udzayiwala za manyazi zimene zinakuchitikira nthawi ya unyamata wako ndipo za manyazi zimene zinakuchitikira pa nthawi ya umasiye wako sudzazikumbukanso.
Nie bój się, bo nie zostaniesz zawstydzona, nie rumień się, bo nie doznasz hańby, gdyż zapomnisz o wstydzie swojej młodości i o niesławie swego wdowieństwa już więcej nie wspomnisz.
5 Pakuti Mlengi wako ali ngati mwamuna wako, dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse. Woyerayo wa Israeli ndiye Mpulumutsi wanu; dzina lake ndi Mulungu wa dziko lonse lapansi.
Bo twoim małżonkiem jest twój Stwórca, PAN zastępów – to jego imię, a twoim Odkupicielem jest Święty Izraela – będzie nazywany Bogiem całej ziemi.
6 Yehova wakuyitananso, uli ngati mkazi wosiyidwa ndi wodzaza ndi chisoni mu mtima, mkazi amene anakwatiwa pa unyamata wake kenaka nʼkukanidwa,” akutero Mulungu wako.
PAN bowiem powołał cię jak żonę opuszczoną i przygnębioną na duchu, jak młodą żonę, gdy była porzucona, mówi twój Bóg.
7 “Kwa kanthawi kochepa, Ine ndinakusiya, koma ndidzakutenganso chifukwa ndimakukonda kwambiri.
Na krótką chwilę cię opuściłem, ale w wielkim miłosierdziu przygarniam cię.
8 Ndinakufulatira kwa kanthawi kochepa ndili wokwiya kwambiri. Koma ndi kukoma mtima kwanga kwa muyaya, ndidzakuchitira chifundo,” akutero Yehova Mpulumutsi wako.
W niewielkim gniewie ukryłem na chwilę swoją twarz przed tobą, ale zlituję się nad tobą w wiecznym miłosierdziu, mówi PAN, twój Odkupiciel.
9 “Kwa ine zimenezi zili ngati mmene zinalili mʼnthawi ya Nowa. Monga ndinalumbira nthawi imeneyo kuti sindidzawononganso dziko lapansi ndi madzi. Kotero tsopano ndalumbira kuti sindidzakupseraninso mtima, sindidzakudzudzulaninso.
Jest to bowiem dla mnie tak, jak [było] przy potopie Noego: jak przysięgałem, że wody Noego już więcej nie będą rozlewać się po ziemi, tak [też] przysięgałem, że nie rozgniewam się na ciebie ani nie będę cię gromić.
10 Ngakhale mapiri atagwedezeka ndi zitunda kusunthidwa, koma chikondi changa chosasinthika pa iwe sichidzatha. Pangano langa lamtendere silidzasintha,” akutero Yehova amene amakuchitira chifundo.
A choćby i góry się poruszyły i pagórki się zachwiały, moje miłosierdzie nie odstąpi od ciebie, a przymierze mojego pokoju nie zachwieje się, mówi PAN, który lituje się nad tobą.
11 “Iwe mzinda wozunzika, wokunthidwa ndi namondwe ndiponso wopanda wokutonthoza, Ine ndidzakongoletsa miyala yako. Maziko ako ndidzamanga ndi miyala ya safiro.
O utrapiona, smagana wichrem, niepocieszona! Oto położę twoje kamienie na błyszczących kamieniach, a twoje fundamenty na szafirach.
12 Ndidzamanga nsanja zako zankhondo ndi miyala yokongola ya rubi. Ndidzamanga zipata zako ndi miyala yonyezimira ngati moto, ndipo linga lako lonse lidzakhala la miyala yamtengowapatali.
I uczynię twoje okna z kryształu, twoje bramy z kamienia rubinowego i wszystkie twoje [mury] graniczne z drogich kamieni.
13 Yehova adzaphunzitsa ana ako onse, ndipo ana ako adzakhala ndi mtendere wochuluka.
A wszystkie twoje dzieci będą wyuczone przez PANA, wielki będzie pokój twoich dzieci.
14 Udzakhazikika mʼchilungamo chenicheni: Sudzakhalanso wopanikizika, chifukwa sudzaopa kanthu kalikonse. Sudzakhalanso ndi mantha chifukwa manthawo sadzafika pafupi ndi iwe.
W sprawiedliwości będziesz utwierdzona, będziesz daleka od ucisku, bo nie będziesz się go bać; i od trwogi, bo nie zbliży się do ciebie.
15 Ngati wina adzakuthirani nkhondo, si ndine amene ndachititsa; aliyense amene adzalimbana nanu adzagonja chifukwa cha iwe.
Oto zbiorą się razem, ale nie przeze mnie. Ktokolwiek zbierze się przeciwko tobie, upadnie ze względu na ciebie.
16 “Taona, ndi Ine amene ndinalenga munthu wosula zitsulo amene amakoleza moto wamakala ndi kusula zida zoti azigwiritse ntchito. Ndipo ndine amene ndinalenga munthu wosakaza kuti awononge;
Oto stworzyłem kowala, który dmie na węgiel w ogniu i wyciąga narzędzia do obróbki. Ja stworzyłem też burzyciela, aby niszczył.
17 palibe chida chopangidwa ndi mdani chimene chidzakupweteke, ndipo onse okuneneza pa mlandu udzawatsutsa. Umu ndimo adzapezekere atumiki a Yehova. Chipambano chawo chichokera kwa Ine,” akutero Yehova.
Żadna broń przeciw tobie sporządzona nie będzie skuteczna, a każdy język, który w sądzie występuje przeciw tobie, potępisz. To jest dziedzictwo sług PANA, a ich sprawiedliwość [pochodzi] ode mnie, mówi PAN.

< Yesaya 54 >

A Dove is Sent Forth from the Ark
A Dove is Sent Forth from the Ark